< Genesis 3 >

1 Ndipo njoka inali yochenjera kuposa nyama yakuthengo iliyonse imene Yehova Mulungu anapanga. Njokayo inati kwa mkaziyo, “Kodi Mulungu ananenadi kuti, ‘Inu musadye zipatso za mtengo uliwonse mʼmundamu?’”
Now the serpent was more cunning than any beast of the field which Jehovah God had made. And he said to the woman, Yea, has God said, Ye shall not eat of any tree of the garden?
2 Mkaziyo anati kwa njokayo, “Tikhoza kudya zipatso za mʼmitengo ya mʼmundawu,
And the woman said to the serpent, Of the fruit of the trees of the garden we may eat,
3 koma Mulungu anati, ‘Musadye zipatso za mu mtengo umene uli pakati pa munda, ndipo musadzawukhudze kuti mungadzafe.’”
but of the fruit of the tree which is in the midst of the garden, God has said, Ye shall not eat of it, nor shall ye touch it, lest ye die.
4 “Ndithudi simudzafa,” inatero njokayo kwa mkaziyo.
And the serpent said to the woman, Ye shall not surely die.
5 “Pakuti Mulungu akudziwa kuti tsiku limene mudzadye zipatso za mu mtengowo, maso anu adzatsekuka, ndipo mudzakhala ngati Mulungu, wodziwa zabwino ndi zoyipa.”
For God knows that in the day ye eat of it, then your eyes shall be opened, and ye shall be as gods, knowing good and evil.
6 Pamene mkaziyo anaona kuti mtengowo unali wabwino kudya ndi wokongola ndi kuti unali wopatsa nzeru, anatengako zipatso zake nadya. Zina anamupatsako mwamuna wake amene anali naye pomwepo ndipo naye anadyanso.
And when the woman saw that the tree was good for food, and that it was a delight to the eyes, and that the tree was to be desired to make wise, she took of the fruit of it, and ate. And she also gave to her husband with her, and he ate.
7 Kenaka maso awo anatsekuka, ndipo anazindikira kuti anali maliseche. Choncho anasoka masamba a mkuyu nadzipangira zovala.
And the eyes of them both were opened, and they knew that they were naked. And they sewed fig leaves together, and made themselves aprons.
8 Kenaka munthu uja ndi mkazi wake anamva mtswatswa wa Yehova Mulungu akuyendayenda mʼmundamo madzulo a tsikulo, ndipo iwo anabisala pamaso pa Yehova Mulungu pakati pa mitengo ya mʼmundamo.
And they heard the voice of Jehovah God walking in the garden in the cool of the day. And the man and his wife hid themselves from the presence of Jehovah God amongst the trees of the garden.
9 Yehova Mulungu anayitana munthu uja kuti, “Uli kuti?”
And Jehovah God called to the man, and said to him, Where are thou?
10 Iye anayankha, “Ndinakumvani mʼmundamo, ndipo ndimaopa chifukwa ndinali maliseche; choncho ndinabisala.”
And he said, I heard thy voice in the garden, and I was afraid, because I was naked. And I hid myself.
11 Ndipo anamufunsa, “Ndani anakuwuza kuti uli maliseche? Kodi wadya zipatso za mtengo umene ndinakulamulira kuti usadye?”
And he said, Who told thee that thou was naked? Have thou eaten of the tree, of which I commanded thee that thou should not eat?
12 Koma munthu uja anati, “Mkazi amene munandipatsa kuti ndizikhala nayeyu anandipatsako chipatso cha mtengowo ndipo ndinadya.”
And the man said, The woman whom thou gave to be with me, she gave me of the tree, and I ate.
13 Tsono Yehova Mulungu anati kwa mkaziyo, “Wachitachi nʼchiyani?” Mkaziyo anati, “Njoka inandinamiza, ndipo ndinadya.”
And Jehovah God said to the woman, What is this thou have done? And the woman said, The serpent beguiled me, and I ate.
14 Choncho Yehova Mulungu anati kwa njokayo, “Popeza wachita zimenezi, “Ndiwe wotembereredwa kuposa ziweto zonse ndi nyama zakuthengo zonse. Udzayenda chafufumimba ndipo udzadya fumbi masiku onse a moyo wako.
And Jehovah God said to the serpent, Because thou have done this, cursed are thou above all cattle, and above every beast of the field. Upon thy belly thou shall go, and dust thou shall eat all the days of thy life.
15 Ndipo ndidzayika chidani pakati pa iwe ndi mkaziyo, pakati pa mbewu yako ndi mbewu yake; Iye adzaphwanya mutu wako ndipo iwe udzaluma chidendene chake.”
And I will put enmity between thee and the woman, and between thy seed and her seed. He shall bruise thy head, and thou shall bruise his heel.
16 Kwa mkaziyo Iye anati, “Ndidzachulukitsa ululu wako kwambiri pamene uli ndi pakati; ndipo udzamva ululu pa nthawi yako yobereka ana. Udzakhumba mwamuna wako, ndipo adzakulamulira.”
To the woman he said, I will greatly multiply thy pain and thy childbearing, in pain thou shall bring forth children. And thy desire shall be to thy husband, and he shall rule over thee.
17 Ndipo kwa Adamu Mulungu anati, “Chifukwa wamvera mkazi wako ndipo wadya zipatso za mu mtengo umene ndinakulamulira kuti, ‘Usadye.’ “Nthaka yatembereredwa chifukwa cha iwe, movutikira udzadya zochokera mʼnthakamo masiku onse a moyo wako.
And to Adam he said, Because thou have hearkened to the voice of thy wife, and have eaten of the tree, of which I commanded thee, saying, Thou shall not eat of it, cursed is the ground for thy sake. In toil thou shall eat of it all the days of thy life.
18 Mʼnthakamo mudzamera minga ndi nthula ndipo udzadya zomera zakuthengo.
Also, thorns and thistles it shall bring forth to thee, and thou shall eat the herb of the field.
19 Kuti upeze chakudya udzayenera kukhetsa thukuta, mpaka utabwerera ku nthaka pakuti unachokera kumeneko; pakuti ndiwe fumbi ku fumbi komweko udzabwerera.”
In the sweat of thy face thou shall eat bread, till thou return to the ground, for out of it thou were taken. For thou are dust, and to dust thou shall return.
20 Munthu uja anatcha mkazi wake Hava, chifukwa iyeyu adzakhala mayi wa anthu onse amoyo.
And the man called his wife's name Eve, because she was the mother of all living.
21 Yehova Mulungu anapangira Adamu ndi mkazi wake zovala zachikopa ndipo anawaveka.
And Jehovah God made for Adam and for his wife coats of skins, and clothed them.
22 Ndipo Yehova Mulungu anati, “Tsopano munthu uyu wasanduka mmodzi wa ife, wodziwa zabwino ndi zoyipa. Iyeyu asaloledwe kutambasula dzanja ndi kutengako zipatso za mu mtengo wopatsa moyo uja kuti angakhale ndi moyo mpaka muyaya.”
And Jehovah God said, Behold, the man has become as one of us, to know good and evil, and now, lest he put forth his hand, and take also of the tree of life, and eat, and live forever-
23 Kotero Yehova Mulungu anatulutsa Adamu Mʼmunda wa Edeni kuti azilima mʼnthaka imene anachokera.
therefore Jehovah God sent him forth from the garden of Eden, to till the ground from where he was taken.
24 Atamuthamangitsa munthu uja, Yehova anayika Akerubi mbali ya kummawa kwa Munda wa Edeni ndi lupanga lamoto limene limayendayenda ponsepo, kuteteza njira ya ku mtengo wopatsa moyo.
So he drove out the man. And he placed at the east of the garden of Eden the cherubim, and the flame of a sword which turned every way, to guard the way of the tree of life.

< Genesis 3 >