< Mlaliki 1 >

1 Mawu a Mlaliki, mwana wa Davide, mfumu ya ku Yerusalemu:
The words of the Preacher, the son of David, king in Jerusalem.
2 “Zopandapake! Zopandapake!” atero Mlaliki. “Zopandapake kotheratu! Zopandapake.”
Vanity of vanities, says the Preacher, vanity of vanities, all is vanity.
3 Kodi munthu amapindulanji pa ntchito zake zonse zimene amasautsidwa nazo pansi pano?
What profit has man from all his labor in which he labors under the sun?
4 Mibado imabwera ndipo mibado imapita, koma dziko lapansi limakhalapobe nthawi zonse.
One generation goes, and another generation comes, but the earth abides forever.
5 Dzuwa limatuluka ndipo dzuwa limalowa ndipo limapita mwamsanga kumene limatulukira.
The sun also arises, and the sun goes down and hastens to its place where it arises.
6 Mphepo imawombera cha kummwera ndi kukhotera cha kumpoto; imawomba mozungulirazungulira, kumangobwererabwerera komwe yachokera.
The wind goes toward the south, and turns around to the north. It turns around continually in its course, and the wind returns again to its circuits.
7 Mitsinje yonse imakathira ku nyanja, koma nyanjayo sidzaza; kumene madziwo amachokera, amabwereranso komweko.
All the rivers run into the sea, yet the sea is not full. To the place from where the rivers come, there they go again.
8 Zinthu zonse ndi zotopetsa, kutopetsa kwake ndi kosaneneka. Maso satopa ndi kuona kapena khutu kukwaniritsidwa ndi kumva.
All things are full of weariness, man cannot utter it. The eye is not satisfied with seeing, nor the ear filled with hearing.
9 Zomwe zinalipo kale zidzakhalaponso, zomwe zinachitika kale zidzachitikanso. Ndiye kuti chatsopano palibiretu pansi pano.
That which has been is that which shall be, and that which has been done is that which shall be done. And there is no new thing under the sun.
10 Kodi chilipo chinthu chimene wina anganene kuti, “Taona! Ichi ndiye chatsopano?” Chinalipo kale, kalekale; chinalipo ife kulibe.
Is there a thing of which it may be said, See, this is new? It has been long ago, in the ages which were before us.
11 Anthu akale sakumbukiridwa, ngakhale amene adzabwera mʼtsogolomu sadzakumbukiridwa ndi iwo amene adzabwere pambuyo pawo.
There is no remembrance of the former things, nor shall there be any remembrance of the latter that are to come, among those who shall come after.
12 Ine, Mlalikine, ndinali mfumu ya Israeli mu Yerusalemu.
I the Preacher was king over Israel in Jerusalem.
13 Ndinayika mtima wanga pophunzira ndi kufunafuna mwa nzeru zinthu zonse zimene zimachitika pansi pa thambo. Ndi ntchito yolemetsa ndithu imene Mulungu anayipereka kwa anthu!
And I applied my heart to seek and to search out by wisdom concerning all that is done under heaven. It is a great tribulation that God has given to the sons of men to be exercised therewith.
14 Ine ndaona zinthu zonse zochitika pansi pano; zinthu zonsezo ndi zopandapake, nʼkungodzivuta chabe.
I have seen all the works that are done under the sun, and, behold, all is vanity and a striving after wind.
15 Chinthu chokhota sichingathe kuwongoledwa; chimene palibe sichingathe kuwerengedwa.
That which is crooked cannot be made straight, and that which is wanting cannot be numbered.
16 Ine ndinaganiza mu mtima mwanga, “Taona, ine ndakula ndi kukhala wa nzeru zochuluka kupambana aliyense amene analamulirapo Yerusalemu ndisanabadwe; ndaphunzira nzeru zochuluka ndi luntha.”
I communed with my own heart, saying, Lo, I have gotten for me great wisdom above all who were before me in Jerusalem. Yea, my heart has had great experience of wisdom and knowledge.
17 Ndipo ndinadzipereka kuti ndithe kumvetsa kuti nzeru nʼchiyani, misala nʼchiyani, uchitsiru nʼchiyani, koma ndinazindikira ichi, kuti kuteronso nʼkungodzivuta chabe.
And I applied my heart to know wisdom, and to know madness and folly. I perceived that this also was a striving after wind.
18 Pakuti nzeru zochuluka zimabweretsa chisoni chochulukanso: chidziwitso chochuluka, zowawa zochulukanso.
For in much wisdom is much grief, and he who increases knowledge increases sorrow.

< Mlaliki 1 >