< Oweruza 20 >

1 Ndipo Aisraeli onse kuyambira ku dziko la Dani mpaka ku Beeriseba ndiponso ku dziko la Giliyadi ananyamuka ngati munthu mmodzi nakasonkhana pamaso pa Yehova ku Mizipa.
Then all the sons of Israel went out. And the congregation was assembled as one man, from Dan even to Beersheba, with the land of Gilead, to Jehovah at Mizpah.
2 Atsogoleri a anthu onse ndi a mafuko onse Aisraeli anali nawo pa msonkhano wa anthu a Mulungu. Onse pamodzi analipo asilikali oyenda pansi 400,000 atanyamula malupanga.
And the chiefs of all the people, even of all the tribes of Israel, presented themselves in the assembly of the people of God, four hundred thousand footmen who drew a sword.
3 Anthu a fuko la Benjamini anali atamva kuti Aisraeli apita ku Mizipa. Tsono Aisraeli anati, “Tiwuzeni, zinthu zoyipa izi zinachitika bwanji.”
(Now the sons of Benjamin heard that the sons of Israel had gone up to Mizpah.) And the sons of Israel said, Tell us, how was this wickedness brought to pass?
4 Choncho Mlevi uja, mwamuna wa mkazi wophedwa uja anayankha nati, “Ine ndinapita ku Gibeya mʼdziko la Benjamini pamodzi ndi mzikazi wanga kuti tikagone kumeneko.
And the Levite, the husband of the woman who was murdered, answered and said, I came into Gibeah that belongs to Benjamin, I and my concubine, to lodge.
5 Usiku anthu a ku Gibeya anandiwukira, nazinga nyumba munali ine. Ankafuna kundipha ndipo anagona ndi mzikazi wanga momukakamiza mpaka anafa.
And the men of Gibeah rose against me, and beset the house round about me by night. They thought to have me slain, and they forced my concubine, and she is dead.
6 Ine ndinatenga mzikazi wangayo ndi kumudula nthulinthuli ndikuzitumiza kwa fuko lililonse la Aisraeli. Anthu amenewa, zedi achita chinthu chonyansa kwambiri mʼdziko lino la Israeli.
And I took my concubine, and cut her in pieces, and sent her throughout all the country of the inheritance of Israel, for they have committed lewdness and folly in Israel.
7 Ndi zimenezotu inu Aisraeli nonse; yankhulaponi mawu ndi kupereka maganizo anu.”
Behold, ye sons of Israel, all of you, give here your advice and counsel.
8 Anthu onse anayimirira ngati munthu mmodzi nanena kuti, “Palibe mmodzi wa ife amene apite ku nyumba kwake. Palibe amene abwerere ku nyumba kwake.
And all the people arose as one man, saying, We will not any of us go to his tent, neither will we any of us turn to his house.
9 Koma tsopano chimene ife tichite ndi dziko la Gibeya ndi ichi: Tidzapita kukamenyana nawo potsatira zimene maere anene.
But now this is the thing which we will do to Gibeah: We will go up against it by lot,
10 Mʼmafuko onse a Aisraeli tidzasankha anthu khumi pa anthu 100 aliwonse: ndiye kuti anthu 100 pa anthu 1,000 aliwonse kapena anthu 1,000 pa anthu 10,000 aliwonse. Anthu amenewa adzasonkhanitsa zakudya za ankhondo, ndipo ankhondowo adzapita kukalipsira anthu a ku Geba mʼdziko la Benjamini chifukwa chochita chinthu chonyansa chotere mʼdziko la Israeli.”
and we will take ten men of a hundred throughout all the tribes of Israel, and a hundred of a thousand, and a thousand out of ten thousand, to fetch provision for the people, that they may do, when they come to Gibeah of Benjamin, according to all the folly that they have wrought in Israel.
11 Choncho anthu a ku Israeli anasonkhana pamodzi nagwirizana chimodzi, kukalimbana ndi mzindawo.
So all the men of Israel were gathered against the city, knit together as one man.
12 Mafuko a Israeli anatumiza anthu kwa fuko lonse la Benjamini kukafunsa kuti, “Kodi zoyipa zachitika pakati panuzi ndi zotani?
And the tribes of Israel sent men through all the tribe of Benjamin, saying, What wickedness is this that has come to pass among you?
13 Tsono tikuti mutipatse anthu achabechabe a ku Gibeya kuti tiwaphe kuti tichotse chinthu choyipachi mʼdziko la Israeli.” Koma fuko la Benjamini silinafune kumvera zimene ananena Aisraeli anzawo.
Now therefore deliver up the men, the base fellows, who are in Gibeah, that we may put them to death, and put away evil from Israel. But Benjamin would not hearken to the voice of their brothers the sons of Israel.
14 Mʼmalo mwake, Abenjaminiwo anatuluka mʼmizinda yawo ku Gibeya kukamenyana ndi Aisraeli.
And the sons of Benjamin gathered themselves together out of the cities to Gibeah, to go out to battle against the sons of Israel.
15 Tsiku limenelo Abenjamini anasonkhanitsa kuchokera ku mizinda yawo ankhondo 26,000 amalupanga awo, osawerengera anthu ena 700 a ku Gibeya amene anasankhidwa.
And the sons of Benjamin were numbered on that day out of the cities twenty-six thousand men who drew a sword, besides the inhabitants of Gibeah, who were numbered seven hundred chosen men.
16 Mwa onsewa panali ankhondo 70 amanzere amene aliyense anali wodziwa kulasa ngakhale tsitsi limodzi ndi mwala osaphonya.
Among all this people there were seven hundred chosen men left-handed. Every one could sling stones at a hair-breadth, and not miss.
17 Aisraeli, kupatula fuko la Benjamini, anasonkhanitsa anthu 400,000 a malupanga, onse odziwa bwino nkhondo.
And the men of Israel, besides Benjamin, were numbered four hundred thousand men who drew a sword. All these were men of war.
18 Ndipo Aisraeli ananyamuka kupita ku Beteli kukafunsira kwa Mulungu. Iwo anati, “Ndani mwa ife amene angayambe kukamenyana ndi fuko la Benjamini?” Yehova anayankha kuti, “Fuko la Yuda ndilo liyambe.”
And the sons of Israel arose, and went up to Bethel, and asked counsel of God. And they said, Who shall go up for us first to battle against the sons of Benjamin? And Jehovah said, Judah first.
19 Mmawa mwake Israeli ananyamuka nakamanga msasa moyangʼanana ndi Gibeya.
And the sons of Israel rose up in the morning, and encamped against Gibeah.
20 Aisraeli anapita kukachita nkhondo ndi fuko la Benjamini ndipo anandandalika ankhondo awo moyangʼanana ndi Gibeya.
And the men of Israel went out to battle against Benjamin. And the men of Israel set the battle in array against them at Gibeah.
21 A fuko la Benjamini anatuluka ku Gibeya ndipo tsiku limenelo anapha Aisraeli 22,000 ku nkhondoko.
And the sons of Benjamin came forth out of Gibeah, and destroyed down to the ground of the Israelites on that day twenty-two thousand men.
22 Koma ankhondo a Israeli analimbikitsananso mtima ndipo anasonkhanitsanso kachiwiri ankhondo awo pa malo pamene anawandandalika poyamba paja.
And the people, the men of Israel, encouraged themselves, and set the battle again in array in the place where they set themselves in array the first day.
23 Aisraeli anapita kukalira pamaso pa Yehova mpaka madzulo. Iwo anafunsa Yehova kuti, “Kodi tipitenso kukamenyana ndi a fuko la Benjamini abale athu?” Yehova anayankha kuti, “Pitani mukalimbane nawo.”
And the sons of Israel went up and wept before Jehovah until evening. And they asked of Jehovah, saying, Shall I again draw near to battle against the sons of Benjamin my brother? And Jehovah said, Go up against him.
24 Ndipo Aisraeli anayandikiranso pafupi ndi fuko la Benjamini tsiku lachiwiri lake kuti amenyane nawo.
And the sons of Israel came near against the sons of Benjamin the second day.
25 Pa tsiku lachiwiri lomwelo Abenjamini anatulukanso mu mzinda wa Gibeya ndipo anaphanso ankhondo 18,000. Onse amene anawaphawo anali odziwa kugwiritsa ntchito bwino malupanga.
And Benjamin went forth against them out of Gibeah the second day, and destroyed down to the ground of the sons of Israel again eighteen thousand men. All these drew the sword.
26 Tsono Aisraeli onse, gulu lonse la ankhondo, anapita ku Beteli kukalira pamaso pa Yehova. Anakhala pansi nasala zakudya tsiku lonse mpaka madzulo. Anapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano pamaso pa Yehova.
Then all the sons of Israel, and all the people, went up, and came to Bethel, and wept, and sat there before Jehovah, and fasted that day until evening, and they offered burnt offerings and peace offerings before Jehovah.
27 Bokosi la Chipangano cha Yehova linali kumeneko.
And the sons of Israel asked of Jehovah (for the ark of the covenant of God was there in those days,
28 Finehasi mwana wa Eliezara mwana wa Aaroni ndiye ankatumikira nthawi imeneyo. Tsono Aisraeli anafunsa Yehova kuti, “Kodi tipitenso kukachita nkhondo ndi mʼbale athu Abenjamini, kapena ayi?” Yehova anayankha kuti, “Pitaninso chifukwa mawa ndidzawapereka mʼmanja mwanu.”
and Phinehas, the son of Eleazar, the son of Aaron, stood before it in those days), saying, Shall I yet again go out to battle against the sons of Benjamin my brother, or shall I cease? And Jehovah said, Go up, for tomorrow I will deliver him into thy hand.
29 Choncho Aisraeli anayika anthu obisalira mozungulira Gibeya.
And Israel set an ambushment against Gibeah round about.
30 Tsiku lachitatu anapita kukamenyana ndi Benjamini ndipo anayika ankhondo mʼmalo mwawo kuti amenyane ndi Gibeya monga anachitira poyamba.
And the sons of Israel went up against the sons of Benjamin on the third day, and set themselves in array against Gibeah, as at other times.
31 Abenjamini anatuluka kukamenyana nawo anthuwo ndipo anapita kutali ndi mzindawo. Iwo anayamba kupha Aisraeli monga poyamba paja, kotero kuti anapha anthu pafupifupi makumi atatu. Mitembo ya ena inali mu misewu yayikulu yopita ku Beteli ndi ku Gibeya, ndipo ina inali kwina poyera.
And the sons of Benjamin went out against the people, and were drawn away from the city. And they began to smite and kill of the people as at other times, in the highways, of which one goes up to Bethel, and the other to Gibeah, in the field about thirty men of Israel.
32 Abenjamini ankanena kuti, “Tikuwagonjetsa monga poyamba.” Koma Aisraeli ankanena kuti, “Tiyeni tithawe kuti apite ku msewu chapatali ndi mzinda wawo.”
And the sons of Benjamin said, They are smitten down before us as at the first. But the sons of Israel said, Let us flee, and draw them away from the city to the highways.
33 Choncho Aisraeli onse anachoka mʼmalo mwawo ndi kukandanda ku Baala-Tamara, ndipo Aisraeli obisalira aja anatuluka mʼmalo awo kummawa kwa Geba.
And all the men of Israel rose up out of their place, and set themselves in array at Baal-tamar, and the ambushment of Israel broke forth out of their place, even out of Maareh-geba.
34 Aisraeli osankhidwa 10,000 ndiwo anabwera kudzalimbana ndi mzinda wa Gibeya. Nkhondoyo inafika poyipa kwambiri mwakuti Abenjamini samadziwa kuti zoopsa zili pafupi kuwagwera.
And there came opposite Gibeah ten thousand chosen men out of all Israel, and the battle was severe, but they knew not that evil was close upon them.
35 Tsono Yehova anagonjetsa Abenjamini pamaso pa Israeli motero kuti Aisraeli anapha ankhondo a Abenjamini 25,100 tsiku limenelo.
And Jehovah smote Benjamin before Israel, and the sons of Israel destroyed of Benjamin that day twenty-five thousand and a hundred men. All these drew the sword.
36 Choncho Abenjamini anaona kuti agonjetsedwa. Paja Aisraeli anathawa fuko la Benjamini chifukwa ankadalira anthu amene anawayika kuti abisalire mzinda wa Gibeya.
So the sons of Benjamin saw that they were smitten, for the men of Israel gave place to Benjamin because they trusted to the ambushment whom they had set against Gibeah.
37 Tsono anthu amene anabisala aja anachita changu kuwuthira nkhondo mzinda wa Gibeyawo. Ndipo anapha anthu onse a mu mzindawo ndi lupanga.
And the ambushment hastened, and rushed upon Gibeah. And the ambushment drew themselves along, and smote all the city with the edge of the sword.
38 Chizindikiro chimene Aisraeli anapangana ndi anthu obisalira aja chinali chakuti obisalira aja akangofukiza utsi wambiri ngati mtambo mu mzindamo,
Now the appointed sign between the men of Israel and the ambushment was, that they should make a great cloud of smoke rise up out of the city.
39 ndiye kuti Aisraeli enawo abwerere ku nkhondo. Pa nthawiyo nʼkuti Abenjamini atayamba kale kumenya Aisraeliwo kwambiri ndi kupha pafupifupi anthu makumi atatu. Ndipo iwo ankanena kuti, “Ndithu tawapha monga poyamba paja.”
And the men of Israel turned in the battle, and Benjamin began to smite and kill of the men of Israel about thirty persons, for they said, Surely they are smitten down before us as in the first battle.
40 Koma pamene utsi wa chizindikiro uja unayamba kukwera tolotolo mmwamba kuchoka mu mzindamo, Abenjamini anayangʼana mʼmbuyo ndipo anangoona utsi mu mzinda onse uli tolotolo kukwera mmwamba.
But when the cloud began to arise up out of the city in a pillar of smoke, the Benjamites looked behind them, and, behold, the whole of the city went up in smoke to heaven.
41 Kenaka Aisraeli anabwerera ndipo Abenjamini anachita mantha, chifukwa anaona kuti zoopsa zili pafupi kuwagwera.
And the men of Israel turned, and the men of Benjamin were dismayed, for they saw that evil had come upon them.
42 Choncho anathawa pamaso pa Aisraeli kudzera njira ya ku chipululu, koma nkhondo inawapeza. Ndipo anaphedwa kumeneko ndi Aisraeli amene anachokera mu mzindamo.
Therefore they turned their backs before the men of Israel to the way of the wilderness. But the battle followed hard after them, and those who came out of the cities destroyed them in the midst of it.
43 Anawazungulira Abenjaminiwo, nawathamangitsa ndi kuwagonjetseratu osawachitira chifundo mpaka ku dera la kummawa kwa Gibeya.
They enclosed the Benjamites round about, and chased them, and trod them down at their resting-place, as far as opposite Gibeah toward the sunrise.
44 Abenjamini 18,000 olimba mtima anaphedwa.
And there fell of Benjamin eighteen thousand men. All these were men of valor.
45 Koma ena anatembenuka nathawira ku chipululu ku thanthwe la Rimoni. Mwa iwowa Aisraeli anapha Abenjamini 5,000 mʼmisewu yayikulu. Anawapitikitsabe Abenjaminiwo mpaka kufika ku Gidomu ndi kuphanso ena 2,000.
And they turned and fled toward the wilderness to the rock of Rimmon. And they gleaned of them in the highways five thousand men, and followed hard after them to Gidom, and smote of them two thousand men.
46 Pa tsiku limenelo Abenjamini olimba mtima okhala ndi malupanga okwana 25,000 anafa.
So that all who fell that day of Benjamin were twenty-five thousand men who drew the sword. All these were men of valor.
47 Koma anthu 700 anabwerera ndi kuthawira ku chipululu ku thanthwe la Rimoni kumene anakhalako miyezi inayi.
But six hundred men turned and fled toward the wilderness to the rock of Rimmon, and abode in the rock of Rimmon four months.
48 Aisraeli anabwerera kukamenyana ndi Abenjamini otsala ndi kuwapha ndi lupanga kuphatikizapo ziweto ndi zonse anali nazo. Ndipo anayatsa moto mizinda yonse anayipeza.
And the men of Israel turned again upon the sons of Benjamin, and smote them with the edge of the sword, both the entire city, and the cattle, and all that they found. Moreover they set on fire all the cities which they found.

< Oweruza 20 >