< Levitiko 4 >

1 Yehova anayankhula ndi Mose kuti,
And Jehovah spoke to Moses, saying,
2 “Awuze Aisraeli kuti, ‘Munthu akachimwa mosadziwa ndi kuchita chilichonse chimene Yehova walamula kuti asachite, azichita izi:
Speak to the sons of Israel, saying, If a soul shall sin unwittingly, in any of the things which Jehovah has commanded not to be done, and shall do any one of them,
3 “‘Ngati wansembe wodzozedwa achimwa, ndi kuchimwitsa anthu onse, iyeyu ayenera kupereka mwana wangʼombe wamphongo wopanda chilema chifukwa cha tchimo limene wachitalo. Imeneyi ndi nsembe ya Yehova yopepesera tchimo lake.
if the anointed priest shall sin so as to bring guilt on the people, then let him offer for his sin, which he has sinned, a young bullock without blemish to Jehovah for a sin offering.
4 Wansembeyo abwere nayo ngʼombeyo pa khomo la tenti ya msonkhano pamaso pa Yehova. Asanjike dzanja lake pamutu pa ngʼombeyo ndipo ayiphe pamaso pa Yehova.
And he shall bring the bullock to the door of the tent of meeting before Jehovah. And he shall lay his hand upon the head of the bullock, and kill the bullock before Jehovah.
5 Kenaka wansembe wodzozedwa atengeko magazi a ngʼombeyo ndi kulowa nawo mu tenti ya msonkhano.
And the anointed priest shall take of the blood of the bullock, and bring it to the tent of meeting.
6 Iye aviyike chala chake mʼmagazi, ndipo awawaze kasanu ndi kawiri pamaso pa Yehova, patsogolo pa katani yotchinga malo wopatulika.
And the priest shall dip his finger in the blood, and sprinkle of the blood seven times before Jehovah, before the veil of the sanctuary.
7 Kenaka wansembe apake magaziwo pa nyanga za guwa lofukizira lubani limene lili pamaso pa Yehova mu tenti ya msonkhano. Magazi ena otsalawo awathire pa tsinde pa guwa lansembe zopsereza, limene lili pa khomo la tenti ya msonkhano.
And the priest shall put of the blood upon the horns of the altar of sweet incense before Jehovah, which is in the tent of meeting, and all the blood of the bullock he shall pour out at the base of the altar of burnt offering, which is at the door of the tent of meeting.
8 Pambuyo pake achotse mafuta onse a ngʼombe yayimuna yopepesera machimoyo: mafuta okuta zamʼkati kapena mafuta onse amʼkatimo.
And all the fat of the bullock of the sin offering he shall take off from it. The fat that covers the innards, and all the fat that is upon the innards,
9 Achotsenso ndi kubwera ndi impsyo zonse ziwiri pamodzi ndi mafuta onse ndiponso mafuta onse amene aphimba chiwindi ndi impsyo
and the two kidneys, and the fat that is upon them, which is by the loins, and the caul upon the liver, with the kidneys, he shall take away,
10 monga momwe amachotsera mafuta a ngʼombe yoperekedwa kuti ikhale chopereka chachiyanjano. Tsono wansembe atenthe zimenezi pa guwa lansembe zopsereza.
as it is taken off from the ox of the sacrifice of peace offerings. And the priest shall burn them upon the altar of burnt offering.
11 Koma chikopa cha ngʼombe yayimunayo ndi mnofu wake wonse, pamodzi ndi mutu ndi miyendo, zamʼkati ndi matumbo,
And the skin of the bullock, and all its flesh, with its head, and with its legs, and its innards, and its dung,
12 kapena kuti ngʼombe yonse yotsalayo apite nayo kunja kwa msasa ku malo woyeretsedwa, kumene amatayako phulusa ndi kuyitentha pa nkhuni, pa phulusapo.
even the whole bullock he shall carry forth outside the camp to a clean place, where the ashes are poured out, and burn it on wood with fire. It shall be burnt where the ashes are poured out.
13 “‘Ngati gulu lonse la Aisraeli lichimwa mosadziwa, nachita chomwe ndi choletsedwa ndi Yehova, ngakhale kuti gulu lonselo silikudziwa kuti lachimwa, anthuwo ndi olakwa ndithu.
And if the whole congregation of Israel err, and the thing be hid from the eyes of the assembly, and they have done any of the things which Jehovah has commanded not to be done, and are guilty,
14 Akazindikira tchimo limene achita, gulu lonse lipereke mwana wangʼombe wamphongo kuti akhale chopereka chopepesera tchimo ndipo abwere naye pa khomo la tenti ya msonkhano.
when the sin by which they have sinned is known, then the assembly shall offer a young bullock for a sin offering, and bring it before the tent of meeting.
15 Akuluakulu a anthuwo asanjike manja awo pa mutu pa ngʼombe pamaso pa Yehova, ndipo ayiphe pomwepo pamaso pa Yehova.
And the elders of the congregation shall lay their hands upon the head of the bullock before Jehovah, and the bullock shall be killed before Jehovah.
16 Tsono wansembe wodzozedwa atengeko magazi a ngʼombeyo ndi kulowa nawo mu tenti ya msonkhano.
And the anointed priest shall bring of the blood of the bullock to the tent of meeting.
17 Aviyike chala chake mʼmagaziwo ndi kuwawaza pamaso pa Yehova kasanu ndi kawiri patsogolo pa nsalu yotchinga.
And the priest shall dip his finger in the blood, and sprinkle it seven times before Jehovah, before the veil.
18 Pambuyo pake iye apake magaziwo pa nyanga za guwa limene lili pamaso pa Yehova mu tenti ya msonkhano. Magazi ena otsalawo awathire pa tsinde pa guwa lansembe zopsereza limene lili pa khomo la tenti ya msonkhano.
And he shall put of the blood upon the horns of the altar which is before Jehovah, that is in the tent of meeting, and all the blood he shall pour out at the base of the altar of burnt offering, which is at the door of the tent of meeting.
19 Kenaka achotse mafuta onse a ngʼombeyo ndi kuwatentha pa guwa,
And all the fat of it he shall take off from it, and burn it upon the altar.
20 ndipo achite ndi ngʼombe yayimunayi monga anachitira ndi ngʼombe yayimuna yopepesera machimo. Potero, wansembe adzapereka nsembe yopepesera anthu, ndipo machimo awo adzakhululukidwa.
Thus he shall do with the bullock, as he did with the bullock of the sin offering, so he shall do with this. And the priest shall make atonement for them, and they shall be forgiven.
21 Kenaka atulutse ngʼombeyo kunja kwa msasa ndi kuyitentha monga anatenthera ngʼombe yoyamba ija. Imeneyi ndiyo nsembe yopepesera machimo a gulu lonse.
And he shall carry forth the bullock outside the camp, and burn it as he burned the first bullock. It is the sin offering for the assembly.
22 “‘Ngati mtsogoleri achimwa mosadziwa nachita zimene ndi zoletsedwa ndi Yehova Mulungu wake, ndiye kuti wapalamula.
When a ruler sins, and does unwittingly any one of all the things which Jehovah his God has commanded not to be done, and is guilty,
23 Ndipo ngati wauzidwa za tchimo limene wachita, iye abwere ndi mbuzi yayimuna yopanda chilema kuti ikhale chopereka chake.
if his sin, by which he has sinned, be made known to him, he shall bring for his oblation a goat, a male without blemish.
24 Asanjike dzanja lake pa mutu wa mbuziyo ndi kuyiphera pamalo pamene amaphera zopereka zopsereza pamaso pa Yehova. Ichi ndi chopereka chopepesera tchimo.
And he shall lay his hand upon the head of the goat, and kill it in the place where they kill the burnt offering before Jehovah. It is a sin offering.
25 Pambuyo pake wansembe atengeko magazi a chopereka chopepesera tchimocho ndi chala chake, ndipo awapake pa nyanga za guwa lansembe zopsereza. Athire magazi otsalawo pa tsinde la guwalo.
And the priest shall take of the blood of the sin offering with his finger, and put it upon the horns of the altar of burnt offering, and the blood of it he shall pour out at the base of the altar of burnt offering.
26 Wansembeyo atenthe mafuta onse pa guwapo monga amatenthera chopereka chachiyanjano. Pochita zimenezi, wansembe adzapereka nsembe yopepesera tchimo la munthuyo, ndipo adzakhululukidwa.
And all the fat of it he shall burn upon the altar, as the fat of the sacrifice of peace offerings. And the priest shall make atonement for him as concerning his sin, and he shall be forgiven.
27 “‘Ngati munthu wamba achimwa mosadziwa nachita zimene ndi zoletsedwa ndi Yehova, ndiye kuti wapalamula.
And if any soul of the common people sin unwittingly, in doing any of the things which Jehovah has commanded not to be done, and be guilty,
28 Ndipo ngati wauzidwa za tchimo limene wachita, abweretse mbuzi yayikazi yopanda chilema kuti ikhale chopereka chopepesera tchimo.
if his sin, which he has sinned, be made known to him, then he shall bring for his oblation a goat, a female without blemish, for his sin which he has sinned.
29 Asanjike dzanja lake pamutu pa mbuziyo ndipo ayiphe pamalo pamene amaphera chopereka chopsereza.
And he shall lay his hand upon the head of the sin offering, and kill the sin offering in the place of burnt offering.
30 Ndipo wansembe atenge magazi ndi chala chake ndi kuwapaka pa nyanga za guwa lansembe zopsereza ndi kuthira magazi wotsalawo pa tsinde la guwalo.
And the priest shall take of the blood of it with his finger, and put it upon the horns of the altar of burnt offering, and all the blood of it he shall pour out at the base of the altar.
31 Kenaka iye achotse mafuta onse monga momwe anachotsera mafuta a chopereka chachiyanjano, ndipo awatenthe pa guwa kuti akhale fungo lokomera Yehova. Potero, wansembe adzapereka nsembe yopepesera tchimo la munthuyo ndipo adzakhululukidwa.
And all the fat of it he shall take away, as the fat is taken away from off the sacrifice of peace offerings, and the priest shall burn it upon the altar for a sweet savor to Jehovah. And the priest shall make atonement for him, and he shall be forgiven.
32 “‘Ngati munthu apereka mwana wankhosa ngati chopereka chopepesera tchimo lake, abwere ndi mwana wankhosa wamkazi wopanda chilema.
And if he brings a lamb as his oblation for a sin offering, he shall bring it a female without blemish.
33 Asanjike dzanja lake pa mutu wa mwana wankhosayo ndipo amuphe pamalo pamene amaphera chopereka chopsereza.
And he shall lay his hand upon the head of the sin offering, and kill it for a sin offering in the place where they kill the burnt offering.
34 Kenaka wansembe atengeko ndi chala chake magazi a mwana wankhosa uja ndi kuwapaka pa nyanga za guwa lansembe zopsereza. Magazi otsalawo athire pa tsinde la guwalo.
And the priest shall take of the blood of the sin offering with his finger, and put it upon the horns of the altar of burnt offering, and all the blood of it he shall pour out at the base of the altar.
35 Iye achotse mafuta onse, monga amachotsera mafuta a mwana wankhosa wa chopereka chachiyanjano, ndipo wansembe awatenthe pa guwa pamodzi ndi zopereka zina zopsereza za Yehova. Potero, wansembe adzapereka nsembe yopepesera tchimo limene munthuyo anachita ndipo adzakhululukidwa.
And all the fat of it he shall take away, as the fat of the lamb is taken away from the sacrifice of peace offerings, and the priest shall burn them on the altar, upon the offerings of Jehovah made by fire. And the priest shall make atonement for him concerning his sin that he has sinned, and he shall be forgiven.

< Levitiko 4 >