< Yesaya 23 >

1 Uthenga wonena za Turo: Lirani mofuwula, inu oyendetsa sitima za pa madzi za ku Tarisisi: pakuti mzinda wa Turo wawonongedwa ndipo mulibe nyumba kapena dooko. Zimenezi anazimva pochokera ku Kitimu.
The burden of Tyre. Howl, ye ships of Tarshish, for it is laid waste, so that there is no house, no entering in. It is revealed to them from the land of Kittim.
2 Khalani chete inu anthu okhala mʼmbali mwa nyanja, inu amalonda a ku Sidoni, iwe amene unalemera ndi anthu oyenda pa nyanja.
Be still, ye inhabitants of the coast, thou whom the merchants of Sidon, who pass over the sea, have replenished.
3 Pa nyanja zazikulu panabwera tirigu wa ku Sihori; zokolola za ku Nailo, ndipo munachita malonda ndi anthu a mitundu ina.
And on great waters the seed of the Shihor, the harvest of the Nile, was her revenue, and she was the mart of nations.
4 Chita manyazi, iwe Sidimu pakuti nyanja yayankhula, linga la ku nyanja (Turo) layankhula kuti, “Sindinamvepo zowawa za kubereka kapena kuberekapo mwana; sindinalerepo ana aamuna kapena kulera ana aakazi.”
Be thou ashamed, O Sidon, for the sea has spoken, the stronghold of the sea, saying, I have not travailed, nor brought forth, neither have I nourished young men, nor brought up virgins.
5 Mawuwa akadzamveka ku Igupto, iwo adzachita mantha akadzamva kuti Turo wawonongeka.
When the report comes to Egypt, they shall be greatly pained at the report of Tyre.
6 Wolokerani ku Tarisisi, lirani mofuwula, inu anthu okhala mʼmbali mwa nyanja.
Pass ye over to Tarshish. Wail, ye inhabitants of the coast.
7 Kodi uwu si mzinda wachisangalalo uja, mzinda wakalekale, umene anthu ake ankapita kukakhala ku mayiko akutali?
Is this your joyous city, whose antiquity is of ancient days, whose feet carried her afar off to sojourn?
8 Kodi ndani anakonza zimenezi kuti zigwere Turo, mzinda umene unakhazikitsa mizinda ina, mzinda umene amalonda ake ndi akalonga ndi otchuka pa dziko lapansi?
Who has purposed this against Tyre, the bestower of crowns, whose merchants are rulers, whose traders are the honored of the earth?
9 Yehova Wamphamvuzonse anakonza zimenezi kuti athetse kunyada kwawo ndi kutsitsa anthu otchuka a pa dziko lapansi.
Jehovah of hosts has purposed it, to stain the pride of all glory, to bring into contempt all the honorable of the earth.
10 Mubalalike mʼdziko mwanu ngati mtsinje wa Nailo inu anthu a ku Tarisisi, pakuti mulibenso chokutetezani.
Pass through thy land as the Nile, O daughter of Tarshish, there is no restraint any more.
11 Yehova watambasula dzanja lake kuloza ku nyanja ndipo wagwedeza maufumu ake. Iye walamula kuti Kanaani agwetse malinga ake.
He has stretched out his hand over the sea. He has shaken the kingdoms. Jehovah has given commandment concerning Canaan, to destroy the strongholds of it.
12 Iye anati, “Simudzakondwanso konse, inu anthu opanikizidwa a ku Sidoni, tsopano wamphwanyidwa! “Ngakhale muwolokere ku Kitimu, kumeneko simukapezako mpumulo.”
And he said, Thou shall no more rejoice, O thou oppressed virgin daughter of Sidon. Arise, pass over to Kittim, even there shall thou have no rest.
13 Onani dziko la Ababuloni, anthu amenewa tsopano atheratu! Asiriya asandutsa Turo kukhala malo a zirombo za ku chipululu; anamanga nsanja zawo za nkhondo, anagumula malinga ake ndipo anawasandutsa bwinja.
Behold, the land of the Chaldeans. This people once was not. The Assyrian founded it for those who dwell in the wilderness. They set up their towers. They raised up the palaces of it. Then they made it a ruin.
14 Lirani mofuwula, inu anthu oyendetsa sitima za pa madzi za ku Tarisisi; chifukwa malinga ako agwetsedwa!
Howl, ye ships of Tarshish, for your stronghold is laid waste.
15 Pa nthawi imeneyo Turo adzayiwalika pa zaka 70, amene ndi masiku a moyo wa mfumu. Koma potsiriza pa zaka 70 zimenezi, Turo adzakhala ngati mkazi wachiwerewere woyimbidwa mu nyimbo:
And it shall come to pass in that day, that Tyre shall be forgotten seventy years, according to the days of one king. After the end of seventy years it shall be to Tyre as in the song of the harlot:
16 “Tenga zeze wako uzungulire mzinda, iwe mkazi wachiwerewere woyiwalika; imba zeze mokometsera, imba nyimbo zambiri, kuti anthu akukumbukire.”
Take a harp, go about the city, thou harlot who has been forgotten. Make sweet melody, sing many songs, that thou may be remembered.
17 Pakutha pa zaka 70, Yehova adzachitapo kanthu pa Turo. Iye adzabwerera ku ntchito yake yakale monga mkazi wachiwerewere ndipo adzachita zachiwerewere ndi maufumu onse a dziko lapansi.
And it came to pass after the end of seventy years, that Jehovah examined Tyre, and she has repented of her gift, that she play the harlot with all the kingdoms of the world upon the face of the earth.
18 Koma phindu lake ndi malipiro ake adzazipereka kwa Yehova; sadzazikundika kapena kuzisunga. Phindu lake lidzapita kwa mtumiki wa Yehova kuti agule zakudya zambiri ndi zovala zokongola.
And her merchandise and her pay shall be holiness to Jehovah. It shall not be treasured nor laid up, for her merchandise shall be for those who dwell before Jehovah, to eat sufficiently, and for durable clothing.

< Yesaya 23 >