< Eksodo 17 >

1 Gulu lonse la Aisraeli linachoka ku chipululu cha Sini, ndi kumayenda malo ndi malo monga momwe anawalamulira Yehova. Iwo anamanga misasa yawo ku Refidimu koma kunalibe madzi woti anthu onse ndi kumwa.
And all the congregation of the sons of Israel journeyed from the wilderness of Sin, by their journeys, according to the commandment of Jehovah, and encamped in Rephidim. And there was no water for the people to drink.
2 Kotero iwo anakangana ndi Mose nati, “Tipatse madzi akumwa.” Mose anayankha kuti, “Chifukwa chiyani mukukangana ndi ine? Chifukwa chiyani mukumuyesa Yehova?”
Therefore the people contended with Moses, and said, Give us water that we may drink. And Moses said to them, Why do ye contend with me? Why do ye challenge Jehovah?
3 Koma anthu anali ndi ludzu pamenepo ndipo anangʼungʼudza pamaso pa Mose namufunsa kuti, “Kodi nʼchifukwa chiyani unatitulutsa mʼdziko la Igupto kuti ife, ana athu pamodzi ndi ziweto zathu tife ndi ludzu?”
And the people thirsted there for water. And the people murmured against Moses, and said, Why have thou brought us up out of Egypt, to kill us and our sons and our cattle with thirst?
4 Ndipo Mose anapemphera kwa Yehova, “Kodi ndichite chiyani ndi anthu awa? Iwo atsala pangʼono kundigenda ndi miyala.”
And Moses cried to Jehovah, saying, What shall I do to this people? They are almost ready to stone me.
5 Yehova anati kwa Mose, “Pita patsogolo pa anthuwo. Tenga ndodo imene unamenyera nyanja ya Nailo pamodzi ndi akuluakulu ena a Israeli ndi kunyamuka.
And Jehovah said to Moses, Pass on before the people, and take with thee from the elders of Israel, and thy rod, with which thou smote the river, take in thy hand, and go.
6 Ine ndidzayima patsogolo pako pafupi ndi thanthwe la ku Horebu. Ukamenye thanthwelo, madzi adzatuluka kuti anthu amwe.” Motero Mose anachita zimenezi pamaso pa akuluakulu a Israeli.
Behold, I will stand before thee there upon the rock in Horeb, and thou shall smite the rock, and there shall come water out of it, that the people may drink. And Moses did so in the sight of the elders of Israel.
7 Ndipo iye anatcha malowo Masa ndi Meriba chifukwa Aisraeli anakangana ndi kuyesa Yehova ponena kuti, “Kodi pakati pathu pali Yehova kapena palibe?”
And he called the name of the place Massah and Meribah, because of the contending of the sons of Israel, and because they challenged Jehovah, saying, Is Jehovah among us, or not?
8 Amaleki anabwera ku Refidimu kudzamenyana ndi Aisraeli.
Then Amalek came, and fought with Israel in Rephidim.
9 Mose anati kwa Yoswa, “Sankha amuna amphamvu ndipo upite ukamenyane ndi Amaleki. Mawa ndidzayima pamwamba pa phiri nditagwira ndodo ya Mulungu.”
And Moses said to Joshua, Choose us out men, and go out, fight with Amalek. Tomorrow I will stand on the top of the hill with the rod of God in my hand.
10 Ndipo Yoswa anachitadi monga Mose anamulamulira. Iye anapita kukamenyana ndi Aamaleki ndipo Mose, Aaroni ndi Huri anapita pamwamba pa phiri.
So Joshua did as Moses had said to him, and fought with Amalek. And Moses, Aaron, and Hur went up to the top of the hill.
11 Mose ankati akakweza manja ake, Aisraeli amapambana, koma akatsitsa manja akewo Amaleki amapambana.
And it came to pass, when Moses held up his hand, that Israel prevailed, and when he let down his hand, Amalek prevailed.
12 Manja a Mose atatopa, Aaroni ndi Huri anatenga mwala ndi kuyika pansi ndipo Mose anakhalapo. Aaroni ndi Huri anagwirizitsa manja a Mose wina mbali ina winanso mbali ina. Choncho manja a Mose analimba mpaka kulowa kwa dzuwa.
But Moses' hands were heavy. And they took a stone, and put it under him, and he sat on it. and Aaron and Hur held up his hands, the one on the one side, and the other on the other side. And his hands were steady until the going down of the sun.
13 Kotero Yoswa anagonjetsa asilikali ankhondo a Amaleki ndi lupanga.
And Joshua weakened Amalek and his people with the edge of the sword.
14 Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Lemba izi mʼbuku kuti zidzakumbukirike ndipo uwonetsetse kuti Yoswa amve zimenezi, chifukwa Ine ndidzafafaniziratu Amaleki pa dziko lapansi, kotero kuti palibe amene adzawakumbukire.”
And Jehovah said to Moses, Write this for a memorial in a book, and rehearse it in the ears of Joshua: that I will utterly blot out the remembrance of Amalek from under heaven.
15 Mose anamanga guwa lansembe ndipo analitcha Yehova Chipambano Changa (Yehova Nisi).
And Moses built an altar, and called the name of it Jehovah-nissi.
16 Ndipo anati, “Kwezani mbendera ya Yehova. Yehova adzachitabe nkhondo ndi mibado yonse ya Aamaleki.”
And he said, Jehovah has sworn, Jehovah will have war with Amalek from generation to generation.

< Eksodo 17 >