< Eksodo 14 >

1 Kenaka Yehova anati kwa Mose,
And Jehovah spoke to Moses, saying,
2 “Uza Aisraeli abwerere ndi kukagona pafupi ndi Pihahiroti, pakati pa Migidoli ndi nyanja. Inu mumange zithando mʼmbali mwa nyanja moyangʼanana ndi Baala-Zefoni.
Speak to the sons of Israel, that they turn back and encamp before Pihahiroth, between Migdol and the sea, before Baal-zephon. Ye shall encamp opposite it by the sea.
3 Farao adzaganiza kuti ‘Aisraeli asokonezeka nʼkumangozungulirazungulira mu dzikomo, chipululu chitawazinga.’
And Pharaoh will say of the sons of Israel, They are entangled in the land; the wilderness has shut them in.
4 Ndidzawumitsa mtima wa Farao ndipo adzathamangira Aisraeliwo. Choncho ndikadzagonjetsa Farao ndi gulu lake lonse la nkhondo, Ine ndidzalemekezedwa.” Choncho Aisraeli aja anachita zimenezi.
And I will harden Pharaoh's heart, and he shall follow after them, and I will get for me honor upon Pharaoh, and upon all his army, and the Egyptians shall know that I am Jehovah. And they did so.
5 Farao, mfumu ya Igupto atamva kuti anthu aja athawa, iye pamodzi ndi nduna zake anasintha maganizo awo pa Israeli ndipo anati, “Ife tachita chiyani? Tawalola Aisraeli kuti apite ndi kuleka kutitumikira?”
And it was told the king of Egypt that the people were fled. And the heart of Pharaoh and of his servants was changed towards the people, and they said, What is this we have done, that we have let Israel go from serving us?
6 Choncho anakonzetsa galeta lake ndipo ananyamuka pamodzi ndi ankhondo ake.
And he made ready his chariot, and took his people with him.
7 Iye anatenga magaleta 600 abwino kwambiri pamodzi ndi magaleta ena a dziko la Igupto. Anatenganso akuluakulu onse ankhondo.
And he took six hundred chosen chariots, and all the chariots of Egypt, and captains over all of them.
8 Yehova anawumitsa mtima wa Farao mfumu ya dziko la Igupto, kotero iye anawathamangira Aisraeli amene ankachoka mʼdzikomo mosavutika.
And Jehovah hardened the heart of Pharaoh king of Egypt, and he pursued after the sons of Israel, for the sons of Israel went out with a high hand.
9 Aigupto aja (kutanthauza akavalo ndi magaleta onse a Farao, okwera akavalowo pamodzi ndi gulu lonse la nkhondo) analondola Aisraeli aja ndipo anakawapeza pamalo pamene anamanga zithando paja, mʼmbali mwa nyanja, pafupi ndi Pihahiroti, moyangʼanana ndi Baala-Zefoni.
And the Egyptians pursued after them, all the horses and chariots of Pharaoh, and his horsemen, and his army, and overtook them encamping by the sea, beside Pihahiroth, before Baal-zephon.
10 Tsono Farao anayandikira. Ndipo Aisraeli ataona kuti Aigupto akuwatsatira, anachita mantha aakulu ndipo anafuwula kwa Yehova.
And when Pharaoh drew near, the sons of Israel lifted up their eyes, and, behold, the Egyptians were marching after them, and they were very afraid. And the sons of Israel cried out to Jehovah,
11 Iwo anafunsa Mose kuti, “Kodi nʼchifukwa chakuti kunalibe manda ku dziko la Igupto kuti iwe utibweretse muno mʼchipululu kuti tidzafe? Chimene watichitachi nʼchiyani, kutitulutsa mʼdziko la Igupto?
and they said to Moses, Because there were no graves in Egypt, have thou taken us away to die in the wilderness? Why have thou dealt thus with us, to bring us forth out of Egypt?
12 Kodi sindizo zimene tinakuwuza mʼdziko la Igupto? Ife tinati, ‘Tileke titumikire Aigupto?’ Zikanatikomera kutumikira Aigupto kulekana ndi kufa mʼchipululu muno.”
Is not this the word that we spoke to thee in Egypt, saying, Let us alone, that we may serve the Egyptians? For it were better for us to serve the Egyptians, than that we should die in the wilderness.
13 Mose anayankha anthu kuti, “Musachite mantha. Imani, ndipo muone chipulumutso chimene Yehova akuchitireni lero. Aigupto amene mukuwaona lerowa simudzawaonanso.
And Moses said to the people, Fear ye not. Stand still, and see the salvation of Jehovah, which he will work for you today, for the Egyptians whom ye have seen today, ye shall see them again no more forever.
14 Yehova adzakumenyerani nkhondo. Inu mungokhala chete.”
Jehovah will fight for you, and ye shall keep silent.
15 Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Chifukwa chiyani ukufuwulira kwa ine? Uwuze Aisraeli aziyenda.
And Jehovah said to Moses, Why do thou cry to me? Speak to the sons of Israel, that they go forward.
16 Nyamula ndodo yako ndi kutambasula dzanja lako kuloza ku nyanja, kugawa madzi kuti Aisraeli awoloke powuma.
And lift thou up thy rod, and stretch out thy hand over the sea, and divide it, and the sons of Israel shall go into the midst of the sea on dry ground.
17 Ine ndidzawumitsa mitima ya Aigupto kotero kuti adzatsatirabe Aisraeli. Ndipo ine ndikadzagonjetsa Farao ndi asilikali ake onse ankhondo, okwera magaleta ndi akavalo, ndidzapeza ulemerero.
And I, behold, I will harden the hearts of the Egyptians, and they shall go in after them, and I will get for me honor upon Pharaoh, and upon all his army, upon his chariots, and upon his horsemen.
18 Aigupto adzadziwa kuti Ine ndine Yehova akadzaona mmene ndipambanire Farao ndi magaleta ndi owayendetsa ake.”
And the Egyptians shall know that I am Jehovah, when I have gotten for me honor upon Pharaoh, upon his chariots, and upon his horsemen.
19 Ndipo mngelo wa Mulungu amene amayenda patsogolo pa gulu lankhondo la Israeli anachoka ndi kupita kumbuyo kwawo. Chipilala cha mtambo chinasunthanso kuchoka kutsogolo ndi kupita kumbuyo kwawo.
And the agent of God, who went before the camp of Israel, moved and went behind them, and the pillar of cloud moved from before them, and stood behind them.
20 Choncho mtambowo unakhala pakati pa asilikali ankhondo a dziko la Igupto ndi a dziko la Israeli. Choncho panali mdima motero kuti magulu awiri ankhondowa sanathe kuyandikizana usiku wonse.
And it came between the camp of Egypt and the camp of Israel. And the cloud and the darkness was there, yet it gave light by night. And the one did not come near the other all the night.
21 Kenaka Mose anatambalitsa dzanja lake pa nyanja, ndipo Yehova pogwiritsa ntchito mphepo yamphamvu ya kummawa imene inawomba usiku wonse anabweza madzi ndi kuwumitsa nyanja ija. Choncho nyanja ija inagawanika.
And Moses stretched out his hand over the sea, and Jehovah caused the sea to go back by a strong east wind all the night, and made the sea dry land, and the waters were divided.
22 Ndipo Aisraeli anawoloka pakati pa nyanja powuma, madzi atasanduka khoma kumanja ndi kumanzere kwawo.
And the sons of Israel went into the midst of the sea upon the dry ground, and the waters were a wall to them on their right hand, and on their left.
23 Aigupto onse, Farao, ndi onse okwera pa magaleta ndi akavalo anawalondola ndipo analowa mʼmadzi.
And the Egyptians pursued, and went in after them into the midst of the sea, all Pharaoh's horses, his chariots, and his horsemen.
24 Kutatsala pangʼono kucha, Yehova ali mu chipilala chamoto ndi chamtambo, anayangʼana asilikali ankhondo a Igupto ndipo anabweretsa chisokonezo pakati pawo.
And it came to pass in the morning watch, that Jehovah looked forth upon the army of the Egyptians through the pillar of fire and of cloud, and troubled the army of the Egyptians.
25 Yehova anamanga matayala a magaleta kotero kuti ankavutika kuyenda. Ndipo Aigupto anati, “Tiyeni tiwathawe Aisraeli! Yehova akuwamenyera nkhondo kulimbana nafe.”
And he took off their chariot wheels, and they drove them with difficulty, so that the Egyptians said, Let us flee from the face of Israel, for Jehovah fights for them against the Egyptians.
26 Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Tambasula dzanja lako pa nyanja kuti madzi amize Aigupto ndi magaleta awo ndi okwera pa akavalo.”
And Jehovah said to Moses, Stretch out thy hand over the sea, that the waters may come again upon the Egyptians, upon their chariots, and upon their horsemen.
27 Mose anatambasula dzanja lake pa nyanja, ndipo mmene kumacha nyanja inabwerera mʼmalo mwake. Aigupto pothawa anakumana nayo, ndipo Yehova anawakokera mʼnyanja momwemo.
And Moses stretched forth his hand over the sea, and the sea returned to its strength when the morning appeared, and the Egyptians fled against it, and Jehovah overthrew the Egyptians in the midst of the sea.
28 Madzi anabwerera ndi kumiza magaleta ndi okwera akavalo, asilikali ankhondo onse amene anatsatira Aisraeli mʼnyanja, palibe ndi mmodzi yemwe amene anapulumuka.
And the waters returned, and covered the chariots, and the horsemen, even all the army of Pharaoh who went in after them into the sea, there remained not so much as one of them.
29 Koma Aisraeli aja anawoloka nyanja pansi pali powuma, madzi atachita khoma kumanja ndi kumanzere kwawo.
But the sons of Israel walked upon dry land in the midst of the sea, and the waters were a wall to them on their right hand, and on their left.
30 Tsiku limeneli Yehova anapulumutsa Israeli mʼmanja mwa Aigupto ndipo Israeli anaona Aigupto ali lambalamba mʼmbali mwa nyanja atafa
Thus Jehovah saved Israel that day out of the hand of the Egyptians, and Israel saw the Egyptians dead upon the sea-shore.
31 Choncho Aisraeli anaona dzanja lamphamvu la Yehova limene linagonjetsa Aigupto aja, ndipo iwo anaopa Yehova ndi kumukhulupirira pamodzi ndi mtumiki wake Mose.
And Israel saw the great work which Jehovah did upon the Egyptians. And the people feared Jehovah, and they believed in Jehovah, and in his servant Moses.

< Eksodo 14 >