< Eksodo 18 >

1 Yetero wansembe wa ku Midiyani amenenso anali mpongozi wa Mose, anamva zonse zimene Mulungu anachitira Mose ndi anthu ake a Aisraeli ndi mmene Yehova anawatulutsira mʼdziko la Igupto.
Now Jethro, the priest of Midian, Moses' father-in-law, heard of all that God had done for Moses, and for Israel his people, how that Jehovah had brought Israel out of Egypt.
2 Mose atamubweza Zipora, mkazi wake, Yetero, mpongozi wake anamulandira
And Jethro, Moses' father-in-law, took Zipporah, Moses' wife, after he had sent her away,
3 mwana wake wamkaziyo pamodzi ndi ana ake aamuna awiri. Mose anamupatsa mwana wachisamba dzina loti Geresomu popeza anati, “Ndakhala mlendo mʼdziko lachilendo.”
and her two sons, of whom the name of the one was Gershom, for he said, I have been a sojourner in a foreign land.
4 Ndipo mwana wake wachiwiri anamupatsa dzina loti Eliezara, pakuti anati, “Mulungu wa makolo anga anali thandizo langa. Iye anandipulumutsa ku lupanga la Farao.”
And the name of the other was Eliezer, for he said, The God of my father was my help, and delivered me from the sword of Pharaoh.
5 Yetero, mpongozi wa Mose pamodzi ndi ana a Mose aamuna awiri ndi mkazi wake anabwera kwa Mose ku chipululu pa phiri la Mulungu kumene Mose anamanga misasa.
And Jethro, Moses' father-in-law, came with his sons and his wife to Moses into the wilderness where he was encamped, at the mount of God.
6 Yetero anali atatumiza uthenga kwa Mose kuti, “Ine Yetero, mpongozi wako, ndikubwera ndi mkazi wako ndi ana ake awiri.”
And he said to Moses, I, thy father-in-law Jethro, have come to thee, and thy wife, and her two sons with her.
7 Kotero Mose anatuluka kukakumana ndi mpongozi wake ndipo anawerama ndi kupsompsona. Atalonjerana anakalowa mu tenti
And Moses went out to meet his father-in-law, and did obeisance, and kissed him. And they asked each other of their welfare, and they came into the tent.
8 Mose anafotokozera mpongozi wake zonse zimene Yehova anamuchita Farao ndi Aigupto chifukwa cha Israeli komanso zowawa zonse anakumana nazo mʼnjira. Mose anafotokozanso momwe Yehova anawapulumutsira.
And Moses told his father-in-law all that Jehovah had done to Pharaoh and to the Egyptians for Israel's sake, all the travail that had come upon them by the way, and how Jehovah delivered them.
9 Yetero anakondwa kwambiri atamva zabwino zonse zimene Yehova anachitira Aisraeli powapulumutsa mʼdzanja la Aigupto.
And Jethro rejoiced for all the goodness which Jehovah had done to Israel, in that he had delivered them out of the hand of the Egyptians.
10 Iye anati, “Alemekezeke Yehova amene wakupulumutsani mʼdzanja la Aigupto ndi Farao. Wapulumutsanso anthuwa mʼdzanja la Aigupto.
And Jethro said, Blessed be Jehovah, who has delivered you out of the hand of the Egyptians, and out of the hand of Pharaoh, who has delivered the people from under the hand of the Egyptians.
11 Tsopano ndikudziwa kuti Yehova ndi wopambana milungu ina yonse, pakuti anachita izi kwa amene ananyoza Israeli.”
Now I know that Jehovah is greater than all gods, yea, in the thing wherein they dealt proudly against them.
12 Ndipo Yetero, mpongozi wa Mose anapereka nsembe yopsereza ndi nsembe zina kwa Mulungu. Aaroni ndi akuluakulu onse a Israeli anabwera kudzadya chakudya pamodzi ndi mpongozi wa Mose pamaso pa Mulungu.
And Jethro, Moses' father-in-law, took a burnt offering and sacrifices for God. And Aaron came, and all the elders of Israel, to eat bread with Moses' father-in-law before God.
13 Mmawa mwake, Mose anakhala pa mpando kuti aweruze milandu ya anthu. Anthu anayima momuzungulira kuyambira mmawa mpaka madzulo.
And it came to pass on the morrow, that Moses sat to judge the people, and the people stood about Moses from the morning to the evening.
14 Mpongozi wa Mose ataona zonse zimene iye amawachitira anthu anati, “Nʼchiyani chimene mukuwachitira anthuwa? Nʼchifukwa chiyani mulipo nokha woweruza, pamene anthu onsewa ayimirira kuyambira mmawa mpaka madzulo?”
And when Moses' father-in-law saw all that he did to the people, he said, What is this thing that thou do to the people? Why do thou sit by thyself, and all the people stand about thee from morning to evening?
15 Mose anamuyankha kuti, “Chifukwa anthuwa anabwera kwa ine kudzafunsa zimene Mulungu akufuna.
And Moses said to his father-in-law, Because the people come to me to inquire of God.
16 Ngati munthu akangana ndi mʼbale wake, onse awiri amabwera kwa ine, ndipo ine ndimawaweruza. Ndimawawuzanso malamulo a Mulungu ndi malangizo ake.”
When they have a matter, they come to me, and I judge between a man and his neighbor. And I make them know the statutes of God, and his laws.
17 Mpongozi wa Mose anayankha kuti, “Zimene mukuchitazi si zabwino.
And Moses' father-in-law said to him, The thing that thou do is not good.
18 Ntchitoyi ndi yayikulu kuposa mphamvu zanu. Inu simungathe kuyigwira nokha. Inu pamodzi ndi anthuwa amene amabwera kwa inu mudzatopa.
Thou will surely wear away, both thou, and this people that is with thee, for the thing is too heavy for thee. Thou are not able to perform it thyself alone.
19 Tsono tamverani ndikulangizeni, ndipo Mulungu akhale nanu. Inu muziwayimirira anthuwa pamaso pa Mulungu, ndipo mikangano yawo muzibwera nayo kwa Iye.
Hearken now to my voice. I will give thee counsel, and God be with thee. Be thou for the people toward God, and bring thou the cases to God.
20 Aphunzitseni mawu ndi malangizo a Mulungu. Aphunzitseni mmene ayenera kukhalira ndi zimene ayenera kuchita.
And thou shall teach them the statutes and the laws, and shall show them the way in which they must walk, and the work that they must do.
21 Koma sankhani amuna odziwa ntchito yawo, anthu owopa Mulungu, anthu odalirika amene amadana ndi kupeza phindu mwachinyengo. Tsono muwayike kuti akhale oyangʼanira anthu motere: atsogoleri a anthu 1,000, ena a anthu 100, ena a anthu 50 ndi ena a anthu khumi.
Moreover thou shall provide out of all the people able men, such as fear God, men of truth, hating unjust gain, and place such over them, to be rulers of thousands, rulers of hundreds, rulers of fifties, and rulers of tens,
22 Tsono amenewa aziweruza anthu nthawi zonse. Mlandu uliwonse waukulu azibwera nawo kwa inu, koma mlandu waungʼono aziweruza okha. Izi zidzachititsa kuti ntchito yanu ipepuke, popeza mudzagwira ntchito mothandizana.
and let them judge the people at all seasons. And it shall be, that every great matter they shall bring to thee, but every small matter they shall judge themselves. So shall it be easier for thyself, and they shall bear the burden with thee.
23 Ngati mutsatira malangizowa monga mmene Mulungu wakulamulirani ndiye kuti simudzafowoka ndipo anthu onsewa adzapita kwawo mu mtendere.”
If thou shall do this thing, and God command thee so, then thou shall be able to endure, and all this people also shall go to their place in peace.
24 Mose anamvera mpongozi wake ndi kuchita zonse zimene iye ananena.
So Moses hearkened to the voice of his father-in-law, and did all that he had said.
25 Iye anasankha amuna odziwa bwino ntchito zawo ndipo anawayika kuti akhale atsogoleri, oyangʼanira anthu motere: atsogoleri a anthu 1,000, ena a anthu 500, ena a anthu makumi asanu ndi ena a anthu khumi.
And Moses chose able men out of all Israel, and made them heads over the people, rulers of thousands, rulers of hundreds, rulers of fifties, and rulers of tens,
26 Iwowa ankaweruza anthu nthawi zonse. Milandu yovuta ankabwera nayo kwa Mose, koma yosavuta ankayiweruza okha.
and they judged the people at all seasons. The hard cases they brought to Moses, but every small matter they judged themselves.
27 Kenaka Mose analola kuti mpongozi wake, Yetero anyamuke kubwerera ku dziko la kwawo.
And Moses let his father-in-law depart, and he went his way into his own land.

< Eksodo 18 >