< Yeremiya 9 >

1 Aa, ndikanakonda kuti mutu wanga ukanakhala chitsime cha madzi, ndi maso anga ngati kasupe wa misozi! Ndikanalira usana ndi usiku kulirira anthu anga amene aphedwa.
Oh that my head were waters, and my eyes a fountain of tears, that I might weep day and night for the slain of the daughter of my people!
2 Ndani adzandipatsa malo ogona mʼchipululu kuti ndiwasiye anthu anga ndi kuwachokera kupita kutali; pakuti onse ndi achigololo, ndiponso gulu la anthu onyenga.
Oh that I had in the wilderness a lodging-place of wayfaring men, that I might leave my people, and go from them! For they are all adulterers, an assembly of treacherous men.
3 “Amapinda lilime lawo ngati uta. Mʼdzikomo mwadzaza ndi mabodza okhaokha osati zoonadi. Amapitirirabe kuchita zoyipa; ndipo sandidziwa Ine.” Akutero Yehova.
And they bend their tongue-their bow-for falsehood, and they have grown strong in the land, but not for truth. For they proceed from evil to evil, and they do not know me, says Jehovah.
4 “Aliyense achenjere ndi abwenzi ake; asadalire ngakhale abale ake. Aliyense amafuna kumudyera mʼbale wake masuku pa mutu. Choncho aliyense amachitira bwenzi lake ugogodi.
Take ye heed each one of his neighbor, and trust ye not in any brother, for every brother will utterly supplant, and every neighbor will go about with slanders.
5 Aliyense amamunamiza mʼbale wake ndipo palibe amene amayankhula choonadi. Anapazoloweza pakamwa pawo kunena zabodza; amalimbika kuchita machimo.
And they will deceive each one his neighbor, and will not speak the truth. They have taught their tongue to speak lies. They weary themselves to commit iniquity.
6 Iwe wakhalira mʼchinyengo ndipo ukukana kundidziwa Ine,” akutero Yehova.
Thy habitation is in the midst of deceit. Through deceit they refuse to know me, says Jehovah.
7 Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Taonani, Ine ndidzawasungunula ngati chitsulo ndi kuwayesa. Kodi ndingachite nawonso bwanji chifukwa cha machimo awo?
Therefore thus says Jehovah of hosts: Behold, I will melt them, and try them, for how else should I do, because of the daughter of my people?
8 Lilime lawo lili ngati muvi wakuthwa; limayankhula zachinyengo. Aliyense ndi pakamwa pake amayankhula mawu achikondi kwa mnansi wake, koma mu mtima mwake amakonzekera zomuchita chiwembu.
Their tongue is a deadly arrow; it speaks deceit. He speaks peaceably to his neighbor with his mouth, but in his heart he lies wait for him.
9 Kodi ndilekerenji kuwalanga chifukwa cha zimenezi? akutero Yehova. ‘Kodi ndisawulipsire mtundu wotere wa anthu?’”
Shall I not visit them for these things? says Jehovah. Shall not my soul be avenged on such a nation as this?
10 Ndidzakhetsa misozi ndi kulira kwamphamvu chifukwa cha mapiri ndipo ndidzadandaula chifukwa cha msipu wa ku chipululu. Malo onsewo awonongeka ndipo palibe amene amapitako, ndipo sikumveka kulira kwa ngʼombe. Mbalame zamlengalenga zathawa ndipo nyama zakuthengo zachokako.
For the mountains I will take up a weeping and wailing, and for the pastures of the wilderness a lamentation, because they are burned up, so that none passes through, nor can men hear the voice of the cattle. Both the birds of the heavens and the beasts have fled; they are gone.
11 Ndipo Yehova anati, “Ndidzasandutsa Yerusalemu kukhala bwinja, malo okhalamo ankhandwe; ndipo ndidzawononga mizinda ya Yuda kotero kuti palibe munthu amene adzakhalemo.”
And I will make Jerusalem heaps, a dwelling-place of jackals. And I will make the cities of Judah a desolation, without inhabitant.
12 Ine ndinati, “Kodi munthu wanzeru ndani woti nʼkumvetsa zimenezi? Kodi ndani amene Yehova anayankhula naye zimenezi kuti akafotokozere ena? Nʼchifukwa chiyani dziko lawonongeka ndi kusanduka chipululu, mʼmene anthu sadutsamo?”
Who is the wise man, who may understand this, and he to whom the mouth of Jehovah has spoken, that he may declare it? Why has the land perished and burned up like a wilderness, so that none passes through?
13 Yehova anati, “Nʼchifukwa chakuti anthuwa analeka kutsata malamulo anga amene ndinawapatsa; sanandimvere kapena kuwasamala.
And Jehovah says, Because they have forsaken my law which I set before them, and have not obeyed my voice, nor walked in it,
14 Mʼmalo mwake, anatsatira zolakwa za mʼmitima yawo; anapembedza Abaala ngati momwe makolo awo anawaphunzitsira.”
but have walked after the stubbornness of their own heart, and after the Baalim, which their fathers taught them.
15 Tsono chimene Ine Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli ndidzachite ndi anthu amenewa ndi ichi: “Ndidzawadyetsa chakudya cha ziphe ndi kuwamwetsa madzi a ndulu.
Therefore thus says Jehovah of hosts, the God of Israel: Behold, I will feed them, even this people, with wormwood, and give them water of gall to drink.
16 Ndidzawabalalitsa pakati pa mitundu ya anthu imene iwowo kapena makolo awo sanayidziwe, ndipo ndidzawalondola ndi ankhondo mpaka nditawawononga.”
I will scatter them also among the nations, whom neither they nor their fathers have known. And I will send the sword after them, till I have consumed them.
17 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Tsopano ganizirani! Muyitane akazi olira mwachisoni kuti abwere; itanani akazi odziwa kulira bwino.”
Thus says Jehovah of hosts, Consider ye, and call for the mourning women, that they may come, and send for the skilful women, that they may come.
18 Anthu akuti, “Abwere mofulumira kuti adzatilire mpaka mʼmaso mwathu mutatuluka misozi ndi kuti msidze zathu zinyowe ndi madzi.
And let them make haste, and take up a wailing for us, that our eyes may run down with tears, and our eyelids gush out with waters.
19 Kulira mwachisoni kukumveka kuchokera mu Ziyoni akuti, ‘Aa! Ife tawonongeka! Tachita manyazi kwambiri! Tiyenera kuchoka mʼdziko lathu chifukwa atipirikitsa mʼnyumba zathu.’”
For a voice of wailing is heard out of Zion, How we are ruined! We are greatly confounded, because we have forsaken the land, because they have cast down our dwellings.
20 Tsono inu amayi, imvani mawu a Yehova; tcherani makutu anu kuti mumve mawu a Yehova. Phunzitsani ana anu aakazi kulira mwachisoni; aliyense aphunzitse mnzake nyimbo ya maliro.
Yet hear the word of Jehovah, O ye women, and let your ear receive the word of his mouth, and teach your daughters wailing, and each one her neighbor lamentation.
21 Imfa yatifikira kudzera mʼmazenera athu ndipo yalowa mʼnyumba zathu zotetezedwa; yapha ana athu mʼmisewu, ndi achinyamata athu mʼmabwalo.
For death has come up into our windows. It has entered into our palaces, to cut off the sons from outside, the young men from the streets.
22 Yehova anandiwuza kuti ndinene izi kuti, “‘Mitembo ya anthu idzakhala ili lambalamba ngati ndowe mʼminda, ngati mapesi mʼmbuyo mwa wokolola, popanda munthu woyitola.’”
Speak, Thus says Jehovah: The dead bodies of men shall fall as dung upon the open field, and as the handful after the harvestman, and none shall gather.
23 Yehova akuti, “Munthu wanzeru asanyadire nzeru zake, kapena munthu wamphamvu kunyadira nyonga zake, kapena munthu wolemera kunyadira chuma chake,
Thus says Jehovah: Let not the wise man glory in his wisdom, nor let the mighty man glory in his might. Let not the rich man glory in his riches,
24 koma ngati munthu akufuna kunyadira, anyadire chinthu ichi: kuti iye amamvetsa za Ine ndipo amandidziwa, kuti ndine Yehova, amene ndimakonda chifundo, chilungamo ndiponso ungwiro pa dziko lapansi. Zimenezi ndizo ndimakondwera nazo,” akutero Yehova.
but let him who boasts boast in this, that he has understanding, and knows me, that I am Jehovah who exercises loving kindness, justice, and righteousness, in the earth. For in these things I delight, says Jehovah.
25 “Nthawi ikubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzalanga onse amene anachita mdulidwe koma mu mtima sasamala nʼkomwe.
Behold, the days come, says Jehovah, that I will punish all those who are circumcised in their uncircumcision:
26 Ndidzalanga anthu a ku Igupto, Yuda, Edomu, Amoni, Mowabu, ndiponso onse amene amakhala kutali ku chipululu. Mitundu ina yonseyi ndi yosachita mdulidwe, ngakhalenso Aisraeli nawonso sanachite mdulidwe wa mu mtima.”
Egypt, and Judah, and Edom, and the sons of Ammon, and Moab, and all who have the corners of their hair cut off, who dwell in the wilderness. For all the nations are uncircumcised, and all the house of Israel are uncircumcised in heart.

< Yeremiya 9 >