< Deuteronomo 11 >

1 Muzikonda Yehova Mulungu wanu ndipo nthawi zonse muzitsata zimene Iyeyo anakulamulani, malangizo, zikhazikitso ndi malamulo ake.
Therefore thou shall love Jehovah thy God, and keep his charge, and his statutes, and his ordinances, and his commandments, always.
2 Lero kumbukirani kuti si ana anu amene anaona ndi kulawa chilango cha Yehova Mulungu wanu: ukulu wake, dzanja lake lamphamvu, mkono wake wotambasuka;
And ye know this day, for it is not with your sons who have not known, and who have not seen the chastisement of Jehovah your God, his greatness, his mighty hand, and his outstretched arm,
3 zizindikiro zozizwitsa zimene anazionetsa ndi zinthu zimene anazichita mʼkati mwa Igupto, Farao mfumu ya Igupto ndi kwa dziko lake lonse;
and his signs, and his works, which he did in the midst of Egypt to Pharaoh the king of Egypt, and to all his land,
4 zimene Iye anachita kwa gulu lankhondo la Aigupto, kwa akavalo ndi magaleta awo, mmene Iye anawamizira ndi madzi a mu Nyanja Yofiira pamene amakuthamangitsani, ndi mmene Yehova anawagonjetsera kufikira lero.
and what he did to the army of Egypt, to their horses, and to their chariots, how he made the water of the Red Sea to overflow them as they pursued after you, and how Jehovah has destroyed them to this day,
5 Si ana anu amene anaona zimene Iye anakuchitirani mʼchipululu kufikira pamene munafika pa malo anu,
and what he did to you in the wilderness, until ye came to this place,
6 ndi zimene anachitira Datani ndi Abiramu, ana aamuna a Eliabu mwana wa Rubeni, pamene nthaka inatsekula pakamwa pake pakati pa Aisraeli onse ndi kuwameza pamodzi ndi katundu wawo, matenti awo ndi chilichonse chawo.
and what he did to Dathan and Abiram, the sons of Eliab, the son of Reuben, how the earth opened its mouth, and swallowed them up, and their households, and their tents, and every living thing that followed them, in the midst of all Israel,
7 Koma ndinuyo amene munaona ntchito zonse zikuluzikulu zimenezi Yehova anakuchitirani.
but your eyes have seen all the great work of Jehovah which he did.
8 Tsono muzisunga malamulo onse amene ndikukupatsani lero kuti mukhale ndi mphamvu ndi kuti mupite kukalanda mʼdziko limene mwakhala pangʼono kulowamo mukawoloka Yorodani,
Therefore ye shall keep all the commandment which I command thee this day, that ye may be strong, and go in and possess the land, where ye go over to possess it,
9 ndiponso kuti mukhalitse mʼdziko limene Yehova analumbira kupatsa makolo anu ndi zidzukulu zawo, lomwe ndi dziko loyenda mkaka ndi uchi.
and that ye may prolong your days in the land, which Jehovah swore to your fathers to give to them and to their seed, a land flowing with milk and honey.
10 Dziko limene mukukalanda ndi kulowamo silokhala ngati dziko la ku Igupto kumene mukuchokera ayi, kuja mumadzala mbewu ndi kumathirira ndi mapazi anu ngati ku dimba.
For the land, where thou go in to possess it, is not as the land of Egypt, from where ye came out, where thou sowed thy seed, and watered it with thy foot, as a garden of herbs,
11 Koma dziko limene mukalande mukawoloka Yorodani ndi dziko la mapiri ndi zigwa, dziko limene limalandira mvula kuchokera kumwamba.
but the land, where ye go over to possess it, is a land of hills and valleys, and drinks water from the rain of heaven,
12 Ili ndi dziko limene Yehova Mulungu wanu amalisamalira. Maso a Yehova Mulungu wanu amaliyangʼanira nthawi zonse kuchokera ku mayambiriro a chaka mpaka kumapeto kwake.
a land which Jehovah thy God cares for. The eyes of Jehovah thy God are always upon it, from the beginning of the year even to the end of the year.
13 Choncho mukasunga mokhulupirika malamulo amene ndikukupatsani lero lino, kukonda Yehova Mulungu wanu ndi kumutumikira Iyeyo ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse,
And it shall come to pass, if ye shall hearken diligently to my commandments which I command you this day, to love Jehovah your God, and to serve him with all your heart and with all your soul,
14 pamenepo ndidzatumiza mvula mʼdziko mwanu pa nthawi yake mʼnyengo ya dzinja ndi chilimwe, kuti mudzakolole tirigu wambiri ndi kuti mudzakhale ndi vinyo watsopano ndi mafuta.
that I will give the rain of your land in its season, the former rain and the latter rain, that thou may gather in thy grain, and thy new wine, and thine oil.
15 Ndidzakupatsani udzu mʼminda mwanu woti muzidzadyetsera ngʼombe zanu ndipo inuyo mudzadya ndi kukhuta.
And I will give grass in thy fields for thy cattle, and thou shall eat and be full.
16 Dzisamalireni nokha, kuopa kuti mungakopeke mtima ndi kubwerera mʼmbuyo kuyamba kutumikira milungu ina ndi kumayigwadira.
Take heed to yourselves, lest your heart be deceived, and ye turn aside, and serve other gods, and worship them,
17 Mukatero Yehova Mulungu wanu adzakukwiyirani kwambiri, nadzaletsa thambo kuti lisabweretsenso mvula ndipo dziko silidzapereka zokolola. Choncho mudzawonongeka msanga mʼdziko limene Yehova akukupatsani.
and the anger of Jehovah be kindled against you, and he shut up the heavens, so that there shall be no rain, and the land shall not yield its fruit, and ye perish quickly from off the good land which Jehovah gives you.
18 Sungani mawu amenewa mu mtima mwanu ndi mʼmaganizo mwanu, muwamangirire pa mikono yanu ndipo muwayike pamphumi panu.
Therefore ye shall lay up these my words in your heart and in your soul. And ye shall bind them for a sign upon your hand, and they shall be for frontlets between your eyes.
19 Mawuwa muziphunzitsa ana anu, muzikamba za iwo pamene mukhala pansi mʼnyumba zanu, pamene mukuyenda mʼnjira, pamene mugona ndi pamene mukudzuka.
And ye shall teach them to your sons, talking of them when thou sit in thy house, and when thou walk by the way, and when thou lie down, and when thou rise up.
20 Muwalembe pa mphuthu za nyumba zanu ndi pa zipata zanu,
And thou shall write them upon the door-posts of thy house, and upon thy gates,
21 kuti inu ndi ana anu mukhale mʼdziko limene Yehova analumbira kupatsa makolo anu mpaka kalekale monga umakhalira mlengalenga pamwamba pa dziko.
that your days may be multiplied, and the days of your sons, in the land which Jehovah swore to your fathers to give them, as the days of the heavens above the earth.
22 Mukatsatira mosamalitsa malamulo amene ndikukupatsaniwa, kukonda Yehova Mulungu wanu, kuyenda mʼnjira zake zonse ndi kumugwiritsitsa Iye
For if ye shall diligently keep all this commandment which I command you, to do it, to love Jehovah your God, to walk in all his ways, and to cling to him,
23 Yehova adzapirikitsa mitundu ina yonseyi inu musanafike ndipo mudzagonjetsa mitundu ikuluikulu ndi yamphamvu kuposa inu.
then will Jehovah drive out all these nations from before you, and ye shall dispossess nations greater and mightier than yourselves.
24 Malo aliwonse amene mudzaponda adzakhala anu: dziko lanu lidzachokera ku chipululu mpaka ku Lebanoni, ndi ku Mtsinje wa Yufurate mpaka ku nyanja ya kumadzulo.
Every place on which the sole of your foot shall tread shall be yours, from the wilderness, and Lebanon, from the river, the river Euphrates, even to the hinder sea shall be your border.
25 Palibe munthu amene adzalimbana nanu. Monga analonjezera, Yehova adzachititsa kuti anthu onse mʼdziko limene mukupitalo adzachite nanu mantha ndi kukuopani.
There shall no man be able to stand before you. Jehovah your God shall lay the fear of you and the dread of you upon all the land that ye shall tread upon, as he has spoken to you.
26 Taonani, lero ndikuyika dalitso ndi temberero pakati panu,
Behold, I set before you this day a blessing and a curse:
27 dalitso ngati mumvera malamulo a Yehova Mulungu wanu amene ndikukupatsani lero.
the blessing, if ye shall hearken to the commandments of Jehovah your God, which I command you this day,
28 Temberero ngati simumvera malamulo a Yehova Mulungu wanu ndi kupatuka pa njira imene ndikulamulirani lero potsata milungu ina imene simunayidziwe.
and the curse, if ye shall not hearken to the commandments of Jehovah your God, but turn aside out of the way which I command you this day to go after other gods, which ye have not known.
29 Yehova Mulungu wanu akakakufikitsani mʼdziko mukukalandalo kuti mulowemo mukanene za madalitso pa Phiri la Gerizimu, ndi za matemberero pa Phiri la Ebala.
And it shall come to pass, when Jehovah thy God shall bring thee into the land where thou go to possess it, that thou shall set the blessing upon mount Gerizim, and the curse upon mount Ebal.
30 Monga mudziwa, mapiriwa ali kutsidya kwa Yorodani, kumadzulo kolowera dzuwa, kufupi ndi mitengo ya thundu ya More, mʼdziko la Akanaani aja okhala ku Araba moyangʼanana ndi Giligala.
Are they not beyond the Jordan, behind the way of the going down of the sun, in the land of the Canaanites who dwell in the Arabah, opposite Gilgal, beside the oaks of Moreh?
31 Mwatsala pangʼono kuwoloka Yorodani kuti mulowe ndi kutenga dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani. Mukadzalitenga dzikolo ndi kukhalamo,
For ye are to pass over the Jordan to go in to possess the land which Jehovah your God gives you, and ye shall possess it, and dwell in it.
32 mudzaonetsetse kuti mukumvera malangizo ndi malamulo amene ndikukuwuzani lero.
And ye shall observe to do all the statutes and the ordinances which I set before you this day.

< Deuteronomo 11 >