< Yeremiya 6 >

1 “Thawani, inu anthu a ku Benjamini! Tulukani mu Yerusalemu! Lizani lipenga ku Tekowa! Kwezani mbendera ku Beti-Hakeremu! Pakuti tsoka lalikulu likubwera kuchokera kumpoto, ndipo chiwonongekocho nʼchachikulu.
Flee for safety, ye sons of Benjamin, out of the midst of Jerusalem. And blow the trumpet in Tekoa, and raise up a signal on Beth-haccherem. For evil looks forth from the north, and a great destruction.
2 Kodi mzinda wa Ziyoni suli ngati msipu wokongola kwambiri, kumene abusa amafikako ndi ziweto zawo?
The comely and delicate one, the daughter of Zion, I will cut off.
3 Abusa ndi nkhosa zawo adzabwera kudzalimbana nawo; adzamanga matenti awo mowuzinga, ndipo aliyense adzakhazika anthu ake pamalo pake.”
Shepherds with their flocks shall come to her. They shall pitch their tents against her round about. They shall feed every one in his place.
4 Adzanena kuti, “Konzekani kuwuthira nkhondo mzindawo! Nyamukani, kuti tiwuthire nkhondo mzindawu masana ano. Koma tili ndi tsoka, dzuwa lapendeka, ndipo zithunzithunzi za kumadzulo zikunka zitalika.
Prepare ye war against her. Arise, and let us go up at noon. Woe to us! For the day declines; for the shadows of the evening are stretched out.
5 Tsono nyamukani kuti tiwuthire nkhondo mzindawu usiku uno ndi kuwononga malinga ake!”
Arise, and let us go up by night, and let us destroy her palaces.
6 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Dulani mitengo ndipo mumange mitumbira yankhondo kulimbana ndi Yerusalemu. Mzinda umenewu uyenera kulangidwa; wadzaza ndi kuponderezana.
For thus has Jehovah of hosts said: Hew ye down trees, and cast up a mound against Jerusalem. This is the city to be visited. She has oppression completely in the midst of her.
7 Monga momwe chitsime chimatulutsira madzi ndi mmenenso Yerusalemu amatulutsira zoyipa zake. Chiwawa ndi chiwonongeko ndi zomwe zimamveka mu mzindamo; nthenda yake ndi mabala ake ndimaziona nthawi zonse.
As a well casts forth its waters, so she casts forth her wickedness. Violence and destruction is heard in her. Continually before me is sickness and wounds.
8 Iwe Yerusalemu, tengapo phunziro, kuopa kuti chikondi changa pa iwe chingakuchokere ndi kusandutsa dziko lako kukhala bwinja mopanda munthu wokhalamo.”
Be thou instructed, O Jerusalem, lest my soul be alienated from thee, lest I make thee a desolation, a land not inhabited.
9 Yehova Wamphamvuzonse anandiwuza kuti, “Adani adzawakunkha ndithu anthu otsala a Israeli, monga momwe amachitira populula mphesa. Tsono iwe yesetsa kupulumutsa amene ungathe monga mmene amachitira munthu wokolola mphesa.”
Thus says Jehovah of hosts: They shall thoroughly glean the remnant of Israel as a vine. Turn again thy hand as a grape gatherer into the baskets.
10 Kodi ndiyankhule ndi yani ndi kumuchenjeza? Ndinene mawu ochenjeza kwa yani kuti amve? Makutu awo ndi otsekeka kotero kuti sangathe kumva. Mawu a Yehova ndi onyansa kwa iwo; sasangalatsidwa nawo.
To whom shall I speak and testify, that they may hear? Behold, their ear is uncircumcised, and they cannot hearken. Behold, the word of Jehovah has become to them a reproach; they have no delight in it.
11 Koma ine ndadzazidwa ndi mkwiyo wa Yehova, ndipo ndatopa ndi kusunga mkwiyo wa Yehova. Yehova anandiwuza kuti, “Tsono ndidzawutulutsira mkwiyo umenewu pa ana oyenda mʼmisewu ndi pa achinyamata amene asonkhana pamodzi; pakutinso mwamuna ndi mkazi wake adzatengedwa, pamodzi ndi okalamba amene ali ndi zaka zochuluka.
Therefore I am full of the wrath of Jehovah. I am weary with holding in. Pour it out upon the sons in the street, and upon the assembly of young men together. For even the husband with the wife shall be taken, the aged with him who is full of days.
12 Nyumba zawo adzazipereka kwa ena, pamodzi ndi minda yawo ndi akazi awo. Ndidzatambasula dzanja langa kukantha anthu okhala mʼdzikomo,” akutero Yehova.
And their houses shall be turned to others, their fields and their wives together. For I will stretch out my hand upon the inhabitants of the land, says Jehovah.
13 “Kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, onse ali ndi dyera lofuna kupeza phindu mwa kuba; aneneri pamodzi ndi ansembe omwe, onse amachita zachinyengo.
For from the least of them even to the greatest of them everyone is given to covetousness. And from the prophet even to the priest everyone deals falsely.
14 Amapoletsa zilonda za anthu anga pamwamba pokha. Iwo amanena kuti, ‘Mtendere, mtendere,’ pamene palibe mtendere.
They have also lightly healed the hurt of my people, saying, Peace, peace, when there is no peace.
15 Kodi amachita manyazi akamachita zonyansazo? Ayi, sachita manyazi ndi pangʼono pomwe; sadziwa ndi kugwetsa nkhope komwe. Choncho iwo adzagwera pakati pa anzawo amene agwa kale; adzagwa pansi tsiku limene ndidzawalange,” akutero Yehova.
Were they ashamed when they had committed abomination? No, they were not at all ashamed, nor could they blush. Therefore they shall fall among those who fall. At the time that I visit them they shall be cast down, says Jehovah.
16 Yehova akuti, “Imani pa mphambano ndipo mupenye; kumeneko ndiye kuli njira zakale, funsani kumene kuli njira yabwino. Yendani mʼmenemo, ndipo mudzapeza mpumulo wa miyoyo yanu. Koma inu munati, ‘Ife sitidzayenda njira imeneyo.’
Thus says Jehovah, Stand ye in the ways and see. And ask for the old paths where is the good way. And walk in it, and ye shall find rest for your souls. But they said, We will not walk.
17 Ine ndinakupatsani alonda oti akuyangʼanireni ndipo ndinati, ‘Imvani kulira kwa lipenga!’ koma inu munati, ‘Sitidzamvera.’
And I set watchmen over you, saying, Hearken to the sound of the trumpet. But they said, We will not hearken.
18 Nʼchifukwa chake imvani, inu anthu a mitundu ina; yangʼanitsitsani, inu amene mwasonkhana pano, chimene chidzawachitikire anthuwo.
Therefore hear, ye nations, and know, O congregation, what is among them.
19 Imvani, inu anthu okhala pa dziko lapansi, ndikubweretsa masautso pa anthu awa. Zimenezi ndi mphotho ya ntchito zawo. Iwowa sanamvere mawu anga ndipo anakana lamulo langa.
Hear, O earth: Behold, I will bring evil upon this people, even the fruit of their thoughts, because they have not hearkened to my words. And as for my law, they have rejected it.
20 Kodi pali phindu lanji ngakhale mubwere ndi lubani kuchokera ku Seba, kapena zonunkhira zina kuchokera ku dziko lakutali? Nsembe zanu zopsereza Ine sindidzalandira; nsembe zanu sizindikondweretsa.”
To what purpose does there come to me frankincense from Sheba, and the sweet cane from a far country? Your burnt offerings are not acceptable, nor your sacrifices pleasing to me.
21 Choncho Yehova akuti, “Ndidzayika zokhumudwitsa pamaso pa anthu awa. Abambo ndi ana awo aamuna onse adzapunthwa ndi kugwa; anansi awo ndi abwenzi awo adzawonongeka.”
Therefore thus says Jehovah: Behold, I will lay stumbling-blocks before this people, and the fathers and the sons together shall stumble against them. The neighbor and his friend shall perish.
22 Yehova akunena kuti, “Taonani, gulu lankhondo likubwera kuchokera kumpoto; mtundu wa anthu amphamvu wanyamuka kuchokera kumathero a dziko lapansi.
Thus says Jehovah, Behold, a people comes from the north country, and a great nation shall be stirred up from the outermost parts of the earth.
23 Atenga mauta ndi mikondo; ndi anthu ankhanza ndi opanda chifundo. Phokoso lawo lili ngati mkokomo wa nyanja. Akwera pa akavalo awo ndipo akonzekera ngati anthu ankhondo, kudzakuthirani nkhondo anthu a ku Ziyoni.”
They lay hold on bow and spear. They are cruel, and have no mercy. Their voice roars like the sea, and they ride upon horses. Each one set in array, as a man to the battle, against thee, O daughter of Zion.
24 A ku Ziyoni akuti “Ife tamva mbiri yawo, ndipo manja anthu alefukiratu. Nkhawa yatigwira, ndipo tikumva ululu ngati mayi pa nthawi yake yochira.
We have heard the report of it. Our hands grow feeble. Anguish has taken hold of us, and pangs as of a woman in travail.
25 Musapite ku minda kapena kuyenda mʼmisewu, pakuti mdani ali ndi lupanga, ndipo ponseponse anthu akuchita mantha.
Go not forth into the field, nor walk by the way, for the sword of the enemy, and terror, are on every side.
26 Inu anthu anga, valani ziguduli ndipo gubudukani pa phulusa; lirani mwamphamvu ngati munthu wolirira mwana wake mmodzi yekha, pakuti mwadzidzidzi wowonongayo adzabwera kudzatipha.
O daughter of my people, gird thee with sackcloth, and wallow thyself in ashes. Make thee mourning, as for an only son, a most bitter lamentation. For the destroyer shall suddenly come upon us.
27 “Iwe Yeremiya, ndakuyika kuti ukhale choyesera zitsulo. Uwayese anthu anga monga ungayesere chitsulo kuti uwone makhalidwe awo.
I have made thee a prover and a fortress among my people, that thou may know and try their way.
28 Onsewo ali ndi khalidwe lokanika ndi lowukira ndipo akunka nanena zamiseche. Iwo ndi olimba ngati mkuwa ndi chitsulo. Onse amangochita zoyipa zokhazokha.
They are all grievous revolters, going about with slanders. They are brass and iron. They all of them deal corruptly.
29 Moto mu mvukuto ukuyaka kwambiri; mtovu watha kusungunuka ndi moto. Koma ntchito yosungunulayo sikupindula chifukwa zoyipa sizikuchokapo.
The bellows blow fiercely, the lead is consumed of the fire. In vain do they go on refining, for the wicked are not plucked away.
30 Iwo ali ngati siliva wotayidwa, chifukwa Yehova wawakana.”
Waste silver, men shall call them, because Jehovah has rejected them.

< Yeremiya 6 >