< Yeremiya 10 >

1 Inu Aisraeli, imvani zimene Yehova akunena.
Hear ye the word which Jehovah speaks to you, O house of Israel.
2 Yehova akuti, “Musatsatire makhalidwe a anthu a mitundu ina kapena kuchita mantha ndi zizindikiro zamlengalenga, ngakhale anthu a mitundu ina amachita nazo mantha.
Thus says Jehovah: Learn not the way of the nations, and be not dismayed at the signs of heaven, for the nations are dismayed at them.
3 Pakuti miyambo ya mitundu inayo ndiyachabechabe. Iwo amakadula mtengo ku nkhalango ndipo mmisiri amawusema ndi sompho.
For the customs of the peoples are vanity. For a man cuts a tree out of the forest, the work of the hands of the workman with the axe.
4 Amakongoletsa chosemacho ndi siliva ndi golide; kenaka amachikhomerera ndi misomali kuti chisagwedezeke.
They deck it with silver and with gold. They fasten it with nails and with hammers, that it not move.
5 Mafano awo ali ngati mtengo wakanjedza woopsezera mbalame mʼmunda wa minkhaka. Mafanowo sangathe nʼkuyankhula komwe ndipo ayenera kunyamulidwa popeza sangathe nʼkuyenda komwe. Musachite nawo mantha popeza sangathe kukuchitani choyipa ndiponso alibe mphamvu yochitira chabwino chilichonse.”
They are like a palm tree, of turned work, and do not speak. They must be carried, because they cannot go. Be not afraid of them, for they cannot do evil, nor is it in them to do good.
6 Palibe wofanana nanu, Inu Yehova; Inu ndinu wamkulu, ndipo dzina lanu lili ndi mphamvu yayikulu.
There is none like thee, O Jehovah. Thou are great, and thy name is great in might.
7 Ndani amene angaleke kukuopani, inu Mfumu ya mitundu ya anthu? Chimenechi ndicho chokuyenerani. Pakati pa anthu anzeru onse komanso mafumu onse a mitundu ya anthu, palibe wina wofanana nanu.
Who should not fear thee, O King of the nations? For to thee it appertains, inasmuch as among all the wise men of the nations, and in all their royal estate, there is none like thee.
8 Onsewo ndi opusa ndi opanda nzeru; malangizo awo amawatenga kuchokera kwa mafano achabechabe opanga ndi mitengo.
But they are together brutish and foolish, the instruction of idols! It is but a block of wood.
9 Siliva wosula amabwera naye kuchokera ku Tarisisi ndipo golide amachokera naye ku Ufazi. Mafanowo ndi ntchito ya anthu aluso ndi odziwa kuzokota golide. Tsono mafanowo amawaveka zovala za mtundu wamtambo ndi pepo. Yonseyo ndi ntchito ya anthu a luso.
There is silver beaten into plates, which is brought from Tarshish, and gold from Uphaz, the work of the artificer and of the hands of the goldsmith, blue and purple for their clothing. They are all the work of skilful men.
10 Koma Yehova ndiye Mulungu woona; Iyeyo ndiye Mulungu wamoyo, Mfumu yamuyaya. Akakwiya, dziko limagwedezeka; anthu a mitundu ina sangathe kupirira ukali wakewo.
But Jehovah is the true God. He is the living God, and an everlasting King. At his wrath the earth trembles, and the nations are not able to abide his indignation.
11 “Awuze anthu awa kuti, ‘Milungu iyi, imene sinalenge dziko lakumwamba ndi dziko lapansi, idzawonongeka pa dziko lapansi ndi pansi pa thambo.’”
Thus ye shall say to them: The gods that have not made the heavens and the earth, these shall perish from the earth, and from under the heavens.
12 Koma Mulungu analenga dziko lapansi ndi mphamvu zake; Iye anapanga dziko lonse ndi nzeru zake ndipo anayala thambo mwaluso lake.
He has made the earth by his power. He has established the world by his wisdom, and by his understanding he has stretched out the heavens.
13 Iye akayankhula, kumamveka mkokomo wamadzi akumwamba; Iyeyo amabweretsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi. Amabweretsa mphenzi pamodzi ndi mvula ndi kutulutsa mphepo yamkuntho kumalo kumene osungirako.
When he utters his voice, there is a tumult of waters in the heavens, and he causes the vapors to ascend from the ends of the earth. He makes lightnings for the rain, and brings forth the wind out of his treasuries.
14 Anthu onse ndi opusa ndiponso opanda nzeru; mmisiri aliyense wosula golide akuchita manyazi ndi mafano ake. Mafano akewo ndi abodza; alibe moyo mʼkati mwawo.
Every man has become brutish, without knowledge. Every goldsmith is put to shame by his graven image. For his molten image is falsehood, and there is no breath in them.
15 Mafanowo ndi achabechabe, zinthu zosekedwa nazo. Pamene anthuwo azidzaweruzidwa, mafanowo adzawonongedwa.
They are vanity, a work of delusion. In the time of their visitation they shall perish.
16 Koma Yehova amene ndi Cholowa cha Yakobo sali ngati mafanowo. Iyeyu ndi Mlengi wa zinthu zonse kuphatikizapo Israeli, mtundu umene anawusankha kuti ukhale anthu ake. Dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
The portion of Jacob is not like these. For he is the former of all things, and Israel is the tribe of his inheritance. Jehovah of hosts is his name.
17 Sonkhanitsani katundu wanu, inu amene mukukhala mʼlinga la ankhondo.
Gather up thy wares out of the land, O thou who abides in the siege.
18 Pakuti Yehova akuti, “Tsopano Ine ndidzachotsa anthu onse amene akukhala mʼdziko lino; adzakhala pa mavuto mpaka adzamvetsa.”
For thus says Jehovah, Behold, I will sling out the inhabitants of the land at this time, and will distress them, that they may feel it.
19 Aliyense ankangoti, “Mayo ine, chifukwa cha kupweteka kwanga! Chilonda changa nʼchachikulu!” Koma ine ndinkaganiza kuti, “Ndithu, ili ndi vuto langa basi, choncho ndingolipirira.”
Woe is me because of my hurt! My wound is grievous, but I said, Truly this is my grief, and I must bear it.
20 Tenti yanga yawonongeka, zingwe zake zonse zaduka. Ana anga andisiya ndipo kulibenso. Palibenso amene adzandimangire tenti, kapena kufunyulula nsalu yake.
My tent is destroyed, and all my cords are broken. My sons have gone forth from me, and they are not. There is none to spread my tent any more, and to set up my curtains.
21 Abusa ndi opusa ndipo sanapemphe nzeru kwa Yehova; choncho palibe chimene anapindula ndipo nkhosa zawo zonse zabalalika.
For the shepherds have become brutish, and have not inquired of Jehovah. Therefore they have not prospered, and all their flocks are scattered.
22 Tamvani! kukubwera mphekesera, phokoso lalikulu la gulu la a ankhondo likumveka kuchokera kumpoto! Lidzasandutsa bwinja mizinda ya ku Yuda, malo okhala nkhandwe.
The voice of news. Behold, it comes, and a great commotion out of the north country, to make the cities of Judah a desolation, a dwelling-place of jackals.
23 Inu Yehova, ndikudziwa kuti moyo umene munthu ali nawo si wake; munthuyo sangathe kuwongolera mayendedwe ake.
O Jehovah, I know that the way of man is not in himself. It is not in man who walks to direct his steps.
24 Inu Yehova, langizeni, komatu mwachilungamo, osati ndi mkwiyo wanu, mungandiwononge kotheratu.
O Jehovah, correct me, but in measure, not in thine anger, lest thou bring me to nothing.
25 Tsanulirani ukali wanu pa mitundu ya anthu amene sakudziwani, ndiye kuti mitundu ya anthu amene satama pa dzina lanu mopemba. Iwo aja anasakaza Yakobo; amusakaza kotheratu ndipo awononga dziko lake.
Pour out thy wrath upon the nations that know thee not, and upon the families that call not on thy name. For they have devoured Jacob. Yea, they have devoured him and consumed him, and have laid waste his habitation.

< Yeremiya 10 >