< Yobu 16 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Then Job answered, and said,
2 “Ndinamvapo zambiri monga zimenezi; nonsenu ndinu anthu osatha kutonthoza mtima mnzanu.
I have heard many such things. Miserable comforters are ye all.
3 Kodi mawu anu ochulukawo adzatha? Kodi chikukuvutani nʼchiyani kuti muzingoyankhula mawu otsutsawa?
Shall vain words have an end? Or what provokes thee that thou answer?
4 Inenso ndikanatha kuyankhula monga inu, inuyo mukanakhala monga ndilili inemu; Ine ndikanatha kuyankhula mawu omveka bwino kutsutsana nanu ndi kukupukusirani mutu wanga.
I also could speak as ye do, if your soul were in my soul's stead. I could join words together against you, and shake my head at you.
5 Ndipo mawu a pakamwa panga akanakulimbikitsani; chitonthozo chochokera pa milomo yanga chikanachepetsa ululu wanu.
But I would strengthen you with my mouth, and the solace of my lips would assuage your grief.
6 “Koma ine ndikati ndiyankhule ululu wanga sukuchepa; ndipo ndikati ndikhale chete, ululu wanga sukuchokabe.
Though I speak, my grief is not assuaged, and though I forbear, what am I eased?
7 Ndithudi, Inu Mulungu mwanditha mphamvu; mwawononga banja langa lonse.
But now he has made me weary. Thou have made desolate all my company.
8 Inu mwandimanga ndipo kundimangako kwakhala umboni; kuwonda kwanga kwandiwukira ndipo kukuchita umboni wonditsutsa.
And thou have laid fast hold on me, which is a witness against me. And my leanness rises up against me; it testifies to my face.
9 Mulungu amabwera kwa ine mwankhanza ndipo amadana nane, amachita kulumira mano; mdani wanga amandituzulira maso.
He has torn me in his wrath, and persecuted me. He has gnashed upon me with his teeth. My adversary sharpens his eyes upon me.
10 Anthu amatsekula pakamwa pawo kundikuwiza; amandimenya pa tsaya mwachipongwe ndipo amagwirizana polimbana nane.
They have gaped upon me with their mouth. They have smitten me upon the cheek reproachfully. They gather themselves together against me.
11 Mulungu wandipereka kwa anthu ochita zoyipa ndipo wandiponyera mʼmanja mwa anthu oyipa mtima.
God delivers me to the perverse, and casts me into the hands of the wicked.
12 Ine ndinali pamtendere, koma Mulungu ananditswanya; anandigwira pa khosi ndi kundiphwanya. Iye anandisandutsa choponyera chandamale chake;
I was at ease, and he broke me apart. Yea, he has taken me by the neck, and dashed me to pieces. He has also set me up for his mark.
13 anthu ake oponya mauta andizungulira. Mopanda kundimvera chisoni, Iye akulasa impsyo zanga ndipo akutayira pansi ndulu yanga.
His archers encompass me round about. He splits my reins apart, and does not spare. He pours out my gall upon the ground.
14 Akundivulaza kawirikawiri, akuthamangira pa ine monga munthu wankhondo.
He breaks me with breach upon breach. He runs upon me like a giant.
15 “Ndasokerera chiguduli pa thupi langa ndipo ndayika mphamvu zanga pa fumbi.
I have sewed sackcloth upon my skin, and have laid my horn in the dust.
16 Maso anga afiira ndi kulira, ndipo zikope zanga zatupa;
My face is red with weeping, and the shadow of death is on my eyelids,
17 komatu manja anga sanachite zachiwawa ndipo pemphero langa ndi lolungama.
although there is no violence in my hands, and my prayer is pure.
18 “Iwe dziko lapansi, usakwirire magazi anga; kulira kwanga kofuna thandizo kusalekeke!
O earth, do not cover thou my blood, and let my cry have no resting place.
19 Ngakhale tsopano mboni yanga ili kumwamba; wonditchinjiriza pa mlandu wanga ali komweko.
Even now, behold, my witness is in heaven, and he who vouches for me is on high.
20 Wondipembedzera ndi bwenzi langa, pamene maso anga akukhuthula misozi kwa Mulungu;
My friends scoff at me. My eye pours out tears to God
21 iye, mʼmalo mwanga, amamudandaulira Mulungu monga munthu amadandaulira bwenzi lake.
that he would maintain the right of a man with God, and of a son of man with his neighbor!
22 “Pakuti sipapita zaka zambiri ndisanayende mʼnjira imene sindidzabwerera.”
For when a few years are come, I shall go the way where I shall not return.

< Yobu 16 >