< Yesaya 22 >

1 Uthenga wonena za Chigwa cha Masomphenya: Kodi chachitika nʼchiyani, kuti nonsenu mukwere pa madenga?
The burden of the valley of vision. What troubles thee now, that thou have wholly gone up to the housetops?
2 Iwe mzinda wodzaza ndi chisangalalo chodzaza tsaya, iwe mzinda waphokoso ndi wosokonekera? Anthu ako ophedwa aja sanaphedwe ndi lupanga, kapena kufera pa nkhondo.
O thou that are full of shoutings, a tumultuous city, a joyous town. Thy slain are not slain with the sword, nor are they dead in battle.
3 Atsogoleri ako onse ngakhale anathawa limodzi; koma anagwidwa osadziteteza nʼkomwe. Inu munapezeka ndipo nonse pamodzi munatengedwa ukapolo, ngakhale munathawa pamene mdani akanali patali.
All thy rulers fled away together. They were bound by the archers. All who were found of thee were bound together; they fled afar off.
4 Nʼchifukwa chake Ine ndinati, “Chokani pamaso panga; ndilekeni ndilire ndi mtima wowawa. Musayesere kunditonthoza chifukwa cha kuwonongeka kwa anthu anga.”
Therefore I said, Look away from me. I will weep bitterly. Labor not to comfort me for the destruction of the daughter of my people.
5 Lero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse walola kuti tione mavuto ndi kugonjetsedwa ndiponso chisokonezo mʼChigwa cha Masomphenya. Malinga agumuka, komanso anthu akanalira mofuwula ku mapiri.
For it is a day of trouble, and of treading down, and of perplexity, from the Lord, Jehovah of hosts, in the valley of vision, a breaking down of the walls, and a crying to the mountains.
6 Ankhondo a ku Elamu anadza pa magaleta ndi akavalo ali ndi mivi mʼmanja. Ankhondo a ku Kiri anakonzeka ndi zishango.
And Elam bore the quiver, with chariots of men and horsemen, and Kir uncovered the shield.
7 Zigwa zanu zachonde ndi zodzaza ndi magaleta, ndipo asilikali okwera pa akavalo ayikidwa pa zipata za mzinda;
And it came to pass, that thy choicest valleys were full of chariots, and the horsemen set themselves in array at the gate.
8 zonse zoteteza Yuda zachotsedwa. Ndipo tsiku limenelo munayangʼanayangʼana zida zankhondo zomwe zinali mʼnyumba yaufumu ya nkhalango;
And he took away the covering of Judah, and thou looked in that day to the armor in the house of the forest.
9 inu munaona kuti makoma ambiri a mzinda wa Davide anali ndi malo ambiri ogumuka; munasunga madzi mu chidziwe chakumunsi.
And ye saw the breaches of the city of David, that they were many. And to fortify the wall, ye gathered together the waters of the lower pool,
10 Munawerenga nyumba zonse za mu Yerusalemu ndipo munagwetsa nyumba zina kuti mulimbitse linga logumuka lija.
and ye numbered the houses of Jerusalem, and ye broke down the houses.
11 Pakati pa makoma awiri munamanga chitsime chosungiramo madzi ochokera ku dziwe lakale, koma inu simunadalire Mulungu amene anapanga zimenezi, kapena kusamalako za Iye amene anazilenga kale lomwe.
Ye also made a reservoir between the two walls for the water of the old pool. But ye did not look to him who had done this, nor had ye respect to him who purposed it long ago.
12 Pa tsiku limenelo, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse anakuyitanani kuti mulire ndi kukhetsa misozi; kumeta mutu wanu mpala ndi kuvala ziguduli.
And in that day the Lord, Jehovah of hosts, called for weeping, and for mourning, and for baldness, and for girding with sackcloth.
13 Koma mʼmalo mwake inu munakondwa ndi kusangalala; munapha ngʼombe ndi nkhosa; munadya nyama ndi kumwa vinyo. Inu mumati, “Tiyeni tidye ndi kumwa pakuti mawa tifa!”
And, behold, joy and gladness, slaying oxen and killing sheep, eating flesh and drinking wine. Let us eat and drink, for tomorrow we shall die.
14 Yehova Wamphamvuzonse wandiwululira mondinongʼoneza kuti, “Tchimo limeneli sindidzakhululuka mpaka tsiku la kufa kwanu,” akutero Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse.
And Jehovah of hosts revealed himself in my ears, Surely this iniquity shall not be forgiven you till ye die, says the Lord, Jehovah of hosts.
15 Chimene Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Pita, ukanene kwa Sabina kapitawo, amene amayangʼanira nyumba yaufumu:
Thus says the Lord, Jehovah of hosts, Go, get thee to this treasurer, even to Shebna, who is over the house, and say,
16 Kodi ukuchita chiyani kuno, nanga ndani anakupatsa chilolezo kuti udzikumbire manda kuno, kudzikumbira manda pa phiri ndi kudzisemera malo opumulira mʼthanthwe?
What are thou doing here? And whom have thou here, that thou have hewed thee out here a sepulcher? Hewing him out a sepulcher on high, carving a habitation for himself in the rock!
17 “Samalira, Yehova watsala pangʼono kukugwira zolimba ndi kukuponya mwamphamvu, iwe munthu wamphamvu.
Behold, Jehovah, like a strong man, will hurl thee away violently. Yea, he will wrap thee up closely.
18 Iye adzakukulunga kwambiri ngati mpira ndipo adzakuponyera mʼdziko lalikulu. Kumeneko ndiko ukafere ndipo kumeneko ndiko kudzatsalire magaleta ako. Ndipo udzasanduka wochititsa manyazi nyumba ya mbuye wako.
He will surely wind thee round and round, tossing like a ball into a large country. There thou shall die, and there the chariots of thy glory shall be, thou shame of thy lord's house.
19 Ine ndidzakuchotsa pa ukapitawo wako ndipo ndidzakutsitsa pa udindo wako.
And I will thrust thee from thine office, and thou shall be pulled down from thy station.
20 “Tsiku limenelo ndidzayitanitsa mtumiki wanga, Eliyakimu mwana wa Hilikiya.
And it shall come to pass in that day, that I will call my servant Eliakim the son of Hilkiah.
21 Ndidzamuveka mkanjo wako ndi kumangira lamba wako mʼchiwuno mwake ndi kumupatsa ulamuliro wako. Iye adzakhala kholo la amene amakhala mu Yerusalemu ndiponso a fuko la Yuda.
And I will clothe him with thy robe, and strengthen him with thy belt. And I will commit thy government into his hand, and he shall be a father to the inhabitants of Jerusalem, and to the house of Judah.
22 Ndidzamupatsa ulamuliro wa banja la Davide. Adzatsekula ndipo palibe adzatseke, adzatseka popanda wina kutsekula.
And I will lay the key of the house of David upon his shoulder, and he shall open, and none shall shut, and he shall shut, and none shall open.
23 Ufumu wake udzakhala wokhazikika ngati chikhomo chokhomedwa pa malo olimba. Anthu adzalemekeza nyumba ya abale ake chifukwa cha iye.
And I will fasten him as a nail in a sure place, and he shall be for a throne of glory to his father's house.
24 Ana ndi abale a nyumba ya abambo ake adzakhala ngati katundu pa iye ngati ziwiya zopanda ntchito zimene zapachikidwa pa chikhomo.
And they shall hang upon him all the glory of his father's house, the offspring and the issue, every small vessel, from the cups even to all the flagons.
25 “Yehova Wamphamvuzonse akunena kuti, ‘Tsiku limeneli chikhomo chokhomedwa kwambiri chija sichidzalimbanso; chidzazuka ndipo chidzagwa ndipo zonse zopachikidwa zidzawonongedwa.’” Yehova wayankhula chomwechi.
In that day, says Jehovah of hosts, the nail that was fastened in a sure place shall give way, and it shall be hewn down, and fall. And the burden that was upon it shall be cut off, for Jehovah has spoken it.

< Yesaya 22 >