< Yeremiya 11 >

1 Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
The word that came to Jeremiah from Jehovah, saying,
2 “Imvani mawu a pangano ili, ndipo uwawuze anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu.
Hear ye the words of this covenant, and speak to the men of Judah, and to the inhabitants of Jerusalem,
3 Awuze kuti Yehova, Mulungu wa Israeli akuti ‘adzakhala wotembereredwa munthu amene samvera mawu a pangano ili.
and say thou to them, Thus says Jehovah, the God of Israel: Cursed be the man who does not hear the words of this covenant,
4 Awa anali mawu amene ndinalamulira makolo anu nditawatulutsa mu Igupto, kuchoka mʼngʼanjo yamoto.’ Ine ndinati, ‘Mverani Ine ndi kuchita chilichonse chimene ndakulamulirani. Mukatero mudzakhala anthu anga ndi Ine ndidzakhala Mulungu wanu.
which I commanded your fathers in the day that I brought them forth out of the land of Egypt, out of the iron furnace, saying, Obey my voice, and do them, according to all which I command you, so ye shall be my people, and I will be your God,
5 Tsono Ine ndidzakwaniritsa lumbiro lomwe ndinalumbira kwa makolo anu kuti ndidzawapatsa dziko loyenda mkaka ndi uchi,’ dziko lomwe inu lero mukukhalamo.” Tsono Ine ndinayankha kuti, “Ameni, Yehova.”
that I may establish the oath which I swore to your fathers, to give them a land flowing with milk and honey, as at this day. Then I answered, and said, Truly, O Jehovah.
6 Yehova anandiwuza kuti, “Lengeza mawu onsewa mʼmizinda yonse ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu: ‘Mverani mawu a pangano ili ndi kuzitsatira.
And Jehovah said to me, Proclaim all these words in the cities of Judah, and in the streets of Jerusalem, saying, Hear ye the words of this covenant, and do them.
7 Kuyambira nthawi imene ndinatulutsa makolo anu ku Igupto mpaka lero, ndakhala ndi kuwachenjeza kawirikawiri kuti, ‘Mverani Ine.’
For I earnestly protested to your fathers in the day that I brought them up out of the land of Egypt, even to this day, rising early and protesting, saying, Obey my voice.
8 Koma sanamvere kapena kulabadirako. Aliyense anawumirira kuchita zoyipa za mʼmitima yawo. Ngakhale ndinawalamulira kuti asunge pangano langa koma iwo sanasunge. Choncho ndinawalanga monga ndinaneneramo.’”
Yet they obeyed not, nor inclined their ear, but walked each one in the stubbornness of his evil heart. Therefore I brought upon them all the words of this covenant, which I commanded them to do, but they did them not.
9 Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Anthu a ku Yuda ndi ku Yerusalemu andiwukira.
And Jehovah said to me, A conspiracy is found among the men of Judah, and among the inhabitants of Jerusalem.
10 Abwereranso ku machimo a makolo awo, amene anakana kumvera mawu anga. Akutsata milungu ina ndi kumayitumikira. Aisraeli ndi Ayuda aphwanya pangano limene ndinachita ndi makolo awo.
They have turned back to the iniquities of their forefathers, who refused to hear my words, and they have gone after other gods to serve them. The house of Israel and the house of Judah have broken my covenant which I made with their fathers.
11 Choncho Yehova akuti, ‘Ndidzawagwetsera mavuto amene sadzatha kuwalewa. Ngakhale adzandilirire, sindidzawamvera.
Therefore thus says Jehovah, Behold, I will bring evil upon them, which they shall not be able to escape. And they shall cry to me, but I will not hearken to them.
12 Anthu a mʼmizinda ya Yuda ndi anthu a ku Yerusalemu adzapita ndi kukalirira milungu imene ankayifukizira lubani, koma milunguyo sidzawathandiza ndi pangʼono pomwe mavuto akadzafika.
Then the cities of Judah and the inhabitants of Jerusalem shall go and cry to the gods to which they offer incense, but they will not save them at all in the time of their trouble.
13 Iwe Yuda, uli ndi milungu yochuluka ngati chiwerengero cha mizinda yako; chiwerengero cha maguwa ansembe amene umafukizirapo lubani kwa Baala chili ngati misewu ya mu Yerusalemu.’
For according to the number of thy cities are thy gods, O Judah, and according to the number of the streets of Jerusalem ye have set up altars to the shameful thing, even altars to burn incense to Baal.
14 “Tsono iwe Yeremiya usawapempherere anthu amenewa ngakhale kuwadandaulira kapena kuwapepesera, chifukwa sindidzawamvera akadzandiyitana pa nthawi ya mavuto awo.
Therefore do not pray thou for this people, nor lift up cry nor prayer for them, for I will not hear them in the time that they cry to me because of their trouble.
15 “Kodi anthu anga okondedwa akudzachita chiyani mʼNyumba yanga? Kodi suja iwowa amachita zoyipa zambiri? Kodi mungathe kupulumuka, tsoka osakugwerani chifukwa cha nsembe zanuzo?”
What has my beloved to do in my house, seeing she has wrought lewdness with many, and the holy flesh has passed from thee? When thou do evil, then thou rejoice.
16 Kale Yehova ankakutchani mtengo wa olivi wa masamba obiriwira, wokhala ndi zipatso zokongola. Koma tsopano adzawutentha ndi mkuntho wamkokomo ndipo nthambi zake zidzapserera.
Jehovah called thy name, A green olive tree, fair with goodly fruit. With the noise of a great tumult he has kindled fire upon it, and the branches of it are broken.
17 Yehova Wamphamvuzonse, amene anakudzalani, walamula kuti mavuto akugwereni. Inu a banja la Yuda ndi a banja la Israeli munachitira Yehova zoyipa ndi kumukwiyitsa pamene munkapereka nsembe zanu kwa Baala.
For Jehovah of hosts, who planted thee, has pronounced evil against thee because of the evil of the house of Israel and of the house of Judah, which they have wrought for themselves in provoking me to anger by offering incense to Baal.
18 Yehova anandiwululira ndipo ndinadziwa. Iye anatsekula maso anga kuti ndione chiwembu chawocho.
And Jehovah gave me knowledge of it, and I knew it. Then thou showed me their doings.
19 Ndinali ngati mwana wankhosa wofatsa amene akupita naye kukamupha; sindinkadziwa kuti chiwembu chimene ankakonzekeracho chinkaloza ine. Iwo amati: “Tiyeni timuphe munthu ameneyu kuti dzina lake lisadzakumbukiridwenso.”
But I was like a gentle lamb that is led to the slaughter. And I knew not that they had devised devices against me, saying, Let us destroy the tree with the fruit of it. And let us cut him off from the land of the living, that his name may no more be remembered.
20 Koma, Inu Yehova Wamphamvuzonse, Inu amene mumaweruza molungama ndi kuyesa mitima ndi maganizo, lolani kuti ine ndione kuti mwawalipsira, pakuti mlandu wanga ndawupereka mʼmanja mwanu.
But, O Jehovah of hosts, who judges righteously, who tries the heart and the mind, I shall see thy vengeance on them, for to thee I have revealed my case.
21 “Nʼchifukwa chake Yehova akunena za anthu a ku Anatoti amene akufuna kuwononga moyo wako namanena kuti, ‘Usanenere mʼdzina la Yehova, ukatero ife tidzakupha ndi manja athu,’
Therefore thus says Jehovah concerning the men of Anathoth, who seek thy life, saying, Thou shall not prophesy in the name of Jehovah, that thou not die by our hand.
22 koma Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Ine ndidzawalanga. Achinyamata awo adzaphedwa ndi lupanga, ana awo aamuna ndi aakazi adzafa ndi njala.
Therefore thus says Jehovah of hosts: Behold, I will punish them. The young men shall die by the sword. Their sons and their daughters shall die by famine,
23 Sipadzakhala otsala ndi mmodzi yemwe, chifukwa ndidzalanga anthu a ku Anatoti chikadzafika chaka chawo cha chilango.’”
and there shall be no remnant to them. For I will bring evil upon the men of Anathoth, even the year of their visitation.

< Yeremiya 11 >