< Amosi 5 >

1 Israeli, imva mawu awa, nyimbo ya maliro imene ndikuyimba za iweyo:
Hear ye this word which I take up for a lamentation over you, O house of Israel.
2 “Namwali Israeli wagwa, moti sadzadzukanso, wasiyidwa mʼdziko lake lomwe, popanda woti ndi kumudzutsa.”
The virgin of Israel is fallen; she shall no more rise. She is cast down upon her land; there is none to raise her up.
3 Ambuye Yehova akuti, “Mzinda umene udzapite ku nkhondo ndi anthu 1,000 amphamvu udzatsala ndi anthu 100 okha; mzinda umene udzapite ku nkhondo ndi anthu 100 amphamvu udzatsala ndi anthu khumi okha basi.”
For thus says the lord Jehovah: The city that went forth a thousand shall have a hundred left, and that which went forth a hundred shall have ten left, to the house of Israel.
4 Zimene Yehova akunena kwa nyumba ya Israeli ndi izi: “Mundifunefune kuti mukhale ndi moyo;
For thus says Jehovah to the house of Israel: Seek ye me, and ye shall live.
5 musafunefune Beteli, musapite ku Giligala, musapite ku Beeriseba. Pakuti Giligala adzatengedwa ndithu kupita ku ukapolo, ndipo Beteli adzawonongekeratu.”
But seek not Bethel, nor enter into Gilgal, and pass not to Beersheba. For Gilgal shall surely go into captivity, and Bethel shall come to naught.
6 Funani Yehova kuti mukhale ndi moyo, mukapanda kutero Iye adzatentha nyumba ya Yosefe ngati moto; motowo udzawononga, ndipo sipadzakhala wina wozimitsa motowo ku Beteli.
Seek Jehovah, and ye shall live, lest he break out like fire in the house of Joseph, and it devour, and there be none to quench it in Bethel.
7 Inu amene mumasandutsa chiweruzo cholungama kukhala chowawa ndi kunyoza chilungamo.
Ye who turn justice to wormwood, and cast down righteousness to the earth,
8 (Iye amene analenga nyenyezi za Nsangwe ndi Akamwiniatsatana, amene amasandutsa mdima kuti ukhale mmawa ndi kudetsa usana kuti ukhale usiku, amene amayitana madzi a mʼnyanja ndi kuwathira pa dziko lapansi, Yehova ndiye dzina lake.
seek him who makes the Pleiades and Orion, and turns the shadow of death into the morning, and makes the day dark with night, who calls for the waters of the sea, and pours them out upon the face of the earth (Jehovah is his name),
9 Iyeyo amabweretsa chiwonongeko modzidzimutsa pa anthu amphamvu ndi kuwononga mizinda yotetezedwa),
who brings sudden destruction upon the strong, so that destruction comes upon the fortress.
10 inu mumadana ndi amene amadzudzula mʼbwalo la milandu ndi kunyoza amene amanena zoona.
They hate him who reproves in the gate, and they abhor him who speaks uprightly.
11 Mumapondereza munthu wosauka ndi kumukakamiza kuti akupatseni tirigu. Nʼchifukwa chake, ngakhale mwamanga nyumba zamiyala yosema, inuyo simudzakhalamo. Ngakhale mwalima minda yabwino ya mphesa, inu simudzamwa vinyo wake.
Inasmuch therefore as ye trample upon the poor, and take exactions of wheat from him. Ye have built houses of hewn stone, but ye shall not dwell in them. Ye have planted pleasant vineyards, but ye shall not drink the wine thereof.
12 Pakuti Ine ndikudziwa kuchuluka kwa zolakwa zanu ndi kukula kwa machimo anu. Inu mumapondereza anthu olungama ndi kulandira ziphuphu ndipo anthu osauka simuwaweruza mwachilungamo mʼmabwalo anu amilandu.
For I know how manifold are your transgressions, and how mighty are your sins-ye who afflict the just man, who take a bribe, and who turn aside the needy in the gate.
13 Nʼchifukwa chake pa nthawi yotere munthu wanzeru sayankhulapo kanthu, popeza ndi nthawi yoyipa.
Therefore he who is prudent shall keep silence in such a time, for it is an evil time.
14 Muyike mtima wanu pa zabwino osati pa zoyipa, kuti mukhale ndi moyo. Mukatero Yehova Mulungu Wamphamvuzonse adzakhala nanu, monga mmene mumanenera kuti ali nanu.
Seek good, and not evil, that ye may live, and so Jehovah, the God of hosts, will be with you, as ye say.
15 Mudane ndi zoyipa, mukonde zabwino; mukhazikitse chiweruzo cholungama mʼmabwalo anu amilandu. Mwina mwake Yehova Mulungu Wamphamvuzonse adzachitira chifundo anthu otsala a mʼbanja la Yosefe.
Hate the evil, and love the good, and establish justice in the gate. It may be that Jehovah, the God of hosts, will be gracious to the remnant of Joseph.
16 Choncho izi ndi zimene Ambuye, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, akunena: “Mʼmisewu monse mudzakhala kulira mofuwula, ndi kulira chifukwa cha kuwawa kwa masautso kudzakhala paliponse. Adzayitana alimi kuti adzalire, ndipo anthu odziwa maliridwe anthetemya adzalira mofuwula.
Therefore thus says Jehovah, the God of hosts, the Lord: Wailing shall be in all the broad ways. And they shall say in all the streets, Alas! Alas! And they shall call the husbandman to mourning, and such as are skilful in lamentation to wailing.
17 Mʼminda yonse ya mpesa mudzakhala kulira kokhakokha, pakuti Ine ndidzadutsa pakati panu,” akutero Yehova.
And in all vineyards shall be wailing, for I will pass through the midst of thee, says Jehovah.
18 Tsoka kwa inu amene mumalakalaka tsiku la Yehova! Chifukwa chiyani mumalakalaka tsiku la Yehova? Tsikulo kudzakhala mdima osati kuwala.
Woe to you who desire the day of Jehovah! Why would ye have the day of Jehovah? It is darkness, and not light.
19 Lidzakhala ngati tsiku limene munthu pothawa mkango amakumana ndi chimbalangondo, ngati pamene munthu walowa mʼnyumba, natsamira dzanja lake pa khoma ndipo njoka nʼkuluma.
As if a man fled from a lion, and a bear met him, or went into the house and leaned his hand on the wall, and a serpent bit him.
20 Kodi tsiku la Yehova silidzakhala mdima osati kuwala, mdima wandiweyani, popanda powala pena paliponse?
Shall not the day of Jehovah be darkness, and not light, even very dark, and no brightness in it?
21 “Ndimadana nawo masiku anu achikondwerero ndipo ndimawanyoza; sindikondwera nayo misonkhano yanu.
I hate, I despise your feasts, and I will take no delight in your solemn assemblies.
22 Ngakhale mupereke nsembe zopsereza ndi nsembe zachakudya, Ine sindidzazilandira. Ngakhale mupereke nsembe zabwino zachiyanjano, Ine sindidzaziyangʼana nʼkomwe.
Yea, though ye offer me your burnt offerings and meal offerings, I will not accept them, nor will I regard the peace offerings of your fat beasts.
23 Musandisokose nazo nyimbo zanu! Sindidzamvetsera kulira kwa azeze anu.
Take thou away from me the noise of thy songs, for I will not hear the melody of thy viols.
24 Koma chiweruzo cholungama chiyende ngati madzi, chilungamo ngati mtsinje wosaphwa!
But let justice roll down as waters, and righteousness as a mighty stream.
25 “Kodi pa zaka makumi anayi zimene munakhala mʼchipululu muja munkandibweretsera nsembe ndi zopereka, inu nyumba ya Israeli?
Did ye bring sacrifices and offerings to me in the wilderness forty years, O house of Israel?
26 Inu mwanyamula kachisi wa mfumu yanu, ndi nyenyezi ija Kaiwani, mulungu wanu, mafano amene munadzipangira.
Yea, ye have borne the tabernacle of Moloch, and the star of your god Remphan, your images which ye made to yourselves.
27 Nʼchifukwa chake Ine ndidzakupititsani ku ukapolo, kutali kupitirira ku Damasiko,” akutero Yehova, amene dzina lake ndi Mulungu Wamphamvuzonse.
Therefore I will cause you to go into captivity beyond Damascus, says Jehovah, whose name is the God of hosts.

< Amosi 5 >