< Oweruza 18 >

1 Masiku amenewo munalibe mfumu mu Israeli. Ndipo anthu a fuko la Dani amafunafuna malo okhalamo ngati cholowa chawo, chifukwa kufikira nthawi imeneyo anali asanalandire cholowa chawo pakati pa mafuko a Israeli.
In those days there was no king in Israel. And in those days the tribe of the Danites sought for them an inheritance to dwell in, for to that day their inheritance had not fallen to them among the tribes of Israel.
2 Choncho fuko la Dani linatumiza kuchokera ku mabanja awo onse anthu olimba mtima asanu. Anthuwa anachokera ku Zora ndi ku Esitaoli ndipo anatumidwa kukazonda ndi kuliyendera dzikolo. Anthu amenewa ankayimira fuko lonse la Dani. Anthuwa anawawuza kuti, “Pitani mukazonde dzikolo.” Anthuwa anafika ku dziko la mapiri la Efereimu ndi kupita ku nyumba ya Mika komwe anakagona.
And the sons of Dan sent of their family five men from their whole number, men of valor, from Zorah, and from Eshtaol, to spy out the land, and to search it. And they said to them, Go, search the land. And they came to the hill-country of Ephraim to the house of Micah, and lodged there.
3 Ali ku nyumba ya Mika anazindikira mawu a mnyamata, Mlevi uja. Choncho anapita kwa iye namufunsa kuti, “Unabwera ndi ndani kuno? Nanga ukuchita chiyani ku malo ano? Komanso nʼchifukwa chiyani uli kuno?”
When they were by the house of Micah, they recognized the voice of the young man the Levite. And they turned aside there, and said to him, Who brought thee here? And what are thou doing in this place? And what have thou here?
4 Iye anawawuza zimene Mika anamuchitira ndipo anati, “Iye anandilemba ntchito ndipo ndine wansembe wake.”
And he said to them, Thus and thus has Micah dealt with me, and he has hired me, and I have become his priest.
5 Kenaka iwo anati kwa iye, “Chonde tifunsire kwa Mulungu kuti tidziwe ngati ulendo wathuwu tiyende bwino.”
And they said to him, Ask counsel, we pray thee, of God, that we may know whether our way which we go shall be prosperous.
6 Wansembeyo anawayankha kuti, “Pitani mu mtendere, Yehova ali ndi inu pa ulendo wanuwu.”
And the priest said to them, Go in peace. Your way is before Jehovah in which ye go.
7 Choncho anthu asanuwo ananyamuka ndipo anafika ku Laisi, kumene anaona kuti anthu ankakhala mwabata monga anthu a ku Sidoni. Anali anthu opanda chowavuta ndiponso aphee. Tsono popeza mʼdziko mwawo analibe chosowa, iwo anali a chuma. Anaonanso kuti anthuwo ankakhala kutali ndi Sidoni ndipo analibe ubale ndi wina aliyense.
Then the five men departed, and came to Laish, and saw the people that were in it, how they dwelt in security, according to the manner of the Sidonians, quiet and secure, for there was none in the land possessing authority, that might put them to shame in anything. And they were far from the Sidonians, and had no dealings with any man.
8 Ozonda dziko aja atabwerera kwa abale awo ku Zora ndi Esitaoli, abale awowo anawafunsa kuti, “Mwaonako zotani?”
And they came to their brothers to Zorah and Eshtaol. And their brothers said to them, What say ye?
9 “Tiyeni tikamenyane nawo nkhondo popeza taliona dziko lawolo kuti ndi lachonde kwambiri. Kodi simuchitapo kanthu? Musachite mphwayi kupita mʼdzikomo ndi kukalilanda.
And they said, Arise, and let us go up against them, for we have seen the land, and, behold, it is very good, and are ye idle? Be not slothful to go and to enter in to possess the land.
10 Mukalowa, mukapeza anthu amene ali osatekeseka ndi dziko lalikulu. Yehova wakupatsani dziko limeneli. Malowo ngosasowa kanthu kalikonse kopezeka pa dziko lapansi.”
When ye go, ye shall come to a people secure. And the land is large, for God has given it into your hand, a place where there is no want of anything that is on the earth.
11 Kenaka anthu 600 a fuko la Dani ananyamuka ku Zora ndi Esitaoli atanyamula zida za nkhondo.
And there set forth from there of the family of the Danites, out of Zorah and out of Eshtaol, six hundred men girded with weapons of war.
12 Tsono anakamanga msasa ku Kiriati-Yearimu mʼdziko la Yuda. Malowa ali kumadzulo kwa Kiriati-Yearimu. Ichi ndi chifukwa chake malowo akutchedwa Mahane Dani mpaka lero.
And they went up, and encamped in Kiriath-jearim, in Judah. Therefore they called that place Mahaneh-dan, to this day. Behold, it is behind Kiriath-jearim.
13 Kuchokera kumeneko anapita ku dziko lamapiri la Efereimu ndipo anafika ku nyumba ya Mika.
And they passed from there to the hill-country of Ephraim, and came to the house of Micah.
14 Anthu asanu amene anakazonda dziko la Laisi anati kwa abale awo, “Kodi mukudziwa kuti imodzi mwa nyumba izi muli efodi, mafano a mʼnyumba otchedwa terafimu, fano losema ndiponso fano lokuta ndi siliva? Ndiye mudziwe chochita.”
Then the five men who went to spy out the country of Laish, answered and said to their brothers, Do ye know that there is in these houses an ephod, and teraphim, and a graven image, and a molten image? Now therefore consider what ye have to do.
15 Choncho anthuwa anapatuka napita ku nyumba ya Mika kumene mnyamata, Mlevi uja ankakhala ndipo anamufunsa za mmene zinthu zilili.
And they turned aside there, and came to the house of the young man the Levite, even to the house of Micah, and asked him of his welfare.
16 Nthawi imeneyi nʼkuti anthu 600 a fuko la Dani aja atayima pa chipata atanyamula zida za nkhondo.
And the six hundred men girded with their weapons of war, who were of the sons of Dan, stood by the entrance of the gate.
17 Anthu asanu amene anakazonda dziko aja analowa ndi kukatenga fano losema, efodi, fano la mʼnyumba lotchedwa terafimu, ndi fano lokutidwa ndi siliva. Nthawiyi nʼkuti wansembe uja ndi anthu 600 okhala ndi zida za nkhondo aja ali chiyimire pa chipata.
And the five men who went to spy out the land went up, and came in there, and took the graven image, and the ephod, and the teraphim, and the molten image. And the priest stood by the entrance of the gate with the six hundred men girded with weapons of war.
18 Anthuwo atalowa mʼnyumba ya Mika ndi kutenga fano losema, efodi, fano la mʼnyumba, ndi fano lokutidwa ndi siliva, wansembeyo anawafunsa kuti, “Kodi mukuchita chiyani?”
And when these went into Micah's house, and fetched the graven image, the ephod, and the teraphim, and the molten image, the priest said to them, What do ye?
19 Iwo anamuyankha kuti, “Khala chete usayankhule. Tsagana nafe ndipo udzakhala mlangizi wathu ndi wansembe wathu. Kodi si kwabwino kwa iwe kukhala wansembe wa fuko lonse la Israeli mʼmalo mokhala wansembe wa munthu mmodzi yekha?”
And they said to him, Hold thy peace, lay thy hand upon thy mouth, and go with us, and be to us a father and a priest. Is it better for thee to be priest to the house of one man, or to be priest to a tribe and a family in Israel?
20 Wansembeyo anakondwera ndipo anatenga efodi, fano la mʼnyumba ndi fano losema natsagana nawo.
And the priest's heart was glad, and he took the ephod, and the teraphim, and the graven image, and went in the midst of the people.
21 Choncho iwo anatembenuka nachoka, atatsogoza ana, zoweta ndi katundu wawo yense.
So they turned and departed, and put the little ones and the cattle and the goods before them.
22 Atayenda mtunda pangʼono kuchokera pa nyumba ya Mika, anthu amene amakhala pafupi ndi nyumba ya Mika anasonkhana kulondola a fuko la Dani aja, ndipo anawapeza.
When they were a good way from the house of Micah, the men who were in the houses near to Micah's house were gathered together, and overtook the sons of Dan.
23 Atawafuwulira, a fuko la Dani aja anachewuka ndipo anafunsa Mika kuti, “Chavuta nʼchiyani kuti usonkhanitse anthu chotere?”
And they cried out to the sons of Dan. And they turned their faces, and said to Micah, What troubles thee that thou come with such a company?
24 Iye anayankha kuti, “Inu mwanditengera milungu imene ndinapanga pamodzi ndi wansembe nʼkumapita. Tsono ine ndatsala ndi chiyani? Ndiye inu mungafunse kuti chavuta nʼchiyani?”
And he said, ye have taken away my gods which I made, and the priest, and have gone away, and what have I more? And how do ye then say to me, What troubles thee?
25 Anthu a fuko la Dani aja anayankha kuti, “Usayankhuleponso kanthu chifukwa anthu awa angapse mtima nakumenya ndipo iwe ndi banja lako lonse nʼkutayapo miyoyo yanu.”
And the sons of Dan said to him, Let not thy voice be heard among us, lest angry fellows fall upon you, and thou lose thy life, with the lives of thy household.
26 Choncho anthu a fuko la Dani anapitiriza ulendo wawo. Mika ataona kuti anthuwo anali amphamvu kuposa iye, anangotembenuka kubwerera kwawo.
And the sons of Dan went their way. And when Micah saw that they were too strong for him, he turned and went back to his house.
27 Anthu a fuko la Dani aja anatenga zinthu zimene Mika anapanga pamodzi ndi wansembe uja. Iwo anakafika ku Laisi kwa anthu a phee, osatekeseka aja ndipo anawathira nkhondo, nawapha ndi kutentha mzindawo ndi moto.
And they took that which Micah had made, and the priest whom he had, and came to Laish, to a people quiet and secure, and smote them with the edge of the sword, and they burnt the city with fire.
28 Panalibe wowapulumutsa chifukwa anali kutali ndi Sidoni ndiponso sanali pa ubale ndi wina aliyense. Mzindawo unali mʼchigwa cha Beti-Rehobu. Anthu a fuko la Adaniwo anawumanganso mzindawo ndi kumakhalamo.
And there was no deliverer because it was far from Sidon, and they had no dealings with any man, and it was in the valley that lies by Beth-rehob. And they built the city, and dwelt in it.
29 Iwo anawutcha mzindawo Dani, kutengera dzina la kholo lawo Dani, amene anali mwana wa Israeli, ngakhale kuti mzindawo poyamba unali Laisi.
And they called the name of the city Dan, after the name of Dan their father who was born to Israel. However the name of the city was Laish at first.
30 Anthu a fuko la Dani anayimiritsa fano losema lija. Yonatani mwana wa Geresomu, mwana wa Mose pamodzi ndi ana ake onse anakhala ansembe a fuko la Dani mpaka pa tsiku la ukapolo wa dzikolo.
And the sons of Dan set up for themselves the graven image. And Jonathan, the son of Gershom, the son of Moses, he and his sons were priests to the tribe of the Danites until the day of the captivity of the land.
31 Choncho anthu a fuko la Dani ankapembedza fano limene Mika anapanga nthawi yonse pamene nyumba ya Mulungu inali ku Silo.
So they set up for them Micah's graven image which he made, all the time that the house of God was in Shiloh.

< Oweruza 18 >