< Deuteronomo 5 >

1 Mose anayitanitsa Aisraeli onse nati: Tamverani inu Aisraeli, malangizo ndi malamulo amene ndikuwuzeni lero. Muwaphunzire ndi kuonetsetsa kuti mukuwatsata.
And Moses called to all Israel, and said to them, Hear, O Israel, the statutes and the ordinances which I speak in your ears this day, that ye may learn them, and observe to do them.
2 Yehova Mulungu wathu anachita pangano ndi ife ku Horebu.
Jehovah our God made a covenant with us in Horeb.
3 Yehova sanachite pangano ndi makolo athu koma ndi ife, tonse amene tili moyo lero.
Jehovah did not make this covenant with our fathers, but with us, even us, who are all of us here alive this day.
4 Yehova anayankhula nanu maso ndi maso kuchokera mʼmoto pa phiri paja.
Jehovah spoke with you face to face in the mount out of the midst of the fire
5 (Pa nthawi imeneyo ine ndinayimirira pakati pa Yehova ndi inu kuti ndikuwuzeni mawu a Yehova, chifukwa inu munkachita mantha ndi moto ndipo simunakwere ku phiri). Ndipo Iye anati:
(I stood between Jehovah and you at that time, to show you the word of Jehovah, for ye were afraid because of the fire, and did not go up onto the mount), saying,
6 “Ine ndine Yehova Mulungu wako amene ndinakutulutsa ku Igupto, mʼdziko la ukapolo.
I am Jehovah thy God who brought thee out of the land of Egypt, out of the house of bondage.
7 “Usakhale ndi milungu ina koma Ine ndekha.
Thou shall have no other gods before me.
8 “Usadzipangire chofanizira chinthu chilichonse chakumwamba kapena cha pa dziko lapansi kapena cha mʼmadzi a pansi pa dziko.
Thou shall not make to thee a graven image: any likeness that is in heaven above, or that is on the earth beneath, or that is in the water under the earth.
9 Usazigwadire kapena kuzipembedza, pakuti Ine Yehova Mulungu wako, ndine Mulungu wansanje, wolanga ana chifukwa cha tchimo la makolo awo mpaka mʼbado wachitatu ndi wachinayi wa iwo amene amadana nane,
Thou shall not bow down thyself to them, nor serve them, for I, Jehovah thy God, am a jealous God, visiting the iniquity of the fathers upon the sons, and upon the third and upon the fourth generation of those who hate me,
10 koma ndimaonetsa chikondi chosasinthika ku mibado miyandamiyanda ya anthu amene amandikonda ndi kusunga malamulo anga.
and showing loving kindness to thousands of those who love me and keep my commandments.
11 “Usagwiritse ntchito molakwika dzina la Yehova Mulungu wako, pakuti Yehova adzamutenga kukhala wochimwa aliyense amene akugwiritsa ntchito dzina lakelo molakwika.
Thou shall not take the name of Jehovah thy God in vain, for Jehovah will not hold him guiltless who takes his name in vain.
12 “Uzisunga tsiku la Sabata kuti likhale lopatulika monga momwe Yehova Mulungu wako anakulamulira.
Observe the sabbath day, to keep it holy, as Jehovah thy God commanded thee.
13 Uzigwira ntchito zako zonse masiku asanu ndi limodzi,
Six days thou shall labor, and do all thy work,
14 koma tsiku lachisanu ndi chiwiri ndi Sabata, tsiku loperekedwa kwa Yehova Mulungu wako. Tsiku limeneli musagwire ntchito iliyonse, inuyo kapena mwana wanu wamwamuna kapena mwana wanu wamkazi kapena wantchito wanu wamwamuna kapena mdzakazi wanu kapena ngʼombe yanu kapena bulu wanu kapena ziweto zanu kapena mlendo amene akukhala mʼmudzi mwanu, motero ndiye kuti wantchito wanu wamwamuna ndi wantchito wanu wamkazi adzapumula monga inuyo.
but the seventh day is a sabbath to Jehovah thy God: thou shall not do any work, thou, nor thy son, nor thy daughter, nor thy man-servant, nor thy maid-servant, nor thine ox, nor thy donkey, nor any of thy cattle, nor thy stranger that is within thy gates, that thy man-servant and thy maid-servant may rest as well as thou.
15 Kumbukira kuti unali kapolo ku Igupto ndipo Yehova Mulungu wako anakutulutsa kumeneko ndi dzanja lamphamvu ndi lotambasuka. Choncho Yehova Mulungu wako akukulamula kuti uzisunga tsiku la Sabata.
And thou shall remember that thou were a servant in the land of Egypt, and Jehovah thy God brought thee out from there by a mighty hand and by an outstretched arm, therefore Jehovah thy God commanded thee to keep the sabbath day.
16 “Lemekeza abambo ako ndi amayi ako monga Yehova Mulungu wako wakulamulira iwe kuti ukhale ndi moyo wautali ndi kuti zikuyendere bwino mʼdziko limene Yehova Mulungu wako akukupatsa.
Honor thy father and thy mother, as Jehovah thy God commanded thee, that thy days may be long, and that it may go well with thee in the land which Jehovah thy God gives thee.
17 “Usaphe.
Thou shall not murder.
18 “Usachite chigololo.
Neither shall thou commit adultery.
19 “Usabe.
Neither shall thou steal.
20 “Usapereke umboni womunamizira mnzako.
Neither shall thou bear false witness against thy neighbor.
21 “Usasirire mkazi wa mnzako. Usasirire nyumba ya mnzako kapena munda wake, wantchito wake wamwamuna kapena mdzakazi wake, ngʼombe yake kapena bulu wake, kapena chilichonse cha mnzako.”
Neither shall thou covet thy neighbor's wife. Neither shall thou desire thy neighbor's house, his field, or his man-servant, or his maid-servant, his ox, or his donkey, or anything that is thy neighbor's.
22 Awa ndi malamulo amene Yehova anayankhula ndi mawu okweza kwa gulu lanu lonse pa phiri paja mʼmoto, mtambo ndi mdima woopsa, sanawonjezerepo kanthu. Ndipo anawalemba pa mapale awiri amiyala ndi kundipatsa.
These words Jehovah spoke to all your assembly on the mount out of the midst of the fire, of the cloud, and of the thick darkness, with a great voice, and he added no more. And he wrote them upon two tablets of stone, and gave them to me.
23 Mutamva mawu kuchokera mu mdimawo, phiri lili moto lawilawi, atsogoleri onse a mafuko anu ndi akuluakulu anu anabwera kwa ine.
And it came to pass, when ye heard the voice out of the midst of the darkness, while the mountain was burning with fire, that ye came near to me, even all the heads of your tribes, and your elders.
24 Ndipo munati, “Yehova Mulungu wathu wationetsa ulemerero ndi ukulu wake, ndipo tamva mawu ake kuchokera mʼmoto. Lero taona kuti munthu akhoza kukhala ndi moyo ngakhale Mulungu atayankhula naye.
And ye said, Behold, Jehovah our God has shown us his glory and his greatness, and we have heard his voice out of the midst of the fire. We have seen this day that God speaks with man, and he lives.
25 Koma tsopano tife chifukwa chiyani? Moto waukuluwu utinyeketsa, ndipo tifa tikapitirirabe kumva mawu a Yehova Mulungu wathu.
Now therefore why should we die? For this great fire will consume us. If we hear the voice of Jehovah our God any more, then we shall die.
26 Pakuti ndi munthu uti wolengedwa amene anamvapo mawu a Mulungu wamoyo akuyankhula kuchokera mʼmoto, monga tachitiramu, nakhala ndi moyo?
For who is there of all flesh, who has heard the voice of the living God speaking out of the midst of the fire, as we have, and lived?
27 Pita pafupi kuti ukamvetsere zonse zimene Yehova Mulungu wathu akunena. Kenaka udzatiwuze chilichonse chimene Yehova Mulungu wathu akunena ndipo tidzamvera ndi kuchita.”
Go thou near, and hear all that Jehovah our God shall say. And speak thou to us all that Jehovah our God shall speak to thee, and we will hear it, and do it.
28 Yehova anakumvani pamene munkayankhula kwa ine ndipo Yehova anati kwa ine, “Ndamva zimene anthuwa anena kwa iwe. Chilichonse chimene anena ndi chabwino.
And Jehovah heard the voice of your words, when ye spoke to me. And Jehovah said to me, I have heard the voice of the words of this people, which they have spoken to thee. They have well said all that they have spoken.
29 Zikanakhala bwino akanakhala ndi mtima wondiopa ndi kusunga malamulo anga nthawi zonse kuti zinthu ziziwayendera bwino, iwowo pamodzi ndi ana awo kwamuyaya.
Oh that there were such a heart in them that they would fear me, and keep all my commandments always, that it might be well with them, and with their sons forever!
30 “Pita uwawuze kuti abwerere ku matenti awo.
Go say to them, Return ye to your tents.
31 Koma iwe ukhale kuno ndi ine kuti ndikupatse malamulo, malangizo ndi ziphunzitso zimene azitsatira mʼdziko limene ndiwapatse kuti alitenge.”
But as for thee, stand thou here by me, and I will speak to thee all the commandment, and the statutes, and the ordinances, which thou shall teach them, that they may do them in the land which I give them to possess it.
32 Choncho samalirani kuchita zimene Yehova Mulungu wanu akukulamulirani inu, musapatukire kudzanja lamanja kapena lamanzere.
Ye shall observe to do therefore as Jehovah your God has commanded you. Ye shall not turn aside to the right hand or to the left.
33 Muyende mʼnjira yonse imene Yehova Mulungu wanu wakulamulirani kuti mukhale ndi moyo ndi kupambana, ndi kuti masiku anu achuluke mʼdziko limene mudzatengelo.
Ye shall walk in all the way which Jehovah your God has commanded you, that ye may live, and that it may be well with you, and that ye may prolong your days in the land which ye shall possess.

< Deuteronomo 5 >