< Oweruza 19 >

1 Pa nthawi imeneyo ku Israeli kunalibe mfumu. Mlevi wina ankakhala kutali ku dziko lamapiri la Efereimu. Iyeyu anatenga mzikazi wa ku Betelehemu, mʼdziko la Yuda.
And it came to pass in those days, when there was no king in Israel, that there was a certain Levite sojourning on the farther side of the hill-country of Ephraim, who took to him a concubine out of Bethlehem-judah.
2 Tsiku lina mzikazi uja anakwiyira mwamuna wake ndipo anamuchokera kupita kwa abambo ake ku Betelehemu mʼdziko la Yuda. Anakakhala kumeneko miyezi inayi.
And his concubine played the harlot against him, and went away from him to her father's house to Bethlehem-judah, and was there the space of four months.
3 Mwamuna wake anamulondola kuti akayankhule naye mofatsa kumupempha kuti abwerere. Iye anali ndi antchito ake ndi abulu ake awiri. Anafika ku nyumba kwa mkazi uja ndipo iye anamulowetsa mʼnyumba ya abambo ake. Abambo aja atamuona mnyamata uja anamulandira mwachimwemwe.
And her husband arose, and went after her, to speak kindly to her, to bring her again, having his servant with him, and a couple of donkeys. And she brought him into her father's house, and when the father of the damsel saw him, he rejoiced to meet him.
4 Mpongozi wake, yemwe anali abambo a mtsikanayo, anamupempha kuti aswere. Choncho anakhalako masiku atatu. Ankadya, kumwa ndi kugona komweko.
And his father-in-law, the damsel's father, retained him, and he abode with him three days. So they ate and drank, and lodged there.
5 Tsiku lachinayi anadzuka mʼmamawa kukonzekera kuti azipita kwawo, koma abambo ake a mtsikanayo anawuza mkamwini wawo uja kuti, “Yambani mwadya chakudya, ndipo kenaka mutha kupita.”
And it came to pass on the fourth day, that they arose early in the morning, and he rose up to depart. And the damsel's father said to his son-in-law, Strengthen thy heart with a morsel of bread, and afterward ye shall go your way.
6 Choncho onse awiri anakhala pansi ndi kudya ndi kumwa pamodzi. Atadya, abambo a mtsikanayo anati, “Chonde mugonenso konkuno musangalale.”
So they sat down, and ate and drank, both of them together. And the damsel's father said to the man, Be pleased, I pray thee, to tarry all night, and let thy heart be merry.
7 Ndipo pamene mwamunayo anakonzeka kuti azipita, apongozi ake anamuwumirizanso kuti asapite. Choncho anagona komweko usiku umenewo.
And the man rose up to depart, but his father-in-law urged him, and he lodged there again.
8 Mmawa wa tsiku lachisanu, atadzuka kuti azipita abambo ake a mtsikanayo anamuwuza kuti, “Yambani mwadya chakudya ndipo mutandale mpaka madzulo.” Choncho awiriwo anadya pamodzi.
And he arose early in the morning on the fifth day to depart. And the damsel's father said, Strengthen thy heart, I pray thee, and tarry ye until the day declines. And they ate, both of them.
9 Pambuyo pake munthu uja pamodzi ndi mzikazi wake ndiponso mtumiki anakonzeka kuti azipita. Koma abambo a mtsikana uja anatinso kwa iye, “Onani tsopano kukuda. Gonani konkuno pakuti tsiku latha kale. Gonani ndipo musangalale. Mawa mudzuka mʼmamawa ndi kumapita kwanu.”
And when the man rose up to depart, he, and his concubine, and his servant, his father-in-law, the damsel's father, said to him, Behold, now the day draws toward evening, I pray you tarry all night. Behold, the day grows to an end, lodge here that thy heart may be merry, and tomorrow get early on your way that thou may go home.
10 Koma munthuyo sanafune kugonanso tsiku limenelo. Choncho ananyamuka kumapita, ndipo anakafika ku malo oyangʼanana ndi Yebusi (ndiye kuti Yerusalemu). Iyeyo anali atatenga abulu ake awiri okhala ndi zokhalira zake, ndipo mzikazi wake uja anali naye limodzi.
But the man would not tarry that night, but he rose up and departed, and came opposite Jebus (the same is Jerusalem). And there were with him a couple of saddled donkeys. His concubine was also with him.
11 Akuyandikira ku Yebusi nʼkuti kutada ndithu. Tsono mtumiki uja anawuza mbuye wake kuti, “Tiyeni, tipatukire ku mzinda wa Ayebusiwa ndipo tigone.”
When they were by Jebus, the day was far spent, and the servant said to his master, Come, I pray thee, and let us turn aside into this city of the Jebusites, and lodge in it.
12 Mbuye wake anamuyankha kuti, “Ayi, tisapatukire ku mzinda wa alendo, anthu amene sali Aisraeli. Koma tipitirire mpaka ku Gibeya.”
And his master said to him, We will not turn aside into the city of a foreigner that is not of the sons of Israel, but we will pass over to Gibeah.
13 Tsono anamuwuza mtumiki wake uja kuti, “Tiye tipite ku amodzi a malo awa, ku Gibeya kapena ku Rama ndipo tikagone kumeneko.”
And he said to his servant, Come and let us draw near to one of these places, and we will lodge in Gibeah, or in Ramah.
14 Choncho nayenda ulendo wawo, ndipo dzuwa linawalowera akuyandikira ku Gibeya mʼdziko la Benjamini.
So they passed on and went their way. And the sun went down upon them near to Gibeah, which belongs to Benjamin.
15 Ndipo anapatukira kumeneko kuti alowe mu mzinda wa Gibeya kukagona usiku umenewo. Anakalowa mu mzindamo ndi kukakhala pabwalo popeza panalibe munthu amene anawalandira ku nyumba kwake kuti akagone.
And they turned aside there, to go in to lodge in Gibeah. And he went in, and sat down in the street of the city, for there was no man that took them into his house to lodge.
16 Pambuyo pake anangoona munthu wina wokalamba akuchokera ku ntchito ya ku munda kwake madzulo. Iyeyu anali wa ku dziko la mapiri ku Efereimu, koma ankakhala ku Gibeya. Koma anthu a kumeneko anali a fuko la Benjamini.
And, behold, there came an old man from his work out of the field at evening. Now the man was of the hill-country of Ephraim, and he sojourned in Gibeah, but the men of the place were Benjamites.
17 Munthu wokalamba uja anakweza maso ndipo anaona munthu wa paulendo uja atakhala pabwalo la mzindawo, ndipo anamufunsa kuti, “Kodi mukupita kuti? Nanga mukuchokera kuti?”
And he lifted up his eyes, and saw the wayfaring man in the street of the city. And the old man said, Where do thou go? And from where do thou come?
18 Iye anayankha kuti, “Tikuchokera ku Betelehemu ku dziko la Yuda ndipo tikupita kutali ku dziko lamapiri la Efereimu kumene ndimakhala. Ndinapita ku Betelehemu mʼdziko la Yuda ndipo tsopano ndikubwerera kwathu. Koma palibe aliyense amene wanditengera ku nyumba yake.
And he said to him, We are passing from Bethlehem-judah to the farther side of the hill-country of Ephraim. I am from there, and I went to Bethlehem-judah. And I am now going to the house of Jehovah, and there is no man that takes me into his house.
19 Tili ndi udzu ndi chakudya cha abulu athu. Tilinso ndi buledi ndi vinyo wokwanira ifeyo: ine, mdzakazi wanuyu, ndi mtumiki amene ali nafeyu. Palibe chimene tikusowa.”
Yet there is both straw and provender for our donkeys, and there is bread and wine also for me, and for thy handmaid, and for the young man who is with thy servants. There is no want of anything.
20 Munthu wokalambayo anati, “Mtendere ukhale nanu. Ine ndikuthandizani pa zosowa zanu zonse, koma musagone pabwalo usiku uno.”
And the old man said, Peace be to thee. However let all thy wants lie upon me, only do not lodge in the street.
21 Choncho anapita nawo ku nyumba yake, ndipo anawapatsa abulu ake chakudya. Alendo aja anasamba mapazi awo, nalandira chakudya ndi chakumwa.
So he brought him into his house, and gave the donkeys fodder. And they washed their feet, and ate and drank.
22 Pamene ankadya mosangalala, anangoona anthu ena achabechabe a mu mzindawo azungulira nyumba ija nʼkumamenya chitseko. Tsono anawuza mwini nyumbayo, munthu wokalamba uja kuti, “Mutulutse munthu amene wabwera mʼnyumba yakoyu kuti tigone naye.”
As they were making their hearts merry, behold, the men of the city, certain base fellows, beset the house round about, beating at the door. And they spoke to the master of the house, the old man, saying, Bring forth the man who came into thy house, that we may know him.
23 Koma mwini nyumba uja anatuluka ku bwalo nawawuza kuti, “Ayi, abale anga musachite zoyipa zotere. Popeza munthu uyu walowa mʼnyumba mwanga muno, musachite chinthu chonyansa chotere.
And the man, the master of the house, went out to them, and said to them, No, my brothers, I pray you, do not so wickedly, seeing that this man has come into my house. Do not this folly.
24 Onani, pano pali mwana wanga wamkazi wosadziwa mwamuna pamodzi ndi mzikazi wa mlendoyu. Ndikutulutsirani amenewa tsopano ndipo atengeni ndi kuchita nawo chomwe chikukomerani. Koma musachite chinthu chonyansa ndi munthuyu.”
Behold, here is my daughter a virgin, and his concubine. I will bring them out now, and humble ye them, and do with them what seems good to you, but to this man do not any such folly.
25 Koma anthuwo sanafune kumumvera. Choncho mlendo uja anagwira mzikazi wake namutulutsa kuja kumene kunali iwo. Tsono iwowo anagona naye ndi kuchita naye zonyansa usiku wonse mpaka mmawa. Mʼbandakucha anamulola kuti apite.
But the men would not hearken to him. So the man laid hold on his concubine, and brought her forth to them. And they knew her, and abused her all the night until the morning, and when the day began to spring, they let her go.
26 Ndipo mmawa kukucha mzikazi uja anabwerera nakagwa pansi pa khomo pa nyumba imene mwamuna wake anali, ndipo anakhala pomwepo mpaka kunayera.
Then the woman came in the dawning of the day, and fell down at the door of the man's house where her lord was, till it was light.
27 Mwamuna wake anadzuka mʼmamawa, natsekula chitseko cha nyumba kuti atuluke ndi kumapita. Koma anangoona mzikazi wake uja ali thapsa pa khomo la nyumbayo, manja ake ali pa khonde.
And her lord rose up in the morning, and opened the doors of the house, and went out to go his way, and, behold, the woman his concubine was fallen down at the door of the house, with her hands upon the threshold.
28 Iye anati kwa mkaziyo, “Dzuka tizipita.” Koma sanayankhe kanthu. Kenaka anamukweza pa bulu wake ndipo ananyamuka kumapita kwawo.
And he said to her, Up, and let us be going, but there was no answering. Then he took her up upon the donkey, and the man rose up, and got to his place.
29 Atafika ku nyumba yake, anatenga mpeni, nagwira mzikazi wake uja ndi kuduladula thupi lake nthuli khumi ndi ziwiri. Kenaka anazitumiza ku zigawo zonse za Israeli.
And when he came into his house, he took a knife, and laid hold on his concubine, and divided her, limb by limb, into twelve pieces, and sent her throughout all the borders of Israel.
30 Aliyense amene anaona zimenezi ankanena kuti, “Zoterezi sizinaonekepo kuyambira pamene Aisraeli anatuluka mʼdziko la Igupto mpaka lero lino. Ganizirani bwino chinthu chimenechi ndipo tiwuzeni zoyenera kuchita!”
And it was so, that all who saw it said, There was no such deed done nor seen from the day that the sons of Israel came up out of the land of Egypt to this day. Consider it, take counsel, and speak.

< Oweruza 19 >