< Levitiko 6 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
And Jehovah spoke to Moses, saying,
2 “Ngati munthu wina aliyense achimwa, nachita zinthu mosakhulupirika kwa Yehova chifukwa cha kunyenga mnzake pokana kumubwezera zimene anamusungitsa, kapena kumubera kapenanso kumulanda,
If a soul sins, and commits a trespass against Jehovah, and deals falsely with his neighbor in a matter of deposit, or of bargain, or of robbery, or have oppressed his neighbor,
3 kapena ndi kunama kuti sanatole chinthu chimene chinatayika, kapena kulumbira mwachinyengo pa chinthu chilichonse chimene munthu akachita amachimwa nacho,
or has found that which was lost, and deal falsely by it, and swears to a lie, in any of all these things that a man does, sinning by it,
4 ndi wopalamula ndithu, ndipo ayenera kubweza zimene anabazo, zimene analanda mwachinyengozo, zimene anamusungitsazo, zimene anatolazo
then it shall be, if he has sinned, and is guilty, that he shall restore that which he took by robbery, or the thing which he has gotten by oppression, or the deposit which was committed to him, or the lost thing which he found,
5 kapena zimene analumbira monyengazo. Pa tsiku limene apezeke kuti wapalamuladi, iye ayenera kumubwezera mwini wake zinthu zonsezi ndi kuwonjezerapo chimodzi mwa zigawo zisanu zilizonse.
or anything about which he has sworn falsely, he shall even restore it in full, and shall add the fifth part more to it. He shall give it to him to whom it pertains, in the day of his being found guilty.
6 Pambuyo pake apereke kwa Yehova nsembe yopalamula. Nsembe yake ikhale nkhosa yayimuna yopanda chilema ndipo mtengo wake wogwirizana ndi nsembe yopepesera machimo.
And he shall bring his trespass offering to Jehovah, a ram without blemish out of the flock, according to thy estimation, for a trespass offering, to the priest.
7 Kenaka wansembe achite mwambo wopepesera tchimo la munthuyo pamaso pa Yehova, ndipo adzakhululukidwa chilichonse chomwe anachita kuti akhale wopalamula.”
And the priest shall make atonement for him before Jehovah, and he shall be forgiven concerning whatever he does so as to be guilty by it.
8 Yehova anawuza Mose kuti,
And Jehovah spoke to Moses, saying,
9 “Lamula Aaroni ndi ana ake kuti, ‘Lamulo la nsembe yopsereza ndi ili: Nsembe yopserezayo izikhala pa moto pa guwa usiku wonse mpaka mmawa, ndipo moto wa paguwapo uzikhala ukuyaka nthawi zonse.
Command Aaron and his sons, saying, This is the law of the burnt offering: The burnt offering shall be on the hearth upon the altar all night to the morning, and the fire of the altar shall be kept burning on it.
10 Tsono wansembe avale mkanjo wake wa nsalu yofewa ndi yosalala. Mʼkati avalenso kabudula wofewa, wosalala. Pambuyo pake atenge phulusa la nyama imene yatenthedwa pa guwa lansembe paja ndi kulithira pambali pa guwa lomwelo.
And the priest shall put on his linen garment, and he shall put his linen breeches upon his flesh, and he shall take up the ashes of the fire which has consumed the burnt offering on the altar, and he shall put them beside the altar.
11 Akatero avule zovala zakezo ndi kuvala zovala zina. Kenaka atulutse phulusalo ndi kukaliyika pa malo woyeretsedwa kunja kwa chithando.
And he shall put off his garments, and put on other garments, and carry forth the ashes outside the camp to a clean place.
12 Moto wa pa guwa uzikhala ukuyaka nthawi zonse, usamazime. Mmawa uliwonse wansembe aziwonjezerapo nkhuni pa motopo ndi kukonza nsembe yopsereza, ndi kutentha mafuta a nsembe yachiyanjano pamenepo.
And the fire upon the altar shall be kept burning on it; it shall not go out. And the priest shall burn wood on it every morning, and he shall lay the burnt offering in order upon it, and shall burn the fat of the peace offerings on it.
13 Moto uzikhala ukuyaka pa guwa nthawi zonse ndipo usazimepo.
Fire shall be kept burning upon the altar continually; it shall not go out.
14 “‘Lamulo la nsembe yachakudya ndi ili: ana a Aaroni azibwera nayo nsembeyo pamaso pa Yehova, patsogolo pa guwa.
And this is the law of the meal offering: The sons of Aaron shall offer it before Jehovah, before the altar.
15 Wansembe mmodzi atapeko dzanja limodzi la ufa wosalala wa nsembe yachakudya ija kuti ukhala ufa wachikumbutso ndi mafuta pamodzi ndi lubani yense amene ali pa nsembe ya chakudyacho, ndipo azitenthe pa guwa kuti zilandiridwe ndi Yehova mʼmalo mwa nsembe yonse kuti zikhale nsembe ya fungo lokomera Yehova.
And he shall take up his handful from it, of the fine flour of the meal offering, and of the oil of it, and all the frankincense which is upon the meal offering, and shall burn it upon the altar for a sweet savor, as the memorial of it, to Jehovah.
16 Aaroni ndi ana ake azidya zimene zatsala koma azidya zopanda yisiti ku malo wopatulika, ku bwalo la tenti ya msonkhano.
And that which is left of it Aaron and his sons shall eat. It shall be eaten without leaven in a holy place. They shall eat it in the court of the tent of meeting.
17 Poziphika asathire yisiti. Ndawapatsa zotsalazo kuti zikhale gawo lawo la nsembe zanga zopsereza. Zonsezi ndi zopatulika kwambiri monga nsembe yopepesera tchimo ndiponso nsembe yopepesera machimo.
It shall not be baked with leaven. I have given it as their portion of my offerings made by fire, it is most holy, as the sin offering, and as the trespass offering.
18 Mwana aliyense wamwamuna wa Aaroni azidyako za nsembe zopsereza zopereka kwa Yehova. Ndi gawo lake lokhazikika la chopereka chopsereza kwa Yehova pa mibado yanu yonse. Chilichonse chimene chidzakhudza nsembezo chidzakhala chopatulika.’”
Every male among the sons of Aaron shall eat of it, as a portion forever throughout your generations, from the offerings of Jehovah made by fire. Whoever touches them shall be holy.
19 Yehova anawuzanso Mose kuti,
And Jehovah spoke to Moses, saying,
20 “Nsembe imene Aaroni ndi ana ake ayenera kupereka kwa Yehova pa tsiku limene wansembe akudzozedwa ndi iyi: ufa wosalala kilogalamu imodzi ngati chopereka chachakudya cha nthawi zonse. Azipereka theka limodzi mmawa ndipo theka linalo madzulo.
This is the oblation of Aaron and of his sons, which they shall offer to Jehovah in the day when he is anointed: the tenth part of an ephah of fine flour for a meal offering perpetually, half of it in the morning, and half of it in the evening.
21 Ipangidwe ndi mafuta pa chiwaya ndipo ubwere nayo ili yosakaniza bwino, yophikidwa mitandamitanda monga amachitira ndi nsembe yachakudya. Iphikidwe moti itulutse fungo lokomera Yehova.
It shall be made with oil on a baking-pan. Thou shall bring it in when it is soaked. Thou shall offer the meal offering in baked pieces for a sweet savor to Jehovah.
22 Mwana wa fuko la Aaroni amene adzadzozedwe kukhala wansembe kulowa mʼmalo mwa Aaroni ndiye amene azidzakonza ndi kupereka nsembeyi kwa Yehova nthawi zonse monga kunalembedwera.
And the anointed priest who shall be in his stead from among his sons shall offer it. It shall be wholly burnt to Jehovah by a statute forever.
23 Nsembe iliyonse yachakudya ya wansembe izitenthedwa kwathunthu, isamadyedwe.”
And every meal offering of the priest shall be wholly burnt; it shall not be eaten.
24 Yehova anawuza Mose kuti
And Jehovah spoke to Moses, saying,
25 “Uza Aaroni ndi ana ake kuti, ‘Malamulo a nsembe ya tchimo ndi awa: Nsembeyi iziphedwa pamaso pa Yehova pa malo pamene mumaphera nsembe yopsereza popeza ndi nsembe yopatulika.
Speak to Aaron and to his sons, saying, This is the law of the sin offering: In the place where the burnt offering is killed the sin offering shall be killed before Jehovah. It is most holy.
26 Wansembe amene apereke nsembeyi adyere ku malo wopatulika ndiye kuti mʼbwalo la tenti ya msonkhano.
The priest who offers it for sin shall eat it. It shall be eaten in a holy place, in the court of the tent of meeting.
27 Chilichonse chimene chidzakhudza nsembeyo chidzakhala chopatulika, ndipo ngati magazi ake agwera pa chovala, muchape chovalacho pa malo opatulika.
Whatever shall touch the flesh of it shall be holy. And when there is of the blood sprinkled upon any garment, thou shall wash that on which it was sprinkled in a holy place.
28 Mʼphika wadothi umene aphikira nyamayo auphwanye. Koma ngati yaphikidwa mu mʼphika wa mkuwa, awukweche ndi kuwutsukuluza ndi madzi.
But the earthen vessel in which it is boiled shall be broken, and if it be boiled in a brazen vessel, it shall be scoured, and rinsed in water.
29 Munthu wamwamuna aliyense wa mʼbanja la wansembe angathe kuyidya popeza nsembeyi ndi yopatulika kwambiri.
Every male among the priests shall eat of it. It is most holy.
30 Koma nsembe yopepesera tchimo imene magazi ake amabwera nawo mu tenti ya msonkhano kudzachita mwambo wopepesera tchimo ku malo opatulika isadyedwe, mʼmalo mwake itenthedwe.’”
And no sin offering, from which any of the blood is brought into the tent of meeting to make atonement in the holy place, shall be eaten; it shall be burnt with fire.

< Levitiko 6 >