< Deuteronomo 17 >

1 Musapereke nsembe kwa Yehova Mulungu wanu ngʼombe kapena nkhosa imene ili ndi chilema kapena cholakwika chilichonse, pakuti zimenezi zimamunyansa.
Thou shall not sacrifice to Jehovah thy God an ox, or a sheep, in which is a blemish or anything bad, for that is an abomination to Jehovah thy God.
2 Ngati mwamuna kapena mkazi pakati panu, mʼmizinda imene Yehova akukupatsani apezeka akuchita zoyipa pamaso pa Yehova Mulungu wanu pophwanya pangano lake,
If there be found in the midst of thee, within any of thy gates which Jehovah thy God gives thee, man or woman, who does that which is evil in the sight of Jehovah thy God, in transgressing his covenant,
3 ndipo ngati motsutsana ndi lamulo langa wapembedza milungu ina, kuyigwadira milunguyo, kaya ndi dzuwa kapena mwezi kapena nyenyezi zakumwamba,
and has gone and served other gods, and worshiped them, or the sun, or the moon, or any of the host of heaven, which I have not commanded,
4 ndipo inu nʼkuwuzidwa zimenezi, mufufuze bwinobwino. Ngati ndi zoona, ndipo ngati zatsimikizika kuti chonyansa choterechi chachitikadi mu Israeli,
and it be told thee, and thou have heard of it, then shall thou inquire diligently. And, behold, if it be true, and the thing certain, that such abomination is wrought in Israel,
5 mumutengere mwamuna kapena mkazi amene wachita chonyansa choterechi ku chipata cha mzinda wanu ndi kumupha pomugenda miyala.
then thou shall bring forth that man or that woman, who has done this evil thing, to thy gates, even the man or the woman, and thou shall stone them to death with stones.
6 Munthu aziphedwa pakakhala mboni ziwiri kapena zitatu koma osati mboni imodzi yokha ayi.
At the mouth of two witnesses, or three witnesses, shall he who is to die be put to death. He shall not be put to death at the mouth of one witness.
7 Wochitira umboniwo ndiwo aziyamba kumupha munthuyo, ndipo kenaka anthu onse. Muyenera kuchotsa choyipa pakati panu.
The hand of the witnesses shall be first upon him to put him to death, and afterward the hand of all the people. So thou shall put away the evil from the midst of thee.
8 Ngati akubweretserani milandu mʼmabwalo anu imene ili yovuta kuweruza kaya ndi yokhetsa magazi, kaya ndi yophwanyirana ufulu, kaya ndi yovulazana, muyitengere kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe.
If there arise a matter too hard for thee in judgment, between blood and blood, between plea and plea, and between stroke and stroke, being matters of controversy within thy gates, then thou shall arise, and get thee up to the place which Jehovah thy God shall choose.
9 Mudzapite kwa ansembe Alevi ndi kwa woweruza wa pa nthawi imeneyo. Kawafunseni ndipo iwowo adzakuwuzani zoyenera kuchita.
And thou shall come to the priests the Levites, and to the judge who shall be in those days, and thou shall inquire. And they shall show thee the sentence of judgment.
10 Kachiteni zimene adzakuwuzenizo kuchokera ku malo amene Yehova adzasankhe. Kaonetsetseni kuti mukutsatira zonse zimene akuwuzanizo.
And thou shall do according to the tenor of the sentence which they shall show thee from that place which Jehovah shall choose. And thou shall observe to do according to all that they shall teach thee,
11 Kachiteni motsatira malamulo ndi malangizo amene adzakuwuzeni; osawanyoza, potembenukira kumanja kapena kumanzere.
according to the tenor of the law which they shall teach thee, and according to the judgment which they shall tell thee, thou shall do. Thou shall not turn aside from the sentence, which they shall show thee, to the right hand, nor to the left.
12 Munthu aliyense amene adzanyoza woweruza kapena wansembe amene akutumikira kumeneko mʼmalo mwa Yehova Mulungu wanu, aphedwe ndithu. Muzichotsa choyipa pakati pa Israeli.
And the man who does presumptuously, in not hearkening to the priest who stands to minister there before Jehovah thy God, or to the judge, even that man shall die, and thou shall put away the evil from Israel.
13 Anthu onse adzamva zimenezi ndipo adzachita mantha, choncho sadzadzikuzanso.
And all the people shall hear, and fear, and do no more presumptuously.
14 Mukalowa mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kuti mulitenge, ndipo mukakakhazikika mʼmenemo nimunena kuti, “Tiyeni tisankhe mfumu yoti izitilamulira monga imachitira mitundu yonse yotizungulirayi,”
When thou have come to the land which Jehovah thy God gives thee, and shall possess it, and shall dwell in it, and shall say, I will set a king over me like all the nations that are round about me,
15 mudzakhazikitse mfumu yoti izikakulamulirani, mfumu imene Yehova Mulungu wanu adzasankhe pakati panu. Mudzasankhe mfumuyo kuchokera pakati pa abale anu. Osasankha mlendo, munthu amene sachokera pakati pa abale anu Aisraeli.
thou shall surely set him king over thee whom Jehovah thy God shall choose. Thou shall set a king over thee from among thy brothers. Thou may not put a foreigner over thee who is not thy brother.
16 Komatu mfumuyo isadzikundikire akavalo, kapena kutuma anthu kupita ku Igupto kukayipezera akavalo ena, pakuti Ambuye akuti, “Simuyenera kubweranso ku Igupto mʼnjira yomweyo.”
Only he shall not multiply horses to himself, nor cause the people to return to Egypt, to the end that he may multiply horses, inasmuch as Jehovah has said to you, Ye shall henceforth return no more that way.
17 Asadziwunjikire akazi kuopa kuti mtima wake ungamusocheretse. Asadziwunjikirenso golide ndi siliva wambiri.
Neither shall he multiply wives to himself, that his heart turn not away. Neither shall he greatly multiply to himself silver and gold.
18 Akakhala pa mpando waufumuwo, ayenera kulemba za iye mwini mʼbuku la malamuloli, kuchokera kwa ansembe Alevi.
And it shall be, when he sits upon the throne of his kingdom, that he shall write for him a copy of this law in a book, out of it before the priests the Levites,
19 Asunge zimene walembazo ndipo ayenera kumaziwerenga masiku onse a moyo wake, kuti aphunzire kuopa Yehova Mulungu wake posunga mosamalitsa malamulo ndi malangizowa.
and it shall be with him. And he shall read in it all the days of his life, that he may learn to fear Jehovah his God, to keep all the words of this law and these statutes, to do them,
20 Asadzione kuti iyeyo ndi wopambana kuposa abale ake, nalekeratu kutsatira malamulo. Akasamala zimenezi iye ndi ana ake adzalamulira ufumu wa Israeli kwa nthawi yayitali.
that his heart not be lifted up above his brothers, and that he turn not aside from the commandment, to the right hand, or to the left, to the end that he may prolong his days in his kingdom, he and his sons, in the midst of Israel.

< Deuteronomo 17 >