< Deuteronomo 13 >

1 Ngati mneneri kapena wina aliyense amene amanena zamʼtsogolo mwa maloto atuluka pakati panu, nalengeza za chizindikiro chozizwitsa kapena chodabwitsa,
If there arise in the midst of thee a prophet, or a dreamer of dreams, and he gives thee a sign or a wonder,
2 chinthu nʼkuchitikadi, tsono iyeyo nʼkunena kuti, “Tiyeni titsatire milungu ina, tiyeni tiyipembedze,” (kunena milungu imene simunayidziwe),
and the sign or the wonder comes to pass, of which he spoke to thee, saying, Let us go after other gods, which thou have not known, and let us serve them,
3 musamumvere mneneriyo kapena wolotayo. Yehova Mulungu wanu afuna akuyeseni kuti aone ngati mumamukonda ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.
thou shall not hearken to the words of that prophet, or to that dreamer of dreams, for Jehovah your God proves you, to know whether ye love Jehovah your God with all your heart and with all your soul.
4 Muyenera kutsatira Yehova Mulungu wanu, ndipo ndi Iyeyo amene muyenera kumuopa. Muzisunga malamulo ake ndi kumamumvera, muzimutumikira ndipo kumukangamira Iyeyo.
Ye shall walk after Jehovah your God, and fear him, and keep his commandments, and obey his voice, and ye shall serve him, and cling to him.
5 Mneneri kapena wolotayo ayenera kuphedwa, popeza analalikira zopandukira Yehova Mulungu wanu, amene anakutulutsani ku Igupto ndi kukupulumutsani ku dziko la ukapolo. Wolalikirayo anafuna kukupatutsani pa njira imene Yehova Mulungu wanu anakulamulirani kuti muyitsatire. Muzichotsa choyipa pakati panu.
And that prophet, or that dreamer of dreams, shall be put to death, because he has spoken rebellion against Jehovah your God, who brought you out of the land of Egypt, and redeemed thee out of the house of bondage, to draw thee aside out of the way which Jehovah thy God commanded thee to walk in. So shall thou put away the evil from the midst of thee.
6 Ngati mʼbale wanu weniweni kapena mwana wanu wamwamuna kapena wamkazi, kapena mkazi wanu wokondedwa, kapena mnzanu wapamtima akukakamizani mwachinsinsi, nʼkumati, “Tiyeni tipite tikapembedze milungu ina” (milungu imene inuyo kapena makolo anu sanayidziwe,
If thy brother, the son of thy mother, or thy son, or thy daughter, or the wife of thy bosom, or thy friend, who is as thine own soul, entices thee secretly, saying, Let us go and serve other gods, which thou have not known, thou, nor thy fathers,
7 milungu ya anthu okuzungulirani, kaya ndi apafupi kapena akutali, kuchokera kumapeto mpaka kumapeto kwina kwa dziko lapansi),
of the gods of the peoples that are round about you, near to thee, or far off from thee, from the one end of the earth even to the other end of the earth,
8 musamugonjere kapena kumumvera. Musamumvere chisoni. Musamuleke kapena kumutchinjiriza.
thou shall not consent to him, nor hearken to him. Neither shall thine eye pity him, neither shall thou spare, neither shall thou conceal him,
9 Mumuphe ndithu. Dzanja lanu likhale loyambirira kumupha, kenaka manja a anthu ena onse.
but thou shall surely kill him. Thy hand shall be first upon him to put him to death, and afterwards the hand of all the people.
10 Mumuponye miyala mpaka kumupha, chifukwa anafuna kukupatutsani pa njira ya Yehova Mulungu amene anakutulutsani ku Igupto, dziko la ukapolo.
And thou shall stone him to death with stones, because he has sought to draw thee away from Jehovah thy God, who brought thee out of the land of Egypt, out of the house of bondage.
11 Tsono Aisraeli onse adzamva nachita mantha, ndipo palibe mmodzi pakati panu amene adzachitenso choyipa chotere.
And all Israel shall hear, and fear, and shall no more do any such wickedness as this is in the midst of thee.
12 Ngati mumvetsedwa kuti ku umodzi mwa mizinda imene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kuti mukhalemo,
If thou shall hear tell concerning one of thy cities, which Jehovah thy God gives thee to dwell there, saying,
13 kwapezeka anthu ena oyipa pakati panu ndipo asocheretsa anthu ambiri mʼmizinda yanu, pomanena kuti, “Tiyeni tikapembedze milungu ina” (milungu imene simunayidziwe),
Certain base fellows have gone out from the midst of thee, and have drawn away the inhabitants of their city, saying, Let us go and serve other gods, which ye have not known,
14 mukuyenera kufunsa, kulondola ndi kufufuza bwino nkhaniyo. Ndipo ngati zitatsimikizikadi kuti ndi zoona kuti chinthu chonyansa chotere chachitikadi pakati panu,
then thou shall inquire, and make search, and ask diligently. And, behold, if it be true, and the thing certain, that such abomination is wrought in the midst of thee,
15 muyenera kuwapha onse okhala mu mzinda umenewo. Muwonongeretu kwathunthu mzindawo, anthu ake ndi ziweto zake zomwe.
thou shall surely smite the inhabitants of that city with the edge of the sword, destroying it utterly, and all that is in it, and the cattle in it, with the edge of the sword.
16 Katundu yense wa anthu mu mzindawo mumuwunjike pamodzi pakatikati pa bwalo losonkhanako ndipo mutenthe mzindawo pamodzi ndi katundu wake yense monga nsembe yathunthu yopsereza ya kwa Yehova Mulungu wanu. Mzinda umenewo ukhale bwinja mpaka muyaya, usadzamangidwenso.
And thou shall gather all the spoil of it into the midst of the street of it, and shall burn the city with fire, and all the spoil of it, every whit, to Jehovah thy God, and it shall be a heap forever. It shall not be built again.
17 Musapezeke ndi kanthu kalikonse koyenera kuwonongedwa kuti Yehova abweze mkwiyo wake wochititsa manthawu. Adzakuchitirani chifundo ndi kukumverani chisoni, ndipo adzakuchulukitsani monga analonjeza mwa lumbiro kwa makolo anu,
And nothing of the devoted thing shall cling to thy hand, that Jehovah may turn from the fierceness of his anger, and show thee mercy, and have compassion upon thee, and multiply thee, as he has sworn to thy fathers,
18 chifukwa mumamvera Yehova Mulungu wanu, kusunga malamulo ake onse amene ndikukupatsani lero lino ndi kuchita zoyenera pamaso pake.
when thou shall hearken to the voice of Jehovah thy God, to keep all his commandments which I command thee this day, to do that which is right in the eyes of Jehovah thy God.

< Deuteronomo 13 >