< Yeremiya 7 >

1 Mawu amene Yehova anayankhula kwa Yeremiya ndi awa,
The word that came to Jeremiah from Jehovah, saying,
2 “Ima pa chipata cha Nyumba ya Yehova ndipo kumeneko ukalalikire uthenga uwu: “‘Imvani mawu a Yehova, inu nonse anthu a ku Yuda amene mumalowa pa chipata ichi kudzapembedza Yehova.
Stand in the gate of Jehovah's house, and proclaim there this word, and say, Hear the word of Jehovah, all ye of Judah, who enter in at these gates to worship Jehovah.
3 Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Konzani makhalidwe anu ndi zochita zanu, ndipo ndidzakulolani kukhala pa malo ano.
Thus says Jehovah of hosts, the God of Israel: Amend your ways and your doings, and I will cause you to dwell in this place.
4 Musamakhulupirire mawu anu achinyengo onena kuti, ‘Ino ndi Nyumba ya Yehova, Nyumba ya Yehova, Nyumba ya Yehova!’
Trust ye not in lying words, saying, The temple of Jehovah, the temple of Jehovah, the temple of Jehovah, are these.
5 Ngati mutasinthadi makhalidwe anu ndi zochita zanu, ndi kumachitirana zolungama,
For if ye thoroughly amend your ways and your doings, if ye thoroughly execute justice between a man and his neighbor,
6 ngati mutaleka kuzunza mlendo, ana amasiye kapena akazi amasiye ndi kuleka kupha anthu osalakwa pa malo ano, ndipo ngati muleka kutsatira milungu ina, kuti ingakuwonongeni,
if ye do not oppress the sojourner, the fatherless, and the widow, and shed not innocent blood in this place, nor walk after other gods to your own hurt,
7 Ine ndidzakulolani kukhala pa malo ano, mʼdziko limene ndinapatsa makolo anu mpaka muyaya.
then I will cause you to dwell in this place, in the land that I gave to your fathers from of old even for evermore.
8 Koma onani, inu mukudalira mawu abodza amene alibe phindu.
Behold, ye trust in lying words, that cannot profit.
9 “Kodi inu muziba ndi kupha, kuchita chigololo ndi kulumbira monama, kufukiza lubani kwa Baala ndi kutsatira milungu ina imene simunayidziwe,
Will ye steal, murder, and commit adultery, and swear falsely, and burn incense to Baal, and walk after other gods that ye have not known,
10 ndipo kenaka nʼkubwera kudzayima pamaso panga mʼNyumba ino, Nyumba imene imadziwika ndi Dzina langa, inu nʼkumati, ‘Tapulumuka.’ Mwapulumuka kuti muzichitabe zonyansazi?
and then come and stand before me in this house, which is called by my name, and say, We are delivered, that ye may do all these abominations?
11 Kodi Nyumba ino imene imadziwika ndi Dzina langa, yasanduka phanga la anthu olanda zinthu anzawo mwachifwamba inu mukuona? Komatu ndakhala ndi kuziona zonsezi! akutero Yehova.”
Has this house, which is called by my name, become a den of robbers in your eyes? Behold, I, even I, have seen it, says Jehovah.
12 “‘Pitani tsopano ku malo anga ku Silo, malo amene poyamba ankadziwika ndi Dzina langa, ndipo mukaone zimene ndinachita kumeneko chifukwa cha kuyipa kwa anthu anga Aisraeli.
But go ye now to my place which was in Shiloh, where I caused my name to dwell at the first, and see what I did to it for the wickedness of my people Israel.
13 Tsono popeza munkachita zonsezi, ngakhale Ine kukuyankhulani koma inu osamvera, kukuyitanani koma inu osayankha,
And now, because ye have done all these works, says Jehovah. And I spoke to you, rising up early and speaking, but ye heard not, and I called you, but ye answered not,
14 choncho ndidzachita pa Nyumba imene imadziwika ndi Dzina langayi, Nyumba ya Yehova imene mumayidalira, malo amene ndinapereka kwa inu ndi makolo anu, zomwe ndinachita ku Silo.
therefore I will do to the house, which is called by my name, in which ye trust, and to the place which I gave to you and to your fathers, as I did to Shiloh.
15 Ndidzakuthamangitsani pamaso panga, ngati momwe ndinachitira abale anu onse, anthu a Efereimu.’”
And I will cast you out of my sight, as I have cast out all your brothers, even the whole seed of Ephraim.
16 “Choncho iwe Yeremiya usawapempherere anthu awa ngakhale kuwapepesera kapenanso kuwapembedzera; usandidandaulire, chifukwa Ine sindidzakumvera.
Therefore pray thou not for this people, nor lift up cry nor prayer for them. Neither make intercession to me, for I will not hear thee.
17 Kodi sukuona zimene akuchita mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya ku Yerusalemu?
Do thou not see what they do in the cities of Judah and in the streets of Jerusalem?
18 Ana akutorera nkhuni, abambo akusonkha moto, ndipo amayi akukanda ufa kuti aphike makeke oti akapereke nsembe kwa mfumukazi yazakumwamba. Iwo amathira nsembe ya zakumwa kwa milungu ina kuti andipsetse mtima.
The sons gather wood, and the fathers kindle the fire, and the women knead the dough, to make cakes to the queen of heaven, and to pour out drink offerings to other gods, that they may provoke me to anger.
19 Koma kodi akuvutitsa Ine? Kodi sakungodzivuta okha, ndi kudzichititsa manyazi? akutero Yehova.”
Do they provoke me to anger? says Jehovah, and not themselves, to the confusion of their own faces?
20 “Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti: Ndidzatsanulira mkwiyo wanga pa Nyumba yangayi, anthu, nyama, mitengo ndi zipatso zomwe. Mkwiyowo udzakhala ngati moto wosazimitsika.
Therefore thus says the lord Jehovah: Behold, my anger and my wrath shall be poured out upon this place, upon man, and upon beast, and upon the trees of the field, and upon the fruit of the ground. And it shall burn, and shall not be quenched.
21 “Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Wonjezerani nsembe zanu zopsereza pa nsembe zanu zinazo ndipo mudye nyama yakeyo!
Thus says Jehovah of hosts, the God of Israel: Add your burnt offerings to your sacrifices, and eat ye flesh.
22 Pakuti pamene ndinatulutsa makolo anu ku Igupto ndi kuyankhula nawo, sindinawalamulire kuti azipereka nsembe zopsereza kapena nsembe zinazo,
For I spoke not to your fathers, nor commanded them in the day that I brought them out of the land of Egypt, concerning burnt offerings or sacrifices.
23 koma ndinawalamula kuti: Mverani Ine, ndipo ndidzakhala Mulungu wanu ndipo inu mudzakhala anthu anga. Muzitsata zonse zimene ndakulamulirani, ndipo zinthu zidzakuyenderani bwino.
But this thing I commanded them, saying, Hearken to my voice, and I will be your God, and ye shall be my people. And walk ye in all the way that I command you, that it may be well with you.
24 Koma anthuwo sanamvere kapena kulabadira; mʼmalo mwake anapitirira kusamvera ndi mitima yawo yoyipa. Iwo anabwerera mʼmbuyo mʼmalo mopita patsogolo.
But they hearkened not, nor inclined their ear, but walked in their own counsels, in the stubbornness of their evil heart, and went backward, and not forward.
25 Kuyambira tsiku limene makolo awo anachoka ku Igupto mpaka lero lino, ndakhala ndikuwatumizira atumiki anga, aneneri.
Since the day that your fathers came forth out of the land of Egypt to this day, I have sent to you all my servants the prophets, daily rising up early and sending them.
26 Koma anthuwo sanandimvere kapena kusamalira. Anawumitsa mitima yawo ndi kuchita zoyipa kuposa makolo awo.
Yet they hearkened not to me, nor inclined their ear, but made their neck stiff. They did worse than their fathers.
27 “Ngakhale iwe uwawuze zonsezi koma sadzakumvera. Ngakhale uwayitane koma sadzakuyankha.
And thou shall speak all these words to them, but they will not hearken to thee. Thou shall also call to them, but they will not answer thee.
28 Nʼchifukwa chake udzawawuze kuti, ‘Uwu ndi mtundu wa anthu umene sunamvere Yehova Mulungu wake, wosalola kulangizidwa. Choonadi chatha; chazimirira pa milomo yawo.’
And thou shall say to them, This is the nation that has not hearkened to the voice of Jehovah their God, nor received instruction. Truth has perished, and is cut off from their mouth.
29 “Tsono meta tsitsi lako ndi kulitaya. Ulire kwambiri pa zitunda zopanda zomera, pakuti Yehova waukana ndi kuwusiya mʼbado umene wamukwiyitsawu.”
Cut off thy hair, O Jerusalem, and cast it away, and take up a lamentation on the bare heights. For Jehovah has rejected and forsaken the generation of his wrath.
30 “Anthu a ku Yuda achita zoyipa pamaso panga, akutero Yehova. Ayimika mafano awo onyansa mʼnyumba imene imadziwika ndi Dzina langa ndipo ayipitsa.
For the sons of Judah have done that which is evil in my sight, says Jehovah. They have set their abominations in the house which is called by my name, to defile it.
31 Amanga nsanja yopembedzera Tofeti mʼChigwa cha Hinomu kuti apserezereko ana awo aamuna ndi aakazi. Zimenezi Ine sindinawalamulire ngakhale kuziganizira nʼkomwe.
And they have built the high places of Topheth, which is in the valley of the son of Hinnom, to burn their sons and their daughters in the fire, which I did not command, nor did it come into my mind.
32 Nʼchifukwa chake masiku akubwera, akutero Yehova, pamene anthu sadzawatchulanso malowo Tofeti kapena Chigwa cha Hinomu, koma adzawatchula Chigwa cha Imfa, chifukwa adzakwirira anthu akufa ku Tofeti mpaka osapezekanso malo owayika.
Therefore, behold, the days come, says Jehovah, that it shall no more be called Topheth, nor The valley of the son of Hinnom, but The valley of Slaughter. For they shall bury in Topheth, till there be no place to bury.
33 Ndipo mitembo ya anthu amenewa idzakhala chakudya cha mbalame zamlengalenga ndi zirombo zakuthengo, ndipo palibe wina amene adzazipirikitse.
And the dead bodies of this people shall be food for the birds of the heavens, and for the beasts of the earth, and none shall frighten them away.
34 Ndidzathetsa nyimbo zonse zachisangalalo ndi zachikondwerero mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya ku Yerusalemu. Sikudzamvekanso mawu a chikondwerero a mkwatibwi ndi mkwati pakuti dzikolo lidzasanduka chipululu.”
Then I will cause to cease from the cities of Judah, and from the streets of Jerusalem, the voice of mirth and the voice of gladness, the voice of the bridegroom and the voice of the bride, for the land shall become a waste.

< Yeremiya 7 >