< Genesis 4 >

1 Adamu anagona malo amodzi ndi Hava mkazi wake ndipo mkaziyo anakhala woyembekezera nabala Kaini, ndipo anati, “Ndi thandizo la Yehova ndapeza mwana wamwamuna.”
And the man knew Eve his wife, and she conceived, and bore Cain, and said, I have gotten a man from Jehovah.
2 Kenaka anabereka mʼbale wake Abele. Abele anali woweta nkhosa ndipo Kaini anali mlimi.
And again she bore his brother Abel. And Abel was a keeper of sheep, but Cain was a tiller of the ground.
3 Patapita nthawi, Kaini anatenga zipatso za ku munda nakazipereka kwa Yehova monga nsembe.
And in process of time it came to pass, that Cain brought an offering to Jehovah of the fruit of the ground.
4 Nayenso Abele anatenga ana ankhosa oyamba kubadwa pamodzi ndi mafuta ake nakazipereka ngati nsembe kwa Yehova. Yehova anakondwera ndi Abele ndi nsembe yake.
And Abel, he also brought of the firstlings of his flock and of the fat of it. And Jehovah had respect to Abel and to his offering,
5 Koma sanakondwere ndi Kaini ndi nsembe yake. Kotero Kaini anakwiya kwambiri ndipo nkhope yake inagwa.
but he did not have respect to Cain and to his offering. And Cain was very angry, and his countenance fell.
6 Choncho Yehova anati kwa Kaini, “Chifukwa chiyani wakwiya ndipo bwanji nkhope yako yagwa?
And Jehovah said to Cain, Why are thou angry? And why has thy countenance fallen?
7 Ukanachita zabwino sindikanakulandira kodi? Koma tsopano wachita zoyipa ndipo tchimo likukudikira pa khomo pako, likufuna kukugwira; koma iwe uyenera kugonjetsa tchimolo.”
If thou do well, shall thou not be accepted? And if thou do not well, sin crouches at the door. Its desire shall be for thee, and thou shall rule over it.
8 Tsiku lina Kaini anati kwa mʼbale wake Abele, “Tiye tipite ku munda.” Ndipo ali ku mundako, Kaini anawukira mʼbale wake namupha.
And Cain told Abel his brother. And it came to pass, when they were in the field, that Cain rose up against Abel his brother, and killed him.
9 Ndipo Yehova anamufunsa Kaini kuti, “Ali kuti mʼbale wako Abele?” Iye anayankha kuti, “Sindikudziwa. Kodi ine ndine wosunga mʼbale wanga?”
And Jehovah said to Cain, Where is Abel thy brother? And he said, I know not. Am I my brother's keeper?
10 Yehova anati, “Kodi wachita chiyani? Tamvera! Magazi a mʼbale wako akulirira kwa Ine kuchokera mʼnthaka.
And he said, What have thou done? The voice of thy brother's blood cries to me from the ground.
11 Ndipo tsopano ndiwe wotembereredwa ndipo wachotsedwa mʼdziko limene nthaka yake inatsekula pakamwa pake kulandira magazi a mʼbale wako amene unakhetsa.
And now cursed are thou from the ground, which has opened its mouth to receive thy brother's blood from thy hand.
12 Udzalima munda koma nthakayo sidzakupatsanso zokolola zake. Udzakhala wosakhazikika; womangoyendayenda pa dziko lapansi.”
When thou till the ground, it shall not henceforth yield to thee its strength. A fugitive and a wanderer thou shall be on the earth.
13 Kaini anati kwa Yehova, “Chilango changa ndi chachikulu kuposera mphamvu zanga.
And Cain said to Jehovah, My punishment is greater than I can bear.
14 Lero mukundipirikitsa pa dziko ndi pamaso panu; ndidzakhala wosakhazikika, woyendayenda, ndipo aliyense amene adzandipeze adzandipha.”
Behold, thou have driven me out this day from the face of the ground, and I shall be hid from thy face, and I shall be a fugitive and a wanderer in the earth. And it shall come to pass, that whoever finds me shall slay me.
15 Koma Yehova anamuwuza kuti, “Sizidzatero ayi; aliyense amene adzaphe Kaini adzalangidwa ndi kulipiritsidwa kasanu ndi kawiri.” Pamenepo Yehova anayika chizindikiro pa Kaini kuti aliyense womupeza asamuphe.
And Jehovah said to him, Therefore whoever kills Cain, vengeance shall be taken on him sevenfold. And Jehovah appointed a sign for Cain, lest any who finds him should smite him.
16 Ndipo Kaini anachoka pamaso pa Yehova nakakhala ku dziko la Nodi, kummawa kwa Edeni.
And Cain went out from the presence of Jehovah, and dwelt in the land of Nod, on the east of Eden.
17 Kaini anagona malo amodzi ndi mkazi wake ndipo mkaziyo anakhala woyembekezera nabala Enoki. Kaini nthawi imeneyo nʼkuti akumanga mzinda ndipo anawutcha dzina la mwana wake Enoki.
And Cain knew his wife, and she conceived, and bore Enoch. And Cain built a city, and called the name of the city after the name of his son, Enoch.
18 Enoki anabereka Iradi; Iradi anabereka Mehuyaeli, ndipo Mehuyaeli anabereka Metusela, ndipo Metusela anabereka Lameki.
And to Enoch was born Irad, and Irad begot Mehujael, and Mehujael begot Methushael, and Methushael begot Lamech.
19 Lameki anakwatira akazi awiri, wina dzina lake linali Ada ndi winayo dzina lake linali Zila.
And Lamech took to him two wives. The name of the one was Adah, and the name of the other Zillah.
20 Ada anabereka Yabala; iyeyu anali kholo la onse okhala mʼmatenti ndi oweta ziweto.
And Adah bore Jabal. He was the father of such as dwell in tents and have cattle.
21 Dzina la mʼbale wake linali Yubala; iyeyu anali kholo la onse oyimba zeze ndi chitoliro.
And his brother's name was Jubal. He was the father of all such as handle the harp and pipe.
22 Zila nayenso anali ndi mwana wamwamuna, dzina lake Tubala-Kaini. Iyeyu anali kholo la amisiri onse osula zida za mkuwa ndi chitsulo. Mlongo wake wa Tubala-Kaini anali Naama.
And Zillah, she also bore Tubal-cain, the forger of every cutting instrument of brass and iron. And the sister of Tubal-cain was Naamah.
23 Lameki anawuza akazi akewo kuti, “Ada ndi Zila, ndimvereni; inu akazi anga imvani mawu anga. Ine ndinapha munthu chifukwa anandipweteka. Ndinapha mnyamatayo chifukwa anandimenya.
And Lamech said to his wives, Adah and Zillah, Hear my voice, ye wives of Lamech, hearken to my speech. For I have killed a man for wounding me, and a young man for bruising me.
24 Ngati wopha Kaini amulipsira kasanu nʼkawiri, ndiye kuti wopha ine Lameki adzamulipsira kokwanira 77.”
If Cain shall be avenged seven fold, truly Lamech seventy-seven fold.
25 Adamu anagonanso malo amodzi ndi mkazi wake, ndipo anabereka mwana wamwamuna namutcha Seti, kutanthauza kuti, “Mulungu wandipatsa mwana wina mʼmalo mwa Abele, popeza Kaini anamupha.”
And Adam knew his wife again, and she bore a son, and called his name Seth. For, she said, God has appointed for me another seed instead of Abel, for Cain killed him.
26 Seti naye anali ndi mwana wa mwamuna, ndipo anamutcha Enosi. Pa nthawi imeneyi anthu anayamba kupemphera mʼdzina la Yehova.
And to Seth, to him also there was born a son, and he called his name Enosh. Then men began to call upon the name of Jehovah.

< Genesis 4 >