< Yeremiya 12 >

1 Yehova, Inu mumakhala wokhoza nthawi zonse ndikati nditsutsane nanu. Komabe ndikufuna kuyankhula nanu za mlandu wanga. Chifukwa chiyani anthu oyipa zinthu zimawayendera bwino? Chifukwa chiyani anthu achinyengo amakhala pabwino?
Thou are righteous, O Jehovah, when I contend with thee. Yet I would reason the case with thee. Why does the way of the wicked prosper? Why are all those at ease who deal very treacherously?
2 Inu munawadzala ndipo anamera mizu; amakula ndi kubereka zipatso. Dzina lanu limakhala pakamwa pawo nthawi zonse, koma mitima yawo imakhala kutali ndi Inu.
Thou have planted them. Yea, they have taken root, they grow. Yea, they bring forth fruit. Thou are near in their mouth, and far from their heart.
3 Koma Inu Yehova, ine mumandidziwa; mumandiona ndipo mumayesa zolingalira zanga. Akokeni anthu oyipawo ngati nkhosa zokaphedwa! Ayikeni padera mpaka tsiku loti akaphedwe!
But thou, O Jehovah, know me. Thou see me, and try my heart toward thee. Pull them out like sheep for the slaughter, and prepare them for the day of slaughter.
4 Kodi dziko lidzakhala likulirabe mpaka liti ndipo udzu mʼmunda uliwonse udzakhalabe ofota mpaka liti? Nyama ndi mbalame kulibiretu chifukwa anthu amene amakhalamo ndi oyipa. Iwo amati: “Yehova sangathe kuona ntchito zathu.”
How long shall the land mourn, and the herbs of the whole country wither? For the wickedness of those who dwell therein, the beasts are consumed, and the birds, because they said, He shall not see our latter end.
5 Yehova anayankha kuti, “Ngati kukutopetsa kuthamanga pamodzi ndi anthu nanga ungapikisane bwanji ndi akavalo? Ngati ukupunthwa ndi kugwa pa malo abwino, udzatha bwanji kuthamanga mʼnkhalango za ku Yorodani?
If thou have run with the footmen, and they have wearied thee, then how can thou contend with horses? And though in a land of peace thou are secure, yet how will thou do in the pride of the Jordan?
6 Ngakhale abale ako ndi anansi akuwukira, onsewo amvana zokuyimba mlandu. Usawakhulupirire, ngakhale ayankhule zabwino ndi iwe.
For even thy brothers, and the house of thy father, even they have dealt treacherously with thee, even they have cried aloud after thee. Believe them not, though they speak fair words to thee.
7 “Ine ndawasiya anthu anga; anthu amene ndinawasankha ndawataya. Ndapereka okondedwa anga mʼmanja mwa adani awo.
I have forsaken my house. I have cast off my heritage. I have given the dearly beloved of my soul into the hand of her enemies.
8 Anthu amene ndinawasankha asanduka ngati mkango wa mʼnkhalango. Akundibangulira mwaukali; nʼchifukwa chake Ine ndikudana nawo.
My heritage has become to me as a lion in the forest. She has uttered her voice against me. Therefore I have hated her.
9 Anthu anga amene ndinawasankha asanduka ngati mbalame yolusa yamawangamawanga imene akabawi ayizinga. Pitani, kasonkhanitseni nyama zakuthengo. Mubwere nazo kuti zidzadye mbalameyo.
Is my heritage to me as a speckled bird of prey? Are the birds of prey against her round about? Go ye, assemble all the beasts of the field; bring them to devour.
10 Abusa ambiri anawononga munda wanga wa mpesa, anapondereza munda wanga; munda wanga wabwino uja anawusandutsa chipululu.
Many shepherds have destroyed my vineyard. They have trodden my portion under foot. They have made my pleasant portion a desolate wilderness.
11 Unawusandutsadi chipululu. Ukanali wokhawokha chomwecho ukundilirira Ine. Dziko lonse lasanduka chipululu chifukwa palibe wolisamalira.
They have made it a desolation. It mourns to me, being desolate. The whole land is made desolate, because no man lays it to heart.
12 Anthu onse owononga abalalikira ku zitunda zonse za mʼchipululu. Yehova watuma ankhondo ake kudzawatha kuyambira kumalire ena a dziko mpaka ku malire enanso a dziko, ndipo palibe amene adzakhale pa mtendere.
Destroyers have come upon all the bare heights in the wilderness. For the sword of Jehovah devours from the one end of the land even to the other end of the land. No flesh has peace.
13 Anthu anafesa tirigu koma anatuta minga; anadzitopetsa kugwira ntchito koma osapeza phindu lililonse. Choncho mudzachita manyazi ndi zokolola zanu chifukwa cha mkwiyo wa Yehova.”
They have sown wheat, and have reaped thorns. They have put themselves to pain, and profit nothing. And ye shall be ashamed of your fruits, because of the fierce anger of Jehovah.
14 “Anthu oyipa oyandikana ndi anthu anga Aisraeli, akuwalanda Aisraeliwo dziko, cholowa chimene ndinawapatsa. Nʼchifukwa chake ndidzawachotsa mʼdziko limenelo, ndipo ndidzachotsa banja la Yuda pakati pawo.
Thus says Jehovah against all my evil neighbors, who touch the inheritance which I have caused my people Israel to inherit: Behold, I will pluck them up from off their land, and will pluck up the house of Judah from among them.
15 Komabe nditawachotsa, ndidzawachitiranso chifundo, ndipo ndidzabwezera aliyense cholowa chake ndi dziko lake.
And it shall come to pass, after I have plucked them up, I will return and have compassion on them. And I will bring them again, each man to his heritage, and each man to his land.
16 Ndipo ngati iwo adzaphunzira bwino njira za anthu anga ndi kulumbira mʼdzina langa, namanena kuti, ‘Pali Yehova wamoyo,’ monga iwo anaphunzitsira anthu anga kulumbira mʼdzina la Baala, Ine ndidzawakhazikitsa pakati pa anthu anga.
And it shall come to pass, if they will diligently learn the ways of my people, to swear by my name, As Jehovah lives, even as they taught my people to swear by Baal, then they shall be built up in the midst of my people.
17 Koma ngati mtundu wina uliwonse sudzamvera, Ine ndidzawuchotsa ndi kuwuwonongeratu,” akutero Yehova.
But if they will not hear, then I will pluck up that nation, plucking up and destroying it, says Jehovah.

< Yeremiya 12 >