< Yoswa 24 >

1 Tsono Yoswa anasonkhanitsa mafuko onse a Israeli ku Sekemu. Iye anayitanitsa akuluakulu, atsogoleri, oweruza, ndi akuluakulu a boma la Israeli, ndipo iwo anafika pamaso pa Mulungu.
And Joshua gathered all the tribes of Israel to Shechem, and called for the elders of Israel, and for their heads, and for their judges, and for their officers; and they presented themselves before God.
2 Yoswa anati kwa anthu onse, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Kalekale makolo anu, kuphatikiza Tera, abambo a Abrahamu ndi Nahori ankakhala kutsidya kwa Mtsinje ndipo ankapembedza milungu ina.
And Joshua said to all the people, Thus says Jehovah, the God of Israel: Your fathers dwelt of old time beyond the River, even Terah, the father of Abraham, and the father of Nahor, and they served other gods.
3 Koma ine ndinatenga kholo lanu Abrahamu kumuchotsa ku dziko la kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate ndipo ndinamutsogolera kupita ku dziko la Kanaani. Ndinamupatsa zidzukulu zambiri. Ndinamupatsa Isake,
And I took your father Abraham from beyond the River, and led him throughout all the land of Canaan, and multiplied his seed, and gave him Isaac.
4 ndipo Isake ndinamupatsa Yakobo ndi Esau. Ndinapereka dziko la mapiri la Seiri kwa Esau, koma Yakobo ndi ana ake anapita ku Igupto.
And I gave to Isaac, Jacob and Esau. And I gave to Esau mount Seir to possess it. And Jacob and his sons went down into Egypt.
5 “‘Kenaka ndinatuma Mose ndi Aaroni, ndipo ine ndinazunza Aigupto. Pambuyo pake ndinakutulutsani.
And I sent Moses and Aaron, and I plagued Egypt, according to that which I did in the midst of it, and afterward I brought you out.
6 Nditatulutsa makolo anu ku Igupto ndinafika nawo ku Nyanja Yofiira. Aigupto anawathamangira ndi magaleta ndi okwera pa akavalo mpaka ku Nyanja Yofiira.
And I brought your fathers out of Egypt. And ye came to the sea, and the Egyptians pursued after your fathers with chariots and with horsemen to the Red Sea.
7 Tsono makolo anuwo anapemphera kwa Ine kuti ndiwathandize, ndipo ndinayika mtambo wakuda pakati pawo ndi Aiguptowo, ndipo Nyanja inamiza Aigupto aja. Inu munaona ndi maso anu zimene ndinachita kwa Aiguptowo ndipo inu munakhala mʼchipululu nthawi yayitali.
And when they cried out to Jehovah, he put darkness between you and the Egyptians, and brought the sea upon them, and covered them. And your eyes saw what I did in Egypt, and ye dwelt in the wilderness many days.
8 “‘Pambuyo pake Ine ndinabwera nanu ku dziko la Aamori amene amakhala kummawa kwa Yorodani. Iwo anamenyana nanu koma ndinawapereka mʼdzanja lanu. Ndinawawononga pamaso panu, ndipo inu munalanda dziko lawo.
And I brought you into the land of the Amorites, who dwelt beyond the Jordan. And they fought with you. And I gave them into your hand, and ye possessed their land, and I destroyed them from before you.
9 Balaki mwana wa Zipori, mfumu ya Mowabu, analimbana ndi Israeli. Iye anayitanitsa Balaamu mwana wa Beori kuti akutemberereni.
Then Balak the son of Zippor, king of Moab, arose and fought against Israel. And he sent and called Balaam the son of Beor to curse you,
10 Koma ine sindinamvere Balaamu, kotero iye anakudalitsani mowirikiza ndipo ndinakulanditsani mʼdzanja lake.
but I would not hearken to Balaam. Therefore he blessed you greatly. So I delivered you out of his hand.
11 “‘Ndipo inu munawoloka Yorodani ndi kufika ku Yeriko. Anthu a ku Yeriko analimbana nanu pamodzi ndi Aamori, Aperezi, Akanaani, Ahiti, Agirigasi, Ahivi ndi Ayebusi. Koma Ine ndinawapereka mʼdzanja lanu.
And ye went over the Jordan, and came to Jericho. And the men of Jericho fought against you, the Amorite, and the Perizzite, and the Canaanite, and the Hittite, and the Girgashite, the Hivite, and the Jebusite. And I delivered them into your hand.
12 Ine ndinatumiza mavu amene anapirikitsa mafumu awiri Aamori aja pamaso panu. Inu simunachite izi ndi lupanga ndi uta wanu.
And I sent the hornet before you, which drove them out from before you, even the two kings of the Amorites, not with thy sword, nor with thy bow.
13 Motero ndinakupatsani dziko limene simunalivutikire ndiponso mizinda imene simunamange. Inu mukukhala mʼmenemo ndi kumadya zipatso za mʼmunda wamphesa ndi kuthyola zipatso mʼmitengo ya olivi zimene simunadzale.’
And I gave you a land in which thou had not labored, and cities which ye did not build, and ye dwell in it. Ye eat of vineyards and oliveyards which ye did not plant.
14 “Ndipo tsopano wopani Yehova ndi kumutumikira Iye mokhulupirika ndi moona. Chotsani milungu imene makolo anu ankapembedza kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate ndi ku Igupto ndipo tumikirani Yehova.
Now therefore fear Jehovah, and serve him in sincerity and in truth. And put away the gods which your fathers served beyond the River, and in Egypt, and serve ye Jehovah.
15 Koma ngati kutumikira Yehova kukuyipirani, sankhani lero amene mudzamutumikire, kapena milungu imene makolo anu ankayitumikira kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate, kapena milungu ya Aamori, amene mukukhala mʼdziko lawo. Koma ine ndi banja langa, tidzatumikira Yehova.”
And if it seems evil to you to serve Jehovah, choose you this day whom ye will serve: whether the gods which your fathers served that were beyond the River, or the gods of the Amorites, in whose land ye dwell. But as for me and my house, we will serve Jehovah.
16 Ndipo anthu anayankha, “Sizingatheke kuti timusiye Yehova ndi kutumikira milungu ina!
And the people answered and said, Far be it from us that we should forsake Jehovah, to serve other gods.
17 Yehova Mulungu wathu ndiye amene anatitulutsa ife ndi makolo athu mu ukapolo, mʼdziko la Igupto. Tinaona ndi maso athu zizindikiro zozizwitsa zimene anachita. Iye anatiteteza pa ulendo wathu wonse ndi pakati pa mitundu yonse imene tinkakumana nayo.
For Jehovah our God, he it is who brought us and our fathers up out of the land of Egypt, from the house of bondage, and who did those great signs in our sight, and preserved us in all the way in which we went, and among all the peoples through the midst of whom we passed.
18 Ife tikufika Iye anapirikitsa anthu onse pamodzi ndi Aamori amene ankakhala mʼdzikoli. Ifenso tidzatumikira Yehova chifukwa Iye ndiye Mulungu.”
And Jehovah drove out from before us all the peoples, even the Amorites who dwelt in the land. Therefore we also will serve Jehovah, for he is our God.
19 Koma Yoswa anati kwa anthuwo, “Inutu simungathe kutumikira Yehova. Iye ndi Mulungu woyera, salola kupikisana naye. Sadzakukhululukirani ngati mumuwukira ndi kumuchimwira.
And Joshua said to the people, Ye cannot serve Jehovah, for he is a holy God. He is a jealous God. He will not forgive your transgression nor your sins.
20 Ngati inu musiya Yehova ndi kutumikira milungu yachilendo, adzakufulatirani. Iye adzakulangani ndi kukuwonongani ngakhale kuti poyamba anakuchitirani zabwino.”
If ye forsake Jehovah, and serve foreign gods, then he will turn and do you evil, and consume you, after he has done you good.
21 Koma anthuwo anati kwa Yoswa, “Ayi! Ife tidzatumikira Yehova.”
And the people said to Joshua, No, but we will serve Jehovah.
22 Kenaka Yoswa anati, “Inu mukudzichitira nokha umboni kuti mwasankha kutumikira Yehova.” Iwo anayankha kuti, “Inde ife ndife mboni.”
And Joshua said to the people, Ye are witnesses against yourselves that ye have chosen for you, Jehovah, to serve him. And they said, We are witnesses.
23 Yoswa anati, “Tsono chotsani milungu yachilendo imene ili pakati panu ndipo perekani mitima yanu kwa Yehova Mulungu wa Israeli.”
Now therefore, he said, put away the foreign gods which are among you, and incline your heart to Jehovah, the God of Israel.
24 Ndipo anthuwo anati kwa Yoswa, “Ife tidzatumikira Yehova Mulungu wathu ndi kumvera Iye.”
And the people said to Joshua, we will serve Jehovah our God, and we will hearken to his voice.
25 Choncho pa tsiku limenelo Yoswa anachita pangano mʼmalo mwa anthuwo, ndipo pa Sekemu pomwepo iye anapereka malamulo ndi malangizo kwa anthu aja.
So Joshua made a covenant with the people that day, and set them a statute and an ordinance in Shechem.
26 Ndipo Yoswa analemba zinthu izi mʼbuku la malamulo a Mulungu. Kenaka iye anatenga mwala waukulu nawuyimika pansi pa mtengo wa thundu pa malo wopatulika a Yehova.
And Joshua wrote these words in the book of the law of God. And he took a great stone, and set it up there under the oak that was by the sanctuary of Jehovah.
27 Yoswa anati kwa anthu onse, “Tamvani! Mwala uwu udzakhala mboni yotitsutsa. Mwalawu wamva mawu onse amene Yehova wayankhula kwa ife. Udzakhala mboni yotitsutsa ngati mukhala osakhulupirika kwa Mulungu wanu.”
And Joshua said to all the people, Behold, this stone shall be a witness against us, for it has heard all the words of Jehovah which he spoke to us. It shall be therefore a witness against you, lest ye deny your God.
28 Kenaka Yoswa analola anthu kuti apite, aliyense ku dera lake.
So Joshua sent the people away, every man to his inheritance.
29 Zitatha zinthu izi, Yoswa mwana wa Nuni, mtumiki wa Yehova, anamwalira ali ndi zaka 110,
And it came to pass after these things, that Joshua the son of Nun, the servant of Jehovah, died, being a hundred and ten years old.
30 ndipo anamuyika mʼmanda mʼdziko lake, ku Timnati-Sera dziko lamapiri la ku Efereimu, kumpoto kwa phiri la Gaasi.
And they buried him in the border of his inheritance in Timnathserah, which is in the hill-country of Ephraim, on the north of the mountain of Gaash.
31 Israeli anatumikira Yehova pa nthawi yonse imene Yoswa anali ndi moyo ndiponso pa nthawi ya akuluakulu amene anali moyo Yoswa atamwalira, anthu amene ankadziwa zonse zimene Yehova anachitira Israeli.
And Israel served Jehovah all the days of Joshua, and all the days of the elders who outlived Joshua, and had known all the work of Jehovah that he had wrought for Israel.
32 Ndipo mafupa a Yosefe amene Aisraeli anawatulutsa ku Igupto anawayika mʼmanda a ku Sekemu pa malo amene Yakobo anagula ndi ndalama zasiliva 100 kwa ana a Hamori, abambo a Sekemu. Malo awa anakhala cholowa cha adzukulu a Yosefe.
And they buried the bones of Joseph, which the sons of Israel brought up out of Egypt, in Sicima, in the portion of the land which Jacob bought from the Amorites who dwelt in Sicima for a hundred ewe-lambs. And he gave it to Joseph for a portion.
33 Ndipo Eliezara mwana wa Aaroni anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda ku Gibeya, malo amene anapatsidwa kwa Finehasi mwana wake, mʼdziko lamapiri la Efereimu.
And Eleazar the son of Aaron died. And they buried him in the hill of Phinehas his son, which was given him in the hill-country of Ephraim.

< Yoswa 24 >