< Deuteronomo 8 >

1 Samalani potsata lamulo lililonse limene ndikukupatsani lero, kuti mukhale ndi moyo ndi kuchulukana kuti mulande ndi kulowa mʼdziko limene Yehova analumbira kuti adzapereka kwa makolo anu.
All the commandment which I command thee this day ye shall observe to do, that ye may live, and multiply, and go in and possess the land which Jehovah swore to your fathers.
2 Kumbukirani mmene Yehova Mulungu wanu anakutsogolerani njira yonse mʼchipululu kwa zaka makumi anayi, kukutsitsani ndi kukuyesani kuti adziwe chimene chinali mu mtima mwanu ngati mungathe kusunga malamulo ake kapena ayi.
And thou shall remember all the way which Jehovah thy God has led thee these forty years in the wilderness, that he might humble thee, to prove thee, to know what was in thy heart, whether thou would keep his commandments, or not.
3 Iye anakutsitsani nakumvetsani njala kenaka nʼkukudyetsani mana amene anali osadziwika kwa inu kapena makolo anu, kuti akuphunzitseni kuti munthu sadzakhala ndi moyo ndi chakudya chokha koma ndi mawu aliwonse ochokera mʼkamwa mwa Yehova.
And he humbled thee, and allowed thee to hunger, and fed thee with manna, which thou knew not, neither did thy fathers know, that he might make thee know that man does not live by bread alone, but man lives by everything that proceeds out of the mouth of Jehovah.
4 Mʼzaka makumi anayi zimenezi, zovala zanu sizinangʼambike ndipo mapazi anu sanatupe.
Thy raiment did not grow old upon thee, neither did thy foot swell, these forty years.
5 Tsono dziwani mu mtima mwanu kuti monga abambo amalanga mwana wawo, momwemonso Yehova Mulungu wanu amakulangani.
And thou shall consider in thy heart, that, as a man chastens his son, so Jehovah thy God chastens thee.
6 Samalirani malamulo a Yehova Mulungu wanu, kuyenda mʼnjira yake ndi kumuopa Iye.
And thou shall keep the commandments of Jehovah thy God, to walk in his ways, and to fear him.
7 Pakuti Yehova Mulungu wanu akukulowetsani mʼdziko labwino, dziko lokhala ndi mitsinje ndi mathawale a madzi, akasupe oyenderera mu zigwa ndi mʼmapiri,
For Jehovah thy God brings thee into a good land, a land of brooks of water, of fountains and springs, flowing forth in valleys and hills;
8 dziko lokhala ndi tirigu ndi barele, mpesa ndi mitengo ya mkuyu, makangadza, mafuta a olivi ndi uchi;
a land of wheat and barley, and vines and fig trees and pomegranates, a land of olive trees and honey,
9 dziko limene buledi sadzasowa ndipo simudzasowa chilichonse; dziko limene miyala yake ndi chitsulo ndipo ku mapiri ake mukhoza kukumbako mkuwa.
a land in which thou shall eat bread without scarceness. Thou shall not lack anything in it, a land whose stones are iron, and out of whose hills thou may dig copper.
10 Mukadya ndi kukhuta, yamikani Yehova Mulungu wanu chifukwa cha dziko labwino limene wakupatsani.
And thou shall eat and be full, and thou shall bless Jehovah thy God for the good land which he has given thee.
11 Samalani kuopa kuti mungayiwale Yehova Mulungu wanu posasunga malamulo, zikhazikitso ndi malangizo ake amene ndikukupatsani lero,
Beware lest thou forget Jehovah thy God, in not keeping his commandments, and his ordinances, and his statutes, which I command thee this day.
12 kuopa kuti mukadya ndi kukhuta, mukamanga nyumba zabwino ndi kukhalamo,
Lest, when thou have eaten and are full, and have built goodly houses, and dwelt in it,
13 ndi pamene ngʼombe zanu ndi nkhosa zanu zaswana, ndi siliva ndi golide wanu wachuluka ndiponso kuti zonse zimene muli nazo zachuluka,
and when thy herds and thy flocks multiply, and thy silver and thy gold is multiplied, and all that thou have is multiplied,
14 mtima wanu udzayamba kunyada ndi kuyiwala Yehova Mulungu wanu, amene anakutulutsani ku Igupto, kukuchotsani ku dziko la ukapolo.
then thy heart be lifted up, and thou forget Jehovah thy God, who brought thee forth out of the land of Egypt, out of the house of bondage,
15 Iye anakutsogolerani kudutsa mʼchipululu chachikulu ndi chochititsa mantha, dziko lija la ludzu ndi lopanda madzi, lokhala ndi njoka zaululu ndi zinkhanira. Iye anatulutsa madzi kuchokera mʼthanthwe lowuma.
who led thee through the great and terrible wilderness-fiery serpents and scorpions, and thirsty ground where was no water-who brought thee forth water out of the rock of flint,
16 Iye anakupatsani mana kuti mudye mʼchipululu, zinthu zoti ngakhale makolo anu sanazidziwe, kuti akuchepetseni ndi kukuyesani ndipo kuti pa mapeto pake zikuyendereni bwino.
who fed thee in the wilderness with manna, which thy fathers did not know, that he might humble thee, and that he might prove thee, to do thee good at thy latter end.
17 Mu mtima mwanu mukhoza kuganiza kuti, “Mphamvu zanga ndi kulimbika kwa dzanja langa ndi zimene zandilemeretsa chonchi.”
And lest thou say in thy heart, My power and the might of my hand has gotten me this wealth.
18 Koma kumbukirani Yehova Mulungu chifukwa ndi amene amakupatsani mphamvu zopezera chuma chimenechi kuti atsimikize pangano limene analumbira kwa makolo anu, monga liliri lero lino.
But thou shall remember Jehovah thy God, for it is he who gives thee power to get wealth, that he may establish his covenant which he swore to thy fathers, as at this day.
19 Ine ndine mboni yokutsutsani lero lino, kuti mukayiwala Yehova Mulungu wanu ndi kutsata milungu ina nʼkumayigwadira, mudzawonongeka ndithu.
And it shall be, if thou shall forget Jehovah thy God, and walk after other gods, and serve them, and worship them, I testify against you this day that ye shall surely perish.
20 Monga mitundu ina ya anthu imene Yehova anayiwononga pamaso panu, inunso mudzawonongedwa chifukwa chosamvera Yehova Mulungu wanu.
As the nations that Jehovah makes to perish before you, so shall ye perish, because ye would not hearken to the voice of Jehovah your God.

< Deuteronomo 8 >