< Yesaya 11 >

1 Padzatuluka mphukira pa tsinde la Yese ndipo nthambi idzaphukira kuchokera ku mizu yake.
And there shall come forth a shoot out of the stock of Jesse. And a branch out of his roots shall bear fruit.
2 Mzimu wa Yehova udzakhala pa iye Mzimu wanzeru ndi wa kumvetsa zinthu, Mzimu wauphungu ndi wamphamvu, Mzimu wachidziwitso ndi wakuopa Yehova.
And the Spirit of Jehovah shall rest upon him, the spirit of wisdom and understanding, the spirit of counsel and might, the spirit of knowledge and of the fear of Jehovah.
3 Ndipo kuopa Yehova ndiye chidzakhale chinthu chomukondweretsa. Iye sadzaweruza potsata zooneka pamaso, kapena kugamula mlandu potsata zakumva;
And his delight shall be in the fear of Jehovah. And he shall not judge according to the sight of his eyes, nor decide according to the hearing of his ears,
4 koma amphawi adzawaweruza mwachilungamo, adzaweruza mwachilungamo mlandu wa anthu osauka a dziko lapansi. Iye adzakantha dziko lapansi ndi mawu ake; atalamula Iyeyu anthu oyipa adzaphedwa.
but with righteousness he shall judge the poor, and decide with equity for the meek of the earth. And he shall smite the earth with the rod of his mouth, and with the breath of his lips he shall kill the wicked.
5 Chilungamo chidzakhala ngati lamba wake ndipo kukhulupirika kudzakhala ngati chomangira mʼchiwuno mwake.
And righteousness shall be the belt of his waist, and faithfulness the belt of his loins.
6 Mʼmbulu udzakhala pamodzi ndi mwana wankhosa, kambuku adzagona pansi pamodzi ndi mwana wambuzi, mwana wangʼombe ndi mwana wa mkango adzadyera limodzi ndipo mwana wamngʼono adzaziweta.
And the wolf shall dwell with the lamb, and the leopard shall lie down with the kid, and the calf and the young lion and the fatling together, and a little child shall lead them.
7 Ngʼombe yayikazi ndi chimbalangondo zidzadya pamodzi, ana awo adzagona pamodzi, ndipo mkango udzadya udzu ngati ngʼombe.
And the cow and the bear shall feed; their young ones shall lie down together. And the lion shall eat straw like the ox.
8 Mwana wakhanda adzasewera pa dzenje la mamba, ndipo mwana wamngʼono adzapisa dzanja lake ku phanga la mphiri osalumidwa.
And the sucking child shall play on the hole of the asp, and the weaned child shall put his hand on the adder's den.
9 Sipadzakhala chilichonse chopweteka kapena chowononga pa phiri lopatulika la Yehova, pakuti anthu a dziko lapansi adzadzaza ndi nzeru yotha kudziwa Yehova monga momwe nyanja imadzazira ndi madzi.
They shall not hurt nor destroy in all my holy mountain, for the earth shall be full of the knowledge of Jehovah as the waters cover the sea.
10 Tsiku limenelo mfumu yatsopano yochokera pa Muzu wa Yese idzakhala ngati chizindikiro kwa anthu a mitundu yonse. Mitundu ya anthu idzasonkhana kwa Iye, ndipo malo awo okhalapo adzakhala aulemerero.
And in that day there shall be a root of Jesse, and he who arises to rule over the Gentiles. In him shall the Gentiles hope, and his resting-place shall be glorious.
11 Tsiku limenelo Ambuye adzatambasula dzanja lake kachiwiri kuti awombole anthu ake otsalira ku Asiriya, ku Igupto, ku Patirosi, Kusi, ku Elamu, ku Sinana, ku Hamati ndi pa zilumba za nyanja yamchere.
And it shall come to pass in that day, that the Lord will set his hand again the second time to recover the remnant of his people, who shall remain, from Assyria, and from Egypt, and from Pathros, and from Cush, and from Elam, and from Shinar, and from Hamath, and from the islands of the sea.
12 Adzakwezera mitundu ya anthu mbendera, ndipo adzasonkhanitsa otayika a ku Israeli; Iye adzasonkhanitsa anthu obalalika a ku Yuda kuchokera ku mbali zonse zinayi za dziko lapansi.
And he will set up an ensign for the nations, and will assemble the outcasts of Israel, and gather together the dispersed of Judah from the four corners of the earth.
13 Nsanje ya Efereimu idzatha, ndipo adani a Yuda adzatha; Efereimu sadzachitira nsanje Yuda, ngakhale Yuda sadzamuda Efereimu.
Also the envy of Ephraim shall depart, and those who vex Judah shall be cut off. Ephraim shall not envy Judah, and Judah shall not vex Ephraim.
14 Yuda ndi Efereimu adzathira nkhondo pa Afilisti mbali ya kumadzulo; ndipo onsewo pamodzi adzalanda zinthu za anthu a kummawa. Adzalimbana ndi Edomu ndi Mowabu, ndipo Aamoni adzawagonjera.
And they shall fly down upon the shoulder of the Philistines on the west. Together they shall despoil the sons of the east. They shall put forth their hand upon Edom and Moab, and the sons of Ammon shall obey them.
15 Yehova adzaphwetsa mwendo wa nyanja ya Igupto; adzatambasula dzanja lake ndipo adzawombetsa mphepo yotentha pa mtsinje wa Yufurate. Iye adzawugawa mtsinjewo kukhala timitsinje tisanu ndi tiwiri kuti anthu athe kuwoloka powuma atavala nsapato.
And Jehovah will utterly destroy the tongue of the Egyptian sea. And with his scorching wind he will wave his hand over the River, and will smite it into seven streams, and cause men to march over dry shod.
16 Padzakhala msewu waukulu woti ayendepo anthu ake otsalira amene anatsalira ku Asiriya, monga mmene panali msewu waukulu woyendapo Israeli pamene amachokera ku Igupto.
And there shall be a highway for the remnant of his people, who shall remain, from Assyria, like as there was for Israel in the day that he came up out of the land of Egypt.

< Yesaya 11 >