< Eksodo 16 >

1 Pambuyo pake gulu lonse la Aisraeli linachoka ku Elimu, ndipo pa tsiku la khumi ndi chisanu mwezi wachiwiri chichokere mʼdziko la Igupto, anafika ku chipululu cha Sini chimene chinali pakati pa Elimu ndi Sinai.
And they took their journey from Elim. And all the congregation of the sons of Israel came to the wilderness of Sin, which is between Elim and Sinai, on the fifteenth day of the second month after their departing out of the land of Egypt.
2 Mʼchipululumo gulu lonse linadandaulira Mose ndi Aaroni
And the whole congregation of the sons of Israel murmured against Moses and against Aaron in the wilderness.
3 kuti, “Kukanakhala bwino Yehova akanatiphera mʼdziko la Igupto! Kumeneko timadya nyama ndi buledi mpaka kukhuta, koma inu mwabwera nafe ku chipululu kudzapha mpingo wonsewu ndi njala!”
And the sons of Israel said to them, Would that we had died by the hand of Jehovah in the land of Egypt, when we sat by the flesh-pots, when we ate bread to the full, for ye have brought us forth into this wilderness, to kill this whole assembly with hunger.
4 Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Ine ndidzakupatsani buledi wogwa kuchokera kumwamba ngati mvula. Anthu azituluka tsiku lililonse kukatola buledi wokwanira tsiku limenelo. Ine ndidzawayesa mʼnjira imeneyi kuti ndione ngati adzatsatira malangizo anga.
Then Jehovah said to Moses, Behold, I will rain bread from heaven for you, and the people shall go out and gather a day's portion every day, that I may prove them, whether they will walk in my law, or not.
5 Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi, pamene azidzakonza buledi amene abwera naye, adzapeza kuti ndi wokwanira masiku awiri.”
And it shall come to pass on the sixth day, that they shall prepare that which they bring in, and it shall be twice as much as they gather daily.
6 Kotero Mose ndi Aaroni anati kwa Aisraeli onse, “Nthawi yamadzulo inu mudzadziwa kuti ndi Yehova amene anakutulutsani mʼdziko la Igupto.
And Moses and Aaron said to all the sons of Israel, At evening, then ye shall know that Jehovah has brought you out from the land of Egypt,
7 Ndipo mmawa mudzaona ulemerero wa Yehova pakuti wamva kudandaula kwanu. Kodi ife ndi yani kuti muzitidandaulira?”
and in the morning, then ye shall see the glory of Jehovah, for he hears your murmurings against Jehovah. And what are we, that ye murmur against us?
8 Mose anati, “Yehova adzakupatsani nyama madzulo aliwonse ndi buledi mmawa uliwonse kuti mukhute chifukwa Iye wamva madandawulo anu. Nanga ife ndi yani? Kudandaula kwanu simudandaulira ife, koma Yehova.”
And Moses said, This shall be when Jehovah shall give you flesh to eat in the evening, and bread to the full in the morning, for that Jehovah hears your murmurings which ye murmur against him. And what are we? Your murmurings are not against us, but against Jehovah.
9 Kenaka Mose anawuza Aaroni kuti, “Uza gulu lonse la Aisraeli kuti, ‘Bwerani pamaso pa Yehova pakuti wamva kudandaula kwanu.’”
And Moses said to Aaron, Say to all the congregation of the sons of Israel, Come near before Jehovah, for he has heard your murmurings.
10 Pamene Aaroni amayankhula ndi gulu lonse la Aisraeli, iwo anayangʼana ku chipululu, ndipo ulemerero wa Yehova umaoneka mu mtambo.
And it came to pass, as Aaron spoke to the whole congregation of the sons of Israel, that they looked toward the wilderness, and, behold, the glory of Jehovah appeared in the cloud.
11 Yehova anati kwa Mose,
And Jehovah spoke to Moses, saying,
12 “Ine ndamva kudandaula kwa Aisraeli. Awuze kuti, ‘Madzulo mudzadya nyama ndipo mmawa mudzakhuta buledi. Pamenepo mudzadziwa kuti ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
I have heard the murmurings of the sons of Israel. Speak to them, saying, At evening ye shall eat flesh, and in the morning ye shall be filled with bread. And ye shall know that I am Jehovah your God.
13 Madzulo amenewo panatuluka zinziri zimene zinali ponseponse pa misasa yawo, ndipo mmawa panali mame kuzungulira misasa yawo.
And it came to pass at evening, that the quails came up, and covered the camp. And in the morning the dew lay round about the camp,
14 Mamewo atachoka, pa nthaka mʼchipululumo panaoneka tinthu tina topyapyala komanso totuwa ngati chipale.
and when the dew that lay was gone up, behold, upon the face of the wilderness a small round thing, small as the hoarfrost on the ground.
15 Aisraeli atationa anafunsana wina ndi mnzake nati, “Kodi timeneti nʼchiyani?” Popeza sanatidziwe. Mose anawawuza kuti, “Uyu ndi buledi amene Yehova wakupatsani kuti mudye.
And when the sons of Israel saw it, they said one to another, What is it? For they knew not what it was. And Moses said to them, It is the bread which Jehovah has given you to eat.
16 Yehova walamula kuti, ‘Aliyense atole zomukwanira kudya, malita awiri pa munthu mmodzi molingana ndi chiwerengero cha anthu amene ali mu tenti yanu.’”
This is the thing which Jehovah has commanded, Gather ye of it every man according to his eating, an omer a head. According to the number of your persons, ye shall take it, every man for those who are in his tent.
17 Aisraeli anachita zonse anawawuza. Ena anatola zambiri ena zochepa.
And the sons of Israel did so, and gathered, some more, some less.
18 Ndipo iwo atayeza ndi muyeso wa malita awiri, iye amene anatola zambiri sizinamutsalireko ndipo amene anatola pangʼono sizinamuchepere. Aliyense anatola zomukwanira kudya.
And when they measured it with an omer, he who gathered much had nothing over, and he who gathered little had no lack; they gathered every man according to his eating.
19 Ndipo Mose anawawuza kuti, “Wina aliyense asasunge mpaka mmawa.”
And Moses said to them, Let no man leave of it till the morning.
20 Komabe ena sanamvere Mose, anasungako mpaka mmawa. Koma mmawa mwake tonse tinali mphutsi zokhazokha. Kotero Mose anawapsera mtima.
Notwithstanding they did not hearken to Moses, but some of them left of it until the morning, and it bred worms, and became foul, and Moses was angry with them.
21 Mmawa uliwonse aliyense amatola zimene amazifuna, ndipo dzuwa likatentha zimasungunuka.
And they gathered it morning by morning, every man according to his eating. And when the sun grew hot, it melted.
22 Tsiku lachisanu ndi chimodzi anatuta malita anayi munthu aliyense, ndipo atsogoleri a mpingo wonse anabwera kudzawuza Mose za zimenezi.
And it came to pass, that on the sixth day they gathered twice as much bread, two omers for each one. And all the rulers of the congregation came and told Moses.
23 Iye anawawuza kuti, “Izi ndi zimene Yehova analamula, ‘Mawa ndi tsiku lopumula, Sabata Loyera la Yehova, choncho wotchani ndi kuphika zimene mukufuna. Sungani zotsala mpaka mmawa.’”
And he said to them, This is that which Jehovah has spoken, Tomorrow is a solemn rest, a holy sabbath to Jehovah. Bake that which ye will bake, and boil that which ye will boil, and all that remains over lay up for you to be kept until the morning.
24 Choncho anasunga mpaka mmawa monga Mose anawalamulira, ndipo sananunkhe kapena kuchita mphutsi.
And they laid it up till the morning, as Moses bade, and it did not become foul, neither was there any worm in it.
25 Mose anati, “Idyani lero chifukwa lero ndi Sabata la Yehova. Lero simukapeza chilichonse kunjaku.
And Moses said, Eat that today, for today is a sabbath to Jehovah. Today ye shall not find it in the field.
26 Muzitola chakudya masiku asanu ndi limodzi koma tsiku la chisanu ndi chiwiri ndi la Sabata, simukapeza chilichonse kunjaku.”
Six days ye shall gather it, but on the seventh day is the sabbath, there shall be none in it.
27 Komabe anthu ena anapita kuti akatole chakudya tsiku lachisanu ndi chiwiri, koma sanapeze kanthu.
And it came to pass on the seventh day, that some of the people went out to gather, and they found none.
28 Ndipo Yehova anafunsa Mose nati, “Kodi inu muzipitirira kukana kusunga malamulo ndi malangizo anga mpaka liti?
And Jehovah said to Moses, How long do ye refuse to keep my commandments and my laws?
29 Taonani, popeza Yehova wakupatsani Sabata nʼchifukwa chake tsiku lachisanu ndi chimodzi amakupatsani chakudya cha masiku awiri. Aliyense azikhala pamene ali pa tsiku lachisanu ndi chiwiri, pasapezeke wotuluka kunja.”
See, because Jehovah has given you the sabbath, therefore he gives you on the sixth day the bread of two days. Abide ye every man in his place. Let no man go out of his place on the seventh day.
30 Kotero anthu anapuma tsiku lachisanu ndi chiwiri.
So the people rested on the seventh day.
31 Aisraeli anatchula chakudyacho Mana. Chakudyacho chinkaoneka ngati mbewu zamapira, zoyera. Ndipo chinkakoma ngati chothira uchi.
And the house of Israel called the name of it Manna. And it was like coriander seed, white, and the taste of it was like wafers with honey.
32 Mose anati, “Chimene Yehova walamula ndi ichi: ‘Tengani muyeso wa malita awiri a mana ndi kusungira mibado imene ikubwera, kuti iwo adzaone chakudya chimene Ine ndinakupatsani kuti mudye mʼchipululu pamene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto.’”
And Moses said, This is the thing which Jehovah has commanded. Let an omerful of it be kept throughout your generations, that they may see the bread with which I fed you in the wilderness, when I brought you forth from the land of Egypt.
33 Choncho Mose anati kwa Aaroni, “Tenga mtsuko ndipo uyikemo malita awiri a mana. Ndipo uyike manawo pamaso pa Yehova kusungira mibado imene ikubwera.”
And Moses said to Aaron, Take a pot, and put an omerful of manna in it, and lay it up before Jehovah, to be kept throughout your generations.
34 Monga momwe Yehova analamulira Mose, Aaroni anayika mtsuko uja pafupi ndi bokosi la Chipangano kuti manawo asungike.
As Jehovah commanded Moses, so Aaron laid it up before the Testimony, to be kept.
35 Aisraeli anadya mana zaka 40, mpaka pamene anafika ku dziko kumene amati akakhazikeko. Iwo anadya mana mpaka pamene anafika mʼmalire a Kanaani.
And the sons of Israel ate the manna forty years, until they came to a land inhabited. They ate the manna until they came to the borders of the land of Canaan.
36 (Malita awiri amafanana ndi gawo lakhumi la efa).
Now an omer is the tenth part of an ephah.

< Eksodo 16 >