< Deuteronomo 12 >

1 Awa ndi malangizo ndi malamulo amene muyenera kusamalitsanso kuti muwatsatire mʼdziko limene Yehova Mulungu wa makolo anu wakupatsani kuti mutenge pa nthawi yonse imene muti mudzakhale mʼdzikomo.
These are the statutes and the ordinances which ye shall observe to do in the land which Jehovah, the God of thy fathers, has given thee to possess it all the days that ye live upon the earth.
2 Muwonongeretu kwathunthu malo onse a pamwamba pa mapiri ataliatali ndi pa mapiri angʼonoangʼono ndi pansi pa mtengo uliwonse wotambalala pamene mitundu imene muyilande dzikolo ankapembedzerapo milungu yawo.
Ye shall surely destroy all the places in which the nations that ye shall dispossess served their gods, upon the high mountains, and upon the hills, and under every green tree.
3 Mugumule maguwa awo ansembe, ndi kuphwanya miyala yawo yachipembedzo ndipo mutenthe pa moto mafano awo a Asera: mugwetse mafano a milungu yawo ndi kufafaniza mayina awo mʼmalo amenewo.
And ye shall break down their altars, and dash in pieces their pillars, and burn their Asherim with fire. And ye shall hew down the graven images of their gods, and ye shall destroy their name out of that place.
4 Musapembedze Yehova Mulungu wanu monga mmene amachitira iwowa.
Ye shall not do so to Jehovah your God.
5 Koma inu muzifunafuna kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe pakati pa mafuko anu kuti ayikeko dzina lake ndi kukhalako. Ku malo amenewa muyenera kupitako.
But to the place which Jehovah your God shall choose out of all your tribes, to put his name there, even to his habitation ye shall seek, and there thou shall come.
6 Kumeneko muzipititsako zopereka zanu ndi nsembe zanu zopsereza, ndi chakhumi chanu ndi mphatso zapadera zimene munalonjeza kupereka ndi zopereka zanu zaufulu ndi ana oyamba a ngʼombe zanu ndi nkhosa zanu.
And there ye shall bring your burnt offerings, and your sacrifices, and your tithes, and the heave offering of your hand, and your vows, and your freewill offerings, and the firstlings of your herd and of your flock.
7 Kumeneko, pamaso pa Yehova Mulungu wanu, inu ndi mabanja anu mudzadya ndi kusangalalako pa china chilichonse chimene mudzakhudza, chifukwa Yehova Mulungu wanu wakudalitsani.
And there ye shall eat before Jehovah your God, and ye shall rejoice in all that ye put your hand to, ye and your households, in which Jehovah thy God has blessed thee.
8 Musadzachite monga tikuchitira lero lino, aliyense kumachita zimene akuona kuti ndi zoyenera,
Ye shall not do after all the things that we do here this day, every man whatever is right in his own eyes.
9 pakuti simunafike ku malo opumulirako ndi ku cholowa chimene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.
For ye are not as yet come to the rest and to the inheritance, which Jehovah thy God gives thee.
10 Koma mudzawoloka Yorodani ndi kukhazikika mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa chanu, ndipo Iye adzakupatsani inu mpumulo ku adani anu okuzungulirani kuti mukhale motchinjirizidwa.
But when ye go over the Jordan, and dwell in the land which Jehovah your God causes you to inherit, and he gives you rest from all your enemies round about, so that ye dwell in safety,
11 Tsono kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe kuti azikhalako muzikabweretsako chilichonse chimene ndikulamulirani inu: zopereka ndi nsembe zanu zopsereza, chakhumi chanu ndi mphatso zapadera, ndi chuma chanu chonse chosankhika chimene munalonjeza kwa Yehova.
then it shall come to pass that to the place which Jehovah your God shall choose to cause his name to dwell there, there ye shall bring all that I command you: your burnt offerings, and your sacrifices, your tithes, and the heave offering of your hand, and all your choice vows which ye vow to Jehovah.
12 Ndipo kumeneko inu mukasangalale pamaso pa Yehova Mulungu wanu pamodzi ndi ana anu aamuna ndi ana anu aakazi, antchito anu aamuna ndi adzakazi anu, ndi Alevi a mʼmidzi yanu, amene alibe gawo kapena cholowa chawochawo.
And ye shall rejoice before Jehovah your God, ye, and your sons, and your daughters, and your men-servants, and your maid-servants, and the Levite who is within your gates-inasmuch as he has no portion nor inheritance with you.
13 Musamalitse kuti musakaphere nsembe zanu zopsereza paliponse pamene mungafune.
Take heed to thyself that thou offer not thy burnt offerings in every place that thou see,
14 Mukaphere pa malo okhawo amene Yehova adzawasankhe mwa limodzi la mafuko anu, ndipo kumeneko mukasunge chilichonse chimene ndikulamulireni.
but in the place which Jehovah shall choose in one of thy tribes. There thou shall offer thy burnt offerings, and there thou shall do all that I command thee.
15 Koma mukhoza kumapha ziweto zanu mʼmizinda iliyonse ndi kudya nyama yake mmene mungafunire, ngati kuti ndi agwape kapena mbawala, monga mwadalitso limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani. Woyeretsedwa ndi wosayeretsedwa akhoza kuyidya.
Notwithstanding, thou may kill and eat flesh within all thy gates, after all the desire of thy soul, according to the blessing of Jehovah thy God which he has given thee, the unclean and the clean may eat of it, as of the gazelle, and as of the hart.
16 Koma musamadye magazi. Muziwathira pansi ngati madzi.
Only ye shall not eat the blood. Thou shall pour it out upon the ground as water.
17 Musamadyere mʼmizinda yanu chakhumi cha tirigu wanu ndi vinyo watsopano ndi mafuta, kapena za ana oyamba kubadwa a ngʼombe zanu ndi nkhosa zanu, kapena chilichonse chimene mwalonjeza kuchipereka, nsembe zanu zaufulu, kapena mphatso zapadera,
Thou may not eat within thy gates the tithe of thy grain, or of thy new wine, or of thine oil, or the firstlings of thy herd or of thy flock, nor any of thy vows which thou vow, nor thy freewill offerings, nor the heave offering of thy hand.
18 mʼmalo mwake, muzidya pamaso pa Yehova Mulungu wanu, kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhira inu, ana anu aamuna ndi aakazi, antchito anu aamuna ndi adzakazi anu, ndi Alevi ochokera mʼmizinda yanu, ndipo mudzasangalale pamaso pa Yehova Mulungu wanu pa chilichonse chimene mudzachikhudza.
But thou shall eat them before Jehovah thy God in the place which Jehovah thy God shall choose, thou, and thy son, and thy daughter, and thy man-servant, and thy maid-servant, and the Levite who is within thy gates. And thou shall rejoice before Jehovah thy God in all that thou put thy hand to.
19 Muonetsetse kuti musawataye Alevi pa masiku onse amene mukhale mʼdziko lanumo.
Take heed to thyself that thou not forsake the Levite as long as thou live in thy land.
20 Yehova Mulungu wanu akadzakulitsa dziko lanu monga anakulonjezerani, ndipo mukapukwa nyama mumanena kuti, “Ndikufuna nyama,” pamenepo mudzadya mmene mungafunire.
When Jehovah thy God shall enlarge thy border, as he has promised thee, and thou shall say, I will eat flesh, because thy soul desires to eat flesh, thou may eat flesh, after all the desire of thy soul.
21 Ngati malo amene Yehova Mulungu wanu awasankha kuti ayike Dzina lake ali kutali kwambiri ndi inu, mukhoza kupha ziweto pakati pa ngʼombe ndi nkhosa zimene Yehova wakupatsani, monga ndinakulamulani, ndipo mʼmizinda yanuyanu mukhoza kuzidya mmene mungafunire.
If the place which Jehovah thy God shall choose, to put his name there, be too far from thee, then thou shall kill of thy herd and of thy flock, which Jehovah has given thee, as I have commanded thee, and thou may eat within thy gates, according to all the desire of thy soul.
22 Muzidye ngati mukudya gwape kapena mbawala. Onse oyeretsedwa monga mwa mwambo ndi osayeretsedwa omwe akhoza kudya.
Even as the gazelle and as the hart is eaten, so thou shall eat of it. The unclean and the clean may eat of it alike.
23 Koma muonetsetse kuti musadye magazi, chifukwa magazi ndi moyo, ndipo musamadye moyo pamodzi ndi nyama.
Only be sure that thou not eat the blood. For the blood is the life, and thou shall not eat the life with the flesh.
24 Inu musamadye magazi, muziwathira pansi ngati madzi.
Thou shall not eat it. Thou shall pour it out upon the ground as water.
25 Musamadye magazi kuti zikuyendereni bwino inu pamodzi ndi ana anu a pambuyo panu, popeza mudzakhala mukuchita zoyenera pamaso pa Mulungu.
Thou shall not eat it, that it may go well with thee, and with thy sons after thee, when thou shall do that which is right in the eyes of Jehovah.
26 Koma mutenge zinthu zanu zoyeretsedwa ndi china chilichonse chimene munalumbira kupereka, ndi kupita kumalo kumene Yehova adzasankhe.
Only thy holy things which thou have, and thy vows, thou shall take, and go to the place which Jehovah shall choose.
27 Mupereke nsembe zanu zopsereza pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu, nyama pamodzi ndi magazi omwe. Magazi a nsembe zanu athiridwe pambali pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu, koma nyamayo mukhoza kudya.
And thou shall offer thy burnt offerings, the flesh and the blood, upon the altar of Jehovah thy God, and the blood of thy sacrifices shall be poured out upon the altar of Jehovah thy God, and thou shall eat the flesh.
28 Onetsetsani kuti muzimvera mawu onsewa amene ndikukupatsani kuti zinthu zizikuyenderani bwino nthawi zonse inu ndi ana anu chifukwa mudzakhala mukuchita zabwino ndi zoyenera pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
Observe and hear all these words which I command thee, that it may go well with thee, and with thy sons after thee forever, when thou do that which is good and right in the eyes of Jehovah thy God.
29 Yehova Mulungu wanu adzachotsa pamaso panu mitundu ya anthu amene mukufuna kuwathira nkhondo ndi kuwalanda dzikolo. Koma mukawapirikitsa ndi kukhazikika mʼdziko lawo,
When Jehovah thy God shall cut off the nations from before thee, where thou go in to dispossess them, and thou dispossess them, and dwell in their land,
30 ndipo pamene iwo awonongeka pamaso panu, samalirani kuti musakodwe mu msampha pa kufufuza za milungu yawo, nʼkumati, “Kodi anthu a mitunduwa amatumikira bwanji milungu yawo? Ifenso tichita momwemo.”
take heed to thyself that thou be not ensnared to follow them, after they are destroyed from before thee, and that thou not inquire after their gods, saying, How do these nations serve their gods? Even so I will do likewise.
31 Musapembedze Yehova Mulungu wanu momwe amachitira iwowo, chifukwa popembedza milungu yawoyo amachita zonyansa zamitundumitundu zimene Yehova amadana nazo. Amatentha ngakhale ana awo aamuna ndi aakazi pa moto ngati nsembe za kwa milungu yawo.
Thou shall not do so to Jehovah thy God. For every abomination to Jehovah, which he hates, they have done to their gods, for they even burn their sons and their daughters in the fire to their gods.
32 Onetsetsani kuti mukuchita zimene ndikukulamulirani. Musawonjezerepo kapena kuchotserapo.
Whatever thing I command you, that shall ye observe to do. Thou shall not add to it, nor diminish from it.

< Deuteronomo 12 >