< Genesis 2 >

1 Motero kumwamba, dziko lapansi ndi zonse za mʼmenemo zinatha kulengedwa monga mwa kuchuluka kwawo.
And the heavens and the earth were finished, and all the host of them.
2 Pofika tsiku lachisanu ndi chiwiri Mulungu anamaliza ntchito zonse zimene ankagwira ndipo pa tsiku lachisanu ndi chiwiri anapumula ku ntchito zake zonse.
And on the seventh day God finished his work which he had made, and he rested on the seventh day from all his work which he had made.
3 Ndipo Mulungu anadalitsa tsiku lachisanu ndi chiwiri nalipatula, chifukwa pa tsiku limeneli Iye anapumula ku ntchito yonse yolenga imene anayigwira.
And God blessed the seventh day, and hallowed it, because in it he rested from all his work which God had created and made.
4 Mbiri ya momwe kumwamba ndi dziko lapansi zinalengedwera pa tsiku lija Yehova Mulungu ankazilenga ndi iyi: Yehova Mulungu atapanga dziko lapansi ndi kumwamba,
These are the generations of the heavens and of the earth when they were created, in the day that Jehovah God made earth and heaven.
5 zitsamba zinali zisanamere ndipo chomera chilichonse chinali chisanamerenso popeza Yehova Mulungu anali asanagwetse mvula pa dziko lapansi. Panalibe munthu wolima nthaka,
And no plant of the field was yet in the earth, and no herb of the field had yet sprung up, for Jehovah God had not caused it to rain upon the earth. And there was not a man to till the ground,
6 koma kasupe ankatuluka mʼnthaka ndi kuthirira pa dziko lonse.
but there went up a mist from the earth, and watered the whole face of the ground.
7 Tsono Yehova Mulungu anawumba munthu kuchokera ku dothi nawuziramo mpweya wamoyo mʼmphuno mwake ndipo munthuyo anakhala wamoyo.
And Jehovah God formed man of the dust of the ground, and breathed into his nostrils the breath of life, and man became a living soul.
8 Kenaka Yehova Mulungu anatsekula munda wa Edeni chakummawa; kumeneko anayikako munthu amene anamupanga uja.
And Jehovah God planted a garden eastward, in Eden, and there he put the man whom he had formed.
9 Ndipo Yehova Mulungu anameretsa mʼmundamo mitengo ya mitundu yonse. Inali mitengo yokongola ndi ya zipatso zokoma. Pakati pa munda uja panali mtengo wopatsa moyo ndi mtengo wopatsa nzeru zodziwitsa chabwino ndi choyipa.
And out of the ground Jehovah God made to grow every tree that is pleasant to the sight, and good for food, also the tree of life in the midst of the garden, and the tree of the knowledge of good and evil.
10 Mtsinje wothirira mundawo unkatuluka mu Edeni; kuchokera apo unkagawikana kukhala mitsinje inayi.
And a river went out of Eden to water the garden, and from there it was divided, and became four heads.
11 Dzina la mtsinje woyamba ndi Pisoni; uwu umazungulira dziko lonse la Havila, kumene kuli golide.
The name of the first is Pishon. That is it which encompasses the whole land of Havilah, where there is gold.
12 (Golide wa ku dziko ili ndi wabwino. Kulinso miyala yokongola ya bedola ndi onikisi).
And the gold of that land is good. There is bdellium and the onyx stone.
13 Dzina la mtsinje wachiwiri ndi Gihoni; uwu umazungulira dziko lonse la Kusi.
And the name of the second river is Gihon. The same is it which encompasses the whole land of Cush.
14 Dzina la mtsinje wachitatu ndi Tigirisi; umayenda chakummawa kwa Asiriya. Ndipo mtsinje wachinayi ndi Yufurate.
And the name of the third river is Hiddekel. That is it which goes in front of Assyria. And the fourth river is the Euphrates.
15 Yehova Mulungu anatenga munthu uja ndi kumuyika mʼmunda wa Edeni kuti awulime ndi kuwusamalira.
And Jehovah God took the man, and put him into the garden of Eden to dress it and to keep it.
16 Ndipo Yehova Mulungu analamula munthu uja kuti, “Uzidya zipatso za mu mtengo wina uliwonse mʼmundamu;
And Jehovah God commanded the man, saying, Of every tree of the garden thou may freely eat,
17 koma usadye zipatso za mu mtengo wodziwitsa chabwino ndi choyipa, popeza ukadzadya za mu mtengowu udzafa ndithu.”
but of the tree of the knowledge of good and evil, thou shall not eat of it. For in the day that thou eat of it thou shall surely die.
18 Ndipo Yehova Mulungu anati, “Sibwino kuti munthu akhale yekha. Ndidzamupangira mnzake womuthandiza.”
And Jehovah God said, It is not good that the man should be alone, I will make a help meet for him.
19 Kenaka Yehova Mulungu anawumba ndi dothi nyama zonse zakuthengo ndi mbalame zonse zamlengalenga. Ndipo Iye anapita nazo kwa munthu uja kuti akazipatse mayina; ndipo dzina lililonse limene Adamu anapereka ku chamoyo chilichonse, lomwelo linakhala dzina lake.
And out of the ground Jehovah God formed every beast of the field, and every bird of the heavens, and brought them to the man to see what he would call them, and whatever the man called every living creature, that was the name of it.
20 Choncho Adamu anazitcha mayina ziweto zonse, mbalame zamlengalenga ndi nyama zakuthengo zonse. Komabe munthu uja analibe mnzake womuthandiza.
And the man gave names to all cattle, and to the birds of the heavens, and to every beast of the field, but for man there was not found a help meet for him.
21 Tsono Yehova Mulungu anamugonetsa munthu uja tulo tofa nato; ali mtulo chomwecho, Mulungu anachotsa imodzi mwa nthiti zake ndi kutseka pamalopo ndi mnofu.
And Jehovah God caused a deep sleep to fall upon the man, and he slept. And God took one of his ribs, and closed up the flesh in place of it.
22 Motero Yehova Mulungu anapanga mkazi ndi nthiti ija imene anatenga kwa munthu uja nabwera naye kwa iye.
And the rib, which Jehovah God had taken from the man, he made a woman, and brought her to the man.
23 Munthu uja anati, “Uyu ndiye fupa lochokera ku mafupa anga ndi mnofu wochokera ku mnofu wanga; adzatchedwa ‘mkazi,’ popeza wachokera mwa mwamuna.”
And the man said, This is now bone of my bones, and flesh of my flesh. She shall be called Woman, because she was taken out of Man.
24 Nʼchifukwa chake, mwamuna amasiya abambo ndi amayi ake nakaphatikana ndi mkazi wake ndipo awiriwo amakhala thupi limodzi.
Therefore a man shall leave his father and his mother, and shall cling to his wife, and the two shall be one flesh.
25 Munthu uja ndi mkazi wakeyo, onse awiri anali maliseche ndipo analibe manyazi.
And they were both naked, the man and his wife, and were not ashamed.

< Genesis 2 >