< Yoswa 22 >

1 Pambuyo pake Yoswa anayitanitsa fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase,
Then Joshua called the Reubenites, and the Gadites, and the half-tribe of Manasseh,
2 ndipo anawawuza kuti, “Inu mwachita zonse zimene Mose mtumiki wa Yehova anakulamulani, ndipo mwamvera mu zonse zimene ndinakulamulirani.
and said to them, Ye have kept all that Moses the servant of Jehovah commanded you, and have hearkened to my voice in all that I commanded you.
3 Aisraeli anzanu simunawasiye nthawi yayitali yonseyi mpaka lero lino. Inu mwaonetsetsa kuti mwachita zonse zimene Yehova anakulamulani.
Ye have not left your brothers these many days to this day, but have kept the charge of the commandment of Jehovah your God.
4 Tsono pakuti Yehova Mulungu wanu wapereka mpumulo kwa abale anu monga anayankhulira nawo, bwererani ku nyumba zanu ku dziko limene Mose mtumiki wa Yehova anakupatsani, dziko limene lili pa tsidya la Yorodani kummawa.
And now Jehovah your God has given rest to your brothers, as he spoke to them. Therefore now turn ye, and get you to your tents, to the land of your possession, which Moses the servant of Jehovah gave you beyond the Jordan.
5 Koma samalitsani kuti mumvere malamulo ndi malangizo amene Mose mtumiki wa Yehova anakupatsani: kukonda Yehova Mulungu wanu, kuchita zimene iye amafuna, kumvera malamulo ake, kukhala okhulupirika kwa Iye ndi kumutumikira ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.”
Only take diligent heed to do the commandment and the law which Moses the servant of Jehovah commanded you, to love Jehovah your God, and to walk in all his ways, and to keep his commandments, and to cling to him, and to serve him with all your heart and with all your soul.
6 Ndipo Yoswa anawadalitsa ndi kuwalola kuti apite ndipo anapitadi ku nyumba zawo.
So Joshua blessed them, and sent them away, and they went to their tents.
7 Apa nʼkuti Mose atapereka dziko la Basani ku theka lina la fuko la Manase. Koma theka lina la fuko la Manase Yoswa analipatsa dziko la kumadzulo kwa Yorodani pamodzi ndi abale awo onse. Pamene Yoswa ankawatumiza kwawo anthu amenewa, anawadalitsa,
Now to the one half-tribe of Manasseh Moses had given in Bashan, but to the other half Joshua gave among their brothers beyond the Jordan westward. Moreover when Joshua sent them away to their tents, he blessed them,
8 nawawuza kuti, “Mukubwerera kwanu ndi chuma chambiri. Muli ndi ngʼombe zambiri pamodzi ndi siliva, golide, mkuwa ndi chitsulo, ndiponso zovala zambiri. Izi zimene munafunkha kwa adani anu agawireni abale anu.”
and spoke to them, saying, Return with much wealth to your tents, and with very much cattle, with silver, and with gold, and with brass, and with iron, and with very much raiment. Divide the spoil of your enemies with your brothers.
9 Choncho mafuko a Rubeni, Gadi, pamodzi ndi theka la fuko la Manase anabwerera kwawo. Aisraeli ena onse anawasiya ku Silo mʼdziko la Kanaani. Tsono anapita ku dziko la Giliyadi, dziko limene linali lawo popeza analilandira potsata malamulo a Yehova kudzera mwa Mose.
And the sons of Reuben and the sons of Gad and the half-tribe of Manasseh returned, and departed from the sons of Israel out of Shiloh, which is in the land of Canaan, to go to the land of Gilead, to the land of their possession, of which they were possessed, according to the commandment of Jehovah by Moses.
10 Atafika ku Geliloti, malo amene ali mʼmbali mwa mtsinje wa Yorodani mʼdziko la Kanaani, fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase anamanga guwa lansembe lalikulu pamenepo.
And when they came to the region about the Jordan that is in the land of Canaan, the sons of Reuben and the sons of Gad and the half-tribe of Manasseh built there an altar by the Jordan, a great altar to look upon.
11 Ndipo pamene Aisraeli ena onse anawuzidwa kuti anthu a fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase amanga guwa lansembe mʼmalire a Kanaani ku Geliloti, ku tsidya lathu lino la Yorodani,
And the sons of Israel heard say, Behold, the sons of Reuben and the sons of Gad and the half-tribe of Manasseh have built an altar in the forefront of the land of Canaan, in the region about the Jordan, on the side that pertains to the sons of Israel.
12 gulu lonse la Aisraeli linasonkhana ku Silo kuti lipite kukachita nawo nkhondo.
And when the sons of Israel heard of it, the whole congregation of the sons of Israel gathered themselves together at Shiloh, to go up against them to war.
13 Choncho Aisraeli anatumiza Finehasi mwana wa wansembe, Eliezara ku dziko la Giliyadi kwa mafuko a Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase.
And the sons of Israel sent Phinehas, the son of Eleazar the priest, to the sons of Reuben, and to the sons of Gad, and to the half-tribe of Manasseh, into the land of Gilead,
14 Pamodzi ndi Finehasiyo anatumiza akuluakulu khumi ochokera ku fuko lililonse la Aisraeli. Aliyense mwa akuluakulu amenewa anali mtsogoleri wa banja limodzi la mafuko a Aisraeli.
and with him ten rulers, one ruler of a fathers' house for each of the tribes of Israel. And they were each man of them head of their fathers' houses among the thousands of Israel.
15 Atafika ku Giliyadi anawuza fuko la Rubeni, Gadi ndi theka lija la fuko la Manase kuti,
And they came to the sons of Reuben, and to the sons of Gad, and to the half-tribe of Manasseh, to the land of Gilead, and they spoke with them, saying,
16 “Gulu lonse likukufunsa kuti, ‘Chifukwa chiyani mwachita chinthu chonyansa chotere potsutsana ndi Mulungu wa Israeli? Nʼchifukwa chiyani mwapatuka ndi kuleka kutsata Yehova podzimangira nokha guwa lansembe? Mwapandukiratu Yehova!
Thus says the whole congregation of Jehovah, What trespass is this that ye have committed against the God of Israel, to turn away this day from following Jehovah, in that ye have built for you an altar, to rebel this day against Jehovah?
17 Kodi tchimo lija la ku Peori ndi lochepa kwa inu? Paja Yehova analanga gulu lonse ndi mliri chifukwa cha tchimolo, ndipo mpaka lero tchimo limene lija tikanazunzika nalobe.
Is the iniquity of Peor too little for us, from which we have not cleansed ourselves to this day, although there came a plague upon the congregation of Jehovah,
18 Kodi inu tsono mufuna kupatuka kuleka kumutsata Yehova? “‘Ngati lero mumupandukira Yehovayo, ndiye kuti mawamawali Iye adzakwiyira gulu lonse wa Israeli.
that ye must turn away this day from following Jehovah? And it will be, seeing ye rebel today against Jehovah, that tomorrow he will be angry with the whole congregation of Israel.
19 Ngati dziko limene inu mwatenga ndi loyipitsidwa, bwerani ku dziko la Yehova kumene kuli chihema chake kuja, ndipo mukhale nafe limodzi. Koma inu musawukire Yehova kapena kutisandutsa ife kukhala opanduka podzimangira guwa lansembe, kuwonjezera pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu.
However, if the land of your possession is unclean, then pass ye over to the land of the possession of Jehovah, in which Jehovah's tabernacle dwells, and take possession among us, but do not rebel against Jehovah, nor rebel against us, in building for you an altar besides the altar of Jehovah our God.
20 Kumbukirani pamene Akani mwana wa Zera anakana kumvera lamulo la zinthu zoyenera kuwonongedwa, kodi suja mkwiyo wa Yehova unagwera gulu lonse la Israeli? Akaniyo sanafe yekha chifukwa cha tchimo lakelo.’”
Did not Achan the son of Zerah commit a trespass in what was set apart, and wrath fell upon all the congregation of Israel? And that man did not perish alone in his iniquity.
21 Tsono mafuko a Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase anawayankha atsogoleri a mabanja a Israeli aja kuti,
Then the sons of Reuben and the sons of Gad and the half-tribe of Manasseh answered, and spoke to the heads of the thousands of Israel,
22 “Wamphamvu uja, Mulungu ndiye Yehova! Wamphamvu uja Mulungu ndiye Yehova. Iyeyu ndiye akudziwa chifukwa chiyani tinachita zimenezi. Tikufunanso kuti inu mudziwe. Ngati tinachita izi mopandukira ndiponso moonetsa kusakhulupirira Yehova, lero lomwe lino musatisiye ndi moyo.
The Mighty One, God, Jehovah, the Mighty One, God, Jehovah, he knows, and Israel he shall know, if it is in rebellion, or if in trespass against Jehovah (do not save us this day),
23 Ngati tinapandukira Yehova ndi kuleka kumutsata pamene tinadzimangira guwa loti tizipserezerapo nsembe kapena kupereka nsembe zaufa, kapena nsembe za mtendere, Yehova yekha ndiye atilange.
that we have built us an altar to turn away from following Jehovah, or if to offer burnt offering or meal offering on it, or if to offer sacrifices of peace offerings on it, let Jehovah himself require it,
24 “Ayi! Ife tinachita izi kuopa kuti tsiku lina zidzukulu zanu zingadzanene kwa zidzukulu zathu kuti, ‘Kodi inu mukufuna chiyani kwa Yehova Mulungu wa Israeli?
and if we have not rather out of carefulness done this, from purpose, saying, In time to come your sons might speak to our sons, saying, What have ye to do with Jehovah, the God of Israel?
25 Yehova anayika mtsinje wa Yorodani kukhala malire pakati pa ife ndi inu, anthu a fuko la Rubeni ndi Gadi. Inuyo mulibe gawo mwa Yehova.’ Tsono mwina zidzukulu zanuzo nʼkudzaletsa zathu kupembedza Yehova.
For Jehovah has made the Jordan a border between us and you, ye sons of Reuben and sons of Gad. Ye have no portion in Jehovah. So your sons might make our sons cease from fearing Jehovah.
26 “Nʼchifukwa chake tinaganiza kuti, ‘Tiyeni timange guwa lansembe, koma osati kuti tiziperekapo nsembe zopsereza kapena zopereka.’
Therefore we said, Let us now prepare to build us an altar, not for burnt offering, nor for sacrifice,
27 Koma mosiyana ndi zimenezi, guwali likhale umboni pakati pa ife ndi inu ndiponso mibado imene ikubwerayo, kuti ife timapembedzanso Yehova ndi nsembe zathu zopsereza, zopereka, ndiponso nsembe za mtendere. Motero mʼtsogolo muno zidzukulu zanu sizidzatha kunena kwa zidzukulu zathu kuti, ‘Inu mulibe gawo mwa Yehova!’
but it shall be a witness between us and you, and between our generations after us, that we may do the service of Jehovah before him with our burnt offerings, and with our sacrifices, and with our peace offerings, that your sons may not say to our sons in time to come, Ye have no portion in Jehovah.
28 “Ndipo ife tinati kuti, ‘Ngati iwo adzatiyankhulira kapena kuyankhulira zidzukulu zathu motero mʼtsogolo muno, ife tidzayankha kuti, onani guwa lansembe, lofanana ndi lomwe makolo athu anamanga osati loperekerapo nsembe zopsereza kapena nsembe zina koma ngati umboni pakati pa inu ndi ife.’
Therefore we said, It shall be, when they so say to us or to our generations in time to come, that we shall say, Behold the pattern of the altar of Jehovah, which our fathers made, not for burnt offering, nor for sacrifice, but it is a witness between us and you.
29 “Sizingatheke konse kuti ife lero nʼkupandukira Yehova. Ife sitingapatuke kuleka kumutsata Yehova ndi kumanga guwa lina la nsembe zopsereza, nsembe za zakudya, ndi nsembe zina zopikisana ndi guwa la Yehova, Mulungu wathu limene lili patsogolo pa Hema ya Yehova mʼmene amakhalamo.”
Far be it from us that we should rebel against Jehovah, and turn away this day from following Jehovah, to build an altar for burnt offering, for meal offering, or for sacrifice, besides the altar of Jehovah our God that is before his tabernacle.
30 Tsono Finehasi wansembe ndi atsogoleri a gululo amene anali naye atamva zimene anthu a fuko la Rubeni, Gadi ndi theka lakummawa la fuko la Manase ananena, anakondwera kwambiri.
And when Phinehas the priest, and the rulers of the congregation, even the heads of the thousands of Israel that were with him, heard the words that the sons of Reuben and the sons of Gad and the sons of Manasseh spoke, it pleased them well.
31 Ndipo Finehasi wansembe, mwana wa Eliezara anati kwa mafuko a Rubeni, Gadi ndi Manase, “Lero tadziwa kuti Yehova ali nafe chifukwa zimene mwachitazi simunawukire nazo Yehova. Inu mwapulumutsa Aisraeli onse ku chilango cha Yehova.”
And Phinehas the son of Eleazar the priest said to the sons of Reuben, and to the sons of Gad, and to the sons of Manasseh, This day we know that Jehovah is in the midst of us, because ye have not committed this trespass against Jehovah. Now ye have delivered the sons of Israel out of the hand of Jehovah.
32 Ndipo Finehasi mwana wa wansembe Eliezara, pamodzi ndi atsogoleriwo anachoka ku Giliyadi nasiya anthu a fuko la Rubeni ndi Gadi nabwerera ku Kanaani kwa Aisraeli anzawo, ndipo anakafotokoza zonsezi.
And Phinehas the son of Eleazar the priest, and the rulers, returned from the sons of Reuben, and from the sons of Gad, out of the land of Gilead, to the land of Canaan, to the sons of Israel, and brought them word again.
33 Mawu amenewa anakondweretsa Aisraeli onse ndipo anayamika Mulungu. Choncho sanakambenso zopita ku nkhondo kukawononga dziko limene Arubeni ndi Agadi ankakhalamo.
And the thing pleased the sons of Israel. And the sons of Israel blessed God, and spoke no more of going up against them to war, to destroy the land in which the sons of Reuben and the sons of Gad dwelt.
34 Arubeni ndi Agadi anatcha guwalo kuti Mboni: Mboni pakati pathu kuti Yehova ndi Mulungu.
And the sons of Reuben and the sons of Gad called the altar Witness. For, they said, it is a witness between us that Jehovah is God.

< Yoswa 22 >