< Amosi 6 >

1 Tsoka kwa amene simukulabadira kanthu ku Ziyoni, ndiponso kwa inu amene mukukhala mwamtendere pa Phiri la Samariya, inu anthu otchuka ochokera ku mtundu wa anthu omveka, kumene Aisraeli amafikako!
Woe to those who are at ease in Zion, and to those who are secure in the mountain of Samaria, the notable men of the chief of the nations, to whom the house of Israel come!
2 Pitani ku mzinda wa Kaline mukawuyangʼane; mukapitenso ku Hamati-raba mzinda waukulu uja, ndipo mukatsikirenso ku Gati kwa Afilisti. Kodi mizinda imeneyi ndi yopambana maufumu anu awiriwa? Kodi dziko lawo ndi lalikulu kupambana lanu?
Pass ye to Calneh, and see, and from there go ye to Hamath the great, then go down to Gath of the Philistines. Are they better than these kingdoms? Or is their border greater than your border?
3 Inu simulabadirako kuti tsiku loyipa lidzafika, zochita zanu zimafulumizitsa ulamuliro wankhanza.
Ye who put far away the evil day, and cause the seat of violence to come near,
4 Mumagona pa mabedi owakongoletsa ndi minyanga ya njovu, mumagona pa mipando yanu ya wofuwofu. Mumadya ana ankhosa onona ndi ana angʼombe onenepa.
who lie upon beds of ivory, and stretch themselves upon their couches, and eat the lambs out of the flock, and the calves out of the midst of the stall,
5 Mumayimba azeze anu ndi kumangopeka nyimbo pa zingʼwenyengʼwenye ngati Davide.
who sing idle songs to the sound of the viol, who invent for themselves instruments of music, like David,
6 Mumamwera vinyo mʼzipanda zodzaza ndipo mumadzola mafuta abwino kwambiri, koma simumva chisoni ndi kuwonongeka kwa Yosefe.
who drink wine in bowls, and anoint themselves with the chief oils, but they are not grieved for the affliction of Joseph.
7 Nʼchifukwa chake inu mudzakhala mʼgulu la anthu oyamba kupita ku ukapolo; maphwando ndi zikondwerero zanu zidzatheratu.
Therefore they shall now go captive with the first who go captive, and the revelry of those who stretched themselves shall pass away.
8 Ambuye Yehova walumbira mʼdzina lake. Yehova Mulungu Wamphamvuzonse walengeza kuti, “Ndimanyansidwa ndi kunyada kwa Yakobo, ndimadana ndi nyumba zake zaufumu; Ine ndidzawupereka mzindawu pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo.”
The lord Jehovah has sworn by himself, says Jehovah, the God of hosts: I abhor the excellency of Jacob, and hate his palaces, therefore I will deliver up the city with all that is therein.
9 Ngati anthu khumi otsala adzabisala mʼnyumba imodzi, nawonso adzafa ndithu.
And it shall come to pass, if there remain ten men in one house, that they shall die.
10 Ndipo ngati mʼbale wake wa wina wakufayo, woyenera kusamala za maliro, adzafika kudzatulutsa mitembo mʼnyumbamo nʼkufunsa aliyense amene akubisalabe mʼnyumbamo kuti, “Kodi uli ndi wina wamoyo mʼmenemo?” Ndipo munthu wobisalayo ndi kuyankha kuti, “Ayi,” mʼbaleyo adzanena kuti, “Khala chete! Ife tisayerekeze kutchula dzina la Yehova.”
And when a man's uncle shall take him up, even he who burns him, to bring out the bones out of the house, and shall say to him who is in the innermost parts of the house, Is there yet any with thee? and he shall say, No, then he shall say, Hold thy peace, for we may not make mention of the name of Jehovah.
11 Pakuti Yehova walamula kuti nyumba zikuluzikulu Iye adzazigamulagamula, ndipo nyumba zazingʼono zidzasanduka maduka okhaokha.
For, behold, Jehovah commands, and the great house shall be smitten with breaches, and the little house with clefts.
12 Kodi akavalo amathamanga pa thanthwe? Kodi wina amatipula ndi ngʼombe mʼnyanja? Koma chiweruzo cholungama mwachisandutsa kukhala zinthu zakupha ndipo chipatso cha chilungamo mwachisandutsa kukhala chowawa.
Shall horses run upon the rock? Will a man plow there with oxen? That ye have turned justice into gall, and the fruit of righteousness into wormwood,
13 Inu amene mukunyadira kuti munagonjetsa Lo Debara ndipo mukunena kuti, “Kodi sitinatenge Karinaimu ndi mphamvu zathu zokha?”
ye who rejoice in a thing of nothing, who say, Have we not taken to us horns by our own strength?
14 Koma Yehova Mulungu Wamphamvuzonse akulengeza kuti, “Inu nyumba ya Israeli, ndidzakudzutsirani mtundu wina wa anthu umene udzakuzunzani kuchokera ku Lebo Hamati mpaka ku Chigwa cha Araba.”
For, behold, I will raise up against you a nation, O house of Israel, says Jehovah, the God of hosts, and they shall afflict you from the entrance of Hamath to the brook of the Arabah.

< Amosi 6 >