< Eksodo 35 >

1 Mose anasonkhanitsa gulu lonse la Aisraeli ndipo anawawuza kuti, “Zinthu zimene Yehova wakulamulirani kuti muzichite ndi izi:
And Moses assembled all the congregation of the sons of Israel, and said to them, These are the words which Jehovah has commanded, that ye should do them.
2 Muzigwira ntchito zanu pa masiku asanu ndi limodzi, koma tsiku la chisanu ndi chiwiri likhale la Sabata, tsiku lanu lopuma, lopatulika kwa Yehova. Aliyense amene adzagwira ntchito iliyonse pa tsikuli ayenera kuphedwa.
Six days work shall be done, but on the seventh day there shall be to you a holy day, a sabbath of solemn rest to Jehovah. Whoever does any work in it shall be put to death.
3 Pa tsiku la Sabata musakoleze moto paliponse pamene mukhala.”
Ye shall kindle no fire throughout your habitations upon the sabbath day.
4 Mose ananena kwa gulu lonse la Aisraeli kuti, “Zimene Yehova wakulamulirani ndi izi:
And Moses spoke to all the congregation of the sons of Israel, saying, This is the thing which Jehovah commanded, saying,
5 Kuchokera pa zomwe muli nazo, mutenge chopereka cha Yehova. Aliyense amene ali ndi mtima wofuna kupereka abweretse kwa Yehova zopereka izi: Golide, siliva ndi mkuwa;
Take ye from among you an offering to Jehovah. Whoever is of a willing heart, let him bring it-Jehovah's offering: gold, and silver, and brass,
6 nsalu zobiriwira, zapepo, zofiira, nsalu zofewa; ubweya wambuzi;
and blue, and purple, and scarlet, and fine linen, and goats' hair,
7 zikopa za nkhosa zazimuna za utoto wofiira ndi zikopa za akatumbu; matabwa amtengo wa mkesha,
and rams' skins dyed red, and certain skins, and acacia wood,
8 mafuta anyale a olivi, zonunkhiritsa mafuta odzozera ndi zopangira lubani wonunkhira;
and oil for the light, and spices for the anointing oil, and for the sweet incense,
9 miyala yokongola ya mtundu wa onikisi ndi ina yabwino yoyika pa Efodi ndi pa chovala cha pachifuwa.
and onyx stones, and stones to be set, for the ephod, and for the breastplate.
10 “Anthu onse aluso pakati panu abwere ndi kupanga zonse zimene Yehova walamula:
And let every wise-hearted man among you come, and make all that Jehovah has commanded:
11 Chihema ndi tenti yake ndiponso chophimba chake, ngowe zake, maferemu ake, mitanda yake, mizati yake ndi matsinde ake;
the tabernacle, its tent, and its covering, its clasps, and its boards, its bars, its pillars, and its sockets,
12 Bokosi la Chipangano pamodzi ndi mitengo yake yonyamulira ndiponso chovundikira chake cha bokosilo ndi nsalu zophimba bokosilo;
the ark, and the staves of it, the mercy-seat, and the veil of the screen,
13 tebulo pamodzi ndi mitengo yake yonyamulira pamodzi ndi zipangizo zake zonse ndiponso buledi wokhala pamaso pa Yehova;
the table, and its staves, and all its vessels, and the showbread,
14 choyikapo nyale yowunikira pamodzi ndi zipangizo zake, nyale ndi mafuta anyalezo;
the lampstand also for the light, and its vessels, and its lamps, and the oil for the light,
15 guwa lofukizira lubani pamodzi ndi mitengo yake yonyamulira, mafuta odzozera ndi lubani onunkhira; nsalu yotchinga pa khomo lolowera mʼchihema;
and the altar of incense, and its staves, and the anointing oil, and the sweet incense, and the screen for the door, at the door of the tabernacle,
16 guwa lansembe yopsereza pamodzi ndi sefa yamkuwa, mitengo yake yonyamulira ndi zipangizo zake zonse, beseni losambira lamkuwa ndi miyendo yake;
the altar of burnt offering, with its grating of brass, its staves, and all its vessels, the laver and its base,
17 nsalu yotchingira bwalo pamodzi ndi mizati yake ndi matsinde ake, ndiponso nsalu yotchingira pa khomo lolowera ku bwalo;
the hangings of the court, the pillars of it, and their sockets, and the screen for the gate of the court,
18 zikhomo za tenti ya chihema ndiponso za bwalo, ndi zingwe zake;
the pegs of the tabernacle, and the pegs of the court, and their cords,
19 zovala zolukidwa zovala potumikira kumalo opatulika, zovala zopatulika za wansembe, Aaroni pamodzi ndi za ana ake aamuna pamene akutumikira monga ansembe.”
the finely wrought garments, for ministering in the holy place, the holy garments for Aaron the priest, and the garments of his sons, to minister in the priest's office.
20 Kenaka gulu lonse la Aisraeli linachoka pamaso pa Mose,
And all the congregation of the sons of Israel departed from the presence of Moses.
21 ndipo aliyense amene anakhudzidwa mu mtima mwake nafuna kupereka, anabwera kudzapereka chopereka kwa Yehova cha ntchito yokonza tenti ya msonkhano, cha ntchito zonse za mʼtentimo ndi cha zovala zopatulika.
And they came, everyone whose heart stirred him up, and everyone whom his spirit made willing, and brought Jehovah's offering, for the work of the tent of meeting, and for all the service of it, and for the holy garments.
22 Onse amene anali ndi mtima wofuna, amuna ndi amayi omwe anabwera kudzapereka zodzikometsera zagolide za mtundu uliwonse: zomangira zovala, ndolo, mphete ndi zokometsera. Onse anapereka golide wawo monga nsembe yoweyula pamaso pa Yehova.
And they came, both men and women, as many as were willing-hearted, and brought brooches, and earrings, and signet-rings, and armlets, all jewels of gold, even every man who offered an offering of gold to Jehovah.
23 Aliyense amene anali ndi nsalu ya mtundu wa mtambo, yapepo kapena yofiira kapena yofewa, yosalala, kapena ubweya wambuzi, zikopa za nkhosa zonyika mu utoto wofiira kapena zikopa anazibweretsa.
And every man, with whom was found blue, and purple, and scarlet, and fine linen, and goats' hair, and rams' skins dyed red, and certain skins, brought them.
24 Onse amene anapereka chopereka cha siliva kapena mkuwa anabweretsa monga chopereka kwa Yehova. Ndipo aliyense amene anali ndi matabwa a mtengo wa mkesha kuti awagwiritse ntchito mbali ina iliyonse ya ntchitoyo, anabweretsa.
Everyone who offered an offering of silver and brass brought Jehovah's offering, and every man, with whom was found acacia wood for any work of the service, brought it.
25 Mayi aliyense waluso analuka ndi manja ake ndi kubweretsa chomwe analuka cha mtundu wa mtambo, chapepo kapena chofiira kapena chofewa, chosalala.
And all the women who were wise-hearted spun with their hands, and brought that which they had spun: the blue, and the purple, the scarlet, and the fine linen.
26 Ndipo amayi onse amene anali ndi mtima wofuna ndipo anali ndi luso analuka ubweya wa mbuzi.
And all the women whose heart stirred them up in wisdom spun the goats' hair.
27 Atsogoleri anabweretsa miyala ya onikisi ndi miyala yokongola yoyika pa efodi ndi chovala chapachifuwa.
And the rulers brought the onyx stones, and the stones to be set, for the ephod, and for the breastplate,
28 Anabweretsanso zonunkhiritsa ndiponso mafuta owunikira a olivi ndi odzozera ndi zofukizira zonunkhira.
and the spice, and the oil, for the light, and for the anointing oil, and for the sweet incense.
29 Aisraeli onse aamuna ndi aakazi amene anali ndi mtima wofuna, anabweretsa kwa Yehova chopereka chaufulu ku ntchito yonse ya Yehova imene analamulira kudzera mwa Mose kuti achite.
The sons of Israel brought a freewill offering to Jehovah, every man and woman, whose heart made them willing to bring for all the work, which Jehovah had commanded to be made by Moses.
30 Kenaka Mose anati kwa Aisraeli, “Taonani, Yehova wasankha Bezaleli mwana wa Uri, mwana wa Huri, wa fuko la Yuda,
And Moses said to the sons of Israel, See, Jehovah has called by name Bezalel the son of Uri, the son of Hur, of the tribe of Judah.
31 ndipo wamudzaza ndi Mzimu wa Mulungu kotero kuti ali ndi luso ndi nzeru zomvetsa zinthu, ndipo akudziwa bwino ntchito zonse zamanja monga izi:
And he has filled him with the Spirit of God, in wisdom, in understanding, and in knowledge, and in all manner of workmanship,
32 Kulemba ndondomeko ya ntchito zaluso ndi kupanga zinthu zagolide, zasiliva ndi zamkuwa,
and to devise skilful works, to work in gold, and in silver, and in brass,
33 kusema ndi kuyika miyala yokongola, kukonza zinthu zamatabwa ndiponso kugwira ntchito ina iliyonse yamanja.
and in cutting of stones for setting, and in carving of wood, to work in all manner of skilful workmanship.
34 Ndipo Iye wapereka kwa Bezaleli pamodzi ndi Oholiabu mwana wa Ahisamaki, wa fuko la Dani luso lophunzitsa ena.
And he has put in his heart that he may teach, both he, and Oholiab, the son of Ahisamach, of the tribe of Dan.
35 Mulungu wawapatsa maluso osiyanasiyana, maluso ogoba, olemba ndondomeko, opeta zokometsera pa nsalu zamtundu wamtambo, zapepo ndi zofiira ndiponso zofewa zosalala ndi zoluka. Onsewa ndi amisiri a ntchito zamanja ndi zokonza ndondomeko.
He has filled them with wisdom of heart, to work all manner of workmanship, of the engraver, and of the skilful workman, and of the embroiderer, in blue, and in purple, in scarlet, and in fine linen, and of the weaver, even of those who do any workmanship, and of those who devise skilful works.

< Eksodo 35 >