< Oweruza 4 >

1 Ehudi atamwalira, Aisraeli anachitanso zinthu zoyipira Yehova.
And the sons of Israel again did that which was evil in the sight of Jehovah, when Ehud was dead.
2 Choncho Yehova anawapereka mʼmanja mwa Yabini, mfumu ya ku Kanaani, imene inkalamulira ku Hazori. Mkulu wa ankhondo ake anali Sisera, amene ankakhala ku Haroseti-Hagoyimu.
And Jehovah sold them into the hand of Jabin king of Canaan who reigned in Hazor, the captain of whose army was Sisera who dwelt in Harosheth of the Gentiles.
3 Aisraeli analira kwa Yehova kuti awathandize, chifukwa Sisera anali ndi magaleta achitsulo 900 ndipo anazunza Aisraeli mwankhanza kwa zaka makumi awiri.
And the sons of Israel cried to Jehovah, for he had nine hundred chariots of iron, and he mightily oppressed the sons of Israel twenty years.
4 Debora, mneneri wamkazi, mkazi wake wa Rapidoti ndiye ankatsogolera Israeli nthawi imeneyo.
Now Deborah, a prophetess, the wife of Lappidoth, she judged Israel at that time.
5 Iye ankakhala pansi pa mtengo wa mgwalangwa wa Debora, pakati pa Rama ndi Beteli mʼdziko la ku mapiri la Efereimu, ndipo Aisraeli ankapita kwa iye kuti akaweruze milandu yawo.
And she dwelt under the palm tree of Deborah between Ramah and Bethel in the hill-country of Ephraim, and the sons of Israel came up to her for judgment.
6 Debora uja anatuma munthu kuti akayitane Baraki mwana wa Abinoamu wa ku Kedesi mʼdziko la Nafutali ndipo anati kwa iye, “Yehova Mulungu wa Israeli akukulamula iwe kuti, ‘Pita kasonkhanitse anthu ku phiri la Tabori. Ubwere nawo anthu 10,000 a fuko la Nafutali ndi a fuko la Zebuloni.
And she sent and called Barak the son of Abinoam out of Kedesh-naphtali, and said to him, Has not Jehovah, the God of Israel, commanded, saying, Go and approach to mount Tabor, and take with thee ten thousand men of the sons of Naphtali and of the sons of Zebulun?
7 Ine ndidzakokera Sisera mkulu wa ankhondo a Yabini pamodzi ndi magaleta ake ndi asilikali ake kwa inu ku mtsinje wa Kisoni ndipo ndidzamupereka mʼmanja mwanu.’”
And I will draw Sisera, the captain of Jabin's army, to thee, to the river Kishon, with his chariots and his multitude, and I will deliver him into thy hand.
8 Baraki anamuyankha kuti, “Mukapita nane limodzi ine ndipita. Koma ngati sitipitira limodzi, inenso sindipita.”
And Barak said to her, If thou will go with me, then I will go, but if thou will not go with me, I will not go.
9 Debora anati, “Chabwino, ine ndipita nawe limodzi. Koma mudziwe kuti inu simudzalandirapo ulemu pa zimene mwachitazi popeza Yehova wapereka Sisera mʼmanja mwa munthu wamkazi.” Choncho Debora ananyamuka kupita ku Kedesi pamodzi ndi Baraki.
And she said, I will surely go with thee. Notwithstanding, the journey that thou take shall not be for thine honor, for Jehovah will sell Sisera into the hand of a woman. And Deborah arose, and went with Barak to Kedesh.
10 Baraki anayitana mafuko a Zebuloni ndi Nafutali kuti abwere ku Kedesi. Anthu 10,000 anamutsatira, ndipo Debora anapita naye pamodzi.
And Barak called Zebulun and Naphtali together to Kedesh. And there went up ten thousand men at his feet, and Deborah went up with him.
11 Nthawi imeneyo nʼkuti Mkeni wina dzina lake Heberi atalekana ndi Akeni anzake, zidzukulu za Hobabu, mlamu wa Mose, nakamanga tenti yake pafupi ndi mtengo wa thundu ku Zananimu pafupi ndi Kedesi.
Now Heber the Kenite had separated himself from the Kenites, even from the sons of Hobab the brother-in-law of Moses, and had pitched his tent as far as the oak in Zaanannim, which is by Kedesh.
12 Pamene Sisera anamva kuti Baraki mwana wa Abinoamu wapita ku phiri la Tabori,
And they told Sisera that Barak the son of Abinoam was gone up to mount Tabor.
13 anasonkhanitsa magaleta ake achitsulo 900 ndi anthu onse amene anali naye ndipo anachoka ku Haroseti-Hagoyimu kupita ku mtsinje wa Kisoni.
And Sisera gathered together all his chariots, even nine hundred chariots of iron, and all the people that were with him, from Harosheth of the Gentiles, to the river Kishon.
14 Debora anawuza Baraki kuti, “Dzukani! Paja ndi lero limene Yehova wapereka Sisera mʼmanja mwako. Kodi Yehova sanakhale akukutsogolerani?” Choncho Baraki anatsika phiri la Tabori, anthu 10,000 akumutsata.
And Deborah said to Barak, Up, for this is the day in which Jehovah has delivered Sisera into thy hand. Has not Jehovah gone out before thee? So Barak went down from mount Tabor, and ten thousand men after him.
15 Yehova anasokoneza Sisera ndi magaleta ake pamodzi ndi ankhondo ake onse. Baraki ndi anthu ake anawapirikitsa ndipo Sisera anatsika pa galeta yake nayamba kuthawa pansi.
And Jehovah discomfited Sisera, and all his chariots, and all his army, with the edge of the sword before Barak. And Sisera alighted from his chariot, and fled away on his feet.
16 Baraki analondola magaletawo pamodzi ndi ankhondo onse mpaka ku Haroseti-Hagoyimu, ndipo ankhondo onse a Sisera anaphedwa ndi lupanga. Palibe munthu ndi mmodzi yemwe anatsala.
But Barak pursued after the chariots, and after the army, to Harosheth of the Gentiles. And all the army of Sisera fell by the edge of the sword. There was not a man left.
17 Komabe Sisera anathawa pansi mpaka anakafika ku tenti ya Yaeli mkazi wa Heberi Mkeni uja, chifukwa panali mtendere pakati pa Yabini mfumu ya Hazori ndi banja la Heberi, Mkeni uja.
However Sisera fled away on his feet to the tent of Jael the wife of Heber the Kenite, for there was peace between Jabin the king of Hazor and the house of Heber the Kenite.
18 Yaeli anatuluka kukachingamira Sisera ndipo anati, “Bwerani mbuye wanga, lowani momwemo musaope.” Choncho analowa mʼtenti muja, ndipo anamufunditsa chofunda.
And Jael went out to meet Sisera, and said to him, Turn in, my lord, turn in to me; fear not. And he turned in to her into the tent, and she covered him with a rug.
19 Anati, “Ndili ndi ludzu, chonde patseniko madzi pangʼono akumwa, ndili ndi ludzu.” Mkaziyo anatsekula thumba la chikopa mmene munali mkaka, namupatsa kuti amwe, ndipo anamufunditsanso.
And he said to her, Give me, I pray thee, a little water to drink, for I am thirsty. And she opened a bottle of milk, and gave him drink, and covered him.
20 Kenaka anawuza mkaziyo kuti, “Muyime pa khomo la tentili, ndipo munthu wina akabwera kudzakufunsani kuti, ‘Kodi kwafika munthu wina kuno?’ Inu muyankha kuti, ‘Ayi.’”
And he said to her, Stand in the door of the tent, and it shall be, when any man comes and inquires of thee, and says, Is there any man here? that thou shall say, No.
21 Koma Yaeli mkazi wa Heberi, anatenga chikhomo cha tenti ndi hamara ndi kupita mwakachetechete kwa Sisera uja. Tsono Sisera ali mtulo chifukwa chotopa, mkazi uja anamukhomera chikhomo chija mʼmutu mwake. Chinatulukira kwinaku mpaka kulowa mʼnthaka, ndipo anafa pomwepo.
Then Jael Heber's wife took a tent-pin, and took a hammer in her hand, and went softly to him, and struck the pin into his temples, and it pierced through into the ground, for he was in a deep sleep, so he fainted and died.
22 Baraki atafika akulondola Sisera, Yaeli anatuluka kukamuchingamira namuwuza kuti, “Lowani mudzaone munthu amene mukumufunafuna.” Tsono atalowa anangoona Sisera ali thapsa pansi wakufa ndi chikhomo chili mʼmutu mwake.
And, behold, as Barak pursued Sisera, Jael came out to meet him, and said to him, Come, and I will show thee the man whom thou seek. And he came to her, and, behold, Sisera lay dead, and the tent-pin was in his temples.
23 “Choncho pa tsiku limenelo Mulungu anagonjetsa Yabini mfumu ya Akanaani, pamaso pa Aisraeli.
So God subdued on that day Jabin the king of Canaan before the sons of Israel.
24 Ndipo Aisraeli anapanikizabe Yabini, mfumu ya Akanaani, mpaka kumuwonongeratu.
And the hand of the sons of Israel prevailed more and more against Jabin the king of Canaan until they had destroyed Jabin king of Canaan.

< Oweruza 4 >