< Amosi 3 >

1 Inu Aisraeli, imvani mawu awa amene Yehova wayankhula kutsutsana nanu, kutsutsana ndi banja lonse limene analitulutsa mu Igupto:
Hear this word that Jehovah has spoken against you, O sons of Israel, against the whole family which I brought up out of the land of Egypt, saying,
2 “Inu nokha ndi amene ndinakusankhani pakati pa mabanja onse a dziko lapansi; nʼchifukwa chake ndidzakulangani chifukwa cha machimo anu onse.”
You only I have known of all the families of the earth. Therefore I will visit upon you all your iniquities.
3 Kodi anthu awiri nʼkuyendera limodzi asanapangane?
Shall two walk together unless they have agreed?
4 Kodi mkango umabangula mʼnkhalango usanagwire nyama? Kodi msona wamkango umalira mʼphanga mwake pamene sunagwire kanthu?
Will a lion roar in the forest, when he has no prey? Will a young lion cry out of his den, if he has taken nothing?
5 Kodi mbalame nʼkutera pa msampha pamene palibe nyambo yake? Kodi msampha umafwamphuka usanakole kanthu?
Can a bird fall in a snare upon the earth, where no net is set for him? Shall a snare spring up from the ground, and have taken nothing at all?
6 Kodi pamene lipenga la nkhondo lalira mu mzinda, anthu sanjenjemera? Pamene tsoka lafika mu mzinda, kodi si Yehova amene wachititsa zimenezo?
Shall the trumpet be blown in a city, and the people not be afraid? Shall evil befall a city, and Jehovah has not done it?
7 Zoonadi Ambuye Yehova sachita kanthu asanawulule zimene akufuna kuchita kwa atumiki ake, aneneri.
Surely the lord Jehovah will do nothing unless he reveals his secret to his servants the prophets.
8 Mkango wabangula, ndani amene sachita mantha? Ambuye Yehova wayankhula, ndani amene sanganenere?
The lion has roared, who will not fear? The lord Jehovah has spoken, who can but prophesy?
9 Lengezani zimenezi ku nyumba zaufumu za ku Asidodi ndiponso ku nyumba zaufumu za ku Igupto: “Sonkhanani ku mapiri a ku Samariya; onani chisokonezo pakati pake ndiponso kuponderezana pakati pa anthu ake.”
Publish ye in the palaces at Ashdod, and in the palaces in the land of Egypt, and say, Assemble yourselves upon the mountains of Samaria, and behold what great tumults are in it, and what oppressions are in the midst of it.
10 “Iwo sadziwa kuchita zolungama, ndipo amadzaza malo awo otetezedwa ndi zinthu zolanda ku nkhondo ndi zakuba,” akutero Yehova.
For they do not know to do right, says Jehovah, who store up violence and robbery in their palaces.
11 Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akunena izi: “Mdani adzalizungulira dzikoli; iye adzagwetsa malinga ako, ndi kufunkha nyumba zako zaufumu.”
Therefore thus says the lord Jehovah: An adversary shall be, even round about the land, and he shall bring down thy strength from thee, and thy palaces shall be plundered.
12 Yehova akuti, “Monga mʼbusa amalanditsa mʼkamwa mwa mkango miyendo iwiri yokha kapena msonga yokha ya khutu, moteronso ndimo mmene adzapulumukire Aisraeli amene amakhala mu Samariya pa msonga za mabedi awo, ndi ku Damasiko pa akakhutagona awo.”
Thus says Jehovah: As the shepherd rescues out of the mouth of the lion two legs, or a piece of an ear, so shall the sons of Israel be rescued who sit in Samaria in the corner of a couch, and on the silken cushions of a bed.
13 “Imvani izi ndipo mupereke umboni wotsutsa nyumba ya Yakobo,” akutero Ambuye, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse.
Hear ye, and testify against the house of Jacob, says the lord Jehovah, the God of hosts.
14 “Pa tsiku limene ndidzalange Israeli chifukwa cha machimo ake, ndidzagumula maguwa ansembe a ku Beteli; nyanga za guwa zidzathyoka ndipo zidzagwa pansi.
For in the day that I shall visit the transgressions of Israel upon him, I will also visit the altars of Bethel, and the horns of the altar shall be cut off, and fall to the ground.
15 Ndidzagwetsa nyumba ya pa nthawi yozizira pamodzi ndi nyumba ya pa nthawi yotentha; nyumba zokongoletsedwa ndi minyanga ya njovu zidzawonongedwa ndipo nyumba zikuluzikulu zidzaphwasulidwa,” akutero Yehova.
And I will smite the winter house with the summer house, and the houses of ivory shall perish, and the great houses shall have an end, says Jehovah.

< Amosi 3 >