< Genesis 5 >

1 Ndondomeko ya mibado ya Adamu ndi iyi: Pamene Mulungu analenga munthu, anamulenga mʼchifaniziro cha Mulungu.
This is the book of the generations of Adam. In the day that God created man, in the likeness of God he made him,
2 Iye analenga mwamuna ndi mkazi. Anawadalitsa ndipo anawatcha “Munthu.”
male and female he created them, and blessed them, and called their name Man, in the day when they were created.
3 Pamene Adamu anali ndi zaka 130, anabereka mwana wamwamuna wofanana naye ndipo anamutcha Seti.
And Adam lived a hundred and thirty years, and begot a son in his own likeness, according to his image, and called his name Seth.
4 Atabadwa Seti, Adamu anakhala ndi moyo zaka zina 800 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
And the days of Adam were eight hundred years after he begot Seth. And he begot sons and daughters.
5 Zaka zonse za Adamu zinali 930 ndipo anamwalira.
And all the days that Adam lived were nine hundred and thirty years, and he died.
6 Pamene Seti anali ndi zaka 105, anabereka Enosi.
And Seth lived a hundred and five years, and begot Enosh.
7 Atabadwa Enosi, Seti anakhala ndi moyo zaka zina 807 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
And Seth lived eight hundred and seven years after he begot Enosh, and begot sons and daughters.
8 Zaka zonse za Seti zinali 912 ndipo anamwalira.
And all the days of Seth were nine hundred and twelve years, and he died.
9 Pamene Enosi anali ndi zaka 90, anabereka Kenani.
And Enosh lived ninety years, and begot Kenan.
10 Atabadwa Kenani, Enosi anakhala ndi moyo zaka zina 815 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
And Enosh lived eight hundred and fifteen years after he begot Kenan, and begot sons and daughters.
11 Zaka zonse za Enosi pamodzi zinali 905 ndipo anamwalira.
And all the days of Enosh were nine hundred and five years, and he died.
12 Pamene Kenani anali ndi zaka 70, anabereka Mahalaleli.
And Kenan lived seventy years, and begot Mahalalel.
13 Atabadwa Mahalaleli, Kenani anakhala ndi moyo zaka zina 840 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
And Kenan lived eight hundred and forty years after he begot Mahalalel, and begot sons and daughters.
14 Zaka zonse za Kenani zinali 910, ndipo anamwalira.
And all the days of Kenan were nine hundred and ten years, and he died.
15 Pamene Mahalaleli anali ndi zaka 65, anabereka Yaredi.
And Mahalalel lived sixty-five years, and begot Jared.
16 Atabadwa Yaredi, Mahalaleli anakhala ndi moyo zaka zina 830 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
And Mahalalel lived eight hundred and thirty years after he begot Jared, and begot sons and daughters.
17 Zaka zonse za Mahalaleli zinali 895 ndipo anamwalira.
And all the days of Mahalalel were eight hundred and ninety-five years, and he died.
18 Pamene Yaredi anali ndi zaka 162, anabereka Enoki.
And Jared lived a hundred sixty-two years, and begot Enoch.
19 Atabadwa Enoki, Yaredi anakhala ndi moyo zaka zina 800 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
And Jared lived eight hundred years after he begot Enoch, and begot sons and daughters.
20 Zaka zonse za Yaredi zinali 962 ndipo anamwalira.
And all the days of Jared were nine hundred sixty-two years, and he died.
21 Pamene Enoki anali ndi zaka 65, anabereka Metusela.
And Enoch lived sixty-five years, and begot Methuselah.
22 Atabadwa Metusela, Enoki anayenda ndi Mulungu zaka 300 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
And Enoch walked with God after he begot Methuselah three hundred years, and begot sons and daughters.
23 Zaka zonse za Enoki zinali 365.
And all the days of Enoch were three hundred sixty-five years.
24 Enoki anayenda ndi Mulungu; ndipo iye sanaonekenso chifukwa Mulungu anamutenga.
And Enoch walked with God, and he was not, for God took him.
25 Pamene Metusela anali ndi zaka 187, anabereka Lameki.
And Methuselah lived a hundred eighty-seven years, and begot Lamech.
26 Ndipo atabadwa Lameki, Metusela anakhala ndi moyo zaka zina 782 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
And Methuselah lived seven hundred eighty-two years after he begot Lamech, and begot sons and daughters.
27 Zaka zonse za Metusela zinali 969, ndipo anamwalira.
And all the days of Methuselah were nine hundred sixty-nine years, and he died.
28 Pamene Lameki anali ndi zaka 182, anabereka mwana wamwamuna.
And Lamech lived a hundred eighty-two years, and begot a son.
29 Ndipo anamutcha Nowa ndipo anati, “Iyeyu adzatipumulitsa ku ntchito zathu zolemetsazi, zolima nthaka imene Yehova anayitemberera.”
And he called his name Noah, saying, This same shall comfort us in our work and in the toil of our hands, because of the ground which Jehovah has cursed.
30 Atabadwa Nowa, Lameki anakhala zaka zina 595 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
And Lamech lived five hundred ninety-five years after he begot Noah, and begot sons and daughters.
31 Zaka zonse za Lameki zinali 777, ndipo kenaka anamwalira.
And all the days of Lamech were seven hundred seventy-seven years, and he died.
32 Pamene Nowa anali ndi zaka 500, anabereka Semu, Hamu ndi Yafeti.
And Noah was five hundred years old. And Noah begot Shem, Ham, and Japheth.

< Genesis 5 >