< Yeremiya 8 >

1 Yehova akuti, “‘Pa nthawi imeneyo, mafupa a mafumu ndi a akuluakulu a ku Yuda, mafupa a ansembe ndi a aneneri, ndiponso mafupa a anthu a ku Yerusalemu adzafukulidwa.
At that time, says Jehovah, they shall bring out the bones of the kings of Judah, and the bones of his rulers, and the bones of the priests, and the bones of the prophets, and the bones of the inhabitants of Jerusalem, out of their graves.
2 Adzawamwaza pa nthaka kuyangʼana dzuwa, mwezi ndi nyenyezi zonse zamlengalenga, zimene ankazikonda, kuzitumikira ndi kuzitsatira, kupemphako nzeru ndiponso kuzilambira. Mafupawo sadzawasonkhanitsa kapena kuwakwirira, koma adzakhala ngati ndowe pamwamba pa nthaka.
And they shall spread them before the sun, and the moon, and all the host of heaven, which they have loved, and which they have served, and after which they have walked, and which they have sought, and which they have worshiped. They shall not be gathered, nor be buried. They shall be for dung upon the face of the earth.
3 Otsala onse a mtundu woyipawu adzafuna imfa kopambana moyo kulikonse kumene ndidzawapirikitsirako, akutero Yehova Wamphamvuzonse.’”
And death shall be chosen rather than life by all the residue that remain of this evil family, that remain in all the places where I have driven them, says Jehovah of hosts.
4 “Tsono awuze anthuwa, ‘Yehova akuti: “‘Kodi anthu akagwa sangadzukenso? Munthu akasochera kodi sangathe kubwereranso?
Moreover thou shall say to them, Thus says Jehovah: Shall men fall, and not rise up again? Shall he turn away, and not return?
5 Chifukwa chiyani nanga anthu awa akupitirirabe kuchimwa, osabwerera? Chifukwa chiyani Yerusalemu akubwerera mʼmbuyo? Iwo akangamira chinyengo; akukana kubwerera.
Why then has this people of Jerusalem slid back by a perpetual backsliding? They hold firm deceit. They refuse to return.
6 Ine ndinatchera khutu kumvetsera koma iwo sanayankhulepo zoona. Palibe woyipa amene analapapo zoyipa zake, nʼkumati, ‘Ine ndachita chiyani?’ Aliyense akutsatira njira yake ngati kavalo wothamangira nkhondo.
I hearkened and heard, but they did not speak aright. No man repents of his wickedness, saying, What have I done? Everyone turns to his course as a horse that rushes headlong in the battle.
7 Mbalame yotchedwa kakowa ija imadziwa nthawi yake mlengalenga. Koma nkhunda, namzeze ndi chingalu zimadziwa nthawi yonyamukira ulendo, koma anthu anga sadziwa malamulo a Yehova.
Yea, the stork in the heavens knows her appointed times, and the turtledove and the swallow and the crane observe the time of their coming, but my people know not the law of Jehovah.
8 “‘Inu mukunena bwanji kuti, ‘Ndife anzeru ndipo timasunga malamulo a Yehova?’ Koma ndi alembi anu amene akulemba zabodza.
How can ye say, We are wise, and the law of Jehovah is with us? But behold, the false pen of the scribes has wrought falsely.
9 Anthu anzeru achita manyazi; athedwa nzeru ndipo agwidwa. Iwo anakana mawu a Yehova. Nanga tsono nzeru zawo ziwapinduliranji?
The wise men are put to shame. They are dismayed and taken. Lo, they have rejected the word of Jehovah, and what manner of wisdom is in them?
10 Nʼchifukwa chake akazi awo ndidzawapereka kwa amuna ena ndipo minda yawo ndidzayipereka kwa amene adzawagonjetse. Kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, onse ali ndi khalidwe lofuna kupeza chuma mwakuba. Aneneri pamodzi ndi ansembe omwe, onse amachita zachinyengo.
Therefore I will give their wives to others, and their fields to those who shall possess them. For everyone from the least even to the greatest is given to covetousness. From the prophet even to the priest everyone deals falsely.
11 Iwo amapoletsa zilonda za anthu anga pamwamba chabe nʼkumati, ‘Mtendere, mtendere,’ pamene palibe mtendere.
And they have lightly healed the hurt of the daughter of my people, saying, Peace, peace, when there is no peace.
12 Kodi amachita manyazi akamachita zonyansazi? Ayi, alibe manyazi ndi pangʼono pomwe; iwo sadziwa nʼkugwetsa nkhope komwe. Choncho iwo adzagwera pakati pa anzawo amene agwa kale; adzagwa pansi tsiku limene ndidzawalanga, akutero Yehova.
Were they ashamed when they had committed abomination? No, they were not at all ashamed, nor could they blush. Therefore they shall fall among those who fall. In the time of their visitation they shall be cast down, says Jehovah.
13 “‘Ndidzatenga zokolola zawo, Sipadzakhalanso mphesa pa mpesa kapena nkhuyu pa mkuyu, ndipo masamba ake adzawuma. Zinthu zimene ndinawapatsa ndidzawachotsera.’”
I will utterly consume them, says Jehovah. There shall be no grapes on the vine, nor figs on the fig tree, and the leaf shall fade, and things I have given them shall pass away from them.
14 Koma amati, “Tikukhala pano chifukwa chiyani? Tiyeni tonse pamodzi tithawire ku mizinda yotetezedwa ndi kukafera kumeneko. Pakuti Yehova Mulungu wathu watsimikiza kuti tiyenera kufa. Watipatsa madzi aululu kuti timwe, chifukwa tamuchimwira.
Why do we sit still? Assemble yourselves, and let us enter into the fortified cities, and let us be silent there. For Jehovah our God has put us to silence, and given us water of gall to drink, because we have sinned against Jehovah.
15 Tinkayembekezera mtendere koma palibe chabwino chomwe chinachitika, tinkayembekezera kuchira koma tinakumana ndi zoopsa zokhazokha.
We looked for peace, but no good came, for a time of healing, and, behold, dismay!
16 Kulira kwa ngʼombe zazimuna za mdani kukumveka kuchokera ku Dani; dziko lonse likunjenjemera chifukwa cha kulira kwa akavalowo. Akubwera kudzawononga dziko ndi zonse zimene zili mʼmenemo. Adzawononga mzinda ndi onse okhalamo.”
The snorting of his horses is heard from Dan. At the sound of the neighing of his strong ones the whole land trembles. For they have come, and have devoured the land and all that is in it, the city and those who dwell therein.
17 Yehova akuti, “Onani, ndikukutumizirani njoka zaululu, mphiri zimene munthu sangathe kuzilodza, ndipo zidzakulumani,”
For, behold, I will send serpents, adders, among you, which will not be charmed, and they shall bite you, says Jehovah.
18 Ndadzazidwa ndi chisoni kwambiri, mtima wanga walefukiratu.
Oh that I could comfort myself against sorrow! My heart is faint within me.
19 Imvani kulira kwa anthu anga kuchokera ku dziko lakutali: akuti, “Kodi Yehova sali ku Ziyoni? Kodi mfumu yake sili kumeneko?” “Chifukwa chiyani akundiputa ndi mafano awo osema, ndi milungu yawo yachilendo?”
Behold, the voice of the cry of the daughter of my people from a land that is very far off: Is not Jehovah in Zion? Is not her King in her? Why have they provoked me to anger with their graven images, and with foreign vanities?
20 “Nthawi yokolola yapita, chilimwe chapita, koma sitinapulumuke.”
The harvest is past, the summer is ended, and we are not saved.
21 Chifukwa cha mavuto a anthu anga, ine ndikumva kuwawa; ndikungolira ndipo mantha aakulu andigwira.
For the hurt of the daughter of my people I am hurt. I mourn. Dismay has taken hold on me.
22 Kodi ku Giliyadi kulibe mankhwala ochiritsa? Kodi kumeneko kulibe singʼanga? Nanga chifukwa chiyani mabala a anthu anga sanapole?
Is there no balm in Gilead? Is there no physician there? Why then has not the health of the daughter of my people recovered?

< Yeremiya 8 >