< Deuteronomo 7 >

1 Pamene Yehova Mulungu wanu wakufikitsani mʼdziko limene mukukalowa ndi kulilanda ndi kuthamangitsa pamaso panu mitundu ya anthu iyi: Ahiti, Agirigasi, Aamori, Akanaani, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi; yomwe ndi mitundu isanu ndi iwiri yayikulu ndi yamphamvu kuposa inu;
When Jehovah thy God shall bring thee into the land where thou go to possess it, and shall cast out many nations before thee, the Hittite, and the Girgashite, and the Amorite, and the Canaanite, and the Perizzite, and the Hivite, and the Jebusite, seven nations greater and mightier than thou,
2 Yehova Mulungu wanu akadzawapereka mʼmanja mwanu, ndipo inu mukadzawagonjetsa, mudzawawononge kwathunthu. Musadzachite mgwirizano ndi anthuwo ndiponso musadzawachitire chifundo.
and when Jehovah thy God shall deliver them up before thee, and thou shall smite them, then thou shall utterly destroy them. Thou shall make no covenant with them, nor show mercy to them.
3 Musadzakwatirane nawo. Musadzapereke ana anu aakazi kwa ana awo aamuna kapena kutenga ana anu aamuna ndi kuwapereka kwa ana awo aakazi.
Neither shall thou make marriages with them. Thy daughter thou shall not give to his son, nor his daughter shall thou take to thy son.
4 Mukadzatero, iwo adzasocheretsa ana anu aamuna kuti asanditsatire ndi kutumikira milungu ina. Motero Yehova adzakukwiyirani ndi kukuwonongani mwachangu.
For he will turn away thy son from following me, that they may serve other gods, so the anger of Jehovah will be kindled against you, and he will destroy thee quickly.
5 Koma mukachite izi: Mukagumule maguwa awo ansembe, mukaswe miyala yawo yachipembedzo, mukadule mitengo yawo ya Asera, ndi kutentha mafano awo pa moto.
But thus shall ye deal with them: Ye shall break down their altars, and dash in pieces their pillars, and hew down their Asherim, and burn their graven images with fire.
6 Pakuti inu ndinu anthu opatulika kwa Yehova Mulungu wanu. Yehova Mulungu wanu anakusankhani pakati pa anthu onse pa dziko lapansi kuti mukhale ake, chuma chake cha mtengo wapatali.
For thou are a holy people to Jehovah thy God. Jehovah thy God has chosen thee to be a people for his own possession, above all peoples that are upon the face of the earth.
7 Yehova sanakukondeni chifukwa choti munali ochuluka kuposa ena pakuti inuyo ndiye munali ochepetsetsa mwa anthu onse.
Jehovah did not set his love upon you, nor choose you, because ye were more in number than any people, for ye were the fewest of all peoples,
8 Koma chifukwa chakuti Yehova anakukondani nasunga lumbiro lake limene analumbira kwa makolo anu. Ndi chifukwa chake anakutulutsani ndi mphamvu yake yopanda malire ndi kukupulumutsani ku dziko la ukapolo, kuchoka mʼmanja mwa Farao mfumu ya ku Igupto.
but because Jehovah loves you. And because he would keep the oath which he swore to your fathers, Jehovah has brought you out with a mighty hand, and redeemed you out of the house of bondage, from the hand of Pharaoh king of Egypt.
9 Choncho dziwani kuti Yehova Mulungu wanu, ndi Mulungu. Iye ndi Mulungu wokhulupirika, wosunga pangano lake la chikondi chosasinthika ku mibadomibado, kwa iwo amene amamukonda nasunga malamulo ake.
Know therefore that Jehovah thy God, he is God, the faithful God, who keeps covenant and loving kindness with those who love him and keep his commandments to a thousand generations,
10 Koma iwo amene amamuda adzawabwezera powawononga pamaso pawo; sadzachedwa kuwabwezera iwo amene amadana naye.
and repays those who hate him to their face, to destroy them. He will not be slack to him who hates him. He will repay him to his face.
11 Choncho muziyesetsa kusunga malamulo, malangizo ndi maphunziro amene ndikukulamulani lero lino kuti muchite.
Thou shall therefore keep the commandment, and the statutes, and the ordinances, which I command thee this day, to do them.
12 Mukamvera malamulo amenewa, ndi kusamala kuwatsata, ndiye kuti Yehova Mulungu wanu adzasunga pangano lake la chikondi chosasinthika ndi inu, monga analumbira kwa makolo anu.
And it shall come to pass, because ye hearken to these ordinances, and keep and do them, that Jehovah thy God will keep with thee the covenant and the loving kindness which he swore to thy fathers.
13 Iye adzakukondani nakudalitsani ndi kukuchulukitsani. Adzadalitsa chipatso cha mʼmimba mwanu, zokolola za mʼdziko mwanu, tirigu wanu, vinyo wanu ndi mafuta anu, ana angʼombe zanu ndi ana ankhosa zanu mʼdziko limene analumbirira kwa makolo anu kuti akupatseni inu.
And he will love thee, and bless thee, and multiply thee. He will also bless the fruit of thy body and the fruit of thy ground, thy grain and thy new wine and thine oil, the increase of thy cattle and the young of thy flock, in the land which he swore to thy fathers to give thee.
14 Inu mudzadalitsika kuposa mtundu wina uliwonse wa anthu ndipo palibe mwamuna kapena mkazi aliyense pakati panu amene adzakhale wosabereka. Ziweto zanu nazonso, sipadzapezeka zosabereka.
Thou shall be blessed above all peoples. There shall not be male or female barren among you, or among your cattle.
15 Yehova adzakupewetsani ku matenda aliwonse. Sadzakugwetserani matenda owopsa aja munawadziwa ku Igupto, koma adzawagwetsera pa odana nanu.
And Jehovah will take away from thee all sickness. And none of the evil diseases of Egypt, which thou know, will he put upon thee, but will lay them upon all those who hate thee.
16 Muwononge anthu onse amene Yehova Mulungu wanu awapereka kwa inu. Musawamvere chisoni ndipo musatumikire milungu yawo pakuti umenewo udzakhala msampha kwa inu.
And thou shall consume all the peoples that Jehovah thy God shall deliver to thee. Thine eye shall not pity them. Neither shall thou serve their gods, for that will be a snare to thee.
17 Mukhoza kunena kuti, “Anthu awa ndi amphamvu kuposa ifeyo. Nanga tingawapirikitse bwanji?”
If thou shall say in thy heart, These nations are more than I. How can I dispossess them?
18 Koma musachite nawo mantha, kumbukirani bwino zimene Yehova Mulungu wanu anachita ndi Farao pamodzi ndi Igupto yense.
Thou shall not be afraid of them. Thou shall remember well what Jehovah thy God did to Pharaoh, and to all Egypt:
19 Munadzionera nokha ndi maso anu mayesero aakulu, zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa, mphamvu yake yopanda malire imene Yehova Mulungu wanu anakutulutsirani. Yehova Mulungu adzachita zimenezo ndi anthu onse amene muwaopa tsopano.
the great trials which thine eyes saw, and the signs, and the wonders, and the mighty hand, and the outstretched arm by which Jehovah thy God brought thee out. So shall Jehovah thy God do to all the peoples of whom thou are afraid.
20 Kuwonjezera apo, Yehova Mulungu wanu adzatumiza mavu pakati pawo mpaka atamaliza onse amene adzakubisalirani.
Moreover Jehovah thy God will send the hornet among them until those who are left and hide themselves perish from before thee.
21 Musaopsedwe nawo pakuti Yehova Mulungu wanu, amene ali pakati panu, ndi Mulungu wamkulu ndi woopsa.
Thou shall not be frightened at them, for Jehovah thy God is in the midst of thee, a great God and awesome.
22 Yehova Mulungu wanu adzapirikitsa anthu a mitundu yonse pamaso panu, pangʼonopangʼono. Sadzakulolani kuti muwathe nthawi imodzi, kuti nyama zakuthengo zingadzaswane mokuzungulirani.
And Jehovah thy God will cast out those nations before thee little by little. Thou may not consume them at once, lest the beasts of the field increase upon thee.
23 Koma Yehova Mulungu wanu adzawapereka kwa inu, adzawasokoneza kufikira atawonongedwa.
But Jehovah thy God will deliver them up before thee, and will discomfit them with a great confusion until they be destroyed.
24 Iye adzapereka mafumu awo mʼdzanja lanu, ndipo adzafafaniza mayina awo pa dziko lapansi. Palibe amene adzalimbana nanu, inu mudzawawononga.
And he will deliver their kings into thy hand, and thou shall make their name to perish from under heaven. There shall no man be able to stand before thee, until thou have destroyed them.
25 Muwawotche pa moto mafano a milungu yawo. Musasirire siliva ndi golide amene ali pa mafanoyo. Musamutenge kuti akhale wanu chifukwa mukatero mudzakodwa naye ngati msampha, pakuti Yehova Mulungu wanu amanyansidwa nazo.
Ye shall burn the graven images of their gods with fire. Thou shall not covet the silver or the gold that is on them, nor take it to thee, lest thou be snared by it, for it is an abomination to Jehovah thy God.
26 Musabweretse chinthu chonyansa mʼnyumba mwanu kuopa kuwonongedwa ngati chonyasacho. Muziyipidwa ndi kunyansidwa nacho kwambiri pakuti chidzawonongedwanso.
And thou shall not bring an abomination into thy house, and become a devoted thing like it. Thou shall utterly detest it, and thou shall utterly abhor it, for it is a cursed thing.

< Deuteronomo 7 >