< Deuteronomo 15 >

1 Kumapeto kwa zaka zisanu ndi ziwiri zilizonse, muzikhululukirana ngongole.
At the end of every seven years thou shall make a release.
2 Zimenezi muzichita motere: wobwereketsa aliyense adzakhululukira ngongole imene anabwereketsa kwa Mwisraeli mnzake. Iye asadzafunenso kuti Mwisraeli mnzakeyo kapena mʼbale wake amubwezere chifukwa nthawi ya Ambuye yokhululukirana ngongole yalengezedwa.
And this is the manner of the release: Every creditor shall release that which he has lent to his neighbor. He shall not exact it from his neighbor and his brother, because Jehovah's release has been proclaimed.
3 Mukhoza kulonjerera ngongole kwa mlendo, koma mukhululukire ngongole ina iliyonse imene mʼbale wanu ali nayo.
From a foreigner thou may exact it, but whatever of thine is with thy brother, thy hand shall release.
4 Komabe pasadzakhale wosauka pakati panu chifukwa Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani kwambiri mʼdziko limene adzakupatsani kuti likhale lanu ngati cholowa chanu.
However there shall be no poor with thee (for Jehovah will surely bless thee in the land which Jehovah thy God gives thee for an inheritance to possess it),
5 Adzakudalitsani pokhapokha ngati mudzamveradi Yehova Mulungu wanu posunga ndi kutsatira malamulo onse amene ndikukupatsani lero.
if only thou diligently hearken to the voice of Jehovah thy God, to observe to do all this commandment which I command thee this day.
6 Pakuti Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani monga analonjeza, ndipo inu mudzabwereketsa chuma kwa mitundu yambiri ya anthu koma inu simudzabwereka kwa aliyense. Mudzalamulira mitundu yambiri ya anthu koma inuyo palibe amene adzakulamulireni.
For Jehovah thy God will bless thee as he promised thee, and thou shall lend to many nations, but thou shall not borrow, and thou shall rule over many nations, but they shall not rule over thee.
7 Ngati pali mʼbale wanu wina wosauka mu mzinda wanu wina uliwonse mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, musawumitse mitima yanu kapena kuchita kaligwiritsa kwa mʼbale wanu wosaukayo.
If there be with thee a poor man, one of thy brothers, within any of thy gates in thy land which Jehovah thy God gives thee, thou shall not harden thy heart, nor shut thy hand from thy poor brother,
8 Koma mukhale ofewa manja ndipo mumukongoze mʼbale wanu momasuka pa chilichonse chimene akufuna.
but thou shall surely open thy hand to him, and shall surely lend him sufficient for his need which he wants.
9 Musayesere ndi pangʼono pomwe kusunga maganizo oyipa awa mu mtima mwanu: “Chaka chachisanu ndi chiwiri, chaka chokhululukirana ngongole, chayandikira,” kuti musaonetse mtima woyipa kwa mʼbale wanu wosauka nʼkusamupatsa chilichonse. Iye angadzakunenereni inu mlandu kwa Ambuye, ndipo mudzapezeka wochimwa.
Beware that there not be a base thought in thy heart, saying, The seventh year, the year of release, is at hand, and thine eye be evil against thy poor brother, and thou give him nothing, and he cry to Jehovah against thee, and it be sin to thee.
10 Mumupatse iye mowolowamanja ndipo muchite zimenezi mosasungira kanthu kumtima. Tsono chifukwa cha zimenezi, Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani pa ntchito zanu zonse ndi pa chilichonse chimene mukhudza.
Thou shall surely give him, and thy heart shall not be grieved when thou give to him, because for this thing Jehovah thy God will bless thee in all thy work, and in all that thou put thy hand to.
11 Anthu osauka sadzatha mʼdziko lanu. Chomwecho ndikukulamulani kuti mukhale ofewa manja kwa abale anu ndi kwa osauka, osowa mʼdziko mwanu.
For the poor will never cease out of the land. Therefore I command thee, saying, Thou shall surely open thy hand to thy brother, to thy needy, and to thy poor, in thy land.
12 Ngati mʼbale wanu wamwamuna kapena wamkazi adzigulitsa yekha kwa inu, nakugwirirani ntchito zaka zisanu ndi chimodzi, muzimumasula mʼchaka cha chisanu ndi chiwiri.
If thy brother, a Hebrew man, or a Hebrew woman, is sold to thee, and serves thee six years, then in the seventh year thou shall let him go free from thee.
13 Ndipo pamene mumumasula, musangomulola apite chimanjamanja.
And when thou let him go free from thee, thou shall not let him go empty.
14 Mumupatse mowolowamanja zochokera pa ziweto zanu, kopunthira tirigu ndi kopsinyira vinyo. Inu mumupatse iye monga Yehova Mulungu wanu wakudalitsirani.
Thou shall furnish him liberally out of thy flock, and out of thy threshing-floor, and out of thy winepress. As Jehovah thy God has blessed thee thou shall give to him.
15 Kumbukirani kuti munali akapolo mʼdziko la Igupto ndipo Yehova Mulungu wanu anakupulumutsani. Nʼchifukwa chake ndikukupatsani lamulo ili lero lino.
And thou shall remember that thou were a bondman in the land of Egypt, and Jehovah thy God redeemed thee. Therefore I command thee this thing today.
16 Koma ngati kapoloyo akuwuzani kuti, “Ine sindikufuna kumasulidwa,” chifukwa choti wakukondani inuyo pamodzi ndi banja lanu ndiponso kuti kwamukomera iyeyo kuti azikhalabe nanu,
And it shall be, if he says to thee, I will not go out from thee, because he loves thee and thy house, because he is well with thee,
17 pamenepo muzitenga chobowolera chachitsulo ndi kubowola khutu lake pa chitseko, ndipo mukatero adzakhala kapolo wanu moyo wake wonse. Mdzakazi wanu muzimuchitanso chimodzimodzi.
then thou shall take an awl, and thrust it through his ear to the door, and he shall be thy servant forever. And also to thy maid-servant thou shall do likewise.
18 Musaone ngati chopweteka kumasula wantchito wanu, chifukwa ntchito imene wayigwira pa zaka zisanu ndi chimodzi zimenezi ndi yopindula kawiri pa ntchito imene akanagwira waganyu chabe. Ndipo Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani pa chilichonse chimene mukuchita.
It shall not seem hard to thee when thou let him go free from thee, for he has been worth a double hired servant to thee, in serving thee six years. And Jehovah thy God will bless thee in all that thou do.
19 Mumupatulire Yehova Mulungu wanu choyamba kubadwa chachimuna chilichonse pa ngʼombe ndi nkhosa zanu. Musamazigwiritse ntchito ngʼombe zoyamba kubadwa kapena kumeta nkhosa zoyamba kubadwa.
All the firstling males that are born of thy herd and of thy flock thou shall sanctify to Jehovah thy God. Thou shall do no work with the firstling of thy herd, nor shear the firstling of thy flock.
20 Inuyo ndi banja lanu, chaka chilichonse muzizidya zimenezi pamaso pa Yehova Mulungu wanu pa malo amene Iye adzasankhe.
Thou shall eat it before Jehovah thy God year by year in the place which Jehovah shall choose, thou and thy household.
21 Ngati chiweto chili ndi chilema monga kulumala kapena chosaona, kapena ngati chili ndi cholakwika chachikulu chilichonse, musachipereke nsembe kwa Yehova Mulungu wanu.
And if it has any blemish, as lame or blind, any ill blemish whatever, thou shall not sacrifice it to Jehovah thy God.
22 Muzichidya mʼmizinda yanuyanu. Onse odetsedwa monga mwa mwambo ndi oyeretsedwa omwe akhoza kuchidya monga akudya gwape kapena mbawala.
Thou shall eat it within thy gates. The unclean man and the clean man alike, as the gazelle, and as the hart.
23 Koma musadye magazi ake. Muwathire pansi ngati madzi.
Only thou shall not eat the blood of it. Thou shall pour it out upon the ground as water.

< Deuteronomo 15 >