< Yoswa 23 >

1 Panapita nthawi yayitali kuchokera pamene Yehova anakhazikitsa mtendere pakati pa Aisraeli ndi adani awo owazungulira. Nthawi imeneyi nʼkuti Yoswa atakalamba, ali ndi zaka zambiri.
And it came to pass after many days, when Jehovah had given rest to Israel from all their enemies round about, and Joshua was old and well stricken in years,
2 Yoswayo anayitanitsa Aisraeli onse pamodzi ndi akuluakulu, atsogoleri, oweruza, ndi oyangʼanira anthu antchito ndipo anawawuza kuti, “Ine ndakalamba ndipo ndili ndi zaka zambiri.
that Joshua called for all Israel, for their elders, and for their heads, and for their judges, and for their officers, and said to them, I am old and well stricken in years,
3 Inu mwaona zonse zimene Yehova Mulungu wanu wachita kwa mitundu yonseyi chifukwa cha inu. Ndi Yehova Mulungu wanu amene anakumenyerani nkhondo.
and ye have seen all that Jehovah your God has done to all these nations because of you, for Jehovah your God, he it is who has fought for you.
4 Tsono onani! Mitundu ya anthu otsalawa ndayipereka kwa mafuko anu pamodzi ndi mitundu ya anthu ya pakati pa Yorodani ndi Nyanja Yayikulu ya kumadzulo imene ndinayigonjetsa.
Behold, I have allotted to you these nations that remain, to be an inheritance for your tribes, from the Jordan, with all the nations that I have cut off, even to the great sea toward the going down of the sun.
5 Yehova Mulungu wanu ndiye adzawathamangitsa pamaso panu. Mudzatenga dziko lawo monga Yehova anakulonjezerani.
And Jehovah your God, he will thrust them out from before you, and drive them from out of your sight. And ye shall possess their land, as Jehovah your God spoke to you.
6 “Choncho khalani amphamvu, ndipo samalani kuti mumvere zonse zimene zalembedwa mʼbuku la malamulo a Mose. Musapatuke pa malamulo onse amene alembedwamo.
Therefore be ye very courageous to keep and to do all that is written in the book of the law of Moses, that ye not turn aside therefrom to the right hand or to the left;
7 Musagwirizane ndi mitundu ya anthu imene yatsala pakati panu. Musatchule mayina a milungu yawo kapena kuyitchula polumbira. Musayitumikire kapena kuyigwadira.
that ye do not come among these nations, these that remain among you, neither make mention of the name of their gods, nor cause to swear by them, neither serve them, nor bow yourselves down to them,
8 Koma mukuyenera kugwiritsa Yehova Mulungu wanu, monga mwachitira mpaka lero lino.
but cling to Jehovah your God as ye have done to this day.
9 “Yehova wapirikitsa patsogolo panu mitundu ya anthu ikuluikulu ndi yolimba. Mpaka lero palibe amene watha kulimbana nanu.
For Jehovah has driven out from before you great nations and strong. But as for you, no man has stood before you to this day.
10 Aliyense wa inu atha kuthamangitsa anthu 1,000 chifukwa Yehova Mulungu wanu ndiye amakumenyerani nkhondo, monga momwe analonjezera.
One man of you shall chase a thousand, for Jehovah your God, he it is who fights for you, as he spoke to you.
11 Choncho samalitsani kuti mukonde Yehova Mulungu wanu.
Take good heed therefore to yourselves, that ye love Jehovah your God.
12 “Koma ngati mubwerera mʼmbuyo ndi kuphatikizana ndi mitundu yotsalayi imene ili pakati panu ndi kumakwatirana nayo,
Else if ye do at all go back, and cling to the remnant of these nations, even these that remain among you, and make marriages with them, and go in to them, and they to you,
13 pamenepo mudziwe kuti Yehova, Mulungu wanu, sadzapirikitsa mitundu imeneyi pamaso panu, koma idzakhala ngati msampha kwa inu kapenanso khwekhwe lokukolani. Idzakhala ngati zikwapu pa msana panu kapenanso ngati minga mʼmaso mwanu mpaka mutatha psiti mʼdziko labwinoli limene Yehova Mulungu wanu wakupatsani.
know for a certainty that Jehovah your God will no more drive these nations from out of your sight, but they shall be a snare and a trap to you, and a scourge in your sides, and thorns in your eyes, until ye perish from off this good land which Jehovah your God has given you.
14 “Aliyense wa inu akudziwa mu mtima mwake komanso mʼmoyo mwake kuti zabwino zonse zimene Yehova Mulungu wanu anakulonjezani zachitika. Palibe lonjezo ndi limodzi lomwe limene silinakwaniritsidwe.
And, behold, this day I am going the way of all the earth. And ye know in all your hearts and in all your souls, that not one thing has failed of all the good things which Jehovah your God spoke concerning you. All have come to pass to you; not one thing has failed of it.
15 Monga momwe Yehova Mulungu wanu wakuchitirani zabwino zonse zimene ananena kuti adzachita, Yehovayo angathenso kukuchitirani zoyipa zonse zimene waopseza, mpaka kukuchotsani mʼdziko lokoma limene anakupatsani.
And it shall come to pass, that as all the good things have come upon you of which Jehovah your God spoke to you, so will Jehovah bring upon you all the evil things, until he has destroyed you from off this good land which Jehovah your God has given you.
16 Ngati muphwanya pangano la Yehova Mulungu wanu, limene anakulamulirani nʼkumapita kukatumikira milungu ina ndi kuyigwadira, Yehova adzakukwiyirani, ndiye mudzachotsedwa mʼdziko labwinoli limene Yehova wakupatsani.”
When ye transgress the covenant of Jehovah your God, which he commanded you, and go and serve other gods, and bow down yourselves to them, then the anger of Jehovah will be kindled against you, and ye shall perish quickly from off the good land which he has given to you.

< Yoswa 23 >