< Yeremiya 16 >

1 Kenaka Yehova anandiwuza kuti,
The word of Jehovah came also to me, saying,
2 “Usadzakwatire ndi kubereka ana aamuna kapena aakazi malo ano
Thou shall not take thee a wife, nor shall thou have sons or daughters, in this place.
3 pakuti ana aamuna ndi ana aakazi obadwira mʼdziko muno, komanso amayi awo ndi abambo awo amene anabereka anawo mʼdziko muno,
For thus says Jehovah concerning the sons and concerning the daughters that are born in this place, and concerning their mothers who bore them, and concerning their fathers who begot them in this land:
4 adzafa ndi nthenda zoopsa. Sadzawalira maliro kapena kuyikidwa mʼmanda koma adzakhala ngati ndowe zotayikira pansi. Ena adzaphedwa ku nkhondo ndipo ena adzafa ndi njala. Mitembo yawo idzakhala chakudya cha mbalame zamlengalenga ndi zirombo zakuthengo.”
They shall die grievous deaths. They shall not be lamented, nor shall they be buried; they shall be as dung upon the face of the ground. And they shall be consumed by the sword, and by famine. And their dead bodies shall be food for the birds of the heavens, and for the beasts of the earth.
5 Yehova akuti, “Usalowe mʼnyumba ya maliro; usapite kukalira maliro kapena kukapepesa, chifukwa Ine ndawachotsera madalitso anga, chikondi changa ndi chifundo changa.”
For thus says Jehovah, Enter not into the house of mourning, nor go to lament, nor bemoan them, for I have taken away my peace from this people, says Jehovah, even loving kindness and tender mercies.
6 Akuluakulu ndi angʼonoangʼono omwe adzafa mʼdziko muno. Sadzayikidwa mʼmanda kapena kuliridwa, ndipo palibe amene adzaonetse chisoni podzichekacheka kapena kumeta tsitsi lake chifukwa cha iwo.
Both great and small shall die in this land. They shall not be buried, nor shall men lament for them, nor cut themselves, nor make themselves bald for them,
7 Palibe amene adzapereka chakudya kutonthoza amene akulira maliro, ngakhale kuti womwalirayo ndi abambo ake kapena amayi ake.
nor shall men break bread for them in mourning, to comfort them for the dead, nor shall men give them the cup of consolation to drink for their father or for their mother.
8 “Ndipo usalowe mʼnyumba mmene muli madyerero, nʼkukhala pansi ndi kudya ndi kumwa nawo.
And thou shall not go into the house of feasting to sit with them, to eat and to drink.
9 Pakuti Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akunena kuti, ‘Pa nthawi yanu, inu mukuona ndidzathetsa mawu achimwemwe ndi achisangalalo ndiponso mawu a mkwati ndi mkwatibwi pa malo ano.’
For thus says Jehovah of hosts, the God of Israel: Behold, I will cause to cease out of this place, before your eyes and in your days, the voice of mirth and the voice of gladness, the voice of the bridegroom and the voice of the bride.
10 “Ukawawuza anthu awa zinthu zonsezi akakufunsa kuti, ‘Chifukwa chiyani Yehova wanena kuti tsoka lalikulu lotere lidzatigwere? Kodi talakwa chiyani? Kodi tamuchimwira tchimo lotani Yehova Mulungu wathu?’
And it shall come to pass, when thou shall show this people all these words, and they shall say to thee, Why has Jehovah pronounced all this great evil against us? Or what is our iniquity? Or what is our sin that we have committed against Jehovah our God?
11 Pamenepo ukawawuze kuti, ‘Nʼchifukwa chakuti makolo anu anandisiya Ine,’ akutero Yehova, ‘ndi kutsatira milungu ina, kuyitumikira ndi kuyipembedza. Iwo anandisiya Ine ndipo sanasunge lamulo langa.
Then thou shall say to them, Because your fathers have forsaken me, says Jehovah, and have walked after other gods, and have served them, and have worshiped them, and have forsaken me, and have not kept my law.
12 Komanso inu munachimwa kwambiri kupambana makolo anu. Aliyense wa inu akutsatira zoyipa ndi mtima wake wokanikawo mʼmalo mondimvera Ine.
And ye have done evil more than your fathers, for, behold, ye walk each one after the stubbornness of his evil heart, so that ye hearken not to me.
13 Choncho Ine ndidzakubalalitsani mʼdziko muno ndi kukulowetsani mʼdziko limene inu ndi makolo anu simunalidziwe. Kumeneko mukatumikira milungu ina usana ndi usiku, ndipo sadzakuchitirani chifundo.’”
Therefore I will cast you forth out of this land into the land that ye have not known, neither ye nor your fathers, and there ye shall serve other gods day and night, for I will show you no favor.
14 Yehova akuti, “Komabe masiku akubwera pamene anthu polumbira sadzatinso, ‘Pali Yehova wamoyo, amene anatulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto,’
Therefore, behold, the days come, says Jehovah, that it shall no more be said, As Jehovah lives who brought up the sons of Israel out of the land of Egypt,
15 koma adzanena kuti, ‘Pali Yehova wamoyo, amene anatulutsa Aisraeli ku dziko lakumpoto, ndi ku mayiko onse kumene anawabalalitsirako.’ Pakuti ndidzawabwezera ku dziko limene ndinalipereka kwa makolo awo.”
but, As Jehovah lives who brought up the sons of Israel from the land of the north, and from all the countries where he had driven them. And I will bring them again into their land that I gave to their fathers.
16 Yehova akuti, “Koma tsopano ndidzayitana adani okhala ngati asodzi ambiri, ndipo adzawagwira ngati nsomba. Izi zitatha adani enanso okhala ngati alenje ambiri, adzawasaka pa phiri lililonse, pa chitunda chilichonse ndiponso mʼmapanga onse a mʼmatanthwe.
Behold, I will send for many fishermen, says Jehovah, and they shall fish them up. And afterward I will send for many hunters, and they shall hunt them from every mountain, and from every hill, and out of the clefts of the rocks.
17 Maso anga akuona makhalidwe awo onse; sanabisike pamaso panga. Palibe tchimo limene sindikulidziwa.
For my eyes are upon all their ways. They are not hid from my face, nor is their iniquity concealed from my eyes.
18 Ndidzawalanga mowirikiza chifukwa cha kuyipa kwawo ndi tchimo lawo. Ndidzatero chifukwa ayipitsa dziko langa ndi mafano awo amene ali ngati mitembo, ndiponso adzaza cholowa changa ndi mafano awo onyansa.”
And first I will recompense their iniquity and their sin double, because they have polluted my land with the carcasses of their detestable things, and have filled my inheritance with their abominations.
19 Inu Yehova, ndinu mphamvu yanga ndi linga langa, pothawirapo panga nthawi ya masautso, anthu a mitundu yonse adzabwera kwa Inu kuchokera ku mathero onse a dziko lapansi ndipo adzanena kuti, “Makolo anthu anali ndi milungu yonama, anali ndi mafano achabechabe amene sanawathandize.
O Jehovah, my strength, and my stronghold, and my refuge in the day of affliction, to thee the nations shall come from the ends of the earth, and shall say, Our fathers have inherited nothing but lies, even vanity and things in which there is no profit.
20 Kodi anthu nʼkudzipangira milungu? Atati atero ndiye kuti imeneyo ikhala milungu yachabechabe.”
Shall a man make to himself gods, which yet are no gods?
21 “Choncho Ine ndidzawaphunzitsa, kokha kano kuti adziwe za mphamvu yanga ndi za nyonga zanga. Pamenepo adzadziwa kuti dzina langa ndi Yehova.
Therefore, behold, I will cause them to know, this once I will cause them to know my hand and my might, and they shall know that my name is Jehovah.

< Yeremiya 16 >