< Yesaya 21 >

1 Uthenga wonena za chipululu cha mʼmbali mwa Nyanja. Ankhondo a ku Elamu ndi Mediya adzabwera ngati kamvuluvulu amene akuwomba modutsa mʼmbali ya nyanja, kuchokera ku chipululu, dziko lochititsa mantha.
The burden of the wilderness of the sea. As whirlwinds in the South sweep through, it comes from the wilderness, from a terrible land.
2 Ine ndaona zinthu zoopsa mʼmasomphenya: Wonyenga akunyenga, wofunkha akufunkha komanso owononga akuwononga. Elamu, yambani nkhondo! Mediya, zingani mzinda! Ine ndidzathetsa mavuto onse amene anayambitsa Ababuloni.
A grievous vision is declared to me. The treacherous man deals treacherously, and the destroyer destroys. Go up, O Elam. Besiege, O Media, all the sighing of it I have made to cease.
3 Chifukwa cha zimenezi thupi langa likunjenjemera ndi mantha, ndikumva ululu ngati wa mayi amene akubereka; ndikuvutika kwambiri ndi zimene ndikumva, ndathedwa nzeru ndi zimene ndikuziona.
Therefore my loins are filled with anguish. Pangs have taken hold upon me, as the pangs of a woman in travail. I am pained so that I cannot hear. I am dismayed so that I cannot see.
4 Mtima wanga ukugunda, ndipo ndikunjenjemera ndi mantha; chisisira chimene ndakhala ndikuchifuna chasanduka chinthu choopsa kwa ine.
My heart flutters. Horror has frightened me. The twilight that I desired has been turned into trembling to me.
5 Ankhondo a ku Elamu ndi Mediya akukonza matebulo, akuyala mphasa, akudya komanso kumwa! Mwadzidzidzi anamva mawu akuti, “Dzukani inu ankhondo, pakani mafuta zishango zanu!”
They prepare the table, they set the watch, they eat, they drink. Rise up, ye rulers, anoint the shield.
6 Zimene Ambuye akunena kwa ine ndi izi; “Pita, kayike mlonda kuti azinena zimene akuziona.
For thus has the Lord said to me, Go, set a watchman. Let him declare what he sees.
7 Taonani, anthu akubwera ali pa akavalo ndipo akuyenda awiriawiri, okwera pa bulu kapena okwera pa ngamira, mlondayo akhale tcheru kwambiri.”
and when he sees a troop, horsemen in pairs, a troop of donkeys, a troop of camels, he shall hearken diligently with much heed.
8 Ndipo mlondayo anafuwula kuti, “Ambuye anga, tsiku ndi tsiku ndimakhala pa nsanja yolondera; Usiku uliwonse ndimakhala pa malo anga olondera.
And he cried out as a lion, O Lord, I stand continually upon the watchtower in the daytime, and am set in my ward whole nights,
9 Taonani, uyo munthu akubwera atakwera pa galeta ali ndi gulu la akavalo. Mmodzi wa iwo akuti, ‘Babuloni wagwa, wagwa! Mafano onse a milungu yake agwa pansi ndipo aphwanyika!’”
and, behold, here comes a troop of men, horsemen in pairs. And he answered and said, Fallen, fallen is Babylon. And all the graven images of her gods are broken to the ground.
10 Inu anthu anga opunthidwa ndi kupetedwa ngati tirigu, ine ndikukuwuzani zimene ndamva ndikukuwuzani Uthenga wochokera kwa Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli.
O my threshing, and the grain of my floor! That which I have heard from Jehovah of hosts, the God of Israel, I have declared to you.
11 Uthenga wonena za Duma: Munthu wina akundiyitana kuchokera ku Seiri kuti, “Iwe mlonda, usikuwu utha liti? Iwe mlonda, utha liti kodi usikuwu?”
The burden of Dumah. He calls to me out of Seir, Watchman, what of the night? Watchman, what of the night?
12 Mlonda akuyankha kuti, “Kukucha, koma kudanso. Ngati ukufuna kufunsa, funsa tsopano; ndipo ubwerenso udzafunse.”
The watchman said, The morning comes, and also the night. If ye will inquire, inquire ye; turn ye back, come.
13 Uthenga wonena za Arabiya: Inu anthu amalonda a ku Dedani, amene usiku mumagona mʼzithukuluzi za ku Arabiya,
The burden upon Arabia. In the forest in Arabia ye shall lodge, O ye caravans of Dedanites.
14 perekani madzi kwa anthu aludzu. Inu anthu a ku Tema perekani chakudya kwa anthu othawa nkhondo.
To him who was thirsty they brought water. The inhabitants of the land of Tema met the fugitives with their bread.
15 Iwo akuthawa malupanga, lupanga losololedwa, akuthawa uta wokokakoka ndiponso nkhondo yoopsa.
For they fled away from the swords, from the drawn sword, and from the bent bow, and from the grievousness of war.
16 Zimene Ambuye akunena kwa ine ndi izi: “Chaka chimodzi chisanathe, potsata mmene amawerengera munthu waganyu, ulemerero wonse wa Kedara udzatheratu.
For thus the Lord has said to me, Within a year, according to the years of a hireling, all the glory of Kedar shall fail.
17 Mwa anthu okoka uta, ankhondo a ku Kedara opulumuka adzakhala owerengeka.” Wayankhula ndi Yehova Mulungu wa Israeli.
And the residue of the number of the archers, the mighty men of the sons of Kedar, shall be few. For Jehovah, the God of Israel, has spoken it.

< Yesaya 21 >