< Oweruza 3 >

1 Iyi ndi mitundu ya anthu yomwe Yehova anayisiya kuti ayese nayo Aisraeli amene sanadziwe kumenya nkhondo mu Kanaani
Now these are the nations which Jehovah left to prove Israel by them, (even as many of Israel as had not known all the wars of Canaan,
2 (Yehova anachita izi kuti Aisraeli onse aphunzire kumenya nkhondo; makamaka amene nʼkale lonse sanadziwe kumenya nkhondo.
only that the generations of the sons of Israel might know, to teach them war, at least to such as formerly knew nothing of that):
3 Mitundu ya anthuyo ndi: Mafumu asanu a Afilisti, Akanaani onse, Asidoni, ndi Ahivi amene ankakhala ku mapiri a Lebanoni kuyambira ku phiri la Baala-Herimoni mpaka ku Lebo Hamati.
namely, the five lords of the Philistines, and all the Canaanites, and the Sidonians, and the Hivites that dwelt in mount Lebanon, from mount Baal-hermon to the entrance of Hamath.
4 Iwowa Yehova anawasiya kuti aziyesa nawo Aisraeli kuti aone ngati angamvere malamulo a Yehova, amene anapatsa makolo awo kudzera mwa Mose.
And they were left, to prove Israel by them, to know whether they would hearken to the commandments of Jehovah, which he commanded their fathers by Moses.
5 Choncho Aisraeli anakhala pakati pa Akanaani, Ahiti, Aamori, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi.
And the sons of Israel dwelt among the Canaanites, the Hittites, and the Amorites, and the Perizzites, and the Hivites, and the Jebusites.
6 Tsono Aisraeli aja amalola ana awo aamuna ndi aakazi kuti azikwatira ndi kukwatiwa ndi anthu amitundu ina. Kenaka anayamba kupembedza milungu yawo.
And they took their daughters to be their wives, and gave their own daughters to their sons and served their gods.
7 Aisraeli anachita zinthu zoyipira Yehova. Iwowa anayiwala Yehova Mulungu wawo ndi kumatumikira Abaala ndi Asera.
And the sons of Israel did that which was evil in the sight of Jehovah, and forgot Jehovah their God, and served the Baalim and the Asheroth.
8 Choncho Yehova anawapsera mtima Aisraeliwo ndipo anawagulitsa kwa Kusani-Risataimu mfumu ya ku Mesopotamiya. Choncho Aisraeli anakhala pansi pa ulamuliro wake zaka zisanu ndi zitatu.
Therefore the anger of Jehovah was kindled against Israel, and he sold them into the hand of Cushan-rishathaim king of Mesopotamia, And the sons of Israel served Cushan-rishathaim eight years.
9 Koma pamene Aisraeliwo analirira kwa Yehova, Iye anawawutsira mpulumutsi, Otanieli mwana wamwamuna wa Kenazi, mngʼono wake wa Kalebe. Iyeyu ndiye anawapulumutsa.
And when the sons of Israel cried to Jehovah, Jehovah raised up a savior to the sons of Israel, who saved them, even Othniel the son of Kenaz, Caleb's younger brother.
10 Mzimu wa Yehova unatsika pa iye, choncho anasanduka mtsogoleri wa Israeli. Iye anapita kukamenya nkhondo, ndipo Yehova anapereka Kusani-Risataimu mfumu ya Aaramu mʼmanja mwake. Choncho anayigonjetsa.
And the Spirit of Jehovah came upon him, and he judged Israel. And he went out to war, and Jehovah delivered Cushan-rishathaim king of Mesopotamia into his hand, and his hand prevailed against Cushan-rishathaim.
11 Ndipo mʼdzikomo munakhala mtendere zaka makumi anayi. Kenaka Otanieli mwana wa Kenazi anamwalira.
And the land had rest forty years. And Othniel the son of Kenaz died.
12 Aisraeli anachitanso zinthu zoyipira Yehova. Tsono Yehova anapatsa mphamvu Egiloni, mfumu ya Mowabu kuti alimbane ndi Aisraeli aja popeza anachita zinthu zoyipira Yehova.
And the sons of Israel again did that which was evil in the sight of Jehovah. And Jehovah strengthened Eglon the king of Moab against Israel because they had done that which was evil in the sight of Jehovah.
13 Egiloniyo anamemeza Aamori ndi Aamaleki kupita kukamenyana ndi Israeli, ndipo analanda Yeriko, mzinda wa migwalangwa.
And he gathered to him the sons of Ammon and Amalek, and he went and smote Israel, and they possessed the city of palm trees.
14 Aisraeli anatumikira ngati akapolo Egiloni mfumu ya Mowabu kwa zaka 18.
And the sons of Israel served Eglon the king of Moab eighteen years.
15 Aisraeli analiranso kwa Yehova, ndipo Iye anawawutsira mpulumutsi, Ehudi. Iyeyu anali mwana wa Gera, munthu wamanzere, wa fuko la Benjamini. Aisraeli ankatumiza msonkho kwa Egiloni, mfumu ya Mowabu, kudzera kwa Ehudi.
But when the sons of Israel cried to Jehovah, Jehovah raised up for them a savior, Ehud the son of Gera, the Benjamite, a left-handed man. And the sons of Israel sent tribute by him to Eglon the king of Moab.
16 Ndipo Ehudi anapanga lupanga lakuthwa kuwiri lotalika masentimita makumi asanu, ndipo anamangirira lupangalo pa ntchafu yake ya kumanja mʼkati mwa zovala zake.
And Ehud made for himself a sword which had two edges, a cubit in length. And he girded it under his raiment upon his right thigh.
17 Iye anakapereka msonkho kwa Egiloni, mfumu ya Mowabu, amene anali munthu wonenepa kwambiri.
And he offered the tribute to Eglon king of Moab. Now Eglon was a very fat man.
18 Ehudi atapereka msonkhowo, anawuza anthu amene ananyamula msonkhowo kuti azipita.
And when he had made an end of offering the tribute, he sent away the men who bore the tribute.
19 Iye mwini anabwerera pamalo a miyala yozokotedwa ku Giligala ndipo anati, “Zikomo mfumu, ine ndili ndi mawu achinsinsi kuti ndikuwuzeni.” Mfumuyo inawuza onse amene amayitumikira kuti akhale chete, ndipo kenaka anawatulutsa.
But he himself turned back from the quarries that were by Gilgal, and said, I have a secret errand to thee, O king. And he said, Keep silence. And all who stood by him went out from him.
20 Kenaka Ehudi anayandikira pafupi ndi mfumuyo, ndipo iyo inakhala yokha mʼchipinda chapamwamba, mozizira bwino. Tsono Ehudi anati, “Ndili ndi mawu ochokera kwa Mulungu woti ndikuwuzeni.” Mfumuyo itadzuka pa mpando wake waufumu,
And Ehud came to him. And he was sitting by himself alone in the cool upper room. And Ehud said, I have a message from God to thee. And he arose out of his seat.
21 Ehudi ndi dzanja lake lamanzere, anasolola lupanga pa ntchafu yake ya kumanja ndi kubaya nalo mfumuyo pa mimba.
And Ehud put forth his left hand, and took the sword from his right thigh, and thrust it into his body.
22 Lupanga linalowa mʼmimba pamodzi ndi chogwirira chake. Mafuta anaphimba lupangalo popeza silinatulutsidwe mʼmimbamo. Ndiponso matumbo anatuluka.
And the handle also went in after the blade, and the fat closed upon the blade, for he did not draw the sword out of his body, and it came out behind.
23 Kenaka Ehudi anatuluka panja pa khonde, atatseka ndi kukhoma zitseko za chipinda chapamwambacho.
Then Ehud went forth into the porch, and shut the doors of the upper room upon him, and locked them.
24 Ehudi atachoka, atumiki a mfumu aja anabwera, ndipo ataona kuti zitseko za chipinda chapamwamba zinali zokhoma anaganiza kuti mwina mfumu ikudzithandiza mʼkatimo.
Now when he was gone out, his servants came, and they saw, and, behold, the doors of the upper room were locked. And they said, Surely he is covering his feet in the upper chamber.
25 Iwo anadikira nthawi yayitali koma popanda chochitika. Koma ataona kuti mfumuyo sikutsekulabe zitseko za chipindacho, iwo anatenga makiyi ndi kutsekula zitsekozo, ndipo anangoona mbuye wawo atagwera pansi, ali wakufa.
And they delayed till they were ashamed, and, behold, he did not open the doors of the upper room. Therefore they took the key, and opened, and, behold, their lord was fallen down dead on the earth.
26 Ehudi anathawa pamene iwo ankadikira. Iye anadzera ku malo a miyala yozokotedwa kuja ndi kuthawa kupita ku Seiri.
And Ehud escaped while they delayed, and passed beyond the quarries, and escaped to Seirah.
27 Atafika kumeneko, anayimba lipenga ku dziko la ku mapiri la Efereimu. Iye akutsogolera, Aisraeli onse anatsika naye pamodzi kuchoka ku mapiriko.
And it came to pass, when he came, that he blew a trumpet in the hill-country of Ephraim. And the sons of Israel went down with him from the hill-country, and he before them.
28 Iye anawawuza kuti, “Nditsatireni, chifukwa Yehova wapereka Amowabu, adani anu mʼmanja mwanu.” Choncho anthuwo anamutsatira, nalanda madooko a Yorodani opita ku Mowabu. Iwo sanalole kuti wina aliyense awoloke.
And he said to them, Follow after me, for Jehovah has delivered your enemies the Moabites into your hand. And they went down after him, and took the fords of the Jordan against the Moabites, and did not allow a man to pass over.
29 Nthawi imeneyo anapha Amowabu pafupifupi 10,000. Ophedwawo anali anthu amphamvu komanso odziwa kumenya nkhondo, ndipo panalibe ndi mmodzi yemwe anathawa.
And they smote about ten thousand men of Moab at that time, every robust man, and every man of valor, and there escaped not a man.
30 Tsiku limenelo Amowabu anakhala pansi pa ulamuliro wa Israeli, ndipo dzikolo linakhala pa mtendere kwa zaka 80.
So Moab was subdued that day under the hand of Israel. And the land had rest eighty years.
31 Ehudi atamwalira, panabwera Samugara mwana wa Anati. Iye anapha Afilisti 600 ndi ndodo yomenyera ngʼombe. Nayenso anapulumutsa Israeli.
And after him was Shamgar the son of Anath, who smote six hundred men of the Philistines with an ox-goad, and he also saved Israel.

< Oweruza 3 >