< Oweruza 2 >

1 Mngelo wa Yehova anapita ku Bokimu kuchokera ku Giligala ndipo anati kwa Aisraeli, “Ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto ndikukulowetsani mʼdziko limene ndinalumbira kwa makolo anu. Ndinati ‘Sindidzaswa pangano langa ndi inu,
And the agent of Jehovah came up from Gilgal to Bochim. And he said, I made you go up out of Egypt, and have brought you to the land which I swore to your fathers. And I said, I will never break my covenant with you.
2 ndipo inu musadzachite pangano ndi anthu a dziko lino, koma mudzaphwanye maguwa awo ansembe.’ Koma inu simunamvere lamulo langa. Chifukwa chiyani mwachita zimenezi?
And ye shall make no covenant with the inhabitants of this land. Ye shall break down their altars. But ye have not hearkened to my voice. Why have ye done this?
3 Ndikukuwuzani tsopano kuti sindithamangitsa nzikazo pamene inu mukufika. Ndidzawasandutsa kukhala adani anu ndipo milungu yawo idzakhala ngati msampha kwa inu.”
Therefore I also said, I will not drive them out from before you, but they shall be as thorns in your sides, and their gods shall be a snare to you.
4 Mngelo wa Mulungu atayankhula izi kwa Aisraeli, onse analira mokweza,
And it came to pass, when the agent of Jehovah spoke these words to all the sons of Israel, that the people lifted up their voice, and wept.
5 ndipo anatcha malowo kuti Bokimu (kutanthauza kuti Olira). Pamenepo anapereka nsembe kwa Yehova.
And they called the name of that place Bochim, and they sacrificed there to Jehovah.
6 Yoswa atawuza Aisraeli kuti achoke, iwo anapita kukatenga dzikolo, aliyense dera lake.
Now when Joshua had sent the people away, the sons of Israel went every man to his inheritance to possess the land.
7 Anthuwo anatumikira Yehova masiku onse a moyo wa Yoswa. Atamwalira Yoswa, Aisraeli anatumikirabe Yehova nthawi yonse ya moyo wa akuluakulu amene anaona zazikulu zimene Yehova anawachitira.
And the people served Jehovah all the days of Joshua, and all the days of the elders who outlived Joshua, who had seen all the great work of Jehovah that he had wrought for Israel.
8 Yoswa mwana wa Nuni, mtumiki wa Yehova, anamwalira ali ndi zaka 110.
And Joshua the son of Nun, the servant of Jehovah, died, being a hundred and ten years old.
9 Ndipo anamuyika mʼmanda a mʼdziko lake, ku Timnati-Heresi mʼdziko la mapiri la Efereimu, kumpoto kwa phiri la Gaasi.
And they buried him in the border of his inheritance in Timnath-heres, in the hill-country of Ephraim, on the north of the mountain of Gaash.
10 Mʼbado onse utapita kukakhala ndi anthu a mtundu awo, kenaka panauka mʼbado wina umene sunadziwe Yehova ngakhale ntchito zazikulu zimene Yehova anachitira Aisraeli.
And also all that generation were gathered to their fathers. And there arose another generation after them that did not know Jehovah, nor yet the work which he had wrought for Israel.
11 Choncho Aisraeli anayamba kuchita zinthu zoyipa pamaso pa Yehova ndipo anatumikira Abaala.
And the sons of Israel did that which was evil in the sight of Jehovah, and served the Baalim.
12 Iwo anasiya Yehova Mulungu wa makolo awo, amene anawatulutsa ku Igupto. Ndipo anatsatira ndi kupembedza milungu yosiyanasiyana ya anthu amene anawazungulira. Motero Aisraeli anakwiyitsa Yehova.
And they forsook Jehovah, the God of their fathers, who brought them out of the land of Egypt, and followed other gods, of the gods of the peoples that were round about them, and bowed themselves down to them. And they provoked Jehovah to anger.
13 Iwo anasiya Yehova ndi kumatumikira Baala ndi Asiteroti.
And they forsook Jehovah, and served Baal and the Ashtaroth.
14 Yehova anapsera mtima Aisraeli ndipo anawapereka mʼmanja mwa anthu ofunkha amene ankasakaza zinthu zawo. Ndipo analola kuti adani awo owazungulira amene sanathenso kulimbana nawo, awagonjetse.
And the anger of Jehovah was kindled against Israel, and he delivered them into the hands of spoilers that despoiled them. And he sold them into the hands of their enemies round about, so that they could not any longer stand before their enemies.
15 Nthawi zonse Aisraeli ankati akapita ku nkhondo, Yehova amalimbana nawo kuti agonjetsedwe, monga ananenera molumbira kuti zidzaterodi. Choncho iwo anali pa mavuto aakulu.
Wherever they went out, the hand of Jehovah was against them for evil, as Jehovah had spoken, and as Jehovah had sworn to them. And they were exceedingly distressed.
16 Choncho Yehova anawawutsira atsogoleri amene ankawapulumutsa mʼmanja mwa anthu amene ankasakaza zinthu zawo.
And Jehovah raised up judges who saved them out of the hand of those who despoiled them.
17 Komabe iwo sanawamvere atsogoleri awowo popeza ankapembedza milungu ina ndi kumayigwadira. Iwo anapatuka msangamsanga mu njira imene ankayendamo makolo awo. Iwo aja ankamvera malamulo a Yehova, koma mʼbado uwu ayi.
And yet they did not hearken to their judges, for they played the harlot after other gods, and bowed themselves down to them. They turned aside quickly out of the way in which their fathers walked, obeying the commandments of Jehovah. They did not do so.
18 Nthawi zonse Yehova akawautsira mtsogoleri, Iye amakhala naye, ndipo mtsogoleriyo ankawapulumutsa Aisraeliwo mʼmanja mwa adani awo mʼnthawi imene anali moyo. Yehova ankawamvera chisoni Aisraeli pamene ankabuwula chifukwa cha anthu owazunza ndi kuwasautsa.
And when Jehovah raised up judges for them, then Jehovah was with the judge, and saved them out of the hand of their enemies all the days of the judge. For Jehovah regretted because of their groaning because of those who oppressed them and vexed them.
19 Koma nthawi zonse mtsogoleri akamwalira, Aisraeli ankabwerera mʼmbuyo. Iwo amadzisandutsa oyipa kupambana makolo awo popeza ankatsata milungu ina, kuyitumikira ndi kumayigwadira. Anakana kusiya makhalidwe awo oyipa ndi njira zawo zamakani.
But it came to pass, when the judge was dead, that they turned back, and dealt more corruptly than their fathers, in following other gods to serve them, and to bow down to them. They did not cease from their doings, nor from their stubborn way.
20 Choncho Yehova anawapsera mtima Aisraeli ndipo anati, “Chifukwa mtundu uwu waswa pangano limene ndinakhazikitsa ndi makolo awo ndipo sanandimvere,
And the anger of Jehovah was kindled against Israel, and he said, Because this nation has transgressed my covenant which I commanded their fathers, and has not hearkened to my voice,
21 Inenso sindidzapirikitsanso mtundu uli wonse wa anthu amene Yoswa anawasiya pomwalira.
I also will not henceforth drive out any from before them of the nations that Joshua left when he died,
22 Ndidzatero kuti ndiwayese Aisraeli ndi kuona ngati adzasamala kuyenda mʼnjira ya Ine Yehova monga momwe ankachitira makolo awo.”
that by them I may prove Israel, whether they will keep the way of Jehovah to walk in it, as their fathers kept it, or not.
23 Choncho Yehova anayileka mitundu imeneyi ndipo sanayithamangitse kapena kuyipereka mʼmanja mwa Yoswa.
So Jehovah left those nations, without driving them out quickly. Neither did he deliver them into the hand of Joshua.

< Oweruza 2 >