< Yesaya 10 >

1 Tsoka kwa anthu amene amapanga malamulo opanda chilungamo, kwa iwo amene amalemba zongovutitsa anzawo,
Woe to those who decree unrighteous decrees, and to the writers who write perverseness,
2 kuwalanda anthu osauka ufulu wawo ndi kumana chilungamo osautsidwa pakati pa anthu anga, amalanda zinthu za akazi amasiye ndi kubera ana amasiye.
to turn aside the needy from justice, and to rob the poor of my people of their right, that widows may be their spoil, and that they may make the fatherless their prey!
3 Kodi mudzatani pa tsiku la chilango, pofika chiwonongeko chochokera kutali? Kodi mudzathawira kwa yani kuti akuthandizeni? Nanga chuma chanu mudzachisiya kuti?
And what will ye do in the day of visitation, and in the desolation which shall come from far? To whom will ye flee for help? And where will ye leave your glory?
4 Kudzatsala nʼkungozolika mwamanyazi pakati pa anthu ogwidwa kapena kufa pamodzi ndi ophedwa. Komabe pa zonsezi mkwiyo wake sunawachokere, mkono wake uli chitambasulire.
They shall only bow down under the prisoners, and shall fall under the slain. For all this his anger is not turned away, but his hand is stretched out still.
5 “Tsoka kwa mfumu ya ku Asiriya, chikwapu cha mkwiyo wanga, iye ndiye ndodo ya mkwiyo wanga!
Ho, Assyrian, the rod of my anger, the staff in whose hand is my indignation!
6 Ndidzamutuma kukalimbana ndi mtundu wosapembedza Mulungu, ndidzamutumiza kukalimbana ndi anthu amene amandikwiyitsa Ine, kukafunkha ndi kulanda chuma, ndi kuwapondereza pansi ngati matope a mʼmisewu.
I will send him against a profane nation, and against the people of my wrath. I will give him a charge, to take the spoil, and to take the prey, and to tread them down like the mire of the streets.
7 Koma izi si zimene akufuna kukachita, izi si zimene zili mʼmaganizo mwake; cholinga chake ndi kukawononga, kukapulula mitundu yambiri ya anthu.
However he does not so reason, nor does his heart so think, but it is in his heart to destroy, and to cut off nations not a few.
8 Iye akuti, ‘Kodi atsogoleri anga ankhondo si mafumu okhaokha?’
For he says, Are not my rulers all of them kings?
9 ‘Kodi Kalino sanagonjetsedwe monga Karikemesi? Kodi Hamati sali ngati Aripadi, nanga Samariya sali ngati Damasiko?
Is not Calno as Carchemish? Is not Hamath as Arpad? Is not Samaria as Damascus?
10 Dzanja langa linakantha maufumu a anthu opembedza mafano, mafumu amene mafano awo ndi aakulu kupambana Yerusalemu ndi Samariya;
As my hand has found the kingdoms of the idols, whose graven images excelled those of Jerusalem and of Samaria,
11 nanga Ine nʼkulephera kodi kuwononga Yerusalemu pamodzi ndi mafano ake monga ndinakanthira Samariya pamodzi ndi mafano ake?’”
shall I not, as I have done to Samaria and her idols, so do to Jerusalem and her idols?
12 Ambuye akadzamaliza ntchito yonse yolanga phiri la Ziyoni ndi Yerusalemu adzalanganso mfumu ya ku Asiriya chifukwa cha kudzitama ndi kunyada kwake.
Therefore it shall come to pass, that, when the Lord has performed his whole work upon mount Zion and on Jerusalem, I will punish the fruit of the arrogant heart of the king of Assyria, and the glory of his high looks.
13 Pakuti mfumuyo ikuti, “‘Ndachita zimenezi ndi dzanja langa, ndiponso ndi nzeru zanga, chifukwa ndine wozindikira zinthu. Ndinachotsa malire a mitundu ya anthu, ndinafunkha chuma chawo; ndinagonjetsa mafumu awo monga munthu wamphamvu.
For he has said, By the strength of my hand I have done it, and by my wisdom, for I have understanding. And I have removed the bounds of the peoples, and have robbed their treasures. And like a valiant man I have brought down those who sit on thrones.
14 Dzanja langa lagwira chuma cha mitundu ya anthu ngati momwe munthu amagwirira chisa cha mbalame, ngati momwe anthu amatolera mazira osiyidwa, motero inenso ndinasonkhanitsa mayiko onse; palibe mbalame imene inakupiza mapiko ake, kapena kuyasama kukamwa kuti ilire.’”
And my hand has found as a nest the riches of the peoples. And like a gathering of eggs that are forsaken, I have gathered all the earth. And there was none that moved the wing, or that opened the mouth, or chirped.
15 Kodi nkhwangwa ingathe kudzikuza kupambana woyigwiritsa ntchito, kapena macheka angathe kudzikuza kupambana wowagwiritsa ntchito? Ndiye kukhala ngati kuti chikwapu chikuzunguza munthu amene wachinyamula, kapena ngati kuti ndodo ikuopseza amene wayinyamula!
Shall the axe boast itself against him who hews with it? Shall the saw magnify itself against him who wields it? As if a rod should wield those who lift it up, or as if a staff should lift up him who is not wood.
16 Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova Wamphamvuzonse adzatumiza matenda owondetsa kwa ankhondo amphamvu; kunyada kwa mfumuyo kudzapsa ndi moto wosazima.
Therefore will the Lord, Jehovah of hosts, send among his fat ones, leanness, and under his glory there shall be kindled a burning like the burning of fire.
17 Mulungu, Kuwala kwa Israeli, adzakhala ngati moto, Woyera uja wa Israeli adzakhala ngati malawi a moto. Motowo udzawatentha ndi kuwapsereza ngati minga ndi mkandankhuku pa tsiku limodzi.
And the light of Israel will be for a fire, and his Holy One for a flame, and it will burn and devour his thorns and his briers in one day.
18 Ankhondo ake adzawonongedwa ngati nkhalango yayikulu ndi ngati nthaka yachonde.
And he will consume the glory of his forest, and of his fruitful field, both soul and body. And it shall be as when a standard-bearer faints.
19 Mitengo yotsalira ya mʼnkhalango zake idzakhala yochepa kwambiri, yoti ndi mwana yemwe ndi kuyiwerenga.
And the remnant of the trees of his forest shall be few, so that a child may write them.
20 Tsiku limenelo otsalira a ku Israeli, opulumuka a nyumba ya Yakobo, sadzadaliranso anthu amene anawakantha, koma adzadalira Yehova, Woyerayo wa Israeli.
And it shall come to pass in that day, that the remnant of Israel, and those who are escaped of the house of Jacob, shall no more again lean upon him who smote them, but shall lean upon Jehovah, the Holy One of Israel, in truth.
21 Otsalira adzabwerera, otsalira a Yakobo adzabwerera kwa Mulungu Wamphamvu.
A remnant shall return, even the remnant of Jacob, to the mighty God.
22 Iwe Israeli, ngakhale anthu ako achuluke ngati mchenga wa ku nyanja, otsala okha ndiwo adzabwerere. Chiwonongeko chalamulidwa, chidzaonetsa chilungamo chosefukira.
For though thy people, Israel, be as the sand of the sea, a remnant of them shall return. A destruction is determined, overflowing with righteousness.
23 Ambuye Yehova Wamphamvuzonse adzawononga ndithu dziko lonse monga momwe analamulira.
For a full end, and that determined, the Lord, Jehovah of hosts, will make in the midst of all the earth.
24 Nʼchifukwa chake, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse akunena kuti, “Inu anthu anga okhala mu Ziyoni, musawaope Asiriya, amene amakukanthani ndi ndodo nakumenyani ndi zibonga monga mmene Igupto anachitira.
Therefore thus says the Lord, Jehovah of hosts, O my people who dwell in Zion, be not afraid of the Assyrian, though he smites thee with the rod, and lifts up his staff against thee, according to the manner of Egypt.
25 Patsala pangʼonongʼono kuti mkwiyo wanga uchoke pa inu ndipo ndidzaonetsa ukali wanga pa iwo mpaka kuwawononga.”
For yet a very little while, and the indignation shall be accomplished, and my anger is to his destruction.
26 Yehova Wamphamvuzonse adzawakwapula ndi chikwapu, monga momwe anakwapulira Amidiyani ku thanthwe la Orebu; ndipo adzatukula ndodo yake pa madzi ndikuwalanga monga analangira Igupto pa nyanja.
And Jehovah of hosts will stir up against him a scourge as in the slaughter of Midian at the rock of Oreb. And his rod will be over the sea, and he will lift it up according to the manner of Egypt.
27 Tsiku limenelo katundu wawo adzachotsedwa pa mapewa anu, goli lawo lidzachoka mʼkhosi mwanu; golilo lidzathyoka chifukwa cha kunenepa kwambiri.
And it shall come to pass in that day, that his burden shall depart from off thy shoulder, and his yoke from off thy neck, and the yoke shall be destroyed because of fatness.
28 Adani alowa mu Ayati apyola ku Migironi; asunga katundu wawo ku Mikimasi.
He has come to Aiath. He has passed through Migron. At Michmash he lays up his baggage.
29 Adutsa pa mpata uja, ndipo akuti, “Tikagona ku Geba” Rama akunjenjemera; Gibeya, mzinda wa Saulo ukuthawa.
They have gone over the pass. They have taken up their lodging at Geba. Ramah trembles. Gibeah of Saul has fled.
30 Lilani mokweza, inu anthu a ku Galimu! Tchera khutu, iwe Laisa! Iwe Anatoti wosauka!
Cry aloud with thy voice, O daughter of Gallim! Hearken, O Laishah! O thou poor Anathoth!
31 Anthu a ku Madimena akuthawa; anthu a ku Gebimu bisalani.
Madmenah is a fugitive. The inhabitants of Gebim flee for safety.
32 Lero lomwe lino adaniwo adzayima ku Nobu; adzagwedeza mikono yawo, kuopseza anthu a ku Ziyoni, pa phiri la Yerusalemu.
This very day he shall halt at Nob. He shakes his hand at the mount of the daughter of Zion, the hill of Jerusalem.
33 Taonani, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse, adzadula mwamphamvu nthambi za mitengo, mitengo yodzikweza idzadulidwa, mitengo yayitali idzagwetsedwa.
Behold, the Lord, Jehovah of hosts, will lop off the boughs with terror. And the high of stature shall be hewn down, and the lofty shall be brought low.
34 Yehova adzadula ndi nkhwangwa mitengo ya mʼnkhalango yowirira; Lebanoni adzagwa pamaso pa Wamphamvu.
And he will cut down the thickets of the forest with iron, and Lebanon shall fall by a mighty one.

< Yesaya 10 >