< Yeremiya 13 >

1 Yehova anandiwuza kuti, “Pita kagule lamba wansalu yosalala ndipo ukavale mʼchiwuno mwako, koma usakamuviyike mʼmadzi.”
Thus says Jehovah to me, Go, and buy thee a linen sash, and put it upon thy loins, and do not put it in water.
2 Choncho ndinakagula lambayo, monga momwe anandiwuzira Yehova, ndipo ndinamanga mʼchiwuno mwanga.
So I bought a sash according to the word of Jehovah, and put it upon my loins.
3 Kenaka Yehova anandiyankhulanso kachiwiri kuti,
And the word of Jehovah came to me the second time, saying,
4 “Tenga lamba amene unagula ndi kuvala mʼchiwuno mwako uja. Tsono pita ku mtsinje wa Yufurate ndipo ukamubise lambayo mʼmingʼalu ya mʼmatanthwe.”
Take the sash that thou have bought, which is upon thy loins, and arise, go to the Euphrates, and hide it there in a cleft of the rock.
5 Ndipo ndinapitadi ndi kukabisa lambayo ku Yufurate, monga anenera Yehova.
So I went, and hid it by the Euphrates, as Jehovah commanded me.
6 Patapita masiku ambiri Yehova anandiwuzanso kuti, “Pitanso ku Yufurate ndipo ukatenge lamba amene ndinakuwuza kuti ukamubise kumeneko.”
And it came to pass after many days, that Jehovah said to me, Arise, go to the Euphrates, and take the sash from there, which I commanded thee to hide there.
7 Choncho ndinapita ku Yufurate kukafukula lambayo ndi kumuchotsa pamalo pamene ndinamubisa, koma nthawi imeneyi nʼkuti lambayo atawonongeka kotheratu ndipo analibenso ntchito.
Then I went to the Euphrates, and dug, and took the sash from the place where I had hid it. And, behold, the sash was rotten. It was good for nothing.
8 Pamenepo Yehova anandiwuza kuti,
Then the word of Jehovah came to me, saying,
9 “Izi ndi zimene ine ndikunena: ‘Umu ndi mmene ndidzawonongere zimene akunyadira kwambiri a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu.
Thus says Jehovah, After this manner I will mar the pride of Judah, and the great pride of Jerusalem.
10 Anthuwa ndi oyipa. Iwo akana kumvera mawu anga. Mʼmalo mwake amawumirira kutsata milungu ina, kuyitumikira ndi kuyipembedza. Anthu amenewa adzakhala ngati lamba wopanda ntchitoyu.
This evil people, who refuse to hear my words, who walk in the stubbornness of their heart, and have gone after other gods to serve them, and to worship them, shall even be as this sash, which is good for nothing.
11 Monga momwe lamba amakanirira mʼchiwuno cha munthu, momwemonso ndinakonza kuti nyumba yonse ya Israeli ndi nyumba yonse ya Yuda indikangamire Ine kuti akhale anthu anga, kuti azitamanda dzina langa ndi kulemekeza Ine. Koma iwo sanamvere,’ akutero Yehova.
For as the sash clings to the loins of a man, so I have caused to cling to me the whole house of Israel and the whole house of Judah, says Jehovah, that they may be to me for a people, and for a name, and for a praise, and for a glory, but they would not hear.
12 “Awuze anthuwo kuti, ‘Yehova Mulungu wa Israeli akuti: Mtsuko uliwonse adzawudzaza ndi vinyo.’ Ndipo ngati iwo anena kwa iwe kuti, ‘Kodi ngati ife sitikudziwa kuti mtsuko uliwonse udzadzazidwa ndi vinyo?’
Therefore thou shall speak to them this word. Thus says Jehovah, the God of Israel: Every bottle shall be filled with wine. And they shall say to thee, Do we not certainly know that every bottle shall be filled with wine?
13 Tsono iwe uwawuze kuti, Yehova akuti ‘Ine ndidzaledzeretsa anthu onse okhala mʼdziko muno, kuyambira mafumu amene amakhala pa mpando waufumu wa Davide, ansembe, aneneri, pamodzi ndi anthu onse amene akukhala mu Yerusalemu.
Then thou shall say to them, Thus says Jehovah: Behold, I will fill all the inhabitants of this land, even the kings who sit upon David's throne, and the priests, and the prophets, and all the inhabitants of Jerusalem, with drunkenness.
14 Ndidzawagundanitsa mitu kuti aphwanyane okhaokha ngati mitsuko, makolo ndi ana awo, akutero Yehova. Sindidzawamvera chisoni kapena kuwachitira chifundo kapena kukhudzidwa nawo kuti ndileke kuwawononga.’”
And I will dash them one against another, even the fathers and the sons together, says Jehovah. I will not pity, nor spare, nor have compassion, that I should not destroy them.
15 Imvani inu Aisraeli ndipo tcherani khutu, musadzitukumule, pakuti ndi Yehova amene akuyankhula.
Hear ye, and give ear, be not proud, for Jehovah has spoken.
16 Lemekezani Yehova Mulungu wanu asanagwetse mdima, mapazi anu asanayambe kupunthwa mʼchisisira chamʼmapiri. Asanasandutse kuwala mukuyembekezerako kukhala mdima wandiweyani.
Give glory to Jehovah your God, before he causes darkness, and before your feet stumble upon the dark mountains. And, while ye look for light, he turns it into the shadow of death, and makes it gross darkness.
17 Koma ngati simumvera, ndidzalira kwambiri chifukwa cha kunyada kwanu. Mʼmaso mwanga mwadzaza ndi misozi yowawa chifukwa nkhosa za Yehova zatengedwa ukapolo.
But if ye will not hear it, my soul shall weep in secret for your pride. And my eye shall weep greatly, and run down with tears, because Jehovah's flock is taken captive.
18 Uza mfumu pamodzi ndi amayi ake kuti, “Tsikani pa mipando yaufumuyo, pakuti zipewa zanu zaufumu zokongolazo zagwa pansi.”
Say thou to the king and to the queen-mother: Humble yourselves. Sit down, for your coronets have come down, even the crown of your glory.
19 Mizinda ya ku Negevi yatsekedwa ndipo palibe wina woti nʼkuyitsekula. Yuda yense watengedwa kupita ku ukapolo, watengedwa yense ukapolo.
The cities of the South are shut up, and there is none to open them. Judah is carried away captive, all of it. It is wholly carried away captive.
20 Tukula maso ako kuti uwone amene akubwera kuchokera kumpoto. Kodi nkhosa zimene anakusungitsa zili kuti, nkhosa zanu zokongola zija?
Lift up your eyes, and behold those who come from the north. Where is the flock that was given thee, thy beautiful flock?
21 Kodi udzanena chiyani pamene [Yehova] adzakuyikira anthu amene unkanena kuti ndi abale ako akukugonjetsa ndi kukulamulira? Kodi sudzamva zowawa ngati za mayi pa nthawi yake yochira?
What will thou say when he shall set over thee as head those whom thou thyself have taught to be friends to thee? Shall not sorrows take hold of thee as of a woman in travail?
22 Ndipo ngati udzadzifunsa kuti, “Kodi zimenezi zandichitikira chifukwa chiyani?” Ndi chifukwa cha machimo anu ambiri kuti zovala zanu zingʼambike ndiponso kuti akuchitireni nkhanza.
And if thou say in thy heart, Why have these things come upon me? For the greatness of thine iniquity thy skirts are uncovered, and thy heels suffer violence.
23 Kodi wa dziko la Kusi nʼkusintha khungu lake, kapena kambuku kusintha mawanga ake? Inunso amene munazolowera kuchita zoyipa simungathe kusintha.
Can the Ethiopian change his skin, or the leopard his spots? Then ye also may do good, who are accustomed to do evil.
24 “Ine ndidzakumwazani ngati mankhusu amene amawuluka ndi mphepo ya ku chipululu.
Therefore I will scatter them as the stubble that passes away by the wind of the wilderness.
25 Limeneli ndiye gawo lanu, chilango chimene ndakukonzerani chifukwa chondiyiwala Ine ndi kutumikira milungu yabodza, akutero Yehova.
This is thy lot, the portion measured to thee from me, says Jehovah, because thou have forgotten me, and trusted in falsehood.
26 Ine ndidzakwinya zovala zanu mpaka ku maso kuti umaliseche wanu uwonekere.
Therefore I will also uncover thy skirts upon thy face, and thy shame shall appear.
27 Ndaona zonyansa zanu: zigololo zanu, kutchetcherera kwanu ndi ziwerewere zanu, zochitika pa mapiri ndi mʼminda. Tsoka iwe Yerusalemu! Udzakhala wosayeretsedwa pa zachipembedzo mpaka liti?”
I have seen thine abominations, even thine adulteries, and thy neighings, the lewdness of thy whoredom, on the hills, in the field. Woe to thee, O Jerusalem! Thou will not be made clean. How long shall it yet be?

< Yeremiya 13 >