< Deuteronomo 16 >

1 Samalirani mwezi wa Abibu ndi kukondwerera Paska wa Yehova Mulungu wanu, chifukwa pa mwezi wa Abibu, usiku, Iye anakutulutsani mu Igupto.
Observe the month of Abib, and keep the Passover to Jehovah thy God, for in the month of Abib Jehovah thy God brought thee forth out of Egypt by night.
2 Mumuphere Yehova Mulungu wanu nsembe ya Paska, chiweto chochokera pa nkhosa zanu kapena ngʼombe zanu kumalo kumene Yehova adzasankha kuti akhazikeko dzina lake.
And thou shall sacrifice the Passover to Jehovah thy God, of the flock and the herd, in the place which Jehovah shall choose to cause his name to dwell there.
3 Musadyere pamodzi ndi buledi wopanga ndi yisiti, koma kwa masiku asanu ndi awiri muzidya buledi wopanda yisiti, buledi wa masautso, chifukwa munachoka ku Igupto mwamsangamsanga kuti pa masiku onse a moyo wanu muzikumbukira nthawi imene munanyamukira ku Igupto.
Thou shall eat no leavened bread with it. Seven days thou shall eat unleavened bread with it, even the bread of affliction, for thou came forth out of the land of Egypt in haste, that thou may remember the day when thou came forth out of the land of Egypt all the days of thy life.
4 Yisiti asapezeke kwa masiku asanu ndi awiri pa katundu wanu mʼdziko lanu lonse. Ndipo musasunge nyama imene mwapereka nsembe madzulo a tsiku loyamba mpaka mmawa.
And there shall be no leaven seen with thee in all thy borders seven days. Neither shall any of the flesh, which thou sacrifice the first day at evening, remain all night until the morning.
5 Musamangopereka nsembe ya Paska mu mzinda wina uliwonse umene Yehova Mulungu wanu wakupatsani,
Thou may not sacrifice the Passover within any of thy gates, which Jehovah thy God gives thee,
6 koma ku malo wokhawo amene Iye adzawasankhe kukhazikitsako Dzina lake. Kumeneko ndiye muzikapereka nsembe ya Paska madzulo, pamene dzuwa likulowa, pa tsiku lokumbukira kutuluka mu Igupto.
but at the place which Jehovah thy God shall choose to cause his name to dwell in, there thou shall sacrifice the Passover at evening, at the going down of the sun, at the season that thou came forth out of Egypt.
7 Muyiwotche ndi kuyidya pa malo pamene Yehova Mulungu wanu adzasankhe. Kenaka mmawa mubwerere ku matenti anu.
And thou shall roast and eat it in the place which Jehovah thy God shall choose, and thou shall turn in the morning, and go to thy tents.
8 Kwa masiku asanu ndi limodzi muzidya buledi wopanda yisiti ndipo pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzikhala ndi msonkhano wa Yehova Mulungu wanu ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
Six days thou shall eat unleavened bread, and on the seventh day shall be a solemn assembly to Jehovah thy God. Thou shall do no work.
9 Muziwerenga masabata asanu ndi awiri kuyambira pamene mwatenga chikwakwa ndi kuyamba kumweta tirigu wachilili.
Thou shall number to thee seven weeks. From the time thou begin to put the sickle to the standing grain thou shall begin to number seven weeks.
10 Pamenepo muzichita Chikondwerero cha Masabata pamaso pa Yehova Mulungu wanu popereka chopereka chaufulu mofanana ndi madalitso amene Yehova Mulungu wakupatsani
And thou shall keep the feast of weeks to Jehovah thy God with a tribute of a freewill offering from thy hand, which thou shall give, according as Jehovah thy God blesses thee.
11 Ndipo inu, ana anu aamuna, aakazi, antchito anu aamuna, adzakazi, Alevi a mʼmizinda mwanu, alendo, ana ndi akazi amasiye okhala pakati panu, mukondwere pamaso pa Yehova Mulungu wanu ku malo amene adzawasankhe kukhazikitsako dzina lake.
And thou shall rejoice before Jehovah thy God, thou, and thy son, and thy daughter, and thy man-servant, and thy maid-servant, and the Levite who is within thy gates, and the sojourner, and the fatherless, and the widow, who are in the midst of thee, in the place which Jehovah thy God shall choose to cause his name to dwell there,
12 Kumbukirani kuti inunso munali akapolo ku Igupto, ndiye muzitsatira malangizo awa mosamalitsa.
and thou shall remember that thou were a bondman in Egypt. And thou shall observe and do these statutes.
13 Mukatha kukolola tirigu wanu ndi kupsinya vinyo wanu, muzikhala ndi Chikondwerero cha Misasa kwa masiku asanu ndi awiri.
Thou shall keep the feast of tabernacles seven days after thou have gathered in from thy threshing-floor and from thy winepress.
14 Musangalale pa chikondwerero chanu, inu, ana anu aamuna, aakazi, antchito anu aamuna, adzakazi, Alevi, alendo, ana ndi akazi amasiye amene ali mʼmizinda yanu.
And thou shall rejoice in thy feast, thou, and thy son, and thy daughter, and thy man-servant, and thy maid-servant, and the Levite, and the sojourner, and the fatherless, and the widow, who are within thy gates.
15 Kwa masiku asanu ndi awiri muzichita chikondwererochi kwa Yehova Mulungu wanu kumalo kumene Yehova adzasankhe. Pakuti Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani inu pa zokolola zanu ndi pa ntchito za manja anu, ndipo chimwemwe chanu chidzakhala chathunthu.
Seven days thou shall keep a feast to Jehovah thy God in the place which Jehovah shall choose, because Jehovah thy God will bless thee in all thine increase, and in all the work of thy hands, and thou shall be altogether joyful.
16 Amuna onse azionekera pamaso pa Yehova Mulungu katatu pa chaka ku malo amene Iye adzasankha. Pa Chikondwerero cha Buledi wopanda Yisiti, pa Chikondwerero cha Masabata ndi pa Chikondwerero cha Misasa. Munthu aliyense asadzapite pamaso pa Yehova wopanda kanthu mʼmanja mwake.
Three times in a year all thy males shall appear before Jehovah thy God in the place which he shall choose: in the feast of unleavened bread, and in the feast of weeks, and in the feast of tabernacles. And they shall not appear before Jehovah empty.
17 Aliyense wa inu adzabweretse mphatso molingana ndi momwe Yehova Mulungu wanu wakudalitsirani.
Every man shall give as he is able, according to the blessing of Jehovah thy God which he has given thee.
18 Musankhe oweruza ndi akuluakulu a fuko lanu lililonse mu mzinda uliwonse umene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, ndipo adzaweruza anthuwa mwachilungamo.
Thou shall make judges and officers for thee in all thy gates, which Jehovah thy God gives thee, according to thy tribes, and they shall judge the people with righteous judgment.
19 Musamakhotetse chiweruzo kapena kukondera. Musamalandire chiphuphu pakuti chiphuphu chimadetsa mʼmaso anthu a nzeru ndi kusintha mawu awo kuti mlandu uyipire osalakwa.
Thou shall not distort justice. Thou shall not respect persons, neither shall thou take a bribe, for a bribe blinds the eyes of the wise, and perverts the words of the righteous.
20 Tsatani chilungamo chokhachokha basi kuti mukhale ndi moyo ndi kutenga dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.
Thou shall follow that which is altogether just, that thou may live, and inherit the land which Jehovah thy God gives thee.
21 Musazike mtengo wina uliwonse wa mafano a Asera pambali pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu,
Thou shall not plant for thee an Asherah of any kind of tree beside the altar of Jehovah thy God, which thou shall make for thee.
22 ndipo musayimike mwala wachipembedzo pakuti Yehova Mulungu wanu amadana nazo zimenezi.
Neither shall thou set up a pillar for thee, which Jehovah thy God hates.

< Deuteronomo 16 >