< Amosi 4 >

1 Imvani mawu awa, inu ngʼombe zazikazi za ku Basani, okhala pa Phiri la Samariya, inu akazi amene mumapondereza anthu osauka ndi kuzunza anthu osowa ndi kumanena kwa amuna anu kuti, “Tipatseni zakumwa!”
Hear this word, ye cows of Bashan, who are in the mountain of Samaria, who oppress the poor, who crush the needy, who say to their lords, Bring, and let us drink.
2 Ambuye Yehova, mwa kuyera mtima kwake walumbira kuti, “Nthawi idzafika ndithu pamene adzakukokani ndi ngowe, womaliza wa inu adzakokedwa ndi mbedza.
The lord Jehovah has sworn by his holiness, that, lo, the days shall come upon you, that they shall take you away with hooks, and your residue with fish-hooks.
3 Mudzatulukira mʼmingʼalu ya pa khoma aliyense payekhapayekha, ndipo mudzatayidwa ku Harimoni,” akutero Yehova.
And ye shall go out at the breaches, each one straight before her, and ye shall cast yourselves into Harmon, says Jehovah.
4 “Bwerani ku Beteli mudzachimwe; ndi ku Giligala kuti mudzapitirize kuchimwa. Bweretsani nsembe zanu mmawa uliwonse, bweretsani chakhumi chanu masiku atatu aliwonse.
Come to Bethel and transgress, to Gilgal and multiply transgression. And bring your sacrifices every morning, and your tithes every three days.
5 Wotchani buledi wokhala ndi yisiti ngati nsembe yachiyamiko ndi kumanyadira poyera za zopereka zanu zaufulu. Inu Aisraeli, zinyadireni nsembezo, pakuti izi ndi zimene mumakonda kuchita,” akutero Ambuye Yehova.
And offer a sacrifice of thanksgiving of that which is leavened, and proclaim freewill offerings, and publish them. For this pleases you, O ye sons of Israel, says the lord Jehovah.
6 “Ndine amene ndinakusendetsani milomo mʼmizinda yanu yonse, ndipo munasowa chakudya mʼmizinda yanu. Komatu inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
And I also have given you cleanness of teeth in all your cities, and want of bread in all your places, yet ye have not returned to me, says Jehovah.
7 “Ndinenso amene ndinamanga mvula patangotsala miyezi itatu kuti mukolole. Ndinagwetsa mvula pa mzinda wina, koma pa mzinda wina ayi, mvula inkagwa pa munda wina; koma sinagwe pa munda wina ndipo mbewu zinawuma.
And I also have withheld the rain from you, when there were yet three months to the harvest. And I caused it to rain upon one city, and caused it not to rain upon another city. One piece was rained upon, and the piece upon which it did not rain withered.
8 Anthu ankayenda mzinda ndi mzinda kufuna madzi, koma sanapeze madzi okwanira kumwa. Komabe inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
So two or three cities wandered to one city to drink water, and were not satisfied. Yet ye have not returned to me, says Jehovah.
9 “Nthawi zambiri ndinakantha mbewu zanu ndiponso minda ya mpesa, ndinayikantha ndi chinsikwi ndiponso ndi chiwawu. Dzombe linawononga mikuyu yanu ndi mitengo ya olivi. Komabe inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
I have smitten you with blasting and mildew. The multitude of your gardens and your vineyards and your fig trees and your olive trees the palmer-worm has devoured. Yet ye have not returned to me, says Jehovah.
10 “Ine ndinabweretsa miliri pakati panu monga ndinachitira ku Igupto. Ndinapha anyamata anu ndi lupanga, ndinapereka akavalo anu kwa adani. Ndinakununkhitsani fungo la mitembo lochokera mʼmisasa yanu ya nkhondo. Komatu inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
I have sent among you the pestilence according to the manner of Egypt. I have slain your young men with the sword, and have carried away your horses, and I have made the stench of your camp to come up even into your nostrils. Yet ye have not returned to me, says Jehovah.
11 “Ndinawononga ena mwa inu monga ndinawonongera Sodomu ndi Gomora. Inu munali ngati chikuni choyaka chimene chafumulidwa pa moto. Komabe inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
I have overthrown cities among you, as when God overthrew Sodom and Gomorrah, and ye were as a brand plucked out of the burning. Yet ye have not returned to me, says Jehovah.
12 “Choncho izi ndi zimene ndidzakuchitire iwe Israeli, chifukwa ndidzakuchitira zimenezi, konzekera kukumana ndi Mulungu wako, iwe Israeli.”
Therefore thus I will do to thee, O Israel, and because I will do this to thee, prepare to meet thy God, O Israel.
13 Iye amene amawumba mapiri, amalenga mphepo, ndipo amawululira munthu za mʼmaganizo ake, Iye amene amasandutsa usana kuti ukhale mdima, ndipo amayenda pa zitunda za dziko lapansi, dzina lake ndi Yehova Mulungu Wamphamvuzonse.
For, lo, he who forms the mountains, and creates the wind, and declares to man what is his thought, who makes the morning darkness, and treads upon the high places of the earth-Jehovah, the God of hosts, is his name.

< Amosi 4 >