< Yeremiya 15 >

1 Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Ngakhale Mose ndi Samueli akanayima pamaso panga kupempherera anthu awa, Ine sindikanawachitira chisoni. Achotseni ndipo ndisawaonenso! Aleke apite!
Then Jehovah said to me, Though Moses and Samuel stood before me, yet my mind would not be toward this people. Cast them out of my sight, and let them go forth.
2 Ndipo ngati akufunsa iwe kuti, ‘Kodi tipite kuti?’ uwawuze kuti, ‘Yehova akuti, “‘Oyenera kufa adzafa; oyenera kufa ndi lupanga adzafa ndi lupanga; oyenera kufa ndi njala adzafa ndi njala; oyenera kupita ku ukapolo adzapita ku ukapolo.’
And it shall come to pass, when they say to thee, Where shall we go forth? Then thou shall tell them, Thus says Jehovah: Such as are for death, to death, and such as are for the sword, to the sword, and such as are for the famine, to the famine, and such as are for captivity, to captivity.
3 “Ine ndidzawatumizira mitundu inayi ya zinthu zowononga,” akutero Yehova, “lupanga lowapha, agalu owaluma, mbalame zamumlengalenga ndiponso zirombo zoti ziwadye ndi kuwawononga.
And I will appoint over them four kinds, says Jehovah: the sword to kill, and the dogs to tear, and the birds of the heavens, and the beasts of the earth, to devour and to destroy.
4 Ndidzawasandutsa kukhala chinthu chonyansa kwa anthu a maufumu onse a dziko lapansi chifukwa cha zimene Manase mwana wa Hezekiya mfumu ya Yuda anachita mu Yerusalemu.
And I will cause them to be tossed to and fro among all the kingdoms of the earth, because of Manasseh, the son of Hezekiah, king of Judah, for that which he did in Jerusalem.
5 “Kodi adzakumvera chisoni ndani, Yerusalemu? Kodi adzakulira ndani? Kodi ndani amene adzapatuka kufunsa za moyo wako?
For who will have pity upon thee, O Jerusalem? Or who will bemoan thee? Or who will turn aside to ask of thy welfare?
6 Inu mwandikana Ine,” akutero Yehova. “Inu mukubwererabe mʼmbuyo. Choncho Ine ndidzakukanthani. Ndatopa ndi kukuchitirani chifundo.
Thou have rejected me, says Jehovah. Thou have gone backward. Therefore I have stretched out my hand against thee, and destroyed thee. I am weary with relenting.
7 Ine ndidzakubalalitsani kukuchotsani mʼmizinda ya mʼdzikomo monga mmene amachitira ndi mankhusu popeta ndi lichero. Anthu anga ndinawaliritsa ndi kuwawononga chifukwa sanasinthe makhalidwe awo oyipa.
And I have winnowed them with a fan in the gates of the land. I have bereaved them of sons. I have destroyed my people. They did not return from their ways.
8 Ndinachulukitsa amayi awo amasiye kupambana mchenga wa kunyanja. Amayiwo ndinawawonongera ana awo aamuna dzuwa lili pamutu. Mwadzidzidzi ndinawagwetsera kuwawa mtima ndi mantha.
Their widows have increased to me above the sand of the seas. I have brought upon them, against the mother of the young men, a destroyer at noonday. I have caused anguish and terrors to fall upon her suddenly.
9 Mayi wa ana asanu ndi awiri wakomoka ndipo akupuma wefuwefu. Dzuwa lake lalowa ukanali usana; anamuchititsa manyazi ndipo wathedwa nzeru. Otsala ndidzawapereka mʼmanja mwa adani awo kuti awaphe ndi lupanga,” akutero Yehova.
She who has borne seven, languishes. She has given up the spirit. Her sun has gone down while it was yet day. She has been put to shame and confounded. And the residue of them I will deliver to the sword before their enemies, says Jehovah.
10 Kalanga ine, amayi pakuti munandibereka ine, munthu amene ndikutsutsana ndi kulimbana ndi anthu pa dziko lonse! Ine sindinakongoze kapena kukongola kanthu, komatu aliyense akunditemberera.
Woe is me, my mother, that thou have bore me, a man of strife and a man of contention to the whole earth! I have not lent, nor have men lent to me, yet every one of them curses me.
11 Yehova anati, “Ndithudi, Ine ndidzakulanditsa kuti upeze bwino. Ndithudi, adani ako adzakupempha pa nthawi ya tsoka ndi ya mavuto awo.
Jehovah said, Truly I will strengthen thee for good. Truly I will cause the enemy to make supplication to thee in the time of evil and in the time of affliction.
12 “Palibe munthu amene angathe kudula chitsulo, makamaka chitsulo chochokera kumpoto chosakaniza ndi mkuwa.
Can a man break iron, even iron from the north, and brass?
13 Anthu ako ndi chuma chako ndidzazipereka kwa ofunkha popanda malipiro, chifukwa cha machimo anu onse a mʼdziko lanu lonse.
Thy substance and thy treasures I will give for a spoil without price. And that for all thy sins, even in all thy borders.
14 Ndidzakusandutsani akapolo a adani anu mʼdziko limene inu simulidziwa, chifukwa mkwiyo wanga wayaka ngati moto umene udzakutenthani.”
And I will make them to pass with thine enemies into a land which thou know not. For a fire is kindled in my anger, which shall burn upon you.
15 Ine ndinati, “Inu Yehova, mumadziwa zonse; kumbukireni ndi kundisamalira. Ndilipsireni anthu ondizunza. Ndilezereni mtima musandilande moyo wanga. Onani momwe ndi kuvutikira chifukwa cha Inu.
O Jehovah, thou know. Remember me, and visit me, and avenge me of my persecutors. Take me not away in thy longsuffering. Know that for thy sake I have suffered reproach.
16 Munandiyankhula ndipo mawu anu ndinawalandira bwino. Mawu anu anandipatsa chimwemwe ndipo mtima wanga unasangalala. Paja ine, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, ndimadziwika ndi dzina lanu.
Thy words were found, and I ate them. And thy words were to me a joy and the rejoicing of my heart. For I am called by thy name, O Jehovah, God of hosts.
17 Sindinakhale nawo mʼgulu la anthu amadyera, sindinasangalale nawo anthu amenewo. Ndinakhala ndekha chifukwa choti dzanja lanu linali pa ine ndipo munadzaza mu mtima mwanga ndi mkwiyo.
I did not sit in the assembly of those who make merry, nor did I rejoice. I sat alone because of thy hand, for thou have filled me with indignation.
18 Nanga nʼchifukwa chiyani mavuto anga sakutha? Bwanji chilonda changa sichikupola? Kodi inu mudzakhala ngati mtsinje wowuma nthawi yachilimwe, kapena ngati kasupe wopanda madzi?”
Why is my pain perpetual, and my wound incurable, which refuses to be healed? Will thou indeed be to me as a deceitful brook, as waters that fail?
19 Tsono Yehova anandiyankha kuti, “Ukabwerera kwa Ine, ndidzakulandiranso ndipo udzakhalanso mtumiki wanga. Ngati udzayankhula mawu oyenera osati achabechabe, udzakhalanso mneneri wanga. Anthu adzabwera kwa iwe ndipo sipadzafunika kuti iwe upite kwa iwo.
Therefore thus says Jehovah: If thou return, then I will bring thee again that thou may stand before me. And if thou take forth the precious from the vile, thou shall be as my mouth. They shall return to thee, but thou shall not return to them.
20 Ndidzakusandutsa ngati khoma lolimba ngati mkuwa kwa anthu awa. Adzalimbana nawe koma sadzakugonjetsa, pakuti Ine ndili nawe kukulanditsa ndi kukupulumutsa,” akutero Yehova.
And I will make thee to this people a fortified brazen wall. And they shall fight against thee, but they shall not prevail against thee. For I am with thee to save thee and to deliver thee, says Jehovah.
21 “Ndidzakupulumutsa mʼdzanja la anthu oyipa ndipo ndidzakuwombola kwa anthu ankhanza.”
And I will deliver thee out of the hand of the wicked, and I will redeem thee out of the hand of the terrible.

< Yeremiya 15 >